< Nehemija 5 >

1 I stade velika vika ljudi i žena na braæu njihovu Judejce.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Jer neki govorahu: nas i sinova naših i kæeri naših ima mnogo; da dobavimo žita da jedemo i ostanemo živi.
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 Drugi opet govorahu: da založimo polja svoja i vinograde i kuæe da dobijemo žita u ovoj gladi.
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 Još drugi govorahu: da uzajmimo novaca na polja svoja i vinograde za danak carski.
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 A tijelo je naše kao tijelo braæe naše, sinovi naši kao njihovi sinovi, i eto treba da damo sinove svoje i kæeri svoje u roblje, i neke kæeri naše veæ su robinje, a mi ne možemo ništa, jer polja naša i vinograde naše drže drugi.
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Zato se rasrdih vrlo kad èuh viku njihovu i te rijeèi.
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 I smislih u srcu svom i ukorih knezove i poglavare, i rekoh im: vi meæete bremena svaki na brata svojega. I sazvah veliki zbor njih radi.
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 I rekoh im: mi otkupismo koliko mogosmo braæu svoju Judejce što bjehu prodani narodima; a vi li æete prodavati braæu svoju ili æe se prodavati nama? A oni umukoše i ne naðoše što bi odgovorili.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 I rekoh: nije dobro što radite. Ne treba li vam hoditi u strahu Boga našega da nam se ne rugaju narodi, neprijatelji naši?
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 I ja i braæa moja i momci moji davali smo im novaca i žita; ali oprostimo im taj dug.
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Hajde vratite im danas polja njihova i vinograde i maslinike i kuæe i što im na stotinu uzimate od novca i žita i vina i ulja.
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 A oni odgovoriše: vratiæemo i neæemo iskati od njih; uèiniæemo kako veliš. Tada sazvah sveštenike, i zakleh ih da æe tako uèiniti.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 I istresoh njedra svoja i rekoh: ovako da istrese Bog svakoga iz kuæe njegove i iz truda njegova ko god ne ispuni ove rijeèi, i ovako da se istrese i bude prazan. I sav zbor reèe: amin. I hvališe Gospoda, i uèini narod po toj rijeèi.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 I otkad mi car zapovjedi da im budem upravitelj u zemlji Judinoj, od godine dvadesete do trideset druge godine cara Artakserksa, dvanaest godina, ja i braæa moja ne jedosmo hrane upraviteljske.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 A preðašnji upravitelji koji bijahu prije mene bijahu teški narodu uzimajuæi od njega hljeba i vina osim èetrdeset sikala srebra, i sluge njihove zapovijedahu po narodu; ali ja tako ne èinih bojeæi se Boga.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 Nego i oko graðenja zida radih, i ne kupismo njive; i svi momci moji bijahu skupa ondje na poslu.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 I Judejaca i poglavara sto i pedeset ljudi i koji dolažahu k nama iz okolnijeh naroda bijahu za mojim stolom.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 I gotovljaše se svaki dan po jedno goveèe, šest ovaca izabranijeh, i ptice gotovljahu mi se, i svakih deset dana davaše se svakojakoga vina izobila. I opet ne iskah hrane upraviteljske; jer služba bješe teška narodu.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Pomeni me, Bože moj, na dobro za sve što sam èinio ovomu narodu.
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.

< Nehemija 5 >