< Jov 30 >

1 A sada smiju mi se mlaði od mene, kojima otaca ne bih bio htio metnuti sa psima stada svojega.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 A na što bi mi i bila sila ruku njihovijeh? u njima bješe propala starost.
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Od siromaštva i gladi samoæovahu bježeæi na suha, mraèna, pusta i opustošena mjesta;
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Koji brahu lobodu po èestama, i smrekovo korijenje bješe im hrana.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 Izmeðu ljudi bijahu izgonjeni i vikaše se za njima kao za lupežem.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 Življahu po strašnijem uvalama, po jamama u zemlji i u kamenu.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Po grmovima rikahu, pod trnjem se skupljahu.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Bijahu ljudi nikakvi i bez imena, manje vrijedni nego zemlja.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 I njima sam sada pjesma, i postah im prièa.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Gade se na me, idu daleko od mene i ne ustežu se pljuvati mi u lice.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Jer je Bog odapeo moju tetivu i muke mi zadao te zbaciše uzdu preda mnom.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 S desne strane ustaju momci, potkidaju mi noge, i nasipaju put k meni da me upropaste.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Raskopaše moju stazu, umnožiše mi muke, ne treba niko da im pomaže.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Kao širokim prolomom naviru, i navaljuju preko razvalina.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Strahote navališe na me, i kao vjetar tjeraju dušu moju, i kao oblak proðe sreæa moja.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 I sada se duša moja ražljeva u meni, stigoše me dani muèni.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 Noæu probada mi kosti u meni, i žile moje ne odmaraju se.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Od teške sile promijenilo se odijelo moje, i kao ogrlica u košulje moje steže me.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Bacio me je u blato, te sam kao prah i pepeo.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Vièem k tebi, a ti me ne slušaš; stojim pred tobom, a ti ne gledaš na me.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Pretvorio si mi se u ljuta neprijatelja; silom ruke svoje suprotiš mi se.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Podižeš me u vjetar, posaðuješ me na nj, i rastapaš u meni sve dobro.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Jer znam da æeš me odvesti na smrt i u dom odreðeni svjema živima.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Ali neæe pružiti ruke svoje u grob; kad ih stane potirati, oni neæe vikati.
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Nijesam li plakao radi onoga koji bijaše u zlu? nije li duša moja žalosna bivala radi ubogoga?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Kad se dobru nadah, doðe mi zlo; i kad se nadah svjetlosti, doðe mrak.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Utroba je moja uzavrela, i ne može da se umiri, zadesiše me dani muèni.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Hodim crn, ne od sunca, ustajem i vièem u zboru.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Brat postah zmajevima i drug sovama.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Pocrnjela je koža na meni i kosti moje posahnuše od žege.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Gusle se moje pretvoriše u zapijevku, i svirala moja u plaè.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Jov 30 >