< Isaija 4 >
1 I u ono vrijeme sedam æe žena uhvatiti jednoga èovjeka govoreæi: svoj æemo hljeb jesti i svoje æemo odijelo nositi, samo da se zovemo tvojim imenom, skini s nas sramotu.
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 U ono vrijeme biæe klica Gospodnja na slavu i èast, i plod zemaljski na krasotu i diku ostatku Izrailjevu.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 I ko ostane u Sionu i ko još bude u Jerusalimu, zvaæe se svet, svaki ko bude zapisan za život u Jerusalimu,
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 Kad Gospod opere neèistotu kæeri Sionskih i iz Jerusalima oèisti krv njegovu duhom koji sudi i sažiže.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 Gospod æe stvoriti nad svakim stanom na gori Sionskoj i nad zborovima njezinijem oblak danju s dimom i svjetlost plamena ognjenoga noæu, jer æe nad svom slavom biti zaklon.
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 I biæe koliba, da sjenom zaklanja danju od vruæine i da bude utoèište i zaklon od poplave i od dažda.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.