< Postanak 16 >

1 Ali Sara žena Avramova ne raðaše mu djece. A imaše robinju Misirku, po imenu Agaru.
Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
2 Pa reèe Sara Avramu: Gospod me je zatvorio da ne rodim; nego idi k robinji mojoj, ne bih li dobila djece od nje. I Avram prista na rijeè Sarinu.
ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
3 I Sara žena Avramova uze Agaru Misirku robinju svoju, i dade je za ženu Avramu mužu svojemu poslije deset godina otkako se nastani Avram u zemlji Hananskoj.
Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
4 I on otide k Agari, i ona zatrudnje; a kad vidje da je trudna, ponese se od gospoðe svoje.
Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
5 A Sara reèe Avramu: uvreda moja pada na tebe; ja ti metnuh na krilo robinju svoju, a ona vidjevši da je trudna ponese se od mene. Gospod æe suditi meni i tebi.
Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
6 A Avram reèe Sari: eto, robinja je tvoja u tvojim rukama, èini s njom što ti je volja. I Sara je stade zlostaviti, te ona pobježe od nje.
Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
7 Ali anðeo Gospodnji naðe je kod studenca u pustinji, kod studenca na putu u Sur.
Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
8 I reèe joj: Agaro, robinjo Sarina, otkuda ideš, kuda li ideš? A ona reèe: bježim od Sare gospoðe svoje.
Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
9 A anðeo joj Gospodnji reèe: vrati se gospoði svojoj i pokori joj se.
Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
10 Opet joj reèe anðeo Gospodnji: umnožiæu veoma sjeme tvoje, da se neæe moæi prebrojiti od množine.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
11 Jošte joj reèe anðeo Gospodnji: eto si trudna, i rodiæeš sina, i nadjeni mu ime Ismailo; jer je Gospod vidio muku tvoju.
Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
12 A biæe èovjek ubojica; ruka æe se njegova dizati na svakoga a svaèija na njega, i nastavaæe na pogledu svoj braæi svojoj.
Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
13 Tada Agara prizva ime Gospoda koji govori s njom: ti si Bog, koji vidi. Jer govoraše: zar još gledam iza onoga koji me vidje?
Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
14 Toga radi zove se studenac onaj studenac živoga koji me vidi; a on je izmeðu Kadisa i Varada.
Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
15 I rodi Agara Avramu sina; i nadjede Avram sinu svojemu, kojega mu rodi Agara, ime Ismailo.
Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
16 A bješe Avramu osamdeset i šest godina kad mu Agara rodi Ismaila.
Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

< Postanak 16 >