< Jezekilj 35 >

1 Opet mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sine èovjeèji, okreni lice svoje prema gori Siru i prorokuj protiv nje.
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 I reci: ovako veli Gospod Gospod: evo me na tebe, goro Sire! i dignuæu ruku svoju na te, i opustiæu te sasvijem.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Gradove æu tvoje opustiti, i ti æeš biti pustoš, i poznaæeš da sam ja Gospod.
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Što je u tebe vjeèno neprijateljstvo, i rasipaš sinove Izrailjeve maèem u nevolji njihovoj, kad je kraj bezakonju njihovu,
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 Zato, tako ja bio živ, govori Gospod Gospod, krvi æu te predati i krv æe te goniti, jer ne mrziš na krv, krv æe te goniti.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 I obratiæu goru Sir sasvijem u pustoš, da niko neæe dolaziti ni odlaziti.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 I napuniæu gore njezine pobijenijeh njezinijeh; na humovima tvojim i u dolinama tvojim i po svijem potocima tvojim padaæe pobijeni od maèa.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Vjeènu pustinju naèiniæu od tebe i gradovi se tvoji neæe opraviti, i poznaæete da sam ja Gospod.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Što govoriš: ova dva naroda i ove dvije zemlje moje æe biti, i naslijediæemo ih, ako i jest Gospod bio ondje,
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 Zato, tako ja živ bio, govori Gospod Gospod, uèiniæu po gnjevu tvom i po zavisti tvojoj, s kojom si postupala iz mržnje prema njima, i biæu poznat meðu njima kad ti sudim.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 I poznaæeš da sam ja Gospod èuo sve tvoje hule koje si govorila na gore Izrailjeve rekavši: opustješe, nama su dane da ih jedemo.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 I velièaste se suprot meni ustima svojim, i množiste na me rijeèi svoje; èuo sam.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Ovako veli Gospod Gospod: kad se sva zemlja stane veseliti, tebe æu opustiti.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 Kako si se ti veselila našljedstvu doma Izrailjeva što opustje, tako æu i tebi uèiniti: opustjeæeš, goro Sire, i sva zemljo Edomska; i poznaæe se da sam ja Gospod.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Jezekilj 35 >