< Jezekilj 26 >
1 A jedanaeste godine prvi dan mjeseca doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Sine èovjeèji, što Tir govori za Jerusalim: ha, ha! razbiše se vrata narodima, obratiše se k meni, napuniæu se kad opustje;
“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’
3 Zato ovako veli Gospod Gospod: evo mene na te, Tire, i dovešæu mnoge narode na te kao da bih doveo more s valima njegovijem.
Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja.
4 I oni æe obaliti zidove Tirske i kule u njemu raskopati, i omešæu prah njegov i pretvoriæu ga u go kamen.
Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala.
5 I postaæe mjesto da se razastiru mreže usred mora, jer ja govorih, veli Gospod Gospod, i biæe grabež narodima.
Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina.
6 I kæeri njegove po polju izginuæe od maèa, i poznaæe da sam ja Gospod.
Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
7 Jer ovako veli Gospod Gospod: evo, ja æu dovesti na Tir Navuhodonosora cara Vavilonskoga sa sjevera, cara nad carevima, s konjma i s kolima i s konjicima i s vojskama i mnogim narodom.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo.
8 Kæeri tvoje po polju pobiæe maèem, i naèiniæe prema tebi kule, i iskopaæe opkope prema tebi, i podignuæe prema tebi štitove.
Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe.
9 I namjestiæe ubojne sprave prema zidovima tvojim, i razvaliæe kule tvoje oružjem svojim.
Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake.
10 Od mnoštva konja njegovijeh pokriæe te prah, od praske konjika i toèkova i kola zatrešæe se zidovi tvoji, kad stane ulaziti na tvoja vrata kao što se ulazi u grad isprovaljivan.
Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa.
11 Kopitama konja svojih izgaziæe sve ulice tvoje, pobiæe narod tvoj maèem, i stupovi sile tvoje popadaæe na zemlju.
Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa.
12 I poplijeniæe blago tvoje i razgrabiti trg tvoj, i razvaliæe zidove tvoje i lijepe kuæe tvoje razoriti, i kamenje tvoje i drva tvoja i prah tvoj baciæe u vodu.
Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja.
13 I prekinuæu jeku pjesama tvojih, i glas kitara tvojih neæe se više èuti.
Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso.
14 I uèiniæu od tebe go kamen, biæeš mjesto gdje se razastiru mreže, neæeš se više sazidati; jer ja Gospod govorih, veli Gospod Gospod.
Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
15 Ovako veli Gospod Gospod Tiru: neæe li se zadrmati ostrva od praske padanja tvojega, kad zajaoèu ranjenici, kad pokolj bude u tebi?
“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako.
16 Svi æe knezovi morski siæi s prijestola svojih i skinuæe sa sebe plašte i svuæi sa sebe vezene haljine, i obuæi æe se u strah; sjedeæe na zemlji, i drktaæe svaki èas i èuditi se tebi.
Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera.
17 I naricaæe za tobom i govoriæe ti: kako propade, slavni grade! u kom življahu pomorci, koji bijaše jak na moru, ti i stanovnici tvoji, koji strah zadavahu svjema koji življahu u tebi.
Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe: “‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka, wodzaza ndi anthu a ku nyanja! Unali wamphamvu pa nyanja, iwe ndi nzika zako; unkaopseza anthu onse amene ankakhala kumeneko.
18 Sad æe se uzdrhtati ostrva kad padneš, i smešæe se ostrva po moru od propasti tvoje.
Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera chifukwa cha kugwa kwako; okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu chifukwa cha kugwa kwako.’
19 Jer ovako veli Gospod Gospod: kad te uèinim pustijem gradom, kao što su gradovi u kojima se ne živi, kad pustim na te bezdanu, i velika te voda pokrije,
“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize.
20 I kad te svalim s onima koji slaze u jamu k starom narodu, i namjestim te na najdonjim krajevima zemlje, u pustinji staroj s onima koji slaze u jamu, da se ne živi u tebi, tada æu opet postaviti slavu u zemlji živijeh.
Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo.
21 Uèiniæu da budeš strahota kad te nestane, i tražiæe te i neæeš se naæi dovijeka, govori Gospod Gospod.
Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”