< Ponovljeni Zakon 29 >

1 Ovo su rijeèi zavjeta koji zapovjedi Gospod Mojsiju da uèini sa sinovima Izrailjevijem u zemlji Moavskoj, osim zavjeta koji je uèinio s njima na Horivu.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 I sazva Mojsije sve sinove Izrailjeve i reèe im: vidjeli ste sve što uèini Gospod na vaše oèi u zemlji Misirskoj Faraonu i svijem slugama njegovijem i svoj zemlji njegovoj,
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 Kušanja velika, koja vidješe oèi tvoje, one znake i èudesa velika.
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 Ali vam ne dade Gospod srca, da razumijete, ni oèiju, da vidite, ni ušiju, da èujete do ovoga dana.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 I vodih vas èetrdeset godina po pustinji; ne ovetšaše haljine vaše na vama, niti obuæa tvoja ovetša na nogama tvojima.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 Hljeba ne jedoste, ni piste vina i silovita piæa, da biste poznali da sam ja Gospod Bog vaš.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 I kad doðoste na ovo mjesto, izide Sion car Esevonski i Og car Vasanski pred nas u boj; i pobismo ih.
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 I uzesmo zemlju njihovu, i dadosmo je u našljedstvo plemenu Ruvimovu i plemenu Gadovu i polovini plemena Manasijina.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Zato držite rijeèi ovoga zavjeta i tvorite ih, da biste napredovali u svemu što radite.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Vi stojite danas svi pred Gospodom Bogom svojim, glavari od plemena vaših, starješine vaše i upravitelji vaši, svi ljudi Izrailjci,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 Djeca vaša, žene vaše, i došljak koji je u vašem okolu, i onaj koji ti drva sijeèe, i onaj koji ti vodu nosi.
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 Da pristaneš na zavjet Gospoda Boga svojega i na kletvu njegovu, koju uèini s tobom danas Gospod Bog tvoj,
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 Da te danas postavi sebi za narod i da ti on bude Bog, kao što ti je rekao i kao što se zakleo ocima tvojim, Avramu, Isaku i Jakovu.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 I ne s vama samima èinim ovaj zavjet i ovu kletvu;
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 Nego sa svakim koji danas stoji ovdje s nama pred Gospodom Bogom našim, i sa svakim koji nije danas ovdje s nama.
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 Jer vi znate kako smo živjeli u zemlji Misirskoj, i kako smo prošli kroz narode kroz koje smo prošli.
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 I vidjeli ste gadove njihove i idole njihove od drveta i od kamena, od srebra i od zlata, koji su kod njih.
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 Neka ne bude meðu vama èovjeka ni žene ni porodice ni plemena, kojemu bi se srce odvratilo danas od Gospoda Boga našega da ide da služi bogovima onijeh naroda; neka ne bude meðu vama korijena na kom bi rastao otrov ili pelen,
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 I èuvši rijeèi ove kletve da se ne pohvali u srcu svom govoreæi: biæu miran ako uzidem za onijem što u srcu svom smislim, dodajuæi pijanstvo žeði.
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 Neæe Gospod oprostiti takome, nego æe se onda raspaliti gnjev Gospodnji i revnost njegova na takoga èovjeka, i pašæe na nj sva kletva koja je napisana u ovoj knjizi, i istrijebiæe Gospod ime njegovo pod nebom.
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 I odluèiæe ga Gospod na zlo od svijeh plemena Izrailjevijeh po svijem kletvama zavjeta napisanoga u knjizi ovoga zakona.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 Tada æe govoriti potonji naraštaj, sinovi vaši koji nastanu iza vas, i došljak koji doðe iz daleke zemlje, kad vide zla u zemlji ovoj i bolesti, koje æe Gospod pustiti na nju,
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 Zemlju ovu opaljenu sumporom i solju, gdje se ne sije niti što nièe niti na njoj raste kaka biljka, kao gdje je propao Sodom i Gomor, Adama i Sevojim, koje zatr Gospod u gnjevu svojemu i u jarosti svojoj,
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 Govoriæe svi narodi: zašto uèini ovo Gospod od ove zemlje? kakva je to žestina velikoga gnjeva?
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 I odgovaraæe se: jer odustaviše zavjet Gospoda Boga otaca svojih, koji uèini s njima kad ih izvede iz zemlje Misirske.
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 Jer idoše i služiše drugim bogovima i poklanjaše im se, bogovima kojih ne znaše i koji im ništa ne dadoše.
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 Zato se Gospod razgnjevi na tu zemlju, i pusti na nju sva prokletstva zapisana u ovoj knjizi.
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 I istrijebi ih Gospod Bog iz zemlje njihove u gnjevu i u jarosti i u ljutini velikoj, i izbaci ih u drugu zemlju, kao što se vidi danas.
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 Što je tajno ono je Gospoda Boga našega, a javno je naše i sinova naših dovijeka, da bismo izvršivali sve rijeèi ovoga zakona.
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

< Ponovljeni Zakon 29 >