< 1 Samuelova 28 >
1 I u ono vrijeme skupiše Filisteji vojsku svoju da zavojšte na Izrailja; i reèe Ahis Davidu: znaj da æeš iæi sa mnom na vojsku ti i tvoji ljudi.
Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
2 A David reèe Ahisu: sad æeš vidjeti šta æe uèiniti tvoj sluga. A Ahis reèe Davidu: zato æu te postaviti da si èuvar glave moje svagda.
Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
3 A Samuilo bijaše umro, i plaka za njim sav Izrailj, i pogreboše ga u Rami, u njegovu gradu. I Saul bijaše istrijebio iz zemlje gatare i vraèare.
Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
4 I Filisteji skupivši se doðoše i stadoše u oko kod Sunima; skupi i Saul sve Izrailjce, i stadoše u oko kod Gelvuje.
Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
5 Saul pak videæi vojsku Filistejsku uplaši se, i srce mu uzdrhta veoma.
Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
6 I upita Saul Gospoda, ali mu Gospod ne odgovori ni u snu ni preko Urima, ni preko proroka.
Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
7 I Saul reèe slugama svojim: tražite mi ženu s duhom vraèarskim, da otidem k njoj i upitam je. A sluge mu rekoše: evo u Endoru ima žena u kojoj je duh vraèarski.
Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
8 Tada se Saul preruši obukav druge haljine, i otide sa dva èovjeka, i doðe k onoj ženi noæu; i on joj reèe: hajde vraèaj mi duhom vraèarskim, i dozovi mi onoga koga ti kažem.
Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
9 Ali mu žena reèe: ta ti znaš šta je uèinio Saul i kako je istrijebio iz zemlje gatare i vraèare; zašto dakle meæeš zamku duši mojoj da me ubiješ?
Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
10 A Saul joj se zakle Gospodom govoreæi: tako živ bio Gospod! neæe ti biti ništa za to.
Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
11 Tada reèe žena: koga da ti dozovem? A on reèe: Samuila mi dozovi.
Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
12 A kad žena vidje Samuila, povika iza glasa, i reèe žena Saulu govoreæi: zašto si me prevario? ta ti si Saul.
Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
13 A car joj reèe: ne boj se; nego šta si vidjela? A žena reèe Saulu: bogove sam vidjela gdje izlaze iz zemlje.
Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
14 On joj opet reèe: kakav je? Ona mu reèe: star èovjek izlazi ogrnut plaštem. Tada razumje Saul da je Samuilo, i savi se licem do zemlje i pokloni se.
Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
15 A Samuilo reèe Saulu: zašto si me uznemirio i izazvao? Odgovori Saul: u nevolji sam velikoj, jer Filisteji zavojštiše na me, a Bog je otstupio od mene, i ne odgovara mi više ni preko proroka ni u snu, zato pozvah tebe da mi kažeš šta æu èiniti.
Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
16 A Samuilo reèe: pa što mene pitaš, kad je Gospod otstupio od tebe i postao ti neprijatelj?
Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
17 Gospod je uèinio kako je kazao preko mene; jer je Gospod istrgao carstvo iz tvoje ruke i dao ga bližnjemu tvojemu Davidu;
Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
18 Jer nijesi poslušao glasa Gospodnjega, niti si izvršio žestokoga gnjeva njegova na Amaliku; zato ti je danas Gospod to uèinio.
Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
19 I Gospod æe predati i Izrailja s tobom u ruke Filistejima; te æeš sjutra ti i sinovi tvoji biti kod mene; i oko Izrailjski predaæe Gospod u ruke Filistejima.
Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
20 A Saul ujedanput pade na zemlju kolik je dug, jer se vrlo uplaši od rijeèi Samuilovijeh, i ne bješe snage u njemu, jer ne bješe ništa jeo vas dan i svu noæ.
Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
21 Tada žena pristupi k Saulu, i videæi ga vrlo uplašena reèe mu: evo, sluškinja te je tvoja poslušala, i nijesam za život svoj marila da bih te poslušala što si mi kazao.
Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
22 Nego sada i ti poslušaj šta æe ti sluškinja tvoja kazati: postaviæu ti malo hljeba, te jedi da se okrijepiš da se možeš vratiti svojim putem.
Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
23 A on ne htje, i reèe: neæu jesti. Ali navališe na nj sluge njegove i žena, te ih posluša, i ustavši sa zemlje sjede na postelju.
Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
24 A žena imaše kod kuæe tele ugojeno, i brže ga zakla, i uze brašna te umijesi i ispeèe hljebove prijesne.
Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
25 Potom postavi Saulu i slugama njegovijem, te jedoše. A poslije ustaše i otidoše iste noæi.
Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.