< romi.na.h 10 >
1 he bhraatara israayeliiyalokaa yat paritraa. na. m praapnuvanti tadaha. m manasaabhila. san ii"svarasya samiipe praarthaye|
Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe.
2 yata ii"svare te. saa. m ce. s.taa vidyata ityatraaha. m saak. syasmi; kintu te. saa. m saa ce. s.taa saj naanaa nahi,
Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso.
3 yatasta ii"svaradatta. m pu. nyam avij naaya svak. rtapu. nya. m sthaapayitum ce. s.tamaanaa ii"svaradattasya pu. nyasya nighnatva. m na sviikurvvanti|
Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu.
4 khrii. s.ta ekaikavi"svaasijanaaya pu. nya. m daatu. m vyavasthaayaa. h phalasvaruupo bhavati|
Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.
5 vyavasthaapaalanena yat pu. nya. m tat muusaa var. nayaamaasa, yathaa, yo janastaa. m paalayi. syati sa taddvaaraa jiivi. syati|
Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
6 kintu pratyayena yat pu. nya. m tad etaad. r"sa. m vaakya. m vadati, ka. h svargam aaruhya khrii. s.tam avarohayi. syati?
Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’” (ndiko, kukatsitsa Khristu)
7 ko vaa pretalokam avaruhya khrii. s.ta. m m. rtaga. namadhyaad aane. syatiiti vaak manasi tvayaa na gaditavyaa| (Abyssos )
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos )
8 tarhi ki. m braviiti? tad vaakya. m tava samiipastham arthaat tava vadane manasi caaste, tacca vaakyam asmaabhi. h pracaaryyamaa. na. m vi"svaasasya vaakyameva|
Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira,
9 vastuta. h prabhu. m yii"su. m yadi vadanena sviikaro. si, tathe"svarasta. m "sma"saanaad udasthaapayad iti yadyanta. hkara. nena vi"svasi. si tarhi paritraa. na. m lapsyase|
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
10 yasmaat pu. nyapraaptyartham anta. hkara. nena vi"svasitavya. m paritraa. naartha nca vadanena sviikarttavya. m|
Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa.
11 "saastre yaad. r"sa. m likhati vi"svasi. syati yastatra sa jano na trapi. syate|
Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.”
12 ityatra yihuudini tadanyaloke ca kopi vi"se. so naasti yasmaad ya. h sarvve. saam advitiiya. h prabhu. h sa nijayaacakaana sarvvaan prati vadaanyo bhavati|
Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye
13 yata. h, ya. h ka"scit parame"sasya naamnaa hi praarthayi. syate| sa eva manujo nuuna. m paritraato bhavi. syati|
pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”
14 ya. m ye janaa na pratyaayan te tamuddi"sya katha. m praarthayi. syante? ye vaa yasyaakhyaana. m kadaapi na "srutavantaste ta. m katha. m pratye. syanti? apara. m yadi pracaarayitaaro na ti. s.thanti tadaa katha. m te "sro. syanti?
Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo?
15 yadi vaa preritaa na bhavanti tadaa katha. m pracaarayi. syanti? yaad. r"sa. m likhitam aaste, yathaa, maa"ngalika. m susa. mvaada. m dadatyaaniiya ye naraa. h| pracaarayanti "saante"sca susa. mvaada. m janaastu ye| te. saa. m cara. napadmaani kiid. rk "sobhaanvitaani hi|
Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”
16 kintu te sarvve ta. m susa. mvaada. m na g. rhiitavanta. h| yi"saayiyo yathaa likhitavaan| asmatpracaarite vaakye vi"svaasamakaroddhi ka. h|
Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?”
17 ataeva "srava. naad vi"svaasa ai"svaravaakyapracaaraat "srava. na nca bhavati|
Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu.
18 tarhyaha. m braviimi tai. h ki. m naa"sraavi? ava"syam a"sraavi, yasmaat te. saa. m "sabdo mahii. m vyaapnod vaakya nca nikhila. m jagat|
Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti, “Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi. Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”
19 aparamapi vadaami, israayeliiyalokaa. h kim etaa. m kathaa. m na budhyante? prathamato muusaa ida. m vaakya. m provaaca, ahamuttaapayi. sye taan aga. nyamaanavairapi| klek. syaami jaatim etaa nca pronmattabhinnajaatibhi. h|
Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti, “Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake. Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”
20 apara nca yi"saayiyo. ati"sayaak. sobhe. na kathayaamaasa, yathaa, adhi maa. m yaistu naace. s.ti sampraaptastai rjanairaha. m| adhi maa. m yai rna samp. r.s. ta. m vij naatastai rjanairaha. m||
Ndipo Yesaya molimba mtima akuti, “Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna. Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”
21 kintvisraayeliiyalokaan adhi kathayaa ncakaara, yairaaj naala"nghibhi rlokai rviruddha. m vaakyamucyate| taan pratyeva dina. m k. rtsna. m hastau vistaarayaamyaha. m||
Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti, “Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga kwa anthu osandimvera ndi okanika.”