< yaakuuba.h 1 >

1 ii"svarasya prabho ryii"sukhrii. s.tasya ca daaso yaakuub vikiir. niibhuutaan dvaada"sa. m va. m"saan prati namask. rtya patra. m likhati|
Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana. Landirani moni.
2 he mama bhraatara. h, yuuya. m yadaa bahuvidhapariik. saa. su nipatata tadaa tat puur. naanandasya kaara. na. m manyadhva. m|
Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu.
3 yato yu. smaaka. m vi"svaasasya pariik. sitatvena dhairyya. m sampaadyata iti jaaniitha|
Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro.
4 tacca dhairyya. m siddhaphala. m bhavatu tena yuuya. m siddhaa. h sampuur. naa"sca bhavi. syatha kasyaapi gu. nasyaabhaava"sca yu. smaaka. m na bhavi. syati|
Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.
5 yu. smaaka. m kasyaapi j naanaabhaavo yadi bhavet tarhi ya ii"svara. h saralabhaavena tiraskaara nca vinaa sarvvebhyo dadaati tata. h sa yaacataa. m tatastasmai daayi. syate|
Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa.
6 kintu sa ni. hsandeha. h san vi"svaasena yaacataa. m yata. h sandigdho maanavo vaayunaa caalitasyotplavamaanasya ca samudratara"ngasya sad. r"so bhavati|
Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo.
7 taad. r"so maanava. h prabho. h ki ncit praapsyatiiti na manyataa. m|
Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye.
8 dvimanaa loka. h sarvvagati. su ca ncalo bhavati|
Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.
9 yo bhraataa namra. h sa nijonnatyaa "slaaghataa. m|
Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa.
10 ya"sca dhanavaan sa nijanamratayaa "slaaghataa. myata. h sa t. r.napu. spavat k. saya. m gami. syati|
Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo.
11 yata. h sataapena suuryye. noditya t. r.na. m "so. syate tatpu. spa nca bhra"syati tena tasya ruupasya saundaryya. m na"syati tadvad dhaniloko. api sviiyamuu. dhatayaa mlaasyati|
Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.
12 yo jana. h pariik. saa. m sahate sa eva dhanya. h, yata. h pariik. sitatva. m praapya sa prabhunaa svapremakaaribhya. h pratij naata. m jiivanamuku. ta. m lapsyate|
Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.
13 ii"svaro maa. m pariik. sata iti pariik. saasamaye ko. api na vadatu yata. h paapaaye"svarasya pariik. saa na bhavati sa ca kamapi na pariik. sate|
Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense.
14 kintu ya. h ka"scit sviiyamanovaa nchayaak. r.syate lobhyate ca tasyaiva pariik. saa bhavati|
Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo.
15 tasmaat saa manovaa nchaa sagarbhaa bhuutvaa du. sk. rti. m prasuute du. sk. rti"sca pari. naama. m gatvaa m. rtyu. m janayati|
Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.
16 he mama priyabhraatara. h, yuuya. m na bhraamyata|
Musanyengedwe abale anga okondedwa.
17 yat ki ncid uttama. m daana. m puur. no vara"sca tat sarvvam uurddhvaad arthato yasmin da"saantara. m parivarttanajaatacchaayaa vaa naasti tasmaad diiptyaakaraat pituravarohati|
Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda.
18 tasya s. r.s. tavastuunaa. m madhye vaya. m yat prathamaphalasvaruupaa bhavaamastadartha. m sa svecchaata. h satyamatasya vaakyenaasmaan janayaamaasa|
Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.
19 ataeva he mama priyabhraatara. h, yu. smaakam ekaiko jana. h "srava. ne tvarita. h kathane dhiira. h krodhe. api dhiiro bhavatu|
Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima.
20 yato maanavasya krodha ii"svariiyadharmma. m na saadhayati|
Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu.
21 ato heto ryuuya. m sarvvaam a"sucikriyaa. m du. s.tataabaahulya nca nik. sipya yu. smanmanasaa. m paritraa. ne samartha. m ropita. m vaakya. m namrabhaavena g. rhliita|
Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.
22 apara nca yuuya. m kevalam aatmava ncayitaaro vaakyasya "srotaaro na bhavata kintu vaakyasya karmmakaari. no bhavata|
Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena.
23 yato ya. h ka"scid vaakyasya karmmakaarii na bhuutvaa kevala. m tasya "srotaa bhavati sa darpa. ne sviiya"saariirikavadana. m niriik. samaa. nasya manujasya sad. r"sa. h|
Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi.
24 aatmaakaare d. r.s. te sa prasthaaya kiid. r"sa aasiit tat tatk. sa. naad vismarati|
Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera.
25 kintu ya. h ka"scit natvaa mukte. h siddhaa. m vyavasthaam aalokya ti. s.thati sa vism. rtiyukta. h "srotaa na bhuutvaa karmmakarttaiva san svakaaryye dhanyo bhavi. syati|
Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.
26 anaayattarasana. h san ya. h ka"scit svamano va ncayitvaa sva. m bhakta. m manyate tasya bhakti rmudhaa bhavati|
Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe.
27 kle"sakaale pit. rhiinaanaa. m vidhavaanaa nca yad avek. sa. na. m sa. msaaraacca ni. skala"nkena yad aatmarak. sa. na. m tadeva piturii"svarasya saak. saat "suci rnirmmalaa ca bhakti. h|
Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.

< yaakuuba.h 1 >