< ۲ کَرِنْتھِنَح 12 >

آتْمَشْلاگھا مَمانُپَیُکْتا کِنْتْوَہَں پْرَبھو رْدَرْشَنادیشانامْ آکھْیانَں کَتھَیِتُں پْرَوَرْتّے۔ 1
Ndiyenera kupitiriza kudzitamandira. Ngakhale palibe choti ndipindule, ndipitiriza kufotokoza za masomphenya ndi mavumbulutso ochokera kwa Ambuye.
اِتَشْچَتُرْدَشَوَتْسَریبھْیَح پُورْوَّں مَیا پَرِچِتَ ایکو جَنَسْترِتِییَں سْوَرْگَمَنِییَتَ، سَ سَشَرِیرینَ نِحشَرِیرینَ وا تَتْ سْتھانَمَنِییَتَ تَدَہَں نَ جانامِ کِنْتْوِیشْوَرو جاناتِ۔ 2
Ndikudziwa munthu mwa Khristu amene zaka khumi ndi zinayi zapitazo anatengedwa kupita kumwamba kwachitatu. Sindikudziwa ngati zinachitika ali mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu.
سَ مانَوَح سْوَرْگَں نِیتَح سَنْ اَکَتھْیانِ مَرْتّیَواگَتِیتانِ چَ واکْیانِ شْرُتَوانْ۔ 3
Ndipo ndikumudziwa munthu ameneyu. Sindikudziwa ngati zinachitika mʼthupi kapena ayi, zimenezo akudziwa ndi Mulungu.
کِنْتُ تَدانِیں سَ سَشَرِیرو نِحشَرِیرو واسِیتْ تَنْمَیا نَ جْنایَتے تَدْ اِیشْوَرینَیوَ جْنایَتے۔ 4
Munthuyu anatengedwa kupita ku paradizo. Ndipo anamva zinthu zosatheka kuneneka, zinthu zimene munthu saloledwa kunena.
تَمَدھْیَہَں شْلاگھِشْیے مامَدھِ نانْیینَ کینَچِدْ وِشَیینَ شْلاگھِشْیے کیوَلَں سْوَدَورْبَّلْیینَ شْلاگھِشْیے۔ 5
Ndidzatamanda za munthu ngati ameneyu, koma sindidzadzitamandira ine mwini kupatula za kufowoka kwanga.
یَدْیَہَمْ آتْمَشْلاگھاں کَرْتُّمْ اِچّھییَں تَتھاپِ نِرْبّودھَ اِوَ نَ بھَوِشْیامِ یَتَح سَتْیَمیوَ کَتھَیِشْیامِ، کِنْتُ لوکا ماں یادرِشَں پَشْیَنْتِ مَمَ واکْیَں شْرُتْوا وا یادرِشَں ماں مَنْیَتے تَسْماتْ شْریشْٹھَں ماں یَنَّ گَنَیَنْتِ تَدَرْتھَمَہَں تَتو وِرَںسْیامِ۔ 6
Ngakhale nditafuna kudzitamandira, sindingakhale chitsiru, chifukwa ndikunena zoona. Koma ndimapewa kuti pasapezeke munthu wondiganizira moposera chimene ndili chifukwa cha zimene ndimachita kapena kuyankhula,
اَپَرَمْ اُتْکرِشْٹَدَرْشَنَپْراپْتِتو یَدَہَمْ آتْمابھِمانِی نَ بھَوامِ تَدَرْتھَں شَرِیرَویدھَکَمْ ایکَں شُولَں مَہْیَمْ اَدایِ تَتْ مَدِییاتْمابھِمانَنِوارَنارْتھَں مَمَ تاڈَیِتا شَیَتانو دُوتَح۔ 7
kapena chifukwa cha mavumbulutso aakulu kuposa awa. Choncho, kuti ndisadzitukumule, ndinayikidwa minga mʼthupi langa, wamthenga wa Satana, kuti adzindizunza.
مَتَّسْتَسْیَ پْرَسْتھانَں یاچِتُمَہَں تْرِسْتَمَدھِ پْرَبھُمُدِّشْیَ پْرارْتھَناں کرِتَوانْ۔ 8
Katatu konse ndinapempha Ambuye kuti andichotsere.
تَتَح سَ مامُکْتَوانْ مَمانُگْرَہَسْتَوَ سَرْوَّسادھَکَح، یَتو دَورْبَّلْیاتْ مَمَ شَکْتِح پُورْنَتاں گَچّھَتِیتِ۔ اَتَح کھْرِیشْٹَسْیَ شَکْتِ رْیَنْمامْ آشْرَیَتِ تَدَرْتھَں سْوَدَورْبَّلْیینَ مَمَ شْلاگھَنَں سُکھَدَں۔ 9
Koma anandiwuza kuti, “Chisomo changa ndi chokukwanira, pakuti mphamvu zanga zimaoneka kwathunthu mwa munthu wofowoka.” Choncho ndidzadzitamandira mokondwera chifukwa cha zofowoka zanga, kuti mʼkutero mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.
تَسْماتْ کھْرِیشْٹَہیتو رْدَورْبَّلْیَنِنْدادَرِدْرَتاوِپَکْشَتاکَشْٹادِشُ سَنْتُشْیامْیَہَں۔ یَداہَں دُرْبَّلوسْمِ تَدَیوَ سَبَلو بھَوامِ۔ 10
Tsono, chifukwa cha Khristu, ndimakondwera pamene ndili wofowoka, pamene akundinyoza, pamene ndikumva zowawa, ndi pamene akundizunza ndi kundisautsa. Pakuti pamene ndili wofowoka ndiye kuti ndili wamphamvu.
ایتیناتْمَشْلاگھَنیناہَں نِرْبّودھَ اِوابھَوَں کِنْتُ یُویَں تَسْیَ کارَنَں یَتو مَمَ پْرَشَںسا یُشْمابھِریوَ کَرْتَّوْیاسِیتْ۔ یَدْیَپْیَمْ اَگَنْیو بھَوییَں تَتھاپِ مُکھْیَتَمیبھْیَح پْریرِتیبھْیَح کیناپِ پْرَکارینَ ناہَں نْیُونوسْمِ۔ 11
Ndadzisandutsa wopusa, koma inu mwandichititsa zimenezi. Ndinu amene munayenera kundichitira umboni. Ngakhale kuti sindine kanthu, koma sindine wochepetsetsa kwa “atumwi apamwamba” aja.
سَرْوَّتھادْبھُتَکْرِیاشَکْتِلَکْشَنَیح پْریرِتَسْیَ چِہْنانِ یُشْماکَں مَدھْیے سَدھَیرْیَّں مَیا پْرَکاشِتانِ۔ 12
Ndinapirira pokuonetserani zizindikiro za mtumwi weniweni, pochita pakati panu zizindikiro, zodabwitsa ndi ntchito zamphamvu.
مَمَ پالَنارْتھَں یُویَں مَیا بھاراکْرانْتا نابھَوَتَیتَدْ ایکَں نْیُونَتْوَں وِناپَرابھْیَح سَمِتِبھْیو یُشْماکَں کِں نْیُونَتْوَں جاتَں؟ اَنینَ مَمَ دوشَں کْشَمَدھْوَں۔ 13
Kodi inu munaoneka ochepa motani ku mipingo ina, kupatula kuti sindinali cholemetsa kwa inu? Mundikhululukire cholakwa chimenechi!
پَشْیَتَ ترِتِییَوارَں یُشْمَتْسَمِیپَں گَنْتُمُدْیَتوسْمِ تَتْراپْیَہَں یُشْمانْ بھاراکْرانْتانْ نَ کَرِشْیامِ۔ یُشْماکَں سَمْپَتِّمَہَں نَ مرِگَیے کِنْتُ یُشْمانیوَ، یَتَح پِتْروح کرِتے سَنْتاناناں دھَنَسَنْچَیونُپَیُکْتَح کِنْتُ سَنْتاناناں کرِتے پِتْرو رْدھَنَسَنْچَیَ اُپَیُکْتَح۔ 14
Ndakonzeka tsopano kudzakuyenderani kachitatu, ndipo sindidzakhala cholemetsa kwa inu chifukwa ndikungofuna inuyo osati zinthu zanu. Pakuti ana sasamalira makolo koma makolo ndiwo asamalira ana.
اَپَرَنْچَ یُشْماسُ بَہُ پْرِییَمانوپْیَہَں یَدِ یُشْمَتّولْپَں پْرَمَ لَبھے تَتھاپِ یُشْماکَں پْرانَرَکْشارْتھَں سانَنْدَں بَہُ وْیَیَں سَرْوَّوْیَیَنْچَ کَرِشْیامِ۔ 15
Motero ndidzakondwera kukupatsani zanga zonse zimene ndili nazo ndi kudziperekanso ine mwini chifukwa cha inu. Kodi ine ndikamakukondani kwambiri chotere, inuyo mudzandikonda pangʼono?
یُویَں مَیا کِنْچِدَپِ نَ بھاراکْرانْتا اِتِ سَتْیَں، کِنْتْوَہَں دھُورْتَّح سَنْ چھَلینَ یُشْمانْ وَنْچِتَوانْ ایتَتْ کِں کینَچِدْ وَکْتَوْیَں؟ 16
Ena mwa inu amavomereza kuti sindinali cholemetsa. Komabe ena amaganiza kuti ndine wochenjera, ndipo ndinakuchenjererani.
یُشْمَتْسَمِیپَں مَیا یے لوکاح پْرَہِتاسْتیشامیکینَ کِں مَمَ کوپْیَرْتھَلابھو جاتَح؟ 17
Kodi ndinakudyerani masuku pamutu kudzera mwa wina aliyense amene ndinamutumiza kwa inu?
اَہَں تِیتَں وِنِییَ تینَ سارْدّھَں بھْراتَرَمیکَں پْریشِتَوانْ یُشْمَتَّسْتِیتینَ کِمْ اَرْتھو لَبْدھَح؟ ایکَسْمِنْ بھاوَ ایکَسْیَ پَدَچِہْنیشُ چاواں کِں نَ چَرِتَوَنْتَو؟ 18
Ndinamupempha Tito kuti abwere kwanuko ndipo ndinamutumiza pamodzi ndi mʼbale wathu. Kodi kapena Tito anakudyerani masuku pamutu? Kodi iye ndi ine sitinachite zinthu mofanana ndi Mzimu mmodzi yemweyo?
یُشْماکَں سَمِیپے وَیَں پُنَ رْدوشَکْشالَنَکَتھاں کَتھَیامَ اِتِ کِں بُدھْیَدھْوے؟ ہے پْرِیَتَماح، یُشْماکَں نِشْٹھارْتھَں وَیَمِیشْوَرَسْیَ سَمَکْشَں کھْرِیشْٹینَ سَرْوّانْییتانِ کَتھَیامَح۔ 19
Kodi mukuyesa kuti nthawi yonseyi takhala tikudzitchinjiriza tokha? Takhala tikuyankhula pamaso pa Mulungu monga anthu amene ali mwa Khristu; ndipo abwenzi okondedwa, chilichonse chimene timachita ndi chofuna kukulimbikitsani.
اَہَں یَداگَمِشْیامِ، تَدا یُشْمانْ یادرِشانْ دْرَشْٹُں نیچّھامِ تادرِشانْ دْرَکْشْیامِ، یُویَمَپِ ماں یادرِشَں دْرَشْٹُں نیچّھَتھَ تادرِشَں دْرَکْشْیَتھَ، یُشْمَنْمَدھْیے وِوادَ اِیرْشْیا کْرودھو وِپَکْشَتا پَراپَوادَح کَرْنیجَپَنَں دَرْپَح کَلَہَشْچَیتے بھَوِشْیَنْتِ؛ 20
Pakuti ndikuona kuti pamene ndibwera sindidzakupezani monga mmene ndikufunira kuti muzikhalira, ndipo simungadzandione monga mmene mukufunira kundionera. Ndikuopa kuti pangadzakhale mkangano, nsanje, kupserana mitima, kugawikana, ugogodi, miseche, kudzitukumula ndi chisokonezo.
تیناہَں یُشْمَتْسَمِیپَں پُنَراگَتْیَ مَدِیییشْوَرینَ نَمَیِشْیے، پُورْوَّں کرِتَپاپانْ لوکانْ سْوِییاشُچِتاویشْیاگَمَنَلَمْپَٹَتاچَرَنادْ اَنُتاپَمْ اَکرِتَوَنْتو درِشْٹْوا چَ تانَدھِ مَمَ شوکو جَنِشْیَتَ اِتِ بِبھیمِ۔ 21
Ndikuopa kuti pamene ndidzabwerenso, Mulungu adzandichepetsa pamaso panu, ndipo ndidzamva chisoni ndi ambiri amene anachimwa kale ndipo sanalape zonyansa, zachigololo ndi zilakolako zoyipa zimene anachita.

< ۲ کَرِنْتھِنَح 12 >