< ibriṇaḥ 8 >

1 kathyamānānāṁ vākyānāṁ sārō'yam asmākam ētādr̥śa ēkō mahāyājakō'sti yaḥ svargē mahāmahimnaḥ siṁhāsanasya dakṣiṇapārśvō samupaviṣṭavān
Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba.
2 yacca dūṣyaṁ na manujaiḥ kintvīśvarēṇa sthāpitaṁ tasya satyadūṣyasya pavitravastūnāñca sēvakaḥ sa bhavati|
Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.
3 yata ēkaikō mahāyājakō naivēdyānāṁ balīnāñca dānē niyujyatē, atō hētōrētasyāpi kiñcid utsarjanīyaṁ vidyata ityāvaśyakaṁ|
Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka.
4 kiñca sa yadi pr̥thivyām asthāsyat tarhi yājakō nābhaviṣyat, yatō yē vyavasthānusārāt naivēdyāni dadatyētādr̥śā yājakā vidyantē|
Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo.
5 tē tu svargīyavastūnāṁ dr̥ṣṭāntēna chāyayā ca sēvāmanutiṣṭhanti yatō mūsasi dūṣyaṁ sādhayitum udyatē satīśvarastadēva tamādiṣṭavān phalataḥ sa tamuktavān, yathā, "avadhēhi girau tvāṁ yadyannidarśanaṁ darśitaṁ tadvat sarvvāṇi tvayā kriyantāṁ|"
Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”
6 kintvidānīm asau tasmāt śrēṣṭhaṁ sēvakapadaṁ prāptavān yataḥ sa śrēṣṭhapratijñābhiḥ sthāpitasya śrēṣṭhaniyamasya madhyasthō'bhavat|
Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.
7 sa prathamō niyamō yadi nirddōṣō'bhaviṣyata tarhi dvitīyasya niyamasya kimapi prayōjanaṁ nābhaviṣyat|
Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake.
8 kintu sa dōṣamārōpayan tēbhyaḥ kathayati, yathā, "paramēśvara idaṁ bhāṣatē paśya yasmin samayē'ham isrāyēlavaṁśēna yihūdāvaṁśēna ca sārddham ēkaṁ navīnaṁ niyamaṁ sthirīkariṣyāmyētādr̥śaḥ samaya āyāti|
Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati, “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
9 paramēśvarō'paramapi kathayati tēṣāṁ pūrvvapuruṣāṇāṁ misaradēśād ānayanārthaṁ yasmin dinē'haṁ tēṣāṁ karaṁ dhr̥tvā taiḥ saha niyamaṁ sthirīkr̥tavān taddinasya niyamānusārēṇa nahi yatastai rmama niyamē laṅghitē'haṁ tān prati cintāṁ nākaravaṁ|
Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo, pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija ndipo Ine sindinawasamalire, akutero Ambuye.
10 kintu paramēśvaraḥ kathayati taddināt paramahaṁ isrāyēlavaṁśīyaiḥ sārddham imaṁ niyamaṁ sthirīkariṣyāmi, tēṣāṁ cittē mama vidhīn sthāpayiṣyāmi tēṣāṁ hr̥tpatrē ca tān lēkhiṣyāmi, aparamahaṁ tēṣām īśvarō bhaviṣyāmi tē ca mama lōkā bhaviṣyanti|
Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli: Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye, Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo, ndi kulemba mʼmitima mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
11 aparaṁ tvaṁ paramēśvaraṁ jānīhītivākyēna tēṣāmēkaikō janaḥ svaṁ svaṁ samīpavāsinaṁ bhrātarañca puna rna śikṣayiṣyati yata ākṣudrāt mahāntaṁ yāvat sarvvē māṁ jñāsyanti|
Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake, kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye chifukwa onse adzandidziwa, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.
12 yatō hētōrahaṁ tēṣām adharmmān kṣamiṣyē tēṣāṁ pāpānyaparādhāṁśca punaḥ kadāpi na smariṣyāmi|"
Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
13 anēna taṁ niyamaṁ nūtanaṁ gaditvā sa prathamaṁ niyamaṁ purātanīkr̥tavān; yacca purātanaṁ jīrṇāñca jātaṁ tasya lōpō nikaṭō 'bhavat|
Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

< ibriṇaḥ 8 >