< romiNaH 10 >
1 he bhrAtara isrAyelIyalokA yat paritrANaM prApnuvanti tadahaM manasAbhilaSan Izvarasya samIpe prArthaye|
Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe.
2 yata Izvare teSAM ceSTA vidyata ityatrAhaM sAkSyasmi; kintu teSAM sA ceSTA sajJAnA nahi,
Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso.
3 yatasta IzvaradattaM puNyam avijJAya svakRtapuNyaM sthApayitum ceSTamAnA Izvaradattasya puNyasya nighnatvaM na svIkurvvanti|
Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu.
4 khrISTa ekaikavizvAsijanAya puNyaM dAtuM vyavasthAyAH phalasvarUpo bhavati|
Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.
5 vyavasthApAlanena yat puNyaM tat mUsA varNayAmAsa, yathA, yo janastAM pAlayiSyati sa taddvArA jIviSyati|
Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
6 kintu pratyayena yat puNyaM tad etAdRzaM vAkyaM vadati, kaH svargam Aruhya khrISTam avarohayiSyati?
Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’” (ndiko, kukatsitsa Khristu)
7 ko vA pretalokam avaruhya khrISTaM mRtagaNamadhyAd AneSyatIti vAk manasi tvayA na gaditavyA| (Abyssos )
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos )
8 tarhi kiM bravIti? tad vAkyaM tava samIpastham arthAt tava vadane manasi cAste, tacca vAkyam asmAbhiH pracAryyamANaM vizvAsasya vAkyameva|
Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira,
9 vastutaH prabhuM yIzuM yadi vadanena svIkaroSi, tathezvarastaM zmazAnAd udasthApayad iti yadyantaHkaraNena vizvasiSi tarhi paritrANaM lapsyase|
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
10 yasmAt puNyaprAptyartham antaHkaraNena vizvasitavyaM paritrANArthaJca vadanena svIkarttavyaM|
Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa.
11 zAstre yAdRzaM likhati vizvasiSyati yastatra sa jano na trapiSyate|
Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.”
12 ityatra yihUdini tadanyaloke ca kopi vizeSo nAsti yasmAd yaH sarvveSAm advitIyaH prabhuH sa nijayAcakAna sarvvAn prati vadAnyo bhavati|
Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye
13 yataH, yaH kazcit paramezasya nAmnA hi prArthayiSyate| sa eva manujo nUnaM paritrAto bhaviSyati|
pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”
14 yaM ye janA na pratyAyan te tamuddizya kathaM prArthayiSyante? ye vA yasyAkhyAnaM kadApi na zrutavantaste taM kathaM pratyeSyanti? aparaM yadi pracArayitAro na tiSThanti tadA kathaM te zroSyanti?
Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo?
15 yadi vA preritA na bhavanti tadA kathaM pracArayiSyanti? yAdRzaM likhitam Aste, yathA, mAGgalikaM susaMvAdaM dadatyAnIya ye narAH| pracArayanti zAntezca susaMvAdaM janAstu ye| teSAM caraNapadmAni kIdRk zobhAnvitAni hi|
Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”
16 kintu te sarvve taM susaMvAdaM na gRhItavantaH| yizAyiyo yathA likhitavAn| asmatpracArite vAkye vizvAsamakaroddhi kaH|
Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?”
17 ataeva zravaNAd vizvAsa aizvaravAkyapracArAt zravaNaJca bhavati|
Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu.
18 tarhyahaM bravImi taiH kiM nAzrAvi? avazyam azrAvi, yasmAt teSAM zabdo mahIM vyApnod vAkyaJca nikhilaM jagat|
Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti, “Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi. Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”
19 aparamapi vadAmi, isrAyelIyalokAH kim etAM kathAM na budhyante? prathamato mUsA idaM vAkyaM provAca, ahamuttApayiSye tAn agaNyamAnavairapi| klekSyAmi jAtim etAJca pronmattabhinnajAtibhiH|
Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti, “Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake. Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”
20 aparaJca yizAyiyo'tizayAkSobheNa kathayAmAsa, yathA, adhi mAM yaistu nAceSTi samprAptastai rjanairahaM| adhi mAM yai rna sampRSTaM vijJAtastai rjanairahaM||
Ndipo Yesaya molimba mtima akuti, “Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna. Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”
21 kintvisrAyelIyalokAn adhi kathayAJcakAra, yairAjJAlaGghibhi rlokai rviruddhaM vAkyamucyate| tAn pratyeva dinaM kRtsnaM hastau vistArayAmyahaM||
Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti, “Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga kwa anthu osandimvera ndi okanika.”