< gAlAtinaH 4 >

1 ahaM vadAmi sampadadhikArI yAvad bAlastiSThati tAvat sarvvasvasyAdhipatiH sannapi sa dAsAt kenApi viSayeNa na viziSyate
Chimene ndikunena ndi chakuti, ngati mlowamʼmalo akali wamngʼono, sasiyana ndi kapolo, ngakhale kuti chuma chonse ndi chake.
2 kintu pitrA nirUpitaM samayaM yAvat pAlakAnAM dhanAdhyakSANAJca nighnastiSThati|
Mwanayo ayenera kumvera omulera ndiponso anthu oyangʼanira chuma mpaka nthawi imene abambo ake anakhazikitsa.
3 tadvad vayamapi bAlyakAle dAsA iva saMsArasyAkSaramAlAyA adhInA Asmahe|
Chomwechonso, ife pamene tinali ana, tinali akapolo a miyambo ya dziko lapansi.
4 anantaraM samaye sampUrNatAM gatavati vyavasthAdhInAnAM mocanArtham
Koma nthawi itakwana, Mulungu anatumiza Mwana wake, wobadwa mwa mayi, wobadwa pansi pa lamulo,
5 asmAkaM putratvaprAptyarthaJcezvaraH striyA jAtaM vyavasthAyA adhinIbhUtaJca svaputraM preSitavAn|
kudzawombola amene anali pansi pa lamulo, kuti tilandiridwe monga ana.
6 yUyaM santAnA abhavata tatkAraNAd IzvaraH svaputrasyAtmAnAM yuSmAkam antaHkaraNAni prahitavAn sa cAtmA pitaH pitarityAhvAnaM kArayati|
Ndipo popeza ndinu ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake kuti alowe mʼmitima mwathu, Mzimu amene amafuwula kuti, “Abba, Atate.”
7 ata idAnIM yUyaM na dAsAH kintuH santAnA eva tasmAt santAnatvAcca khrISTenezvarIyasampadadhikAriNo'pyAdhve|
Choncho sindiwenso kapolo, koma mwana wa Mulungu. Tsono popeza ndiwe mwana wake, Mulungu wakusandutsanso mlowamʼmalo.
8 aparaJca pUrvvaM yUyam IzvaraM na jJAtvA ye svabhAvato'nIzvarAsteSAM dAsatve'tiSThata|
Koma poyamba pamene simunkamudziwa Mulungu, munali akapolo a zimene mwachilengedwe si milungu.
9 idAnIm IzvaraM jJAtvA yadi vezvareNa jJAtA yUyaM kathaM punastAni viphalAni tucchAni cAkSarANi prati parAvarttituM zaknutha? yUyaM kiM punasteSAM dAsA bhavitumicchatha?
Koma tsopano pakuti mukumudziwa Mulungu, kapena ndinene kuti Mulungu akukudziwani, nʼchifukwa chiyani mukubwereranso ku miyambo yofowoka ndi yomvetsa chisoni? Kodi mukufuna musandukenso akapolo?
10 yUyaM divasAn mAsAn tithIn saMvatsarAMzca sammanyadhve|
Mumasunga masiku, miyezi ndi nyengo ndi zaka.
11 yuSmadarthaM mayA yaH parizramo'kAri sa viphalo jAta iti yuSmAnadhyahaM bibhemi|
Ine ndikuopa kuti mwina ntchito zanga pa inu ndinagwira pachabe.
12 he bhrAtaraH, ahaM yAdRzo'smi yUyamapi tAdRzA bhavateti prArthaye yato'hamapi yuSmattulyo'bhavaM yuSmAbhi rmama kimapi nAparAddhaM|
Abale, ndikukudandaulirani, mukhale ngati ine, popeza ine ndinakhala ngati inu. Inu simunandilakwire.
13 pUrvvamahaM kalevarasya daurbbalyena yuSmAn susaMvAdam ajJApayamiti yUyaM jAnItha|
Monga inu mukudziwa ndinkakulalikirani Uthenga Wabwino ndili wofowoka.
14 tadAnIM mama parIkSakaM zArIraklezaM dRSTvA yUyaM mAm avajJAya RtIyitavantastannahi kintvIzvarasya dUtamiva sAkSAt khrISTa yIzumiva vA mAM gRhItavantaH|
Ngakhale kuti matendawo anali ngati mayesero kwa inu, simunandinyoze kapena kunyansidwa nane. Komatu inu munandilandira ngati kuti ndinali mngelo wa Mulungu, ngati kuti ndinali Khristu Yesu mwini.
15 atastadAnIM yuSmAkaM yA dhanyatAbhavat sA kka gatA? tadAnIM yUyaM yadi sveSAM nayanAnyutpATya mahyaM dAtum azakSyata tarhi tadapyakariSyateti pramANam ahaM dadAmi|
Kodi chimwemwe chanu chonse chija chili kuti? Ine nditha kuchitira umboni kuti, ngati kukanatheka, inu mukanakolowola maso anu ndi kundipatsa.
16 sAmpratamahaM satyavAditvAt kiM yuSmAkaM ripu rjAto'smi?
Kodi tsopano ine ndasanduka mdani wanu chifukwa ndakuwuzani choonadi?
17 te yuSmatkRte sparddhante kintu sA sparddhA kutsitA yato yUyaM tAnadhi yat sparddhadhvaM tadarthaM te yuSmAn pRthak karttum icchanti|
Anthu amenewo akuchita changu kuti akukopeni, koma changu chawocho sichabwino. Chimene iwo akufuna ndi chakuti akuchotseni inu kwa ife, kuti mukachite changu powathandiza iwowo.
18 kevalaM yuSmatsamIpe mamopasthitisamaye tannahi, kintu sarvvadaiva bhadramadhi sparddhanaM bhadraM|
Nʼkwabwino kuchita changu, ngati cholingacho chili chabwino ndi kukhala otero nthawi zonse osati pokhapo pamene ine ndili ndi inu.
19 he mama bAlakAH, yuSmadanta ryAvat khrISTo mUrtimAn na bhavati tAvad yuSmatkAraNAt punaH prasavavedaneva mama vedanA jAyate|
Ana anga okondedwa, inu amene ine ndikukumveraninso zowawa za kubereka kufikira Khristu atawumbidwa mwa inu,
20 ahamidAnIM yuSmAkaM sannidhiM gatvA svarAntareNa yuSmAn sambhASituM kAmaye yato yuSmAnadhi vyAkulo'smi|
ine ndikanakonda ndikanakhala nanu tsopano kuti ndisinthe mawu anga, chifukwa ndathedwa nanu nzeru.
21 he vyavasthAdhInatAkAGkSiNaH yUyaM kiM vyavasthAyA vacanaM na gRhlItha?
Tandiwuzani, inu, abale amene mukufuna kukhala pansi pa lamulo, kodi simukudziwa chimene lamulo limanena?
22 tanmAM vadata| likhitamAste, ibrAhImo dvau putrAvAsAte tayoreko dAsyAM dvitIyazca patnyAM jAtaH|
Pakuti zinalembedwa kuti Abrahamu anali ndi ana aamuna awiri, wina mayi wake anali kapolo ndipo wina mayi wake anali mfulu.
23 tayo ryo dAsyAM jAtaH sa zArIrikaniyamena jajJe yazca patnyAM jAtaH sa pratijJayA jajJe|
Mwana wake wobadwa mwa kapolo anabadwa mwathupi; koma mwana wake wobadwa mwa mfulu anabadwa monga mwa lonjezo.
24 idamAkhyAnaM dRSTantasvarUpaM| te dve yoSitAvIzvarIyasandhI tayorekA sInayaparvvatAd utpannA dAsajanayitrI ca sA tu hAjirA|
Zinthu izi zinali ngati fanizo, pakuti amayi awiriwa akuyimira mapangano awiri. Pangano limodzi ndi lochokera mʼPhiri la Sinai, ndiye Hagara, ndipo amabereka ana amene ndi akapolo.
25 yasmAd hAjirAzabdenAravadezasthasInayaparvvato bodhyate, sA ca varttamAnAyA yirUzAlampuryyAH sadRzI| yataH svabAlaiH sahitA sA dAsatva Aste|
Tsono Hagara, akuyimira Phiri la Sinai ku Arabiya amene afanizidwa ndi mzinda wa Yerusalemu wa lero, chifukwa ali mu ukapolo pamodzi ndi ana ake.
26 kintu svargIyA yirUzAlampurI patnI sarvveSAm asmAkaM mAtA cAste|
Koma Yerusalemu wakumwamba ndiye mfulu, ndipo ndiye mayi wathu.
27 yAdRzaM likhitam Aste, "vandhye santAnahIne tvaM svaraM jayajayaM kuru| aprasUte tvayollAso jayAzabdazca gIyatAM| yata eva sanAthAyA yoSitaH santate rgaNAt| anAthA yA bhavennArI tadapatyAni bhUrizaH||"
Pakuti kwalembedwa kuti, “Sangalala, iwe mayi wosabala, amene sunabalepo mwana; imba nthungululu ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa.”
28 he bhrAtRgaNa, imhAk iva vayaM pratijJayA jAtAH santAnAH|
Tsono inu abale, ndinu ana alonjezo ngati Isake.
29 kintu tadAnIM zArIrikaniyamena jAtaH putro yadvad Atmikaniyamena jAtaM putram upAdravat tathAdhunApi|
Nthawi imeneyo mwana wobadwa mwathupi anazunza mwana wobadwa mwamphamvu za Mzimu. Zili chimodzimodzinso lero.
30 kintu zAstre kiM likhitaM? "tvam imAM dAsIM tasyAH putraJcApasAraya yata eSa dAsIputraH patnIputreNa samaM nottarAdhikArI bhaviyyatIti|"
Kodi Malemba akuti chiyani? “Muchotse kapoloyo pamodzi ndi mwana wake, chifukwa mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wamfulu.”
31 ataeva he bhrAtaraH, vayaM dAsyAH santAnA na bhUtvA pAtnyAH santAnA bhavAmaH|
Chifukwa chake, abale, ife sindife ana akapolo, koma ana a mfulu.

< gAlAtinaH 4 >