< preritAH 17 >
1 paulasIlau AmphipalyApalloniyAnagarAbhyAM gatvA yatra yihUdIyAnAM bhajanabhavanamekam Aste tatra thiSalanIkInagara upasthitau|
Atadutsa ku Amfipoli ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge ya Ayuda.
2 tadA paulaH svAcArAnusAreNa teSAM samIpaM gatvA vizrAmavAratraye taiH sArddhaM dharmmapustakIyakathAyA vicAraM kRtavAn|
Paulo, monga mwachizolowezi chake, analowa mʼsunagoge, ndipo anakambirana nawo Mawu a Mulungu kwa masabata atatu,
3 phalataH khrISTena duHkhabhogaH karttavyaH zmazAnadutthAnaJca karttavyaM yuSmAkaM sannidhau yasya yIzoH prastAvaM karomi sa IzvareNAbhiSiktaH sa etAH kathAH prakAzya pramANaM datvA sthirIkRtavAn|
kuwafotokozera ndi kuwatsimikizira kuti Khristu anayenera kufa ndi kuuka. Iye anati, “Yesu amene ndikukulalikirani ndiye Khristu.”
4 tasmAt teSAM katipayajanA anyadezIyA bahavo bhaktalokA bahyaH pradhAnanAryyazca vizvasya paulasIlayoH pazcAdgAmino jAtAH|
Ena mwa Ayuda anakopeka mtima ndipo anatsatira Paulo ndi Sila, monganso linachitira gulu lalikulu la Agriki woopa Mulungu, pamodzi ndi amayi odziwika ambiri.
5 kintu vizvAsahInA yihUdIyalokA IrSyayA paripUrNAH santo haTaTsya katinayalampaTalokAn saGginaH kRtvA janatayA nagaramadhye mahAkalahaM kRtvA yAsono gRham Akramya preritAn dhRtvA lokanivahasya samIpam AnetuM ceSTitavantaH|
Koma Ayuda ena anachita nsanje; kotero anasonkhanitsa anthu akhalidwe loyipa ochokera pa msika ndipo napanga gulu nayambitsa chipolowe mu mzindawo. Anathamangira ku nyumba ya Yasoni kukafuna Paulo ndi Sila kuti awabweretse pa gulu la anthu.
6 teSAmuddezam aprApya ca yAsonaM katipayAn bhrAtRMzca dhRtvA nagarAdhipatInAM nikaTamAnIya proccaiH kathitavanto ye manuSyA jagadudvATitavantaste 'trApyupasthitAH santi,
Koma atalephera kuwapeza, anakokera Yasoniyo ndi abale ena ku bwalo la akulu a mzindawo akufuwula kuti, “Anthu awa, Paulo ndi Sila, amene akhala akusokoneza dziko lonse lapansi, tsopano afikanso kuno.
7 eSa yAson AtithyaM kRtvA tAn gRhItavAn| yIzunAmaka eko rAjastIti kathayantaste kaisarasyAjJAviruddhaM karmma kurvvati|
Yasoni ndiye anawalandira mʼnyumba mwake. Onsewa akuchita zotsutsana ndi malamulo a Kaisara pomanena kuti palinso mfumu ina, yotchedwa Yesu.”
8 teSAM kathAmimAM zrutvA lokanivaho nagarAdhipatayazca samudvignA abhavan|
Atamva zimenezi, gulu la anthu ndi akulu a mzinda anavutika mu mtima.
9 tadA yAsonastadanyeSAJca dhanadaNDaM gRhItvA tAn parityaktavantaH|
Iwo analipiritsa Yasoni ndi anzakewo ndipo anawamasula.
10 tataH paraM bhrAtRgaNo rajanyAM paulasIlau zIghraM birayAnagaraM preSitavAn tau tatropasthAya yihUdIyAnAM bhajanabhavanaM gatavantau|
Mdima utagwa, abale anatumiza Paulo ndi Sila ku Bereya. Atafika kumeneko anapita ku sunagoge ya Ayuda.
11 tatrasthA lokAH thiSalanIkIsthalokebhyo mahAtmAna Asan yata itthaM bhavati na veti jJAtuM dine dine dharmmagranthasyAlocanAM kRtvA svairaM kathAm agRhlan|
Tsopano anthu a ku Bereya anali akhalidwe labwino kusiyana ndi Atesalonika, pakuti iwo analandira mawu ndi chidwi chachikulu ndipo ankasanthula Malemba tsiku ndi tsiku kuti aone ngati zimene ankanena Paulozo zinali zoona.
12 tasmAd aneke yihUdIyA anyadezIyAnAM mAnyA striyaH puruSAzcAneke vyazvasan|
Ayuda ambiri anakhulupirira, monga anachitiranso amayi ndi amuna ambiri odziwika a Chigriki.
13 kintu birayAnagare paulenezvarIyA kathA pracAryyata iti thiSalanIkIsthA yihUdIyA jJAtvA tatsthAnamapyAgatya lokAnAM kupravRttim ajanayan|
Ayuda a ku Tesalonika atadziwa kuti Paulo akulalikira Mawu a Mulungu ku Bereya, anapitanso kumeneko, ndi kuwutsa mitima ya anthu nayambitsa chisokonezo.
14 ataeva tasmAt sthAnAt samudreNa yAntIti darzayitvA bhrAtaraH kSipraM paulaM prAhiNvan kintu sIlatImathiyau tatra sthitavantau|
Nthawi yomweyo abale anatumiza Paulo ku nyanja koma Sila ndi Timoteyo anatsalira ku Bereya.
15 tataH paraM paulasya mArgadarzakAstam AthInInagara upasthApayan pazcAd yuvAM tUrNam etat sthAnaM AgamiSyathaH sIlatImathiyau pratImAm AjJAM prApya te pratyAgatAH|
Anthu amene anamuperekeza Paulo nafika naye ku Atene, ndipo anabwerera ku Bereya atawuzidwa kuti Sila ndi Timoteyo amutsatire msanga.
16 paula AthInInagare tAvapekSya tiSThan tannagaraM pratimAbhiH paripUrNaM dRSTvA santaptahRdayo 'bhavat|
Paulo akudikira Timoteyo ndi Sila ku Atene, anavutika mu mtima kwambiri poona kuti mzindawo unali odzaza ndi mafano.
17 tataH sa bhajanabhavane yAn yihUdIyAn bhaktalokAMzca haTTe ca yAn apazyat taiH saha pratidinaM vicAritavAn|
Tsono anakambirana ndi Ayuda ndi Agriki amene amaopa Mulungu mʼsunagoge, komanso anthu amene amapezeka pa msika tsiku ndi tsiku ndi ena amene amakumana nawo.
18 kintvipikUrIyamatagrahiNaH stoyikIyamatagrAhiNazca kiyanto janAstena sArddhaM vyavadanta| tatra kecid akathayan eSa vAcAlaH kiM vaktum icchati? apare kecid eSa janaH keSAJcid videzIyadevAnAM pracAraka ityanumIyate yataH sa yIzum utthitiJca pracArayat|
Gulu la Aepikureya ndi Astoiki, anthu anzeru, anayamba kutsutsana naye. Ena a iwo anafunsa kuti, “Kodi wolongololayu akufuna kunena chiyani?” Enanso anati, “Akuoneka ngati akulalikira milungu yachilendo.” Iwo ananena zimenezi chifukwa Paulo amalalikira Uthenga Wabwino wa Yesu ndi kuuka kwa akufa.
19 te tam areyapAganAma vicArasthAnam AnIya prAvocan idaM yannavInaM mataM tvaM prAcIkaza idaM kIdRzaM etad asmAn zrAvaya;
Kenaka iwo anamutenga nafika naye ku bwalo la Areopagi kumene anamufunsa kuti, “Kodi tingadziweko chiphunzitso chatsopano chimene ukuchifotokozachi?
20 yAmimAm asambhavakathAm asmAkaM karNagocarIkRtavAn asyA bhAvArthaH ka iti vayaM jJAtum icchAmaH|
Iwe ukubweretsa zinthu zina zachilendo mʼmakutu mwathu, ndipo ife tikufuna tidziwe tanthauzo lake.”
21 tadAthInInivAsinastannagarapravAsinazca kevalaM kasyAzcana navInakathAyAH zravaNena pracAraNena ca kAlam ayApayan|
Atene onse ndi alendo amene amakhala kumeneko samachita kanthu kena koma kufotokoza ndi kumvera fundo zatsopano.
22 paulo'reyapAgasya madhye tiSThan etAM kathAM pracAritavAn, he AthInIyalokA yUyaM sarvvathA devapUjAyAm AsaktA ityaha pratyakSaM pazyAmi|
Paulo anayimirira mʼbwalo la Areopagi nati: “Inu anthu a ku Atene! Ine ndikuona kuti mʼnjira zonse ndinu opembedza kwambiri.
23 yataH paryyaTanakAle yuSmAkaM pUjanIyAni pazyan ‘avijJAtezvarAya` etallipiyuktAM yajJavedImekAM dRSTavAn; ato na viditvA yaM pUjayadhve tasyaiva tatvaM yuSmAn prati pracArayAmi|
Pakuti pamene ndimayenda ndi kuona zinthu zimene mumazipembedza, ndapezanso guwa lansembe lolembedwapo kuti, kwa mulungu wosadziwika. Tsopano chimene mumachipembedza osachidziwa ndi chimene ndikuchilalikira.
24 jagato jagatsthAnAM sarvvavastUnAJca sraSTA ya IzvaraH sa svargapRthivyorekAdhipatiH san karanirmmitamandireSu na nivasati;
“Mulungu amene analenga dziko lapansi ndiponso zonse zili mʼmenemo ndiye Ambuye wakumwamba ndi dziko lapansi ndipo sakhala mʼnyumba zachipembedzo zomangidwa ndi manja.
25 sa eva sarvvebhyo jIvanaM prANAn sarvvasAmagrIzca pradadAti; ataeva sa kasyAzcit sAmagyrA abhAvaheto rmanuSyANAM hastaiH sevito bhavatIti na|
Ndipo satumikiridwa ndi manja a anthu ngati kuti Iye amasowa kanthu, chifukwa Iye ndiye amapereka moyo ndi mpweya kwa anthu onse ndi zina zonse.
26 sa bhUmaNDale nivAsArtham ekasmAt zoNitAt sarvvAn manuSyAn sRSTvA teSAM pUrvvanirUpitasamayaM vasatisImAJca niracinot;
Kuchoka kwa munthu mmodzi Iye analenga mtundu uliwonse wa anthu, kuti akakhale pa dziko lonse lapansi; ndipo Iye anakonzeratu nthawi yawo ndiponso malo enieni kumene adzakhale.
27 tasmAt lokaiH kenApi prakAreNa mRgayitvA paramezvarasya tatvaM prAptuM tasya gaveSaNaM karaNIyam|
Mulungu anachita izi kuti anthu amufunefune, ndikuti pomufunafunapo amupeze ngakhale kuti Iye sali kutali ndi aliyense wa ife.
28 kintu so'smAkaM kasmAccidapi dUre tiSThatIti nahi, vayaM tena nizvasanaprazvasanagamanAgamanaprANadhAraNAni kurmmaH, punazca yuSmAkameva katipayAH kavayaH kathayanti ‘tasya vaMzA vayaM smo hi` iti|
‘Pakuti timakhala mwa Iye, kuyenda mwa Iye ndi kukhala moyo mwa Iye.’ Monga olemba ndakatulo anu ena akuti, ‘Ife ndi zidzukulu zake.’
29 ataeva yadi vayam Izvarasya vaMzA bhavAmastarhi manuSyai rvidyayA kauzalena ca takSitaM svarNaM rUpyaM dRSad vaiteSAmIzvaratvam asmAbhi rna jJAtavyaM|
“Tsono popeza ndife ana a Mulungu, tisaganize kuti umulungu wake ndi wofanana ndi ndalama zagolide, zasiliva, mwala, kapenanso fanizo lopangidwa mwaluso la nzeru za anthu.
30 teSAM pUrvvIyalokAnAm ajJAnatAM pratIzvaro yadyapi nAvAdhatta tathApIdAnIM sarvvatra sarvvAn manaH parivarttayitum AjJApayati,
Nthawi imene anthu sankadziwa, Mulungu anawalekerera koma tsopano akulamulira kuti anthu onse, kulikonse atembenuke mtima.
31 yataH svaniyuktena puruSeNa yadA sa pRthivIsthAnAM sarvvalokAnAM vicAraM kariSyati taddinaM nyarUpayat; tasya zmazAnotthApanena tasmin sarvvebhyaH pramANaM prAdAt|
Pakuti Iye wayika tsiku limene adzaweruze dziko lapansi mwa chilungamo kudzera mwa Munthu amene anamusankha. Iye watsimikizira anthu onse zimenezi pomuukitsa.”
32 tadA zmazAnAd utthAnasya kathAM zrutvA kecid upAhaman, kecidavadan enAM kathAM punarapi tvattaH zroSyAmaH|
Atamva za kuuka kwa akufa, ena a iwo anaseka, koma enanso anati, “Ife tikufuna tidzamvenso zimenezi tsiku lina.”
33 tataH paulasteSAM samIpAt prasthitavAn|
Ndipo Paulo anatuluka mʼBwalolo.
34 tathApi kecillokAstena sArddhaM militvA vyazvasan teSAM madhye 'reyapAgIyadiyanusiyo dAmArInAmA kAcinnArI kiyanto narAzcAsan|
Anthu ena ochepa anamutsatira Paulo ndipo anakhulupirira. Pakati pawo panali Dionisiyo mmodzi wa bwalo la Areopagi ndi mayi wina wotchedwa Damalisi ndi enanso.