< preritAH 14 >

1 tau dvau janau yugapad ikaniyanagarasthayihUdIyAnAM bhajanabhavanaM gatvA yathA bahavo yihUdIyA anyadezIyalokAzca vyazvasan tAdRzIM kathAM kathitavantau|
Ku Ikoniya, Paulo ndi Barnaba analowanso mʼsunagoge ya Ayuda. Kumeneko iwo anaphunzitsa momveka bwino kotero kuti anthu ambiri Achiyuda ndi anthu a mitundu ina anakhulupirira.
2 kintu vizvAsahInA yihUdIyA anyadezIyalokAn kupravRttiM grAhayitvA bhrAtRgaNaM prati teSAM vairaM janitavantaH|
Koma Ayuda amene anakana kukhulupirira anawutsa anthu a mitundu ina nawononga maganizo awo kutsutsana ndi abale.
3 ataH svAnugrahakathAyAH pramANaM datvA tayo rhastai rbahulakSaNam adbhutakarmma ca prAkAzayad yaH prabhustasya kathA akSobhena pracAryya tau tatra bahudinAni samavAtiSThetAM|
Ndipo Paulo ndi Barnaba anakhala kumeneko nthawi yayitali, nalalikira molimba mtima za Ambuye amene anawapatsa mphamvu yochitira zozizwitsa ndi zizindikiro zodabwitsa pochitira umboni mawu a chisomo.
4 kintu kiyanto lokA yihUdIyAnAM sapakSAH kiyanto lokAH preritAnAM sapakSA jAtAH, ato nAgarikajananivahamadhye bhinnavAkyatvam abhavat|
Anthu a mu mzindamo anagawikana; ena anali mbali ya Ayuda, ena mbali ya atumwi.
5 anyadezIyA yihUdIyAsteSAm adhipatayazca daurAtmyaM kutvA tau prastarairAhantum udyatAH|
Pamenepo anthu a mitundu ina ndi Ayuda, pamodzi ndi atsogoleri awo anakonza chiwembu choti azunze atumwiwo ndi kuwagenda ndi miyala.
6 tau tadvArttAM prApya palAyitvA lukAyaniyAdezasyAntarvvarttilustrAdarbbo
Koma atazindikira zimenezi, anathawira ku Lusitra ndi Derbe, mizinda ya ku Lukaoniya, ndiponso ku dziko lozungulira mizindayo,
7 tatsamIpasthadezaJca gatvA tatra susaMvAdaM pracArayatAM|
kumene anapitiriza kulalikira Uthenga Wabwino.
8 tatrobhayapAdayozcalanazaktihIno janmArabhya khaJjaH kadApi gamanaM nAkarot etAdRza eko mAnuSo lustrAnagara upavizya paulasya kathAM zrutavAn|
Ku Lusitra kunali munthu wolumala miyendo, amene sanayendepo chibadwire chake.
9 etasmin samaye paulastamprati dRSTiM kRtvA tasya svAsthye vizvAsaM viditvA proccaiH kathitavAn
Iyeyu, amamvetsera pamene Paulo amayankhula. Paulo anamuyangʼanitsitsa ndipo anaona kuti anali ndi chikhulupiriro choti achiritsidwe nacho.
10 padbhyAmuttiSThan Rju rbhava|tataH sa ullamphaM kRtvA gamanAgamane kutavAn|
Ndipo Paulo anamuyitana mofuwula nati, “Imirira!” Atamva zimenezi, munthuyo anayimirira, nayamba kuyenda.
11 tadA lokAH paulasya tat kAryyaM vilokya lukAyanIyabhASayA proccaiH kathAmetAM kathitavantaH, devA manuSyarUpaM dhRtvAsmAkaM samIpam avArohan|
Gulu la anthu litaona zimene Paulo anachitazi, linafuwula mʼChilukaoniya kuti, “Milungu yatitsikira yooneka ngati anthu!”
12 te barNabbAM yUpitaram avadan paulazca mukhyo vaktA tasmAt taM markuriyam avadan|
Barnaba anamutcha Zeusi ndipo Paulo anamutcha Herimesi chifukwa ndiye amatsogolera kuyankhula.
13 tasya nagarasya sammukhe sthApitasya yUpitaravigrahasya yAjako vRSAn puSpamAlAzca dvArasamIpam AnIya lokaiH sarddhaM tAvuddizya samutsRjya dAtum udyataH|
Wansembe wa Zeusi amene nyumba yopembedzera Zeusiyo inali kunja pafupi ndi mzindawo, anabweretsa ngʼombe yayimuna yovekedwa nkhata za maluwa pa chipata cha mzindawo chifukwa iyeyo pamodzi ndi anthu ena onse aja amafuna kudzipereka nsembe kwa Paulo ndi Barnaba.
14 tadvArttAM zrutvA barNabbApaulau svIyavastrANi chitvA lokAnAM madhyaM vegena pravizya proccaiH kathitavantau,
Koma Barnaba ndi Paulo atamva zimenezi, anangʼamba zovala zawo, nathamangira pakati pa gulu la anthuwo, akufuwula kuti,
15 he mahecchAH kuta etAdRzaM karmma kurutha? AvAmapi yuSmAdRzau sukhaduHkhabhoginau manuSyau, yuyam etAH sarvvA vRthAkalpanAH parityajya yathA gagaNavasundharAjalanidhInAM tanmadhyasthAnAM sarvveSAJca sraSTAramamaram IzvaraM prati parAvarttadhve tadartham AvAM yuSmAkaM sannidhau susaMvAdaM pracArayAvaH|
“Anthu inu, bwanji mukuchita zimenezi? Ifenso ndife anthu monga inu nomwe. Ife takubweretserani Uthenga Wabwino, kuti musiye zinthu zachabezi ndi kutsata Mulungu wamoyo, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo.
16 sa IzvaraH pUrvvakAle sarvvadezIyalokAn svasvamArge calitumanumatiM dattavAn,
Kale Iye analola anthu a mitundu ina yonse kutsata njira zawozawo.
17 tathApi AkAzAt toyavarSaNena nAnAprakArazasyotpatyA ca yuSmAkaM hitaiSI san bhakSyairAnanadena ca yuSmAkam antaHkaraNAni tarpayan tAni dAnAni nijasAkSisvarUpANi sthapitavAn|
Komabe wakhala akudzichitira yekha umboni: Iye amaonetsa kukoma mtima kwake pogwetsa mvula kuchokera kumwamba ndi zipatso pa nyengo yake. Amakupatsani chakudya chambiri ndipo amadzaza mitima yanu ndi chimwemwe.”
18 kintu tAdRzAyAM kathAyAM kathitAyAmapi tayoH samIpa utsarjanAt lokanivahaM prAyeNa nivarttayituM nAzaknutAm|
Ngakhale ndi mawu awa, anavutika kuletsa gulu la anthu kuti asapereke nsembe kwa iwo.
19 AntiyakhiyA-ikaniyanagarAbhyAM katipayayihUdIyalokA Agatya lokAn prAvarttayanta tasmAt tai paulaM prastarairAghnan tena sa mRta iti vijJAya nagarasya bahistam AkRSya nItavantaH|
Kenaka kunabwera Ayuda ena kuchokera ku Antiokeya ndi Ikoniya nakopa gulu la anthu lija. Iwo anamugenda miyala Paulo namukokera kunja kwa mzindawo, kuganiza kuti wafa.
20 kintu ziSyagaNe tasya caturdizi tiSThati sati sa svayam utthAya punarapi nagaramadhyaM prAvizat tatpare'hani barNabbAsahito darbbInagaraM gatavAn|
Koma ophunzira atamuzungulira, Pauloyo anayimirira nalowanso mu mzindawo. Mmawa mwake iye ndi Barnaba anachoka ndi kupita ku Derbe.
21 tatra susaMvAdaM pracAryya bahulokAn ziSyAn kRtvA tau lustrAm ikaniyam AntiyakhiyAJca parAvRtya gatau|
Iwo analalikira Uthenga Wabwino mu mzindawo ndipo anthu ambiri anatembenuka mtima ndi kukhala ophunzira. Kenaka anabwerera ku Lusitra, ku Ikoniya ndi ku Antiokeya.
22 bahuduHkhAni bhuktvApIzvararAjyaM praveSTavyam iti kAraNAd dharmmamArge sthAtuM vinayaM kRtvA ziSyagaNasya manaHsthairyyam akurutAM|
Kumeneko analimbikitsa mitima ya ophunzira ndi kuwapatsa mphamvu kuti akhalebe woona mʼchikhulupiriro. Iwo anati, “Ife tiyenera kudutsa mʼmasautso ambiri kuti tikalowe mu ufumu wa Mulungu.”
23 maNDalInAM prAcInavargAn niyujya prArthanopavAsau kRtvA yatprabhau te vyazvasan tasya haste tAn samarpya
Paulo ndi Barnaba anasankha akulu ampingo pa mpingo uliwonse, ndipo atapemphera ndi kusala kudya anawapereka kwa Ambuye amene anamukhulupirira.
24 pisidiyAmadhyena pAmphuliyAdezaM gatavantau|
Atadutsa Pisidiya, anafika ku Pamfiliya.
25 pazcAt pargAnagaraM gatvA susaMvAdaM pracAryya attAliyAnagaraM prasthitavantau|
Atalalikira Mawu ku Perga, anapita ku Ataliya.
26 tasmAt samudrapathena gatvA tAbhyAM yat karmma sampannaM tatkarmma sAdhayituM yannagare dayAlorIzvarasya haste samarpitau jAtau tad AntiyakhiyAnagaraM gatavantA|
Ku Ataliyako, anakwera sitima ya pamadzi kubwerera ku Antiokeya kumene anayitanidwa mwachisomo cha Mulungu kuti agwire ntchito imene tsopano anali atayitsiriza.
27 tatropasthAya tannagarasthamaNDalIM saMgRhya svAbhyAma Izvaro yadyat karmmakarot tathA yena prakAreNa bhinnadezIyalokAn prati vizvAsarUpadvAram amocayad etAn sarvvavRttAntAn tAn jJApitavantau|
Atangofika ku Antiokeya, anasonkhanitsa pamodzi mpingo ndipo anafotokoza zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo ndiponso mmene Iye anatsekulira a mitundu ina njira ya chikhulupiriro.
28 tatastau ziryyaiH sArddhaM tatra bahudinAni nyavasatAm|
Ndipo anakhala kumeneko ndi ophunzira nthawi yayitali.

< preritAH 14 >