< preritAH 1 >

1 he thiyaphila, yIzuH svamanonItAn preritAn pavitreNAtmanA samAdizya yasmin dine svargamArohat yAM yAM kriyAmakarot yadyad upAdizacca tAni sarvvANi pUrvvaM mayA likhitAni|
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 sa svanidhanaduHkhabhogAt param anekapratyayakSapramANauH svaM sajIvaM darzayitvA
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 catvAriMzaddinAni yAvat tebhyaH preritebhyo darzanaM dattvezvarIyarAjyasya varNanama akarot|
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 anantaraM teSAM sabhAM kRtvA ityAjJApayat, yUyaM yirUzAlamo'nyatra gamanamakRtvA yastin pitrAGgIkRte mama vadanAt kathA azRNuta tatprAptim apekSya tiSThata|
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 yohan jale majjitAvAn kintvalpadinamadhye yUyaM pavitra Atmani majjitA bhaviSyatha|
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 pazcAt te sarvve militvA tam apRcchan he prabho bhavAn kimidAnIM punarapi rAjyam isrAyelIyalokAnAM kareSu samarpayiSyati?
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 tataH sovadat yAn sarvvAn kAlAn samayAMzca pitA svavaze'sthApayat tAn jJAtRM yuSmAkam adhikAro na jAyate|
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 kintu yuSmAsu pavitrasyAtmana AvirbhAve sati yUyaM zaktiM prApya yirUzAlami samastayihUdAzomiroNadezayoH pRthivyAH sImAM yAvad yAvanto dezAsteSu yarvveSu ca mayi sAkSyaM dAsyatha|
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 iti vAkyamuktvA sa teSAM samakSaM svargaM nIto'bhavat, tato meghamAruhya teSAM dRSTeragocaro'bhavat|
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 yasmin samaye te vihAyasaM pratyananyadRSTyA tasya tAdRzam Urdvvagamanam apazyan tasminneva samaye zuklavastrau dvau janau teSAM sannidhau daNDAyamAnau kathitavantau,
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 he gAlIlIyalokA yUyaM kimarthaM gagaNaM prati nirIkSya daNDAyamAnAstiSThatha? yuSmAkaM samIpAt svargaM nIto yo yIzustaM yUyaM yathA svargam Arohantam adarzam tathA sa punazcAgamiSyati|
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 tataH paraM te jaitunanAmnaH parvvatAd vizrAmavArasya pathaH parimANam arthAt prAyeNArddhakrozaM durasthaM yirUzAlamnagaraM parAvRtyAgacchan|
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 nagaraM pravizya pitaro yAkUb yohan AndriyaH philipaH thomA barthajamayo mathirAlphIyaputro yAkUb udyogA zimon yAkUbo bhrAtA yihUdA ete sarvve yatra sthAne pravasanti tasmin uparitanaprakoSThe prAvizan|
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 pazcAd ime kiyatyaH striyazca yIzo rmAtA mariyam tasya bhrAtarazcaite sarvva ekacittIbhUta satataM vinayena vinayena prArthayanta|
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 tasmin samaye tatra sthAne sAkalyena viMzatyadhikazataM ziSyA Asan| tataH pitarasteSAM madhye tiSThan uktavAn
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 he bhrAtRgaNa yIzudhAriNAM lokAnAM pathadarzako yo yihUdAstasmin dAyUdA pavitra AtmA yAM kathAM kathayAmAsa tasyAH pratyakSIbhavanasyAvazyakatvam AsIt|
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 sa jano'smAkaM madhyavarttI san asyAH sevAyA aMzam alabhata|
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 tadanantaraM kukarmmaNA labdhaM yanmUlyaM tena kSetramekaM krItam aparaM tasmin adhomukhe bhRmau patite sati tasyodarasya vidIrNatvAt sarvvA nADyo niragacchan|
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 etAM kathAM yirUzAlamnivAsinaH sarvve lokA vidAnti; teSAM nijabhASayA tatkSetraJca hakaldAmA, arthAt raktakSetramiti vikhyAtamAste|
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 anyacca, niketanaM tadIyantu zunyameva bhaviSyati| tasya dUSye nivAsArthaM kopi sthAsyati naiva hi| anya eva janastasya padaM saMprApsyati dhruvaM| itthaM gItapustake likhitamAste|
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 ato yohano majjanam ArabhyAsmAkaM samIpAt prabho ryIzoH svargArohaNadinaM yAvat sosmAkaM madhye yAvanti dinAni yApitavAn
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 tAvanti dinAni ye mAnavA asmAbhiH sArddhaM tiSThanti teSAm ekena janenAsmAbhiH sArddhaM yIzorutthAne sAkSiNA bhavitavyaM|
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 ato yasya rUDhi ryuSTo yaM barzabbetyuktvAhUyanti sa yUSaph matathizca dvAvetau pRthak kRtvA ta Izvarasya sannidhau prAryya kathitavantaH,
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 he sarvvAntaryyAmin paramezvara, yihUdAH sevanapreritatvapadacyutaH
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 san nijasthAnam agacchat, tatpadaM labdhum enayo rjanayo rmadhye bhavatA ko'bhirucitastadasmAn darzyatAM|
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 tato guTikApATe kRte matathirniracIyata tasmAt sonyeSAm ekAdazAnAM praritAnAM madhye gaNitobhavat|
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

< preritAH 1 >