< 1 tImathiyaH 6 >
1 yAvanto lokA yugadhAriNo dAsAH santi te svasvasvAminaM pUrNasamAdarayogyaM manyantAM no ced Izvarasya nAmna upadezasya ca nindA sambhaviSyati|
Onse amene ali mu ukapolo ayenera kuona ambuye awo ngati oyenera kuwachitira ulemu, kuti anthu anganyoze dzina la Mulungu ndi chiphunzitso chathu.
2 yeSAJca svAmino vizvAsinaH bhavanti taiste bhrAtRtvAt nAvajJeyAH kintu te karmmaphalabhogino vizvAsinaH priyAzca bhavantIti hetoH sevanIyA eva, tvam etAni zikSaya samupadiza ca|
Amene ambuye awo ndi okhulupirira, asawapeputse chifukwa ambuye ndi abale mʼchikhulupiriro. Mʼmalo mwake akuyenera kuwatumikira bwino chifukwa ambuye wawo ndi okondedwa monga okhulupirira ndiponso ndi odzipereka kusamalira akapolo awo. Zinthu izi ukuyenera kuziphunzitsa ndi kuwalamula anthu.
3 yaH kazcid itarazikSAM karoti, asmAkaM prabho ryIzukhrISTasya hitavAkyAnIzvarabhakte ryogyAM zikSAJca na svIkaroti
Ngati wina aphunzitsa zosiyana ndi zimenezi, wosagwirizana ndi malangizo woona a Ambuye athu Yesu Khristu ndi chiphunzitso cholemekeza Mulungu,
4 sa darpadhmAtaH sarvvathA jJAnahInazca vivAdai rvAgyuddhaizca rogayuktazca bhavati|
ameneyo ndi wodzitukumula ndipo sakudziwa chilichonse. Iyeyo ali ndi maganizo oyipa, wokonda kusemphana mawu ndi kutsutsana. Zimenezi zimabweretsa nsanje, mikangano, mʼnyozo, kuganizirana zoyipa,
5 tAdRzAd bhAvAd IrSyAvirodhApavAdaduSTAsUyA bhraSTamanasAM satyajJAnahInAnAm IzvarabhaktiM lAbhopAyam iva manyamAnAnAM lokAnAM vivAdAzca jAyante tAdRzebhyo lokebhyastvaM pRthak tiSTha|
ndi kulimbana kosatha pakati pa anthu amitima yopotoka amene alandidwa choonadi ndipo amaganiza kuti kulemekeza Mulungu ndi njira yopezera chuma.
6 saMyatecchayA yuktA yezvarabhaktiH sA mahAlAbhopAyo bhavatIti satyaM|
Koma kulemekeza Mulungu kuli ndi phindu lalikulu.
7 etajjagatpravezanakAle'smAbhiH kimapi nAnAyi tattayajanakAle'pi kimapi netuM na zakSyata iti nizcitaM|
Pakuti sitinabweretse kanthu mʼdziko lapansi, ndipo sitingatengenso kanthu pochoka mʼdziko lapansi.
8 ataeva khAdyAnyAcchAdanAni ca prApyAsmAbhiH santuSTai rbhavitavyaM|
Koma ngati tili ndi chakudya ndi zovala, zimenezi zitikwanire.
9 ye tu dhanino bhavituM ceSTante te parIkSAyAm unmAthe patanti ye cAbhilASA mAnavAn vinAze narake ca majjayanti tAdRzeSvajJAnAhitAbhilASeSvapi patanti|
Anthu amene amafuna kulemera amagwa mʼmayesero ndi mu msampha ndi mʼzilakolako zambiri zopusa ndi zoopsa zimene zimagwetsera anthu mʼchitayiko ndi mʼchiwonongeko.
10 yato'rthaspRhA sarvveSAM duritAnAM mUlaM bhavati tAmavalambya kecid vizvAsAd abhraMzanta nAnAklezaizca svAn avidhyan|
Pakuti kukonda ndalama ndiye muzu wa zoyipa za mitundu yonse. Anthu ena ofunitsitsa ndalama, asochera ndipo asiya njira yachikhulupiriro ndipo adzitengera zowawitsa zambiri.
11 he Izvarasya loka tvam etebhyaH palAyya dharmma Izvarabhakti rvizvAsaH prema sahiSNutA kSAntizcaitAnyAcara|
Koma iwe, munthu wa Mulungu, thawa zinthu zonsezi. Tsatira chilungamo, moyo wolemekeza Mulungu, chikhulupiriro, chikondi, kupirira ndi kufatsa.
12 vizvAsarUpam uttamayuddhaM kuru, anantajIvanam Alambasva yatastadarthaM tvam AhUto 'bhavaH, bahusAkSiNAM samakSaJcottamAM pratijJAM svIkRtavAn| (aiōnios )
Menya nkhondo yabwino yachikhulupiriro. Gwiritsitsa moyo wosatha umene anakuyitanira pamene unavomereza bwino lomwe pamaso pa mboni zambiri. (aiōnios )
13 aparaM sarvveSAM jIvayiturIzvarasya sAkSAd yazca khrISTo yIzuH pantIyapIlAtasya samakSam uttamAM pratijJAM svIkRtavAn tasya sAkSAd ahaM tvAm idam AjJApayAmi|
Ndikukulamula pamaso pa Mulungu amene amapatsa moyo zinthu zonse, ndiponso pamaso pa Khristu Yesu amene pochitira umboni pamaso pa Pontiyo Pilato, ananena zoona zenizeni.
14 IzvareNa svasamaye prakAzitavyam asmAkaM prabho ryIzukhrISTasyAgamanaM yAvat tvayA niSkalaGkatvena nirddoSatvena ca vidhI rakSyatAM|
Usunge lamuloli mopanda banga ndi cholakwa kufikira Ambuye athu Yesu Khristu ataonekera.
15 sa IzvaraH saccidAnandaH, advitIyasamrAT, rAjJAM rAjA, prabhUnAM prabhuH,
Pa nthawi yake Mulungu adzamubweretsa kwa ife. Mulungu ndi wodalitsika ndipo Iye yekha ndiye Wolamulira, Mfumu ya mafumu, Mbuye wa ambuye.
16 amaratAyA advitIya AkaraH, agamyatejonivAsI, marttyAnAM kenApi na dRSTaH kenApi na dRzyazca| tasya gauravaparAkramau sadAtanau bhUyAstAM| Amen| (aiōnios )
Ndiye yekha wosafa ndipo amakhala mʼkuwala koopsa. Mulungu amene munthu aliyense sanamuone. Kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu mpaka muyaya. Ameni. (aiōnios )
17 ihaloke ye dhaninaste cittasamunnatiM capale dhane vizvAsaJca na kurvvatAM kintu bhogArtham asmabhyaM pracuratvena sarvvadAtA (aiōn )
Anthu onse amene ali ndi chuma uwalamule kuti asanyade kapena kuyika mitima yawo pa chuma chimene nʼchosadalirika. Koma chiyembekezo chawo chikhale mwa Mulungu amene amatipatsa mowolowamanja zonse zotisangalatsa. (aiōn )
18 yo'mara Izvarastasmin vizvasantu sadAcAraM kurvvantu satkarmmadhanena dhanino sukalA dAtArazca bhavantu,
Uwalamule kuti azichita zabwino, kuti azikhala olemera pa ntchito zabwino, owolowamanja ndi okonda kugawana zinthu zawo ndi anzawo.
19 yathA ca satyaM jIvanaM pApnuyustathA pAratrikAm uttamasampadaM saJcinvantveti tvayAdizyantAM|
Potero adzadziwunjikira chuma chokhalitsa ngati maziko okhazikika a nthawi zakutsogolo, kuti akalandire moyo, umene ndi moyo weniweni.
20 he tImathiya, tvam upanidhiM gopaya kAlpanikavidyAyA apavitraM pralApaM virodhoktiJca tyaja ca,
Timoteyo, samalitsa zimene unapatsidwa. Upewe nkhani zopanda pake zosalemekeza Mulungu ndiponso maganizo otsutsana amene amaganizidwa molakwika kuti ndi nzeru.
21 yataH katipayA lokAstAM vidyAmavalambya vizvAsAd bhraSTA abhavana| prasAdastava sahAyo bhUyAt| Amen|
Anthu ena chifukwa chovomereza nzeru zotere, asochera nʼkutaya chikhulupiriro chawo. Chisomo chikhale nawe.