< lUkaH 16 >
1 aparanjca yIzuH ziSyEbhyOnyAmEkAM kathAM kathayAmAsa kasyacid dhanavatO manuSyasya gRhakAryyAdhIzE sampattErapavyayE'pavAditE sati
Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho.
2 tasya prabhustam AhUya jagAda, tvayi yAmimAM kathAM zRNOmi sA kIdRzI? tvaM gRhakAryyAdhIzakarmmaNO gaNanAM darzaya gRhakAryyAdhIzapadE tvaM na sthAsyasi|
Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’
3 tadA sa gRhakAryyAdhIzO manasA cintayAmAsa, prabhu ryadi mAM gRhakAryyAdhIzapadAd bhraMzayati tarhi kiM kariSyE'haM? mRdaM khanituM mama zakti rnAsti bhikSitunjca lajjiSyE'haM|
“Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha.
4 ataEva mayi gRhakAryyAdhIzapadAt cyutE sati yathA lOkA mahyam AzrayaM dAsyanti tadarthaM yatkarmma mayA karaNIyaM tan nirNIyatE|
Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’
5 pazcAt sa svaprabhOrEkaikam adhamarNam AhUya prathamaM papraccha, tvattO mE prabhuNA kati prApyam?
“Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’
6 tataH sa uvAca, EkazatAPhakatailAni; tadA gRhakAryyAdhIzaH prOvAca, tava patramAnIya zIghramupavizya tatra panjcAzataM likha|
“Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’ “Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’
7 pazcAdanyamEkaM papraccha, tvattO mE prabhuNA kati prApyam? tataH sOvAdId EkazatAPhakagOdhUmAH; tadA sa kathayAmAsa, tava patramAnIya azItiM likha|
“Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’ “Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000. “Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’
8 tEnaiva prabhustamayathArthakRtam adhIzaM tadbuddhinaipuNyAt prazazaMsa; itthaM dIptirUpasantAnEbhya EtatsaMsArasya santAnA varttamAnakAlE'dhikabuddhimantO bhavanti| (aiōn )
“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. (aiōn )
9 atO vadAmi yUyamapyayathArthEna dhanEna mitrANi labhadhvaM tatO yuSmAsu padabhraSTESvapi tAni cirakAlam AzrayaM dAsyanti| (aiōnios )
Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya. (aiōnios )
10 yaH kazcit kSudrE kAryyE vizvAsyO bhavati sa mahati kAryyEpi vizvAsyO bhavati, kintu yaH kazcit kSudrE kAryyE'vizvAsyO bhavati sa mahati kAryyEpyavizvAsyO bhavati|
“Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri.
11 ataEva ayathArthEna dhanEna yadi yUyamavizvAsyA jAtAstarhi satyaM dhanaM yuSmAkaM karESu kaH samarpayiSyati?
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni?
12 yadi ca paradhanEna yUyam avizvAsyA bhavatha tarhi yuSmAkaM svakIyadhanaM yuSmabhyaM kO dAsyati?
Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?
13 kOpi dAsa ubhau prabhU sEvituM na zaknOti, yata Ekasmin prIyamANO'nyasminnaprIyatE yadvA EkaM janaM samAdRtya tadanyaM tucchIkarOti tadvad yUyamapi dhanEzvarau sEvituM na zaknutha|
“Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”
14 tadaitAH sarvvAH kathAH zrutvA lObhiphirUzinastamupajahasuH|
Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu.
15 tataH sa uvAca, yUyaM manuSyANAM nikaTE svAn nirdOSAn darzayatha kintu yuSmAkam antaHkaraNAnIzvarO jAnAti, yat manuSyANAm ati prazaMsyaM tad Izvarasya ghRNyaM|
Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.
16 yOhana AgamanaparyyanataM yuSmAkaM samIpE vyavasthAbhaviSyadvAdinAM lEkhanAni cAsan tataH prabhRti IzvararAjyasya susaMvAdaH pracarati, EkaikO lOkastanmadhyaM yatnEna pravizati ca|
“Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo.
17 varaM nabhasaH pRthivyAzca lOpO bhaviSyati tathApi vyavasthAyA EkabindOrapi lOpO na bhaviSyati|
Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.
18 yaH kazcit svIyAM bhAryyAM vihAya striyamanyAM vivahati sa paradArAn gacchati, yazca tA tyaktAM nArIM vivahati sOpi paradArAna gacchati|
“Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”
19 EkO dhanI manuSyaH zuklAni sUkSmANi vastrANi paryyadadhAt pratidinaM paritOSarUpENAbhuMktApivacca|
“Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse.
20 sarvvAggE kSatayukta iliyAsaranAmA kazcid daridrastasya dhanavatO bhOjanapAtrAt patitam ucchiSTaM bhOktuM vAnjchan tasya dvArE patitvAtiSThat;
Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse
21 atha zvAna Agatya tasya kSatAnyalihan|
ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.
22 kiyatkAlAtparaM sa daridraH prANAn jahau; tataH svargIyadUtAstaM nItvA ibrAhImaH krOPa upavEzayAmAsuH|
“Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda.
23 pazcAt sa dhanavAnapi mamAra, taM zmazAnE sthApayAmAsuzca; kintu paralOkE sa vEdanAkulaH san UrddhvAM nirIkSya bahudUrAd ibrAhImaM tatkrOPa iliyAsaranjca vilOkya ruvannuvAca; (Hadēs )
Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. (Hadēs )
24 hE pitar ibrAhIm anugRhya aggulyagrabhAgaM jalE majjayitvA mama jihvAM zItalAM karttum iliyAsaraM prEraya, yatO vahnizikhAtOhaM vyathitOsmi|
Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’
25 tadA ibrAhIm babhASE, hE putra tvaM jIvan sampadaM prAptavAn iliyAsarastu vipadaM prAptavAn Etat smara, kintu samprati tasya sukhaM tava ca duHkhaM bhavati|
“Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo.
26 aparamapi yuSmAkam asmAkanjca sthAnayO rmadhyE mahadvicchEdO'sti tata EtatsthAnasya lOkAstat sthAnaM yAtuM yadvA tatsthAnasya lOkA Etat sthAnamAyAtuM na zaknuvanti|
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’
27 tadA sa uktavAn, hE pitastarhi tvAM nivEdayAmi mama pitu rgEhE yE mama panjca bhrAtaraH santi
“Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga,
28 tE yathaitad yAtanAsthAnaM nAyAsyanti tathA mantraNAM dAtuM tESAM samIpam iliyAsaraM prEraya|
pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’
29 tata ibrAhIm uvAca, mUsAbhaviSyadvAdinAnjca pustakAni tESAM nikaTE santi tE tadvacanAni manyantAM|
“Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’
30 tadA sa nivEdayAmAsa, hE pitar ibrAhIm na tathA, kintu yadi mRtalOkAnAM kazcit tESAM samIpaM yAti tarhi tE manAMsi vyAghOTayiSyanti|
“Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’
31 tata ibrAhIm jagAda, tE yadi mUsAbhaviSyadvAdinAnjca vacanAni na manyantE tarhi mRtalOkAnAM kasmiMzcid utthitEpi tE tasya mantraNAM na maMsyantE|
“Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’”