< ရောမိဏး 8 >

1 ယေ ဇနား ခြီၐ္ဋံ ယီၑုမ် အာၑြိတျ ၑာရီရိကံ နာစရန္တ အာတ္မိကမာစရန္တိ တေ'ဓုနာ ဒဏ္ဍာရှာ န ဘဝန္တိ၊
Choncho, tsopano amene ali mwa Khristu Yesu alibe mlandu owatsutsa
2 ဇီဝနဒါယကသျာတ္မနော ဝျဝသ္ထာ ခြီၐ္ဋယီၑုနာ ပါပမရဏယော ရွျဝသ္ထာတော မာမမောစယတ်၊
chifukwa mwa Khristu Yesu, lamulo la Mzimu Woyera amene amapereka moyo, lawamasula ku lamulo la tchimo ndi la imfa.
3 ယသ္မာစ္ဆာရီရသျ ဒုရ္ဗ္ဗလတွာဒ် ဝျဝသ္ထယာ ယတ် ကရ္မ္မာသာဓျမ် ဤၑွရော နိဇပုတြံ ပါပိၑရီရရူပံ ပါပနာၑကဗလိရူပဉ္စ ပြေၐျ တသျ ၑရီရေ ပါပသျ ဒဏ္ဍံ ကုရွွန် တတ္ကရ္မ္မ သာဓိတဝါန်၊
Pakuti zimene Malamulo sanathe kuzichita, popeza anali ofowoka chifukwa cha khalidwe lathu la uchimo, Mulungu anazichita potumiza Mwana wake mʼchifanizo cha munthu ochimwa kuti akhale nsembe yauchimo. Ndipo Iye anagonjetsa tchimo mʼthupi la munthu,
4 တတး ၑာရီရိကံ နာစရိတွာသ္မာဘိရာတ္မိကမ် အာစရဒ္ဘိရွျဝသ္ထာဂြန္ထေ နိရ္ဒ္ဒိၐ္ဋာနိ ပုဏျကရ္မ္မာဏိ သရွွာဏိ သာဓျန္တေ၊
ndi cholinga chakuti chilungamo chofunikira cha lamulo chikwaniritsidwe kwathunthu mwa ife amene sitikhala monga mwachikhalidwe chathu cha uchimo koma mwa Mzimu.
5 ယေ ၑာရီရိကာစာရိဏသ္တေ ၑာရီရိကာန် ဝိၐယာန် ဘာဝယန္တိ ယေ စာတ္မိကာစာရိဏသ္တေ အာတ္မနော ဝိၐယာန် ဘာဝယန္တိ၊
Pakuti anthu amene amakhala monga mwa makhalidwe oyipa a thupi amayika malingaliro awo pa zinthu zathupi. Koma amene amakhala monga mwa Mzimu amayika malingaliro awo pa zinthu za Mzimu.
6 ၑာရီရိကဘာဝသျ ဖလံ မၖတျုး ကိဉ္စာတ္မိကဘာဝသျ ဖလေ ဇီဝနံ ၑာန္တိၑ္စ၊
Kuyika mtima pa zathupi ndi imfa koma kuyika mtima pa za Mzimu ndi moyo ndi mtendere.
7 ယတး ၑာရီရိကဘာဝ ဤၑွရသျ ဝိရုဒ္ဓး ၑတြုတာဘာဝ ဧဝ သ ဤၑွရသျ ဝျဝသ္ထာယာ အဓီနော န ဘဝတိ ဘဝိတုဉ္စ န ၑက္နောတိ၊
Pakuti mtima umene wakhazikika pa zathupi ndi wodana ndi Mulungu. Sunagonjere lamulo la Mulungu ndipo sungathe kutero.
8 ဧတသ္မာတ် ၑာရီရိကာစာရိၐု တောၐ္ဋုမ် ဤၑွရေဏ န ၑကျံ၊
Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.
9 ကိန္တွီၑွရသျာတ္မာ ယဒိ ယုၐ္မာကံ မဓျေ ဝသတိ တရှိ ယူယံ ၑာရီရိကာစာရိဏော န သန္တ အာတ္မိကာစာရိဏော ဘဝထး၊ ယသ္မိန် တု ခြီၐ္ဋသျာတ္မာ န ဝိဒျတေ သ တတ္သမ္ဘဝေါ နဟိ၊
Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lauchimo koma ndi Mzimu ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu si wa Khristu.
10 ယဒိ ခြီၐ္ဋော ယုၐ္မာန် အဓိတိၐ္ဌတိ တရှိ ပါပမ် ဥဒ္ဒိၑျ ၑရီရံ မၖတံ ကိန္တု ပုဏျမုဒ္ဒိၑျာတ္မာ ဇီဝတိ၊
Ndipo ngati Khristu ali mwa inu, thupi lanu ndi lakufa chifukwa cha uchimo, koma mzimu wanu ndi wamoyo chifukwa cha chilungamo.
11 မၖတဂဏာဒ် ယီၑု ရျေနောတ္ထာပိတသ္တသျာတ္မာ ယဒိ ယုၐ္မန္မဓျေ ဝသတိ တရှိ မၖတဂဏာတ် ခြီၐ္ဋသျ သ ဥတ္ထာပယိတာ ယုၐ္မန္မဓျဝါသိနာ သွကီယာတ္မနာ ယုၐ္မာကံ မၖတဒေဟာနပိ ပုန ရ္ဇီဝယိၐျတိ၊
Ndipo ngati Mzimu wa Mulungu amene anaukitsa Yesu kwa akufa akhala mwa inu, Iyeyo amene anaukitsa Khristu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu amene amafa kudzera mwa Mzimu wake amene amakhala mwa inu.
12 ဟေ ဘြာတၖဂဏ ၑရီရသျ ဝယမဓမရ္ဏာ န ဘဝါမော'တး ၑာရီရိကာစာရော'သ္မာဘိ ရ္န ကရ္တ္တဝျး၊
Kotero abale, ife tili ndi zoti tikwaniritse, koma osati za khalidwe lathu lauchimo, kumachita zofuna zake.
13 ယဒိ ယူယံ ၑရီရိကာစာရိဏော ဘဝေတ တရှိ ယုၐ္မာဘိ ရ္မရ္တ္တဝျမေဝ ကိန္တွာတ္မနာ ယဒိ ၑရီရကရ္မ္မာဏိ ဃာတယေတ တရှိ ဇီဝိၐျထ၊
Pakuti ngati inu mukhala monga mwa khalidwe lauchimo, mudzafa. Koma ngati mwa Mzimu mupha ntchito zoyipa zathupi, mudzakhala ndi moyo.
14 ယတော ယာဝန္တော လောကာ ဤၑွရသျာတ္မနာကၖၐျန္တေ တေ သရွွ ဤၑွရသျ သန္တာနာ ဘဝန္တိ၊
Onse amene amatsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu ndi ana a Mulungu.
15 ယူယံ ပုနရပိ ဘယဇနကံ ဒါသျဘာဝံ န ပြာပ္တား ကိန္တု ယေန ဘာဝေနေၑွရံ ပိတး ပိတရိတိ ပြောစျ သမ္ဗောဓယထ တာဒၖၑံ ဒတ္တကပုတြတွဘာဝမ် ပြာပ္နုတ၊
Mzimu amene inu munalandira samakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha, koma Mzimu amakusandutsani ana. Ndipo mwa Iye ife timafuwula kuti, “Abba, Atate.”
16 အပရဉ္စ ဝယမ် ဤၑွရသျ သန္တာနာ ဧတသ္မိန် ပဝိတြ အာတ္မာ သွယမ် အသ္မာကမ် အာတ္မာဘိး သာရ္ဒ္ဓံ ပြမာဏံ ဒဒါတိ၊
Mzimu mwini amavomerezana ndi mzimu wathu kuti ife ndife ana a Mulungu.
17 အတဧဝ ဝယံ ယဒိ သန္တာနာသ္တရှျဓိကာရိဏး, အရ္ထာဒ် ဤၑွရသျ သွတ္တွာဓိကာရိဏး ခြီၐ္ဋေန သဟာဓိကာရိဏၑ္စ ဘဝါမး; အပရံ တေန သာရ္ဒ္ဓံ ယဒိ ဒုးခဘာဂိနော ဘဝါမသ္တရှိ တသျ ဝိဘဝသျာပိ ဘာဂိနော ဘဝိၐျာမး၊
Tsono ngati tili ana ake, ndiye kuti ndife olowa mʼmalo a Mulungu ndi olowa mʼmalo pamodzi ndi Khristu. Ngati ife timva zowawa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye.
18 ကိန္တွသ္မာသု ယော ဘာဝီဝိဘဝး ပြကာၑိၐျတေ တသျ သမီပေ ဝရ္တ္တမာနကာလီနံ ဒုးခမဟံ တၖဏာယ မနျေ၊
Ine ndiganiza kuti masautso amene tikuwamva nthawi ino, sakufanana ndi ulemerero umene udzaonetsedwa mwa ife.
19 ယတး ပြာဏိဂဏ ဤၑွရသျ သန္တာနာနာံ ဝိဘဝပြာပ္တိမ် အာကာင်္က္ၐန် နိတာန္တမ် အပေက္ၐတေ၊
Pakuti chilengedwe chikudikira ndi chiyembekezo kuonetsedwa poyera kwa ana a Mulungu.
20 အပရဉ္စ ပြာဏိဂဏး သွဲရမ် အလီကတာယာ ဝၑီကၖတော နာဘဝတ္
Pakuti chilengedwe sichinasankhe kugonjera zopanda pake, koma mwachifuniro cha Iye amene analola kuti chigonjere. Koma chili ndi chiyembekezo
21 ကိန္တု ပြာဏိဂဏော'ပိ နၑွရတာဓီနတွာတ် မုက္တး သန် ဤၑွရသျ သန္တာနာနာံ ပရမမုက္တိံ ပြာပ္သျတီတျဘိပြာယေဏ ဝၑီကရ္တြာ ဝၑီစကြေ၊
chakuti chidzamasulidwa ku ukapolo wa chivundi ndi kulandiranso ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu.
22 အပရဉ္စ ပြသူယမာနာဝဒ် ဝျထိတး သန် ဣဒါနီံ ယာဝတ် ကၖတ္သ္နး ပြာဏိဂဏ အာရ္တ္တသွရံ ကရောတီတိ ဝယံ ဇာနီမး၊
Ife tikudziwa kuti chilengedwe chonse chakhala chikubuwula ndi ululu ngati ululu wa nthawi yobereka mwana mpaka tsopano lino.
23 ကေဝလး သ ဣတိ နဟိ ကိန္တု ပြထမဇာတဖလသွရူပမ် အာတ္မာနံ ပြာပ္တာ ဝယမပိ ဒတ္တကပုတြတွပဒပြာပ္တိမ် အရ္ထာတ် ၑရီရသျ မုက္တိံ ပြတီက္ၐမာဏာသ္တဒွဒ် အန္တရာရ္တ္တရာဝံ ကုရ္မ္မး၊
Si zokhazo ayi, ngakhale ife tomwe, amene tili ndi zipatso zoyamba za Mzimu, tikubuwulira mʼkati mwathu pomwe tikudikira mwachidwi kusankhidwa kwathu ngati ana, kuwomboledwa kwa matupi athu.
24 ဝယံ ပြတျာၑယာ တြာဏမ် အလဘာမဟိ ကိန္တု ပြတျက္ၐဝသ္တုနော ယာ ပြတျာၑာ သာ ပြတျာၑာ နဟိ, ယတော မနုၐျော ယတ် သမီက္ၐတေ တသျ ပြတျာၑာံ ကုတး ကရိၐျတိ?
Pakuti ife tinapulumutsidwa mʼchiyembekezo ichi. Koma chiyembekezo chimene chimaoneka si chiyembekezo ayi. Kodi ndani amene amayembekezera chimene ali nacho kale?
25 ယဒ် အပြတျက္ၐံ တသျ ပြတျာၑာံ ယဒိ ဝယံ ကုရွွီမဟိ တရှိ ဓဲရျျမ် အဝလမ္ဗျ ပြတီက္ၐာမဟေ၊
Koma ngati ife tiyembekeza chimene tikanalibe, ndiye kuti tikuyembekeza modekha mtima.
26 တတ အာတ္မာပိ သွယမ် အသ္မာကံ ဒုရ္ဗ္ဗလတာယား သဟာယတွံ ကရောတိ; ယတး ကိံ ပြာရ္ထိတဝျံ တဒ် ဗောဒ္ဓုံ ဝယံ န ၑက္နုမး, ကိန္တွသ္ပၐ္ဋဲရာရ္တ္တရာဝဲရာတ္မာ သွယမ် အသ္မန္နိမိတ္တံ နိဝေဒယတိ၊
Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa.
27 အပရမ် ဤၑွရာဘိမတရူပေဏ ပဝိတြလောကာနာံ ကၖတေ နိဝေဒယတိ ယ အာတ္မာ တသျာဘိပြာယော'န္တရျျာမိနာ ဇ္ဉာယတေ၊
Koma Iye amene amasanthula mitima yathu amadziwa maganizo a Mzimu, chifukwa Mzimu amapempherera oyera mtima molingana ndi chifuniro cha Mulungu.
28 အပရမ် ဤၑွရီယနိရူပဏာနုသာရေဏာဟူတား သန္တော ယေ တသ္မိန် ပြီယန္တေ သရွွာဏိ မိလိတွာ တေၐာံ မင်္ဂလံ သာဓယန္တိ, ဧတဒ် ဝယံ ဇာနီမး၊
Ndipo ife tikudziwa kuti zinthu zonse zimathandizana kuwachitira ubwino amene amakonda Mulungu, amene anayitanidwa monga mwa cholinga chake.
29 ယတ ဤၑွရော ဗဟုဘြာတၖဏာံ မဓျေ သွပုတြံ ဇျေၐ္ဌံ ကရ္တ္တုမ် ဣစ္ဆန် ယာန် ပူရွွံ လက္ၐျီကၖတဝါန် တာန် တသျ ပြတိမူရ္တျား သာဒၖၑျပြာပ္တျရ္ထံ နျယုံက္တ၊
Pakuti amene Mulungu anawadziwiratu, anawasankhiratunso kuti akonzedwe mʼchifanizo cha Mwana wake, kuti Iye akhale Mwana woyamba kubadwa mwa abale ambiri.
30 အပရဉ္စ တေန ယေ နိယုက္တာသ္တ အာဟူတာ အပိ ယေ စ တေနာဟူတာသ္တေ သပုဏျီကၖတား, ယေ စ တေန သပုဏျီကၖတာသ္တေ ဝိဘဝယုက္တား၊
Iwo amene anawasankhiratu, anawayitananso. Amene Iye anawayitana anawalungamitsanso ndipo amene anawalungamitsa anawapatsanso ulemerero.
31 ဣတျတြ ဝယံ ကိံ ဗြူမး? ဤၑွရော ယဒျသ္မာကံ သပက္ၐော ဘဝတိ တရှိ ကော ဝိပက္ၐော'သ္မာကံ?
Nanga tsono tidzanena chiyani pa izi? Ngati Mulungu ali mbali yathu, adzatitsutsa ife ndani?
32 အာတ္မပုတြံ န ရက္ၐိတွာ ယော'သ္မာကံ သရွွေၐာံ ကၖတေ တံ ပြဒတ္တဝါန် သ ကိံ တေန သဟာသ္မဘျမ် အနျာနိ သရွွာဏိ န ဒါသျတိ?
Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anamupereka chifukwa cha ife tonse. Iye adzalekeranjinso pamodzi naye kutipatsa ife zinthu zonse mwaulere?
33 ဤၑွရသျာဘိရုစိတေၐု ကေန ဒေါၐ အာရောပယိၐျတေ? ယ ဤၑွရသ္တာန် ပုဏျဝတ ဣဝ ဂဏယတိ ကိံ တေန?
Ndani amene adzabweretsa mlandu kutsutsa amene Mulungu anawasankha? Ndi Mulungu amene amalungamitsa.
34 အပရံ တေဘျော ဒဏ္ဍဒါနာဇ္ဉာ ဝါ ကေန ကရိၐျတေ? ယော'သ္မန္နိမိတ္တံ ပြာဏာန် တျက္တဝါန် ကေဝလံ တန္န ကိန္တု မၖတဂဏမဓျာဒ် ဥတ္ထိတဝါန်, အပိ စေၑွရသျ ဒက္ၐိဏေ ပါရ္ၑွေ တိၐ္ဌန် အဒျာပျသ္မာကံ နိမိတ္တံ ပြာရ္ထတ ဧဝမ္ဘူတော ယး ခြီၐ္ဋး ကိံ တေန?
Ndani amene angatipeze ife olakwa? Palibe. Khristu Yesu amene anafa, kuposera pamenepo, amene anaukitsidwa ndi moyo, amene ali kudzanja lamanja la Mulungu ndiye amene akutipempherera.
35 အသ္မာဘိး သဟ ခြီၐ္ဋသျ ပြေမဝိစ္ဆေဒံ ဇနယိတုံ ကး ၑက္နောတိ? က္လေၑော ဝျသနံ ဝါ တာဍနာ ဝါ ဒုရ္ဘိက္ၐံ ဝါ ဝသ္တြဟီနတွံ ဝါ ပြာဏသံၑယော ဝါ ခင်္ဂေါ ဝါ ကိမေတာနိ ၑက္နုဝန္တိ?
Ndani amene adzatilekanitsa ife ndi chikondi cha Khristu? Kodi ndi masautso, kapena zowawa, kapena mazunzo, kapena njala, kapena umaliseche, kapena choopsa, kapena lupanga?
36 ကိန္တု လိခိတမ် အာသ္တေ, ယထာ, ဝယံ တဝ နိမိတ္တံ သ္မော မၖတျုဝက္တြေ'ခိလံ ဒိနံ၊ ဗလိရ္ဒေယော ယထာ မေၐော ဝယံ ဂဏျာမဟေ တထာ၊
Monga kwalembedwa: “Chifukwa cha inu, ife tikuphedwa tsiku lonse: ife tikutengedwa ngati nkhosa zoti zikaphedwe.”
37 အပရံ ယော'သ္မာသု ပြီယတေ တေနဲတာသု ဝိပတ္သု ဝယံ သမျဂ် ဝိဇယာမဟေ၊
Ayi, mu zonsezi ife ndife oposa agonjetsi mwa Iye amene anatikonda.
38 ယတော'သ္မာကံ ပြဘုနာ ယီၑုခြီၐ္ဋေနေၑွရသျ ယတ် ပြေမ တသ္မာဒ် အသ္မာကံ ဝိစ္ဆေဒံ ဇနယိတုံ မၖတျု ရ္ဇီဝနံ ဝါ ဒိဝျဒူတာ ဝါ ဗလဝန္တော မုချဒူတာ ဝါ ဝရ္တ္တမာနော ဝါ ဘဝိၐျန် ကာလော ဝါ ဥစ္စပဒံ ဝါ နီစပဒံ ဝါပရံ ကိမပိ သၖၐ္ဋဝသ္တု
Pakuti ine ndatsimikiza ndi mtima wonse kuti ngakhale imfa, kapena moyo, ngakhale angelo, kapena ziwanda, ngakhale zinthu zilipo, kapena zili mʼtsogolo, kapena mphamvu zina,
39 ဝဲတေၐာံ ကေနာပိ န ၑကျမိတျသ္မိန် ဒၖဎဝိၑွာသော မမာသ္တေ၊
ngakhale kutalika, kapena kuya, kapena chilichonse mʼchilengedwe chonse, sizingathe kutisiyanitsa ndi chikondi cha Mulungu chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye athu.

< ရောမိဏး 8 >