< ပြကာၑိတံ 6 >

1 အနန္တရံ မယိ နိရီက္ၐမာဏေ မေၐၑာဝကေန တာသာံ သပ္တမုဒြာဏာမ် ဧကာ မုဒြာ မုက္တာ တတသ္တေၐာံ စတုရ္ဏာမ် ဧကသျ ပြာဏိန အာဂတျ ပၑျေတိဝါစကော မေဃဂရ္ဇနတုလျော ရဝေါ မယာ ၑြုတး၊
Ndinaona pamene Mwana Wankhosa anatsekula chomatira choyamba cha zomatira zisanu ndi ziwiri zija. Ndipo ndinamva chimodzi mwa zamoyo zinayi zija chikunena liwu lomveka ngati bingu kuti, “Bwera!”
2 တတး ပရမ် ဧကး ၑုက္လာၑ္စော ဒၖၐ္ဋး, တဒါရူဎော ဇနော ဓနု ရ္ဓာရယတိ တသ္မဲ စ ကိရီဋမေကမ် အဒါယိ တတး သ ပြဘဝန် ပြဘဝိၐျံၑ္စ နိရ္ဂတဝါန်၊
Nditayangʼana patsogolo pake ndinaona kavalo woyera! Wokwerapo wake anali ndi uta ndipo anapatsidwa chipewa chaufumu, ndipo anatuluka kupita kukagonjetsa anthu ena.
3 အပရံ ဒွိတီယမုဒြာယာံ တေန မောစိတာယာံ ဒွိတီယသျ ပြာဏိန အာဂတျ ပၑျေတိ ဝါက် မယာ ၑြုတာ၊
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachiwiri, ndinamva chamoyo chachiwiri chija chikuti, “Bwera!”
4 တတော 'ရုဏဝရ္ဏော 'ပရ ဧကော 'ၑွော နိရ္ဂတဝါန် တဒါရောဟိဏိ ပၖထိဝီတး ၑာန္တျပဟရဏသျ လောကာနာံ မဓျေ ပရသ္ပရံ ပြတိဃာတောတ္ပာဒနသျ စ သာမရ္ထျံ သမရ္ပိတမ်, ဧကော ဗၖဟတ္ခင်္ဂေါ 'ပိ တသ္မာ အဒါယိ၊
Pamenepo kavalo wina wofiira anatulukira. Wokwerapo wake anapatsidwa mphamvu yochotsa mtendere pa dziko lapansi ndi kuchititsa anthu kuti aziphana wina ndi mnzake. Iyeyu anapatsidwa lupanga lalikulu.
5 အပရံ တၖတီယမုဒြာယာံ တန မောစိတာယာံ တၖတီယသျ ပြာဏိန အာဂတျ ပၑျေတိ ဝါက် မယာ ၑြုတာ, တတး ကာလဝရ္ဏ ဧကော 'ၑွော မယာ ဒၖၐ္ဋး, တဒါရောဟိဏော ဟသ္တေ တုလာ တိၐ္ဌတိ
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachitatu, ndinamva chamoyo chachitatu chikuti, “Bwera!” Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wakuda! Wokwerapo wake anali ndi masikelo awiri mʼmanja mwake.
6 အနန္တရံ ပြာဏိစတုၐ္ဋယသျ မဓျာဒ် ဝါဂိယံ ၑြုတာ ဂေါဓူမာနာမေကး သေဋကော မုဒြာပါဒဲကမူလျး, ယဝါနာဉ္စ သေဋကတြယံ မုဒြာပါဒဲကမူလျံ တဲလဒြာက္ၐာရသာၑ္စ တွယာ မာ ဟိံသိတဝျား၊
Ndinamva ngati liwu kuchokera pakati pa zamoyo zinayi zija likuti, “Kilogalamu imodzi ya tirigu mtengo ndi malipiro a tsiku limodzi ndipo makilogalamu atatu a barele mtengo wake ndi malipiro a tsiku limodzi koma usawononge mafuta ndi vinyo!”
7 အနန္တရံ စတုရ္ထမုဒြာယာံ တေန မောစိတာယာံ စတုရ္ထသျ ပြာဏိန အာဂတျ ပၑျေတိ ဝါက် မယာ ၑြုတာ၊
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachinayi, ndinamva chamoyo chachinayi chija chikunena kuti, “Bwera!”
8 တတး ပါဏ္ဍုရဝရ္ဏ ဧကော 'ၑွော မယာ ဒၖၐ္ဋး, တဒါရောဟိဏော နာမ မၖတျုရိတိ ပရလောကၑ္စ တမ် အနုစရတိ ခင်္ဂေန ဒုရ္ဘိက္ၐေဏ မဟာမာရျျာ ဝနျပၑုဘိၑ္စ လောကာနာံ ဗဓာယ ပၖထိဝျာၑ္စတုရ္ထာံၑသျာဓိပတျံ တသ္မာ အဒါယိ၊ (Hadēs g86)
Nditayangʼana patsogolo panga ndinaona kavalo wotuwa! Wokwerapo wake dzina lake linali Imfa ndipo Hade inali kumutsatira pambuyo pake. Anapatsidwa ulamuliro pa gawo limodzi la magawo anayi a dziko lapansi kuti aphe ndi lupanga, njala, mliri, ndi zirombo zakuthengo za mʼdziko lapansi. (Hadēs g86)
9 အနန္တရံ ပဉ္စမမုဒြာယာံ တေန မောစိတာယာမ် ဤၑွရဝါကျဟေတောသ္တတြ သာက္ၐျဒါနာစ္စ ဆေဒိတာနာံ လောကာနာံ ဒေဟိနော ဝေဒျာ အဓော မယာဒၖၑျန္တ၊
Mwana Wankhosa atatsekula chomatira chachisanu, ndinaona kunsi kwa guwa lansembe kunali mizimu ya anthu amene anaphedwa chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi chifukwa chochitira umboni.
10 တ ဥစ္စဲရိဒံ ဂဒန္တိ, ဟေ ပဝိတြ သတျမယ ပြဘော အသ္မာကံ ရက္တပါတေ ပၖထိဝီနိဝါသိဘိ ရွိဝဒိတုံ တသျ ဖလ ဒါတုဉ္စ ကတိ ကာလံ ဝိလမ္ဗသေ?
Iwo anafuwula kuti, “Mudzawaleka mpaka liti, Inu Ambuye wamkulu, woyera ndi woona, osawaweruza anthu okhala mʼdziko lapansi ndi kulipsira magazi athu?”
11 တတသ္တေၐာမ် ဧကဲကသ္မဲ ၑုဘြး ပရိစ္ဆဒေါ 'ဒါယိ ဝါဂိယဉ္စာကထျတ ယူယမလ္ပကာလမ် အရ္ထတော ယုၐ္မာကံ ယေ သဟာဒါသာ ဘြာတရော ယူယမိဝ ဃာနိၐျန္တေ တေၐာံ သံချာ ယာဝတ် သမ္ပူရ္ဏတာံ န ဂစ္ဆတိ တာဝဒ် ဝိရမတ၊
Pamenepo aliyense wa anthuwo anapatsidwa mwinjiro woyera ndipo anawuzidwa kuti adikire pangʼono kufikira chiwerengero cha anzawo ndi abale awo amene anayeneranso kuphedwa ngati iwo, chitakwanira.
12 အနန္တရံ ယဒါ သ ၐၐ္ဌမုဒြာမမောစယတ် တဒါ မယိ နိရီက္ၐမာဏေ မဟာန် ဘူကမ္ပော 'ဘဝတ် သူရျျၑ္စ ဥၐ္ဋြလောမဇဝသ္တြဝတ် ကၖၐ္ဏဝရ္ဏၑ္စန္ဒြမာၑ္စ ရက္တသင်္ကာၑော 'ဘဝတ္
Ndinayangʼanitsitsa pamene ankatsekula chomatira chachisanu ndi chimodzi. Ndipo panachitika chivomerezi champhamvu. Dzuwa linada ngati chiguduli chopanga ndi bweya wambuzi wakuda. Mwezi wonse unafiira ngati magazi,
13 ဂဂနသ္ထတာရာၑ္စ ပြဗလဝါယုနာ စာလိတာဒ် ဥဍုမ္ဗရဝၖက္ၐာတ် နိပါတိတာနျပက္ကဖလာနီဝ ဘူတလေ နျပတန်၊
ndipo nyenyezi zakuthambo zinagwa pa dziko lapansi ngati muja zimagwera nkhuyu zotsalira mu mtengo mphepo yamphamvu ikawomba.
14 အာကာၑမဏ္ဍလဉ္စ သင်္ကုစျမာနဂြန္ထဣဝါန္တရ္ဓာနမ် အဂမတ် ဂိရယ ဥပဒွီပါၑ္စ သရွွေ သ္ထာနာန္တရံ စာလိတား
Thambo linachoka ngati amayalulira mphasa ndipo phiri lililonse ndi chilumba chilichonse zinachotsedwa pa malo pake.
15 ပၖထိဝီသ္ထာ ဘူပါလာ မဟာလ္လောကား သဟသ္တြပတယော ဓနိနး ပရာကြမိဏၑ္စ လောကာ ဒါသာ မုက္တာၑ္စ သရွွေ 'ပိ ဂုဟာသု ဂိရိသ္ထၑဲလေၐု စ သွာန် ပြာစ္ဆာဒယန်၊
Kenaka, mafumu a pa dziko lapansi, ana a mafumu, atsogoleri a ankhondo, olemera, amphamvu, kapolo aliyense, ndi mfulu aliyense anakabisala kumapanga ndi pakati pa matanthwe a ku mapiri.
16 တေ စ ဂိရီန် ၑဲလာံၑ္စ ဝဒန္တိ ယူယမ် အသ္မဒုပရိ ပတိတွာ သိံဟာသနောပဝိၐ္ဋဇနသျ ဒၖၐ္ဋိတော မေၐၑာဝကသျ ကောပါစ္စာသ္မာန် ဂေါပါယတ;
Iwo anafuwulira mapiri ndi matanthwe kuti, “Tigwereni ndi kutivundikira kuti asatione wokhala pa mpando waufumuyo ndi kupulumuka ku mkwiyo wa Mwana Wankhosa!
17 ယတသ္တသျ ကြောဓသျ မဟာဒိနမ် ဥပသ္ထိတံ ကး သ္ထာတုံ ၑက္နောတိ?
Pakuti tsiku lalikulu la mkwiyo wawo lafika ndipo ndi ndani angathe kulimbapo?”

< ပြကာၑိတံ 6 >