< မထိး 22 >

1 အနန္တရံ ယီၑုး ပုနရပိ ဒၖၐ္ဋာန္တေန တာန် အဝါဒီတ်,
Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
2 သွရ္ဂီယရာဇျမ် ဧတာဒၖၑသျ နၖပတေး သမံ, ယော နိဇ ပုတြံ ဝိဝါဟယန် သရွွာန် နိမန္တြိတာန် အာနေတုံ ဒါသေယာန် ပြဟိတဝါန်,
“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
3 ကိန္တု တေ သမာဂန္တုံ နေၐ္ဋဝန္တး၊
Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
4 တတော ရာဇာ ပုနရပိ ဒါသာနနျာန် ဣတျုက္တွာ ပြေၐယာမာသ, နိမန္တြိတာန် ဝဒတ, ပၑျတ, မမ ဘေဇျမာသာဒိတမာသ္တေ, နိဇဝ္ဋၐာဒိပုၐ္ဋဇန္တူန် မာရယိတွာ သရွွံ ခါဒျဒြဝျမာသာဒိတဝါန်, ယူယံ ဝိဝါဟမာဂစ္ဆတ၊
“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
5 တထပိ တေ တုစ္ဆီကၖတျ ကေစိတ် နိဇက္ၐေတြံ ကေစိဒ် ဝါဏိဇျံ ပြတိ သွသွမာရ္ဂေဏ စလိတဝန္တး၊
“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
6 အနျေ လောကာသ္တသျ ဒါသေယာန် ဓၖတွာ ဒေါ်ရာတ္မျံ ဝျဝဟၖတျ တာနဝဓိၐုး၊
Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
7 အနန္တရံ သ နၖပတိသ္တာံ ဝါရ္တ္တာံ ၑြုတွာ ကြုဓျန် သဲနျာနိ ပြဟိတျ တာန် ဃာတကာန် ဟတွာ တေၐာံ နဂရံ ဒါဟယာမာသ၊
Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
8 တတး သ နိဇဒါသေယာန် ဗဘာၐေ, ဝိဝါဟီယံ ဘောဇျမာသာဒိတမာသ္တေ, ကိန္တု နိမန္တြိတာ ဇနာ အယောဂျား၊
“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
9 တသ္မာဒ် ယူယံ ရာဇမာရ္ဂံ ဂတွာ ယာဝတော မနုဇာန် ပၑျတ, တာဝတဧဝ ဝိဝါဟီယဘောဇျာယ နိမန္တြယတ၊
Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
10 တဒါ တေ ဒါသေယာ ရာဇမာရ္ဂံ ဂတွာ ဘဒြာန် အဘဒြာန် ဝါ ယာဝတော ဇနာန် ဒဒၖၑုး, တာဝတဧဝ သံဂၖဟျာနယန်; တတော'ဘျာဂတမနုဇဲ ရွိဝါဟဂၖဟမ် အပူရျျတ၊
Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
11 တဒါနီံ သ ရာဇာ သရွွာနဘျာဂတာန် ဒြၐ္ဋုမ် အဘျန္တရမာဂတဝါန်; တဒါ တတြ ဝိဝါဟီယဝသနဟီနမေကံ ဇနံ ဝီက္ၐျ တံ ဇဂါဒ်,
“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
12 ဟေ မိတြ, တွံ ဝိဝါဟီယဝသနံ ဝိနာ ကထမတြ ပြဝိၐ္ဋဝါန်? တေန သ နိရုတ္တရော ဗဘူဝ၊
Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
13 တဒါ ရာဇာ နိဇာနုစရာန် အဝဒတ်, ဧတသျ ကရစရဏာန် ဗဒ္ဓါ ယတြ ရောဒနံ ဒန္တဲရ္ဒန္တဃရ္ၐဏဉ္စ ဘဝတိ, တတြ ဝဟိရ္ဘူတတမိသြေ တံ နိက္ၐိပတ၊
“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
14 ဣတ္ထံ ဗဟဝ အာဟူတာ အလ္ပေ မနောဘိမတား၊
“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
15 အနန္တရံ ဖိရူၑိနး ပြဂတျ ယထာ သံလာပေန တမ် ဥန္မာထေ ပါတယေယုသ္တထာ မန္တြယိတွာ
Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
16 ဟေရောဒီယမနုဇဲး သာကံ နိဇၑိၐျဂဏေန တံ ပြတိ ကထယာမာသုး, ဟေ ဂုရော, ဘဝါန် သတျး သတျမီၑွရီယမာရ္ဂမုပဒိၑတိ, ကမပိ မာနုၐံ နာနုရုဓျတေ, ကမပိ နာပေက္ၐတေ စ, တဒ် ဝယံ ဇာနီမး၊
Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
17 အတး ကဲသရဘူပါယ ကရော'သ္မာကံ ဒါတဝျော န ဝါ? အတြ ဘဝတာ ကိံ ဗုဓျတေ? တဒ် အသ္မာန် ဝဒတု၊
Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
18 တတော ယီၑုသ္တေၐာံ ခလတာံ ဝိဇ္ဉာယ ကထိတဝါန်, ရေ ကပဋိနး ယုယံ ကုတော မာံ ပရိက္ၐဓွေ?
Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
19 တတ္ကရဒါနသျ မုဒြာံ မာံ ဒရ္ၑယတ၊ တဒါနီံ တဲသ္တသျ သမီပံ မုဒြာစတုရ္ထဘာဂ အာနီတေ
Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
20 သ တာန် ပပြစ္ဆ, အတြ ကသျေယံ မူရ္တ္တိ ရ္နာမ စာသ္တေ? တေ ဇဂဒုး, ကဲသရဘူပသျ၊
ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
21 တတး သ ဥက္တဝါန, ကဲသရသျ ယတ် တတ် ကဲသရာယ ဒတ္တ, ဤၑွရသျ ယတ် တဒ် ဤၑွရာယ ဒတ္တ၊
Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.” Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”
22 ဣတိ ဝါကျံ နိၑမျ တေ ဝိသ္မယံ ဝိဇ္ဉာယ တံ ဝိဟာယ စလိတဝန္တး၊
Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
23 တသ္မိန္နဟနိ သိဒူကိနော'ရ္ထာတ် ၑ္မၑာနာတ် နောတ္ထာသျန္တီတိ ဝါကျံ ယေ ဝဒန္တိ, တေ ယီၑေရန္တိကမ် အာဂတျ ပပြစ္ဆုး,
Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
24 ဟေ ဂုရော, ကၑ္စိန္မနုဇၑ္စေတ် နိးသန္တာနး သန် ပြာဏာန် တျဇတိ, တရှိ တသျ ဘြာတာ တသျ ဇာယာံ ဝျုဟျ ဘြာတုး သန္တာနမ် ဥတ္ပာဒယိၐျတီတိ မူသာ အာဒိၐ္ဋဝါန်၊
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
25 ကိန္တွသ္မာကမတြ ကေ'ပိ ဇနား သပ္တသဟောဒရာ အာသန်, တေၐာံ ဇျေၐ္ဌ ဧကာံ ကနျာံ ဝျဝဟာတ်, အပရံ ပြာဏတျာဂကာလေ သွယံ နိးသန္တာနး သန် တာံ သ္တြိယံ သွဘြာတရိ သမရ္ပိတဝါန်,
Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
26 တတော ဒွိတီယာဒိသပ္တမာန္တာၑ္စ တထဲဝ စကြုး၊
Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
27 ၑေၐေ သာပီ နာရီ မမာရ၊
Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
28 မၖတာနာမ် ဥတ္ထာနသမယေ တေၐာံ သပ္တာနာံ မဓျေ သာ နာရီ ကသျ ဘာရျျာ ဘဝိၐျတိ? ယသ္မာတ် သရွွဧဝ တာံ ဝျဝဟန်၊
Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
29 တတော ယီၑုး ပြတျဝါဒီတ်, ယူယံ ဓရ္မ္မပုသ္တကမ် ဤၑွရီယာံ ၑက္တိဉ္စ န ဝိဇ္ဉာယ ဘြာန္တိမန္တး၊
Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
30 ဥတ္ထာနပြာပ္တာ လောကာ န ဝိဝဟန္တိ, န စ ဝါစာ ဒီယန္တေ, ကိန္တွီၑွရသျ သွရ္ဂသ္ထဒူတာနာံ သဒၖၑာ ဘဝန္တိ၊
Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
31 အပရံ မၖတာနာမုတ္ထာနမဓိ ယုၐ္မာန် ပြတီယမီၑွရောက္တိး,
Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
32 "အဟမိဗြာဟီမ ဤၑွရ ဣသှာက ဤၑွရော ယာကူဗ ဤၑွရ" ဣတိ ကိံ ယုၐ္မာဘိ ရ္နာပါဌိ? ကိန္တွီၑွရော ဇီဝတာမ် ဤၑွရ: , သ မၖတာနာမီၑွရော နဟိ၊
‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
33 ဣတိ ၑြုတွာ သရွွေ လောကာသ္တသျောပဒေၑာဒ် ဝိသ္မယံ ဂတား၊
Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
34 အနန္တရံ သိဒူကိနာမ် နိရုတ္တရတွဝါရ္တာံ နိၑမျ ဖိရူၑိန ဧကတြ မိလိတဝန္တး,
Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
35 တေၐာမေကော ဝျဝသ္ထာပကော ယီၑုံ ပရီက္ၐိတုံ ပပစ္ဆ,
Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
36 ဟေ ဂုရော ဝျဝသ္ထာၑာသ္တြမဓျေ ကာဇ္ဉာ ၑြေၐ္ဌာ?
“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
37 တတော ယီၑုရုဝါစ, တွံ သရွွာန္တးကရဏဲး သရွွပြာဏဲး သရွွစိတ္တဲၑ္စ သာကံ ပြဘော် ပရမေၑွရေ ပြီယသွ,
Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
38 ဧၐာ ပြထမမဟာဇ္ဉာ၊ တသျား သဒၖၑီ ဒွိတီယာဇ္ဉဲၐာ,
Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
39 တဝ သမီပဝါသိနိ သွာတ္မနီဝ ပြေမ ကုရု၊
Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
40 အနယော ရ္ဒွယောရာဇ္ဉယေား ကၖတ္သ္နဝျဝသ္ထာယာ ဘဝိၐျဒွက္တၖဂြန္ထသျ စ ဘာရသ္တိၐ္ဌတိ၊
Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
41 အနန္တရံ ဖိရူၑိနာမ် ဧကတြ သ္ထိတိကာလေ ယီၑုသ္တာန် ပပြစ္ဆ,
Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
42 ခြီၐ္ဋမဓိ ယုၐ္မာကံ ကီဒၖဂ္ဗောဓော ဇာယတေ? သ ကသျ သန္တာနး? တတသ္တေ ပြတျဝဒန်, ဒါယူဒး သန္တာနး၊
“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”
43 တဒါ သ ဥက္တဝါန်, တရှိ ဒါယူဒ် ကထမ် အာတ္မာဓိၐ္ဌာနေန တံ ပြဘုံ ဝဒတိ?
Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
44 ယထာ မမ ပြဘုမိဒံ ဝါကျမဝဒတ် ပရမေၑွရး၊ တဝါရီန် ပါဒပီဌံ တေ ယာဝန္နဟိ ကရောမျဟံ၊ တာဝတ် ကာလံ မဒီယေ တွံ ဒက္ၐပါရ္ၑွ ဥပါဝိၑ၊ အတော ယဒိ ဒါယူဒ် တံ ပြဘုံ ဝဒတိ, ရ္တိဟ သ ကထံ တသျ သန္တာနော ဘဝတိ?
“Ambuye anati kwa Ambuye wanga: ‘Khala pa dzanja langa lamanja mpaka ndiyike adani ako pansi pa mapazi ako.’
45 တဒါနီံ တေၐာံ ကောပိ တဒွါကျသျ ကိမပျုတ္တရံ ဒါတုံ နာၑက္နောတ်;
Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
46 တဒ္ဒိနမာရဘျ တံ ကိမပိ ဝါကျံ ပြၐ္ဋုံ ကသျာပိ သာဟသော နာဘဝတ်၊
Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.

< မထိး 22 >