< မထိး 21 >

1 အနန္တရံ တေၐု ယိရူၑာလမ္နဂရသျ သမီပဝေရ္တ္တိနော ဇဲတုနနာမကဓရာဓရသျ သမီပသ္ထ္တိံ ဗဲတ္ဖဂိဂြာမမ် အာဂတေၐု, ယီၑုး ၑိၐျဒွယံ ပြေၐယန် ဇဂါဒ,
Akuyandikira ku Yerusalemu anafika ku Betifage pa phiri la Olivi, Yesu anatumiza ophunzira awiri,
2 ယုဝါံ သမ္မုခသ္ထဂြာမံ ဂတွာ ဗဒ္ဓါံ ယာံ သဝတ္သာံ ဂရ္ဒ္ဒဘီံ ဟဌာတ် ပြာပ္သျထး, တာံ မောစယိတွာ မဒန္တိကမ် အာနယတံ၊
nawawuza kuti, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukakangolowa mʼmenemo mukapeza bulu womangidwa ali ndi mwana pa mbali pake. Mukawamasule ndipo mubwere nawo kwa Ine.
3 တတြ ယဒိ ကၑ္စိတ် ကိဉ္စိဒ် ဝက္ၐျတိ, တရှိ ဝဒိၐျထး, ဧတသျာံ ပြဘေား ပြယောဇနမာသ္တေ, တေန သ တတ္က္ၐဏာတ် ပြဟေၐျတိ၊
Wina akakayankhula, mukamuwuze kuti Ambuye akuwafuna, ndipo adzawatumiza nthawi yomweyo.”
4 သီယောနး ကနျကာံ ယူယံ ဘာၐဓွမိတိ ဘာရတီံ၊ ပၑျ တေ နမြၑီလး သန် နၖပ အာရုဟျ ဂရ္ဒဘီံ၊ အရ္ထာဒါရုဟျ တဒွတ္သမာယာသျတိ တွဒန္တိကံ၊
Izi zinachitika kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri:
5 ဘဝိၐျဒွါဒိနောက္တံ ဝစနမိဒံ တဒါ သဖလမဘူတ်၊
“Uza mwana wamkazi wa Ziyoni, taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yofatsa ndi yokwera pa bulu, pa kamwana ka bulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.”
6 အနန္တရံ တော် ၑ္ၐျိ ယီၑော ရျထာနိဒေၑံ တံ ဂြာမံ ဂတွာ
Ophunzirawo anapita nachita monga Yesu anawalamulira.
7 ဂရ္ဒဘီံ တဒွတ္သဉ္စ သမာနီတဝန္တော်, ပၑ္စာတ် တဒုပရိ သွီယဝသနာနီ ပါတယိတွာ တမာရောဟယာမာသတုး၊
Anabweretsa bulu ndi mwana wake, nayala zovala zawo pa abuluwo, ndipo Yesu anakwerapo.
8 တတော ဗဟဝေါ လောကာ နိဇဝသနာနိ ပထိ ပြသာရယိတုမာရေဘိရေ, ကတိပယာ ဇနာၑ္စ ပါဒပပရ္ဏာဒိကံ ဆိတွာ ပထိ ဝိသ္တာရယာမာသုး၊
Gulu lalikulu la anthu linayala zovala zawo mu msewu pamene ena anadula nthambi zamitengo ndi kuziyala mu msewumo.
9 အဂြဂါမိနး ပၑ္စာဒ္ဂါမိနၑ္စ မနုဇာ ဥစ္စဲရ္ဇယ ဇယ ဒါယူဒး သန္တာနေတိ ဇဂဒုး ပရမေၑွရသျ နာမ္နာ ယ အာယာတိ သ ဓနျး, သရွွောပရိသ္ထသွရ္ဂေပိ ဇယတိ၊
Magulu amene anali patsogolo pake ndi amene amamutsatira anafuwula kuti, “Hosana Mwana wa Davide!” “Wodala Iye amene abwera mʼdzina la Ambuye!” “Hosana mmwambamwamba!”
10 ဣတ္ထံ တသ္မိန် ယိရူၑာလမံ ပြဝိၐ္ဋေ ကော'ယမိတိ ကထနာတ် ကၖတ္သ္နံ နဂရံ စဉ္စလမဘဝတ်၊
Yesu atalowa mu Yerusalemu, mzinda wonse unatekeseka ndipo anthu anafunsa kuti, “Ndani ameneyu?”
11 တတြ လောကေား ကထယာမာသုး, ဧၐ ဂါလီလ္ပြဒေၑီယ-နာသရတီယ-ဘဝိၐျဒွါဒီ ယီၑုး၊
Magulu a anthu anayankha kuti, “Uyu ndi Yesu, mneneri wochokera ku Nazareti.”
12 အနန္တရံ ယီၑုရီၑွရသျ မန္ဒိရံ ပြဝိၑျ တန္မဓျာတ် ကြယဝိကြယိဏော ဝဟိၑ္စကာရ; ဝဏိဇာံ မုဒြာသနာနီ ကပေါတဝိကြယိဏာဉ္စသနာနီ စ နျုဝ္ဇယာမာသ၊
Yesu analowa mʼdera lina la Nyumba ya Mulungu ndipo anatulutsa kunja anthu onse amene ankachita malonda. Anagubuduza matebulo a osinthira ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda.
13 အပရံ တာနုဝါစ, ဧၐာ လိပိရာသ္တေ, "မမ ဂၖဟံ ပြာရ္ထနာဂၖဟမိတိ ဝိချာသျတိ", ကိန္တု ယူယံ တဒ် ဒသျူနာံ ဂဟွရံ ကၖတဝန္တး၊
Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero koma inu mwayisandutsa phanga la anthu achifwamba.”
14 တဒနန္တရမ် အန္ဓခဉ္စလောကာသ္တသျ သမီပမာဂတား, သ တာန် နိရာမယာန် ကၖတဝါန်၊
Anthu osaona ndi olumala anabwera kwa Iye mʼNyumba ya Mulungu ndipo anawachiritsa.
15 ယဒါ ပြဓာနယာဇကာ အဓျာပကာၑ္စ တေန ကၖတာနျေတာနိ စိတြကရ္မ္မာဏိ ဒဒၖၑုး, ဇယ ဇယ ဒါယူဒး သန္တာန, မန္ဒိရေ ဗာလကာနာမ် ဧတာဒၖၑမ် ဥစ္စဓွနိံ ၑုၑြုဝုၑ္စ, တဒါ မဟာကြုဒ္ဓါ ဗဘူဝး,
Koma akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ataona zodabwitsa zimene anachita, komanso ana akufuwula mʼNyumbayo kuti, “Hosana kwa Mwana wa Davide,” anapsa mtima.
16 တံ ပပြစ္ဆုၑ္စ, ဣမေ ယဒ် ဝဒန္တိ, တတ် ကိံ တွံ ၑၖဏောၐိ? တတော ယီၑုသ္တာန် အဝေါစတ်, သတျမ်; သ္တနျပါယိၑိၑူနာဉ္စ ဗာလကာနာဉ္စ ဝက္တြတး၊ သွကီယံ မဟိမာနံ တွံ သံပြကာၑယသိ သွယံ၊ ဧတဒွါကျံ ယူယံ ကိံ နာပဌတ?
Anamufunsa kuti, “Kodi mukumva zimene anawa akunena?” Yesu anayankha nati, “Inde. Kodi simunawerenge kuti, “Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda mwatuluka mayamiko?”
17 တတသ္တာန် ဝိဟာယ သ နဂရာဒ် ဗဲထနိယာဂြာမံ ဂတွာ တတြ ရဇနီံ ယာပယာမာသ၊
Ndipo anawasiya natuluka mu mzindawo ndi kupita ku Betaniya, kumene anakagona.
18 အနန္တရံ ပြဘာတေ သတိ ယီၑုး ပုနရပိ နဂရမာဂစ္ဆန် က္ၐုဓာရ္တ္တော ဗဘူဝ၊
Mmamawa, pamene amabwera ku mzinda, anamva njala.
19 တတော မာရ္ဂပါရ္ၑွ ဥဍုမ္ဗရဝၖက္ၐမေကံ ဝိလောကျ တတ္သမီပံ ဂတွာ ပတြာဏိ ဝိနာ ကိမပိ န ပြာပျ တံ ပါဒပံ ပြောဝါစ, အဒျာရဘျ ကဒါပိ တွယိ ဖလံ န ဘဝတု; တေန တတ္က္ၐဏာတ် သ ဥဍုမ္ဗရမာဟီရုဟး ၑုၐ္ကတာံ ဂတး၊ (aiōn g165)
Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota. (aiōn g165)
20 တဒ် ဒၖၐ္ဋွာ ၑိၐျာ အာၑ္စရျျံ ဝိဇ္ဉာယ ကထယာမာသုး, အား, ဥဍုမွရပါဒပေါ'တိတူရ္ဏံ ၑုၐ္ကော'ဘဝတ်၊
Ophunzira ataona zimenezi, anadabwa nafunsa kuti, “Kodi mtengo wamkuyuwu wauma msanga bwanji?”
21 တတော ယီၑုသ္တာနုဝါစ, ယုၐ္မာနဟံ သတျံ ဝဒါမိ, ယဒိ ယူယမသန္ဒိဂ္ဓား ပြတီထ, တရှိ ယူယမပိ ကေဝလောဍုမွရပါဒပံ ပြတီတ္ထံ ကရ္တ္တုံ ၑက္ၐျထ, တန္န, တွံ စလိတွာ သာဂရေ ပတေတိ ဝါကျံ ယုၐ္မာဘိရသ္မိန ၑဲလေ ပြောက္တေပိ တဒဲဝ တဒ် ဃဋိၐျတေ၊
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro ndipo simukayika, simudzangochita zokha zachitika kwa mkuyuzi, koma mudzatha kuwuza phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye wekha mʼnyanja,’ ndipo zidzachitikadi.
22 တထာ ဝိၑွသျ ပြာရ္ထျ ယုၐ္မာဘိ ရျဒ် ယာစိၐျတေ, တဒေဝ ပြာပ္သျတေ၊
Ngati mukhulupirira, mudzalandira chilichonse chimene muchipempha mʼpemphero.”
23 အနန္တရံ မန္ဒိရံ ပြဝိၑျောပဒေၑနသမယေ တတ္သမီပံ ပြဓာနယာဇကား ပြာစီနလောကာၑ္စာဂတျ ပပြစ္ဆုး, တွယာ ကေန သာမရ္ထျနဲတာနိ ကရ္မ္မာဏိ ကြိယန္တေ? ကေန ဝါ တုဘျမေတာနိ သာမရ္ထျာနိ ဒတ္တာနိ?
Yesu analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo pamene ankaphunzitsa, akulu a ansembe ndi akuluakulu anabwera kwa Iye namufunsa kuti, “Muchita izi ndi ulamuliro wanji ndipo anakupatsani ndani ulamuliro umenewu?”
24 တတော ယီၑုး ပြတျဝဒတ်, အဟမပိ ယုၐ္မာန် ဝါစမေကာံ ပၖစ္ဆာမိ, ယဒိ ယူယံ တဒုတ္တရံ ဒါတုံ ၑက္ၐျထ, တဒါ ကေန သာမရ္ထျေန ကရ္မ္မာဏျေတာနိ ကရောမိ, တဒဟံ ယုၐ္မာန် ဝက္ၐျာမိ၊
Yesu anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani funso limodzi, mukandiyankha, Inenso ndikukuwuzani ndi ulamuliro wa yani umene ndikuchitira izi.
25 ယောဟနော မဇ္ဇနံ ကသျာဇ္ဉယာဘဝတ်? ကိမီၑွရသျ မနုၐျသျ ဝါ? တတသ္တေ ပရသ္ပရံ ဝိဝိစျ ကထယာမာသုး, ယဒီၑွရသျေတိ ဝဒါမသ္တရှိ ယူယံ တံ ကုတော န ပြတျဲတ? ဝါစမေတာံ ဝက္ၐျတိ၊
Ubatizo wa Yohane unachokera kuti? Kumwamba kapena kwa anthu?” Anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Kuchokera kumwamba,’ Iye adzafunsa kuti, ‘Bwanji simunakhulupirire?’
26 မနုၐျသျေတိ ဝက္တုမပိ လောကေဘျော ဗိဘီမး, ယတး သရွွဲရပိ ယောဟန် ဘဝိၐျဒွါဒီတိ ဇ္ဉာယတေ၊
Koma tikati, ‘Kuchokera kwa anthu,’ ife tikuopa anthuwa, pakuti onse amakhulupirira kuti Yohane anali mneneri.”
27 တသ္မာတ် တေ ယီၑုံ ပြတျဝဒန်, တဒ် ဝယံ န ဝိဒ္မး၊ တဒါ သ တာနုက္တဝါန်, တရှိ ကေန သာမရထျေန ကရ္မ္မာဏျေတာနျဟံ ကရောမိ, တဒပျဟံ ယုၐ္မာန် န ဝက္ၐျာမိ၊
Choncho anamuwuza Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Pamenepo Iye anati, “Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wa yani umene ndichitira izi.”
28 ကသျစိဇ္ဇနသျ ဒွေါ် သုတာဝါသ္တာံ သ ဧကသျ သုတသျ သမီပံ ဂတွာ ဇဂါဒ, ဟေ သုတ, တွမဒျ မမ ဒြာက္ၐာက္ၐေတြေ ကရ္မ္မ ကရ္တုံ ဝြဇ၊
“Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’
29 တတး သ ဥက္တဝါန်, န ယာသျာမိ, ကိန္တု ၑေၐေ'နုတပျ ဇဂါမ၊
“Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.
30 အနန္တရံ သောနျသုတသျ သမီပံ ဂတွာ တထဲဝ ကထ္တိဝါန်; တတး သ ပြတျုဝါစ, မဟေစ္ဆ ယာမိ, ကိန္တု န ဂတး၊
“Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.
31 ဧတယေား ပုတြယော ရ္မဓျေ ပိတုရဘိမတံ ကေန ပါလိတံ? ယုၐ္မာဘိး ကိံ ဗုဓျတေ? တတသ္တေ ပြတျူစုး, ပြထမေန ပုတြေဏ၊ တဒါနီံ ယီၑုသ္တာနုဝါစ, အဟံ ယုၐ္မာန် တထျံ ဝဒါမိ, စဏ္ဍာလာ ဂဏိကာၑ္စ ယုၐ္မာကမဂြတ ဤၑွရသျ ရာဇျံ ပြဝိၑန္တိ၊
“Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?” Anamuyankha nati, “Woyambayo.” Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.”
32 ယတော ယုၐ္မာကံ သမီပံ ယောဟနိ ဓရ္မ္မပထေနာဂတေ ယူယံ တံ န ပြတီထ, ကိန္တု စဏ္ဍာလာ ဂဏိကာၑ္စ တံ ပြတျာယန်, တဒ် ဝိလောကျာပိ ယူယံ ပြတျေတုံ နာခိဒျဓွံ၊
Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.
33 အပရမေကံ ဒၖၐ္ဋာန္တံ ၑၖဏုတ, ကၑ္စိဒ် ဂၖဟသ္ထး က္ၐေတြေ ဒြာက္ၐာလတာ ရောပယိတွာ တစ္စတုရ္ဒိက္ၐု ဝါရဏီံ ဝိဓာယ တန္မဓျေ ဒြာက္ၐာယန္တြံ သ္ထာပိတဝါန်, မာဉ္စဉ္စ နိရ္မ္မိတဝါန်, တတး ကၖၐကေၐု တတ် က္ၐေတြံ သမရ္ပျ သွယံ ဒူရဒေၑံ ဇဂါမ၊
“Tamverani fanizo lina: Panali mwini munda amene anadzala mphesa. Anamanga mpanda kuzungulira mundawo, nakumba moponderamo mphesa ndipo anamanga nsanja. Kenaka anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita pa ulendo.
34 တဒနန္တရံ ဖလသမယ ဥပသ္ထိတေ သ ဖလာနိ ပြာပ္တုံ ကၖၐီဝလာနာံ သမီပံ နိဇဒါသာန် ပြေၐယာမာသ၊
Pamene nthawi yokolola inakwana, anatumiza antchito ake kwa matenanti aja kuti akatenge zipatso zake.
35 ကိန္တု ကၖၐီဝလာသ္တသျ တာန် ဒါသေယာန် ဓၖတွာ ကဉ္စန ပြဟၖတဝန္တး, ကဉ္စန ပါၐာဏဲရာဟတဝန္တး, ကဉ္စန စ ဟတဝန္တး၊
“Alimi aja anagwira antchito ake; namenya mmodzi, napha wina, ndi kumuponya miyala wachitatuyo.
36 ပုနရပိ သ ပြဘုး ပြထမတော'ဓိကဒါသေယာန် ပြေၐယာမာသ, ကိန္တု တေ တာန် ပြတျပိ တထဲဝ စကြုး၊
Kenaka anatumiza antchito ena oposa oyambawo ndipo matenantiwo anawachitira chimodzimodzi.
37 အနန္တရံ မမ သုတေ ဂတေ တံ သမာဒရိၐျန္တေ, ဣတျုက္တွာ ၑေၐေ သ နိဇသုတံ တေၐာံ သန္နိဓိံ ပြေၐယာမာသ၊
Pomalizira anatumiza mwana wake. Anati adzamuchitira ulemu mwana wanga.
38 ကိန္တု တေ ကၖၐီဝလား သုတံ ဝီက္ၐျ ပရသ္ပရမ် ဣတိ မန္တြယိတုမ် အာရေဘိရေ, အယမုတ္တရာဓိကာရီ ဝယမေနံ နိဟတျာသျာဓိကာရံ သွဝၑီကရိၐျာမး၊
“Koma alimiwo ataona mwanayo anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndiye olowa mʼmalo mwa abambo ake. Tiyeni timuphe ndipo titenge cholowa chake.’
39 ပၑ္စာတ် တေ တံ ဓၖတွာ ဒြာက္ၐာက္ၐေတြာဒ် ဗဟိး ပါတယိတွာဗဓိၐုး၊
Pamenepo anamutenga namuponyera kunja kwa munda wamphesa namupha.
40 ယဒါ သ ဒြာက္ၐာက္ၐေတြပတိရာဂမိၐျတိ, တဒါ တာန် ကၖၐီဝလာန် ကိံ ကရိၐျတိ?
“Tsono akabwera mwini munda wamphesa adzachita nawo chiyani matenantiwo?”
41 တတသ္တေ ပြတျဝဒန်, တာန် ကလုၐိဏော ဒါရုဏယာတနာဘိရာဟနိၐျတိ, ယေ စ သမယာနုကြမာတ် ဖလာနိ ဒါသျန္တိ, တာဒၖၑေၐု ကၖၐီဝလေၐု က္ၐေတြံ သမရ္ပယိၐျတိ၊
Iwo anayankha kuti, “Adzawapha moyipa alimi oyipawo ndipo adzabwereketsa mundawo kwa alimi ena amene adzamupatsa gawo lake la mbewu pa nthawi yokolola.”
42 တဒါ ယီၑုနာ တေ ဂဒိတား, ဂြဟဏံ န ကၖတံ ယသျ ပါၐာဏသျ နိစာယကဲး၊ ပြဓာနပြသ္တရး ကောဏေ သဧဝ သံဘဝိၐျတိ၊ ဧတတ် ပရေၑိတုး ကရ္မ္မာသ္မဒၖၐ္ဋာဝဒ္ဘုတံ ဘဝေတ်၊ ဓရ္မ္မဂြန္ထေ လိခိတမေတဒွစနံ ယုၐ္မာဘိး ကိံ နာပါဌိ?
Yesu anawawuza kuti, “Kodi simunawerenge mʼmalemba kuti: “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana, womwewo wasanduka mwala wofunika kwambiri wa pa ngodya. Ambuye wachita izi, ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu.’
43 တသ္မာဒဟံ ယုၐ္မာန် ဝဒါမိ, ယုၐ္မတ္တ ဤၑွရီယရာဇျမပနီယ ဖလောတ္ပာဒယိတြနျဇာတယေ ဒါယိၐျတေ၊
“Nʼchifukwa chake ndi kukuwuzani kuti ufumu wa Mulungu udzalandidwa kwa inu ndipo udzapatsidwa kwa anthu amene adzabereka chipatso chake.
44 ယော ဇန ဧတတ္ပာၐာဏောပရိ ပတိၐျတိ, တံ သ ဘံက္ၐျတေ, ကိန္တွယံ ပါၐာဏော ယသျောပရိ ပတိၐျတိ, တံ သ ဓူလိဝတ် စူရ္ဏီကရိၐျတိ၊
Amene agwa pa mwalawu adzadukaduka, ndipo amene udzamugwere udzamuthudzula.”
45 တဒါနီံ ပြာဓနယာဇကား ဖိရူၑိနၑ္စ တသျေမာံ ဒၖၐ္ဋာန္တကထာံ ၑြုတွာ သော'သ္မာနုဒ္ဒိၑျ ကထိတဝါန်, ဣတိ ဝိဇ္ဉာယ တံ ဓရ္တ္တုံ စေၐ္ဋိတဝန္တး;
Akulu a ansembe ndi Afarisi atamva mafanizo a Yesu, anadziwa kuti ankanena iwo.
46 ကိန္တု လောကေဘျော ဗိဘျုး, ယတော လောကဲး သ ဘဝိၐျဒွါဒီတျဇ္ဉာယိ၊
Pamenepo anafuna njira yoti amugwirire, koma anaopa gulu la anthu chifukwa anthu onse ankakhulupirira kuti Iye anali mneneri.

< မထိး 21 >