< မာရ္ကး 6 >

1 အနန္တရံ သ တတ္သ္ထာနာတ် ပြသ္ထာယ သွပြဒေၑမာဂတး ၑိၐျာၑ္စ တတ္ပၑ္စာဒ် ဂတား၊
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 အထ ဝိၑြာမဝါရေ သတိ သ ဘဇနဂၖဟေ ဥပဒေၐ္ဋုမာရဗ္ဓဝါန် တတော'နေကေ လောကာသ္တတ္ကထာံ ၑြုတွာ ဝိသ္မိတျ ဇဂဒုး, အသျ မနုဇသျ ဤဒၖၑီ အာၑ္စရျျကြိယာ ကသ္မာဇ် ဇာတာ? တထာ သွကရာဘျာမ် ဣတ္ထမဒ္ဘုတံ ကရ္မ္မ ကရ္တ္တာမ် ဧတသ္မဲ ကထံ ဇ္ဉာနံ ဒတ္တမ်?
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 ကိမယံ မရိယမး ပုတြသ္တဇ္ဉာ နော? ကိမယံ ယာကူဗ်-ယောသိ-ယိဟုဒါ-ၑိမောနာံ ဘြာတာ နော? အသျ ဘဂိနျး ကိမိဟာသ္မာဘိး သဟ နော? ဣတ္ထံ တေ တဒရ္ထေ ပြတျူဟံ ဂတား၊
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 တဒါ ယီၑုသ္တေဘျော'ကထယတ် သွဒေၑံ သွကုဋုမ္ဗာန် သွပရိဇနာံၑ္စ ဝိနာ ကုတြာပိ ဘဝိၐျဒွါဒီ အသတ္ကၖတော န ဘဝတိ၊
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 အပရဉ္စ တေၐာမပြတျယာတ် သ ဝိသ္မိတး ကိယတာံ ရောဂိဏာံ ဝပုးၐု ဟသ္တမ် အရ္ပယိတွာ ကေဝလံ တေၐာမာရောဂျကရဏာဒ် အနျတ် ကိမပိ စိတြကာရျျံ ကရ္တ္တာံ န ၑက္တး၊
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 အထ သ စတုရ္ဒိက္သ္ထ ဂြာမာန် ဘြမိတွာ ဥပဒိၐ္ဋဝါန္
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 ဒွါဒၑၑိၐျာန် အာဟူယ အမေဓျဘူတာန် ဝၑီကရ္တ္တာံ ၑက္တိံ ဒတ္တွာ တေၐာံ ဒွေါ် ဒွေါ် ဇနော ပြေၐိတဝါန်၊
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 ပုနရိတျာဒိၑဒ် ယူယမ် ဧကဲကာံ ယၐ္ဋိံ ဝိနာ ဝသ္တြသံပုဋး ပူပး ကဋိဗန္ဓေ တာမြခဏ္ဍဉ္စ ဧၐာံ ကိမပိ မာ ဂြဟ္လီတ,
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 မာရ္ဂယာတြာယဲ ပါဒေၐူပါနဟော် ဒတ္တွာ ဒွေ ဥတ္တရီယေ မာ ပရိဓဒွွံ၊
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 အပရမပျုက္တံ တေန ယူယံ ယသျာံ ပုရျျာံ ယသျ နိဝေၑနံ ပြဝေက္ၐျထ တာံ ပုရီံ ယာဝန္န တျက္ၐျထ တာဝတ် တန္နိဝေၑနေ သ္ထာသျထ၊
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 တတြ ယဒိ ကေပိ ယုၐ္မာကမာတိထျံ န ဝိဒဓတိ ယုၐ္မာကံ ကထာၑ္စ န ၑၖဏွန္တိ တရှိ တတ္သ္ထာနာတ် ပြသ္ထာနသမယေ တေၐာံ ဝိရုဒ္ဓံ သာက္ၐျံ ဒါတုံ သွပါဒါနာသ္ဖာလျ ရဇး သမ္ပာတယတ; အဟံ ယုၐ္မာန် ယထာရ္ထံ ဝစ္မိ ဝိစာရဒိနေ တန္နဂရသျာဝသ္ထာတး သိဒေါမာမောရယော ရ္နဂရယောရဝသ္ထာ သဟျတရာ ဘဝိၐျတိ၊
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 အထ တေ ဂတွာ လောကာနာံ မနးပရာဝရ္တ္တနီး ကထာ ပြစာရိတဝန္တး၊
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 ဧဝမနေကာန် ဘူတာံၑ္စ တျာဇိတဝန္တသ္တထာ တဲလေန မရ္ဒ္ဒယိတွာ ဗဟူန် ဇနာနရောဂါနကာရ္ၐုး၊
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 ဣတ္ထံ တသျ သုချာတိၑ္စတုရ္ဒိၑော ဝျာပ္တာ တဒါ ဟေရောဒ် ရာဇာ တန္နိၑမျ ကထိတဝါန်, ယောဟန် မဇ္ဇကး ၑ္မၑာနာဒ် ဥတ္ထိတ အတောဟေတောသ္တေန သရွွာ ဧတာ အဒ္ဘုတကြိယား ပြကာၑန္တေ၊
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 အနျေ'ကထယန် အယမ် ဧလိယး, ကေပိ ကထိတဝန္တ ဧၐ ဘဝိၐျဒွါဒီ ယဒွါ ဘဝိၐျဒွါဒိနာံ သဒၖၑ ဧကောယမ်၊
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 ကိန္တု ဟေရောဒ် ဣတျာကရ္ဏျ ဘာၐိတဝါန် ယသျာဟံ ၑိရၑ္ဆိန္နဝါန် သ ဧဝ ယောဟနယံ သ ၑ္မၑာနာဒုဒတိၐ္ဌတ်၊
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 ပူရွွံ သွဘြာတုး ဖိလိပသျ ပတ္နျာ ဥဒွါဟံ ကၖတဝန္တံ ဟေရောဒံ ယောဟနဝါဒီတ် သွဘာတၖဝဓူ ရ္န ဝိဝါဟျာ၊
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 အတး ကာရဏာတ် ဟေရောဒ် လောကံ ပြဟိတျ ယောဟနံ ဓၖတွာ ဗန္ဓနာလယေ ဗဒ္ဓဝါန်၊
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 ဟေရောဒိယာ တသ္မဲ ယောဟနေ ပြကုပျ တံ ဟန္တုမ် အဲစ္ဆတ် ကိန္တု န ၑက္တာ,
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 ယသ္မာဒ် ဟေရောဒ် တံ ဓာရ္မ္မိကံ သတ္ပုရုၐဉ္စ ဇ္ဉာတွာ သမ္မနျ ရက္ၐိတဝါန်; တတ္ကထာံ ၑြုတွာ တဒနုသာရေဏ ဗဟူနိ ကရ္မ္မာဏိ ကၖတဝါန် ဟၖၐ္ဋမနာသ္တဒုပဒေၑံ ၑြုတဝါံၑ္စ၊
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 ကိန္တု ဟေရောဒ် ယဒါ သွဇန္မဒိနေ ပြဓာနလောကေဘျး သေနာနီဘျၑ္စ ဂါလီလ္ပြဒေၑီယၑြေၐ္ဌလောကေဘျၑ္စ ရာတြော် ဘောဇျမေကံ ကၖတဝါန္
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 တသ္မိန် ၑုဘဒိနေ ဟေရောဒိယာယား ကနျာ သမေတျ တေၐာံ သမက္ၐံ သံနၖတျ ဟေရောဒသ္တေန သဟောပဝိၐ္ဋာနာဉ္စ တောၐမဇီဇနတ် တတာ နၖပး ကနျာမာဟ သ္မ မတ္တော ယဒ် ယာစသေ တဒေဝ တုဘျံ ဒါသျေ၊
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 ၑပထံ ကၖတွာကထယတ် စေဒ် ရာဇျာရ္ဒ္ဓမပိ ယာစသေ တဒပိ တုဘျံ ဒါသျေ၊
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 တတး သာ ဗဟိ ရ္ဂတွာ သွမာတရံ ပပြစ္ဆ ကိမဟံ ယာစိၐျေ? တဒါ သာကထယတ် ယောဟနော မဇ္ဇကသျ ၑိရး၊
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 အထ တူရ္ဏံ ဘူပသမီပမ် ဧတျ ယာစမာနာဝဒတ် က္ၐဏေသ္မိန် ယောဟနော မဇ္ဇကသျ ၑိရး ပါတြေ နိဓာယ ဒေဟိ, ဧတဒ် ယာစေ'ဟံ၊
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 တသ္မာတ် ဘူပေါ'တိဒုးခိတး, တထာပိ သွၑပထသျ သဟဘောဇိနာဉ္စာနုရောဓာတ် တဒနင်္ဂီကရ္တ္တုံ န ၑက္တး၊
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 တတ္က္ၐဏံ ရာဇာ ဃာတကံ ပြေၐျ တသျ ၑိရ အာနေတုမာဒိၐ္ဋဝါန်၊
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 တတး သ ကာရာဂါရံ ဂတွာ တစ္ဆိရၑ္ဆိတွာ ပါတြေ နိဓာယာနီယ တသျဲ ကနျာယဲ ဒတ္တဝါန် ကနျာ စ သွမာတြေ ဒဒေါ်၊
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 အနနတရံ ယောဟနး ၑိၐျာသ္တဒွါရ္တ္တာံ ပြာပျာဂတျ တသျ ကုဏပံ ၑ္မၑာနေ'သ္ထာပယန်၊
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 အထ ပြေၐိတာ ယီၑေား သန္နိဓော် မိလိတာ ယဒ် ယစ် စကြုး ၑိက္ၐယာမာသုၑ္စ တတ္သရွွဝါရ္တ္တာသ္တသ္မဲ ကထိတဝန္တး၊
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 သ တာနုဝါစ ယူယံ ဝိဇနသ္ထာနံ ဂတွာ ဝိၑြာမျတ ယတသ္တတ္သန္နိဓော် ဗဟုလောကာနာံ သမာဂမာတ် တေ ဘောက္တုံ နာဝကာၑံ ပြာပ္တား၊
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 တတသ္တေ နာဝါ ဝိဇနသ္ထာနံ ဂုပ္တံ ဂဂ္မုး၊
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 တတော လောကနိဝဟသ္တေၐာံ သ္ထာနာန္တရယာနံ ဒဒရ္ၑ, အနေကေ တံ ပရိစိတျ နာနာပုရေဘျး ပဒဲရွြဇိတွာ ဇဝေန တဲၐာမဂြေ ယီၑေား သမီပ ဥပတသ္ထုး၊
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 တဒါ ယီၑု ရ္နာဝေါ ဗဟိရ္ဂတျ လောကာရဏျာနီံ ဒၖၐ္ဋွာ တေၐု ကရုဏာံ ကၖတဝါန် ယတသ္တေ'ရက္ၐကမေၐာ ဣဝါသန် တဒါ သ တာန နာနာပြသင်္ဂါန် ဥပဒိၐ္ဋဝါန်၊
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 အထ ဒိဝါန္တေ သတိ ၑိၐျာ ဧတျ ယီၑုမူစိရေ, ဣဒံ ဝိဇနသ္ထာနံ ဒိနဉ္စာဝသန္နံ၊
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 လောကာနာံ ကိမပိ ခါဒျံ နာသ္တိ, အတၑ္စတုရ္ဒိက္ၐု ဂြာမာန် ဂန္တုံ ဘောဇျဒြဝျာဏိ ကြေတုဉ္စ ဘဝါန် တာန် ဝိသၖဇတု၊
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 တဒါ သ တာနုဝါစ ယူယမေဝ တာန် ဘောဇယတ; တတသ္တေ ဇဂဒု ရွယံ ဂတွာ ဒွိၑတသံချကဲ ရ္မုဒြာပါဒဲး ပူပါန် ကြီတွာ ကိံ တာန် ဘောဇယိၐျာမး?
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 တဒါ သ တာန် ပၖၐ္ဌဝါန် ယုၐ္မာကံ သန္နိဓော် ကတိ ပူပါ အာသတေ? ဂတွာ ပၑျတ; တတသ္တေ ဒၖၐ္ဋွာ တမဝဒန် ပဉ္စ ပူပါ ဒွေါ် မတ္သျော် စ သန္တိ၊
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 တဒါ သ လောကာန် ၑသ္ပောပရိ ပံက္တိဘိရုပဝေၑယိတုမ် အာဒိၐ္ဋဝါန်,
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 တတသ္တေ ၑတံ ၑတံ ဇနား ပဉ္စာၑတ် ပဉ္စာၑဇ္ဇနာၑ္စ ပံက္တိဘိ ရ္ဘုဝိ သမုပဝိဝိၑုး၊
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 အထ သ တာန် ပဉ္စပူပါန် မတ္သျဒွယဉ္စ ဓၖတွာ သွရ္ဂံ ပၑျန် ဤၑွရဂုဏာန် အနွကီရ္တ္တယတ် တာန် ပူပါန် ဘံက္တွာ လောကေဘျး ပရိဝေၐယိတုံ ၑိၐျေဘျော ဒတ္တဝါန် ဒွါ မတ္သျော် စ ဝိဘဇျ သရွွေဘျော ဒတ္တဝါန်၊
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 တတး သရွွေ ဘုက္တွာတၖပျန်၊
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 အနန္တရံ ၑိၐျာ အဝၑိၐ္ဋဲး ပူပဲ ရ္မတ္သျဲၑ္စ ပူရ္ဏာန် ဒွဒၑ ဍလ္လကာန် ဇဂၖဟုး၊
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 တေ ဘောက္တာရး ပြာယး ပဉ္စ သဟသြာဏိ ပုရုၐာ အာသန်၊
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 အထ သ လောကာန် ဝိသၖဇန္နေဝ နာဝမာရောဎုံ သွသ္မာဒဂြေ ပါရေ ဗဲတ္သဲဒါပုရံ ယာတုဉ္စ ၑ္ၐျိန် ဝါဎမာဒိၐ္ဋဝါန်၊
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 တဒါ သ သရွွာန် ဝိသၖဇျ ပြာရ္ထယိတုံ ပရွွတံ ဂတး၊
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 တတး သန္ဓျာယာံ သတျာံ နော်း သိန္ဓုမဓျ ဥပသ္ထိတာ ကိန္တု သ ဧကာကီ သ္ထလေ သ္ထိတး၊
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 အထ သမ္မုခဝါတဝဟနာတ် ၑိၐျာ နာဝံ ဝါဟယိတွာ ပရိၑြာန္တာ ဣတိ ဇ္ဉာတွာ သ နိၑာစတုရ္ထယာမေ သိန္ဓူပရိ ပဒ္ဘျာံ ဝြဇန် တေၐာံ သမီပမေတျ တေၐာမဂြေ ယာတုမ် ဥဒျတး၊
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 ကိန္တု ၑိၐျား သိန္ဓူပရိ တံ ဝြဇန္တံ ဒၖၐ္ဋွာ ဘူတမနုမာယ ရုရုဝုး,
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 ယတး သရွွေ တံ ဒၖၐ္ဋွာ ဝျာကုလိတား၊ အတဧဝ ယီၑုသ္တတ္က္ၐဏံ တဲး သဟာလပျ ကထိတဝါန်, သုသ္ထိရာ ဘူတ, အယမဟံ မာ ဘဲၐ္ဋ၊
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 အထ နော်ကာမာရုဟျ တသ္မိန် တေၐာံ သန္နိဓိံ ဂတေ ဝါတော နိဝၖတ္တး; တသ္မာတ္တေ မနးသု ဝိသ္မိတာ အာၑ္စရျျံ မေနိရေ၊
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 ယတသ္တေ မနသာံ ကာဌိနျာတ် တတ် ပူပီယမ် အာၑ္စရျျံ ကရ္မ္မ န ဝိဝိက္တဝန္တး၊
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 အထ တေ ပါရံ ဂတွာ ဂိနေၐရတ္ပြဒေၑမေတျ တဋ ဥပသ္ထိတား၊
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 တေၐု နော်ကာတော ဗဟိရ္ဂတေၐု တတ္ပြဒေၑီယာ လောကာသ္တံ ပရိစိတျ
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 စတုရ္ဒိက္ၐု ဓာဝန္တော ယတြ ယတြ ရောဂိဏော နရာ အာသန် တာန် သရွွာန ခဋွောပရိ နိဓာယ ယတြ ကုတြစိတ် တဒွါရ္တ္တာံ ပြာပုး တတ် သ္ထာနမ် အာနေတုမ် အာရေဘိရေ၊
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 တထာ ယတြ ယတြ ဂြာမေ ယတြ ယတြ ပုရေ ယတြ ယတြ ပလ္လျာဉ္စ တေန ပြဝေၑး ကၖတသ္တဒွရ္တ္မမဓျေ လောကား ပီဍိတာန် သ္ထာပယိတွာ တသျ စေလဂြန္ထိမာတြံ သ္ပြၐ္ဋုမ် တေၐာမရ္ထေ တဒနုဇ္ဉာံ ပြာရ္ထယန္တး ယာဝန္တော လောကား ပသ္ပၖၑုသ္တာဝန္တ ဧဝ ဂဒါန္မုက္တား၊
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

< မာရ္ကး 6 >