< မာရ္ကး 5 >

1 အထ တူ သိန္ဓုပါရံ ဂတွာ ဂိဒေရီယပြဒေၑ ဥပတသ္ထုး၊
Ndipo anawoloka nyanja napita ku dera la Gerasa.
2 နော်ကာတော နိရ္ဂတမာတြာဒ် အပဝိတြဘူတဂြသ္တ ဧကး ၑ္မၑာနာဒေတျ တံ သာက္ၐာစ် စကာရ၊
Yesu atatuluka mʼbwato, munthu amene anali ndi mzimu woyipa anachoka ku manda ndi kukumana naye.
3 သ ၑ္မၑာနေ'ဝါတ္သီတ် ကောပိ တံ ၑၖင်္ခလေန ဗဒွွာ သ္ထာပယိတုံ နာၑက္နောတ်၊
Munthuyu amakhala ku manda, ndipo panalibe amene akanatha kumumanganso ngakhale ndi unyolo.
4 ဇနဲရွာရံ နိဂဍဲး ၑၖင်္ခလဲၑ္စ သ ဗဒ္ဓေါပိ ၑၖင်္ခလာနျာကၖၐျ မောစိတဝါန် နိဂဍာနိ စ ဘံက္တွာ ခဏ္ဍံ ခဏ္ဍံ ကၖတဝါန် ကောပိ တံ ဝၑီကရ္တ္တုံ န ၑၑက၊
Pakuti nthawi zambiri akamumanga manja ndi miyendo amadula maunyolo ndi kudula zitsulo zimene zinali mʼmapazi ake. Panalibe amene anali ndi mphamvu yoti ndi kumugonjetsa.
5 ဒိဝါနိၑံ သဒါ ပရွွတံ ၑ္မၑာနဉ္စ ဘြမိတွာ စီတ္ၑဗ္ဒံ ကၖတဝါန် ဂြာဝဘိၑ္စ သွယံ သွံ ကၖတဝါန်၊
Usana ndi usiku ankakhala ku manda ndi kumapiri, akulira ndi kudzicheka ndi miyala.
6 သ ယီၑုံ ဒူရာတ် ပၑျန္နေဝ ဓာဝန် တံ ပြဏနာမ ဥစဲရုဝံၑ္စောဝါစ,
Ataona Yesu ali patali, anathamanga nagwa pa mawondo ake pamaso pake.
7 ဟေ သရွွောပရိသ္ထေၑွရပုတြ ယီၑော ဘဝတာ သဟ မေ ကး သမ္ဗန္ဓး? အဟံ တွာမီၑွရေဏ ၑာပယေ မာံ မာ ယာတယ၊
Iye anafuwula kwambiri nati, “Mukufuna muchite nane chiyani, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Lumbirani kwa Mulungu kuti simundizunza!”
8 ယတော ယီၑုသ္တံ ကထိတဝါန် ရေ အပဝိတြဘူတ, အသ္မာန္နရာဒ် ဗဟိရ္နိရ္ဂစ္ဆ၊
Pakuti Yesu anati kwa iye, “Tuluka mwa munthuyu, iwe mzimu woyipa!”
9 အထ သ တံ ပၖၐ္ဋဝါန် ကိန္တေ နာမ? တေန ပြတျုက္တံ ဝယမနေကေ 'သ္မသ္တတော'သ္မန္နာမ ဗာဟိနီ၊
Ndipo Yesu anamufunsa iye, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Dzina langa ndine Legiyo, pakuti tilipo ambiri.”
10 တတောသ္မာန် ဒေၑာန္န ပြေၐယေတိ တေ တံ ပြာရ္ထယန္တ၊
Ndipo anamupempha Yesu mobwerezabwereza kuti asazitulutse mʼderalo.
11 တဒါနီံ ပရွွတံ နိကၐာ ဗၖဟန် ဝရာဟဝြဇၑ္စရန္နာသီတ်၊
Gulu lalikulu la nkhumba limadya mʼmbali mwa phiri limene linali pafupi.
12 တသ္မာဒ် ဘူတာ ဝိနယေန ဇဂဒုး, အမုံ ဝရာဟဝြဇမ် အာၑြယိတုမ် အသ္မာန် ပြဟိဏု၊
Ziwandazo zinapempha Yesu kuti, “Titumizeni pakati pa nkhumbazo; ndipo mutilole tilowe mwa izo.”
13 ယီၑုနာနုဇ္ဉာတာသ္တေ'ပဝိတြဘူတာ ဗဟိရ္နိရျာယ ဝရာဟဝြဇံ ပြာဝိၑန် တတး သရွွေ ဝရာဟာ ဝသ္တုတသ္တု ပြာယောဒွိသဟသြသံင်္ချကား ကဋကေန မဟာဇဝါဒ် ဓာဝန္တး သိန္ဓော် ပြာဏာန် ဇဟုး၊
Iye anazipatsa chilolezo, ndipo mizimu yoyipayo inatuluka ndi kukalowa mu nkhumbazo. Gulu la nkhumba, zokwana pafupifupi 2,000 zinathamanga kutsetserekera ku nyanja ndipo zinamira.
14 တသ္မာဒ် ဝရာဟပါလကား ပလာယမာနား ပုရေ ဂြာမေ စ တဒွါရ္တ္တံ ကထယာဉ္စကြုး၊ တဒါ လောကာ ဃဋိတံ တတ္ကာရျျံ ဒြၐ္ဋုံ ဗဟိရ္ဇဂ္မုး
Omwe amaweta nkhumbazo anathawa ndi kukawuza anthu za izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi, ndipo anthu anapita kukaona zomwe zinachitika.
15 ယီၑေား သန္နိဓိံ ဂတွာ တံ ဘူတဂြသ္တမ် အရ္ထာဒ် ဗာဟိနီဘူတဂြသ္တံ နရံ သဝသ္တြံ သစေတနံ သမုပဝိၐ္ဋဉ္စ ဒၖၐ္ဋွာ ဗိဘျုး၊
Atafika kwa Yesu, anaona munthu amene anagwidwa ndi ziwanda zambiri uja atakhala pansi pomwepo, atavala, ndipo ali bwinobwino. Iwo anachita mantha.
16 တတော ဒၖၐ္ဋတတ္ကာရျျလောကာသ္တသျ ဘူတဂြသ္တနရသျ ဝရာဟဝြဇသျာပိ တာံ ဓဋနာံ ဝရ္ဏယာမာသုး၊
Amene anaona zimenezi anawuza anthu zomwe zinachitika kwa munthu wogwidwa ndi ziwandayo ndipo anawawuzanso za nkhumbazo.
17 တတသ္တေ သွသီမာတော ဗဟိရ္ဂန္တုံ ယီၑုံ ဝိနေတုမာရေဘိရေ၊
Ndipo anthu anayamba kumupempha Yesu kuti achoke mʼdera lawo.
18 အထ တသျ နော်ကာရောဟဏကာလေ သ ဘူတမုက္တော နာ ယီၑုနာ သဟ သ္ထာတုံ ပြာရ္ထယတေ;
Yesu akulowa mʼbwato, munthu amene anagwidwa ndi ziwanda uja anamupempha kuti apite nawo.
19 ကိန္တု သ တမနနုမတျ ကထိတဝါန် တွံ နိဇာတ္မီယာနာံ သမီပံ ဂၖဟဉ္စ ဂစ္ဆ ပြဘုသ္တွယိ ကၖပါံ ကၖတွာ ယာနိ ကရ္မ္မာဏိ ကၖတဝါန် တာနိ တာန် ဇ္ဉာပယ၊
Yesu sanamulole, koma anati, “Pita kwanu ku banja lako ndipo ukawawuze zimene Ambuye wakuchitira, ndi chifundo chimene wakuchitira.”
20 အတး သ ပြသ္ထာယ ယီၑုနာ ကၖတံ တတ္သရွွာၑ္စရျျံ ကရ္မ္မ ဒိကာပလိဒေၑေ ပြစာရယိတုံ ပြာရဗ္ဓဝါန် တတး သရွွေ လောကာ အာၑ္စရျျံ မေနိရေ၊
Pomwepo munthuyo anapita nayamba kuwuza anthu a ku Dekapoli zinthu zimene Yesu anamuchitira. Ndipo anthu onse anadabwa.
21 အနန္တရံ ယီၑော် နာဝါ ပုနရနျပါရ ဥတ္တီရ္ဏေ သိန္ဓုတဋေ စ တိၐ္ဌတိ သတိ တတ္သမီပေ ဗဟုလောကာနာံ သမာဂမော'ဘူတ်၊
Yesu atawolokeranso pa bwato kupita mbali ina ya nyanja, gulu lalikulu la anthu linasonkhana momuzungulira. Ali mʼmbali mwa nyanja,
22 အပရံ ယာယီရ် နာမ္နာ ကၑ္စိဒ် ဘဇနဂၖဟသျာဓိပ အာဂတျ တံ ဒၖၐ္ဋွဲဝ စရဏယေား ပတိတွာ ဗဟု နိဝေဒျ ကထိတဝါန်;
mmodzi wa akulu a mʼsunagoge, dzina lake Yairo anafika pamenepo. Ataona Yesu, anagwa pa mapazi ake,
23 မမ ကနျာ မၖတပြာယာဘူဒ် အတော ဘဝါနေတျ တဒါရောဂျာယ တသျာ ဂါတြေ ဟသ္တမ် အရ္ပယတု တေနဲဝ သာ ဇီဝိၐျတိ၊
ndi kumudandaulira kwambiri nati, “Mwana wanga wamkazi wamngʼono ali pafupi kufa. Chonde tiyeni kuti mukamusanjike manja kuti akachiritsidwe nakhala ndi moyo.”
24 တဒါ ယီၑုသ္တေန သဟ စလိတး ကိန္တု တတ္ပၑ္စာဒ် ဗဟုလောကာၑ္စလိတွာ တာဒ္ဂါတြေ ပတိတား၊
Ndipo Yesu anapita naye. Gulu lalikulu la anthu linamutsata ndi kumamupanikiza Iye.
25 အထ ဒွါဒၑဝရ္ၐာဏိ ပြဒရရောဂေဏ
Pomwepo panali mayi amene amadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri.
26 ၑီရ္ဏာ စိကိတ္သကာနာံ နာနာစိကိတ္သာဘိၑ္စ ဒုးခံ ဘုက္တဝတီ စ သရွွသွံ ဝျယိတွာပိ နာရောဂျံ ပြာပ္တာ စ ပုနရပိ ပီဍိတာသီစ္စ
Iye anavutika kwambiri pamene asingʼanga ambiri ankamusamalira ndipo anagwiritsa ntchito zonse anali nazo, koma mʼmalo mochira, nthenda yake inkakulakulabe.
27 ယာ သ္တြီ သာ ယီၑော ရွာရ္တ္တာံ ပြာပျ မနသာကထယတ် ယဒျဟံ တသျ ဝသ္တြမာတြ သ္ပြၐ္ဋုံ လဘေယံ တဒါ ရောဂဟီနာ ဘဝိၐျာမိ၊
Atamva za Yesu, anabwera kumbuyo kwake mʼgulu la anthu ndipo anakhudza mkanjo wake,
28 အတောဟေတေား သာ လောကာရဏျမဓျေ တတ္ပၑ္စာဒါဂတျ တသျ ဝသ္တြံ ပသ္ပရ္ၑ၊
chifukwa anaganiza kuti, “Ngati nditangokhudza mkanjo wake, ndidzachiritsidwa.”
29 တေနဲဝ တတ္က္ၐဏံ တသျာ ရက္တသြောတး ၑုၐ္ကံ သွယံ တသ္မာဒ် ရောဂါန္မုက္တာ ဣတျပိ ဒေဟေ'နုဘူတာ၊
Nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka ndipo anamva mʼthupi mwake kuti wamasulidwa ku vuto lake.
30 အထ သွသ္မာတ် ၑက္တိ ရ္နိရ္ဂတာ ယီၑုရေတန္မနသာ ဇ္ဉာတွာ လောကနိဝဟံ ပြတိ မုခံ ဝျာဝၖတျ ပၖၐ္ဋဝါန် ကေန မဒွသ္တြံ သ္ပၖၐ္ဋံ?
Pomwepo Yesu anazindikira kuti mphamvu inachoka mʼthupi mwake. Anatembenuka mʼgulu la anthu ndipo anafunsa kuti, “Ndani wakhudza zovala zanga?”
31 တတသ္တသျ ၑိၐျာ ဦစုး ဘဝတော ဝပုၐိ လောကား သံဃရ္ၐန္တိ တဒ် ဒၖၐ္ဋွာ ကေန မဒွသ္တြံ သ္ပၖၐ္ဋမိတိ ကုတး ကထယတိ?
Ophunzira ake anayankha kuti, “Mukuona kuti anthu akukupanikizani, ndipo Inu mukufunsa kuti, ‘Ndani wandikhudza?’”
32 ကိန္တု ကေန တတ် ကရ္မ္မ ကၖတံ တဒ် ဒြၐ္ဋုံ ယီၑုၑ္စတုရ္ဒိၑော ဒၖၐ္ဋဝါန်၊
Koma Yesu anapitirizabe kuyangʼana kuti aone amene anachita zimenezi.
33 တတး သာ သ္တြီ ဘီတာ ကမ္ပိတာ စ သတီ သွသျာ ရုက္ပြတိကြိယာ ဇာတေတိ ဇ္ဉာတွာဂတျ တတ္သမ္မုခေ ပတိတွာ သရွွဝၖတ္တာန္တံ သတျံ တသ္မဲ ကထယာမာသ၊
Kenaka mayi uja pozindikira chimene chinamuchitikira, anabwera ndi kugwa pa mapazi ake, ndipo akunjenjemera ndi mantha, anamuwuza zoona zokhazokha.
34 တဒါနီံ ယီၑုသ္တာံ ဂဒိတဝါန်, ဟေ ကနျေ တဝ ပြတီတိသ္တွာမ် အရောဂါမကရောတ် တွံ က္ၐေမေဏ ဝြဇ သွရောဂါန္မုက္တာ စ တိၐ္ဌ၊
Anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere ndipo khala womasulidwa ku mavuto ako.”
35 ဣတိဝါကျဝဒနကာလေ ဘဇနဂၖဟာဓိပသျ နိဝေၑနာလ် လောကာ ဧတျာဓိပံ ဗဘာၐိရေ တဝ ကနျာ မၖတာ တသ္မာဒ် ဂုရုံ ပုနး ကုတး က္လိၑ္နာသိ?
Pamene Yesu ankayankhulabe, amuna ena anafika kuchokera ku nyumba ya Yairo, mkulu wa sunagoge. Iwo anati, “Mwana wanu wamkazi wamwalira, muvutitsiranjinso aphunzitsiwa?”
36 ကိန္တု ယီၑုသ္တဒ် ဝါကျံ ၑြုတွဲဝ ဘဇနဂၖဟာဓိပံ ဂဒိတဝါန် မာ ဘဲၐီး ကေဝလံ ဝိၑွာသိဟိ၊
Posasamala zomwe ananena, Yesu anamuwuza mkulu wa sunagoge uja kuti, “Usachite mantha; ingokhulupirira.”
37 အထ ပိတရော ယာကူဗ် တဒ္ဘြာတာ ယောဟန် စ ဧတာန် ဝိနာ ကမပိ သွပၑ္စာဒ် ယာတုံ နာနွမနျတ၊
Iye sanalole munthu wina aliyense kuti amutsatire koma Petro, Yakobo ndi Yohane mʼbale wa Yakobo.
38 တသျ ဘဇနဂၖဟာဓိပသျ နိဝေၑနသမီပမ် အာဂတျ ကလဟံ ဗဟုရောဒနံ ဝိလာပဉ္စ ကုရွွတော လောကာန် ဒဒရ္ၑ၊
Atafika ku nyumba ya mkulu wa sunagoge, Yesu anaona chipiringu cha anthu akulira ndi kufuwula kwambiri.
39 တသ္မာန် နိဝေၑနံ ပြဝိၑျ ပြောက္တဝါန် ယူယံ ကုတ ဣတ္ထံ ကလဟံ ရောဒနဉ္စ ကုရုထ? ကနျာ န မၖတာ နိဒြာတိ၊
Analowa nati kwa iwo, “Mukuchita phokoso ndi kulira chifukwa chiyani? Mwanayu sanamwalire koma ali mtulo.”
40 တသ္မာတ္တေ တမုပဇဟသုး ကိန္တု ယီၑုး သရွွာန ဗဟိၐ္ကၖတျ ကနျာယား ပိတရော် သွသင်္ဂိနၑ္စ ဂၖဟီတွာ ယတြ ကနျာသီတ် တတ် သ္ထာနံ ပြဝိၐ္ဋဝါန်၊
Koma anamuseka Iye. Atawatulutsa onse panja, Iye anatenga abambo ndi amayi ake a mwanayo ndi ophunzira omwe anali naye, ndipo analowa mʼmene munali mwanayo.
41 အထ သ တသျား ကနျာယာ ဟသ္တော် ဓၖတွာ တာံ ဗဘာၐေ ဋာလီထာ ကူမီ, အရ္ထတော ဟေ ကနျေ တွမုတ္တိၐ္ဌ ဣတျာဇ္ဉာပယာမိ၊
Anagwira dzanja lake nanena kwa iye, “Talita Kumi!” (Kutanthauza kuti, “Mtsikana, ndikunena ndi iwe, imirira!”)
42 တုနဲဝ တတ္က္ၐဏံ သာ ဒွါဒၑဝရ္ၐဝယသ္ကာ ကနျာ ပေါတ္ထာယ စလိတုမာရေဘေ, ဣတး သရွွေ မဟာဝိသ္မယံ ဂတား၊
Nthawi yomweyo anayimirira nayenda mozungulira (anali wa zaka khumi ndi ziwiri). Pa ichi onse anadabwa kwambiri.
43 တတ ဧတသျဲ ကိဉ္စိတ် ခါဒျံ ဒတ္တေတိ ကထယိတွာ ဧတတ္ကရ္မ္မ ကမပိ န ဇ္ဉာပယတေတိ ဒၖဎမာဒိၐ္ဋဝါန်၊
Anawalamulira kwambiri kuti asawuze wina aliyense za ichi, ndipo anawawuza kuti amupatse kanthu koti adye.

< မာရ္ကး 5 >