< လူကး 20 >

1 အထဲကဒါ ယီၑု ရ္မနိဒရေ သုသံဝါဒံ ပြစာရယန် လောကာနုပဒိၑတိ, ဧတရှိ ပြဓာနယာဇကာ အဓျာပကား ပြာဉ္စၑ္စ တန္နိကဋမာဂတျ ပပြစ္ဆုး
Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
2 ကယာဇ္ဉယာ တွံ ကရ္မ္မာဏျေတာနိ ကရောၐိ? ကော ဝါ တွာမာဇ္ဉာပယတ်? တဒသ္မာန် ဝဒ၊
Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
3 သ ပြတျုဝါစ, တရှိ ယုၐ္မာနပိ ကထာမေကာံ ပၖစ္ဆာမိ တသျောတ္တရံ ဝဒတ၊
Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
4 ယောဟနော မဇ္ဇနမ် ဤၑွရသျ မာနုၐာဏာံ ဝါဇ္ဉာတော ဇာတံ?
‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
5 တတသ္တေ မိထော ဝိဝိစျ ဇဂဒုး, ယဒီၑွရသျ ဝဒါမသ္တရှိ တံ ကုတော န ပြတျဲတ သ ဣတိ ဝက္ၐျတိ၊
Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
6 ယဒိ မနုၐျသျေတိ ဝဒါမသ္တရှိ သရွွေ လောကာ အသ္မာန် ပါၐာဏဲ ရှနိၐျန္တိ ယတော ယောဟန် ဘဝိၐျဒွါဒီတိ သရွွေ ဒၖဎံ ဇာနန္တိ၊
Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
7 အတဧဝ တေ ပြတျူစုး ကသျာဇ္ဉယာ ဇာတမ် ဣတိ ဝက္တုံ န ၑက္နုမး၊
Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
8 တဒါ ယီၑုရဝဒတ် တရှိ ကယာဇ္ဉယာ ကရ္မ္မာဏျေတာတိ ကရောမီတိ စ ယုၐ္မာန် န ဝက္ၐျာမိ၊
Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
9 အထ လောကာနာံ သာက္ၐာတ် သ ဣမာံ ဒၖၐ္ဋာန္တကထာံ ဝက္တုမာရေဘေ, ကၑ္စိဒ် ဒြာက္ၐာက္ၐေတြံ ကၖတွာ တတ် က္ၐေတြံ ကၖၐီဝလာနာံ ဟသ္တေၐု သမရ္ပျ ဗဟုကာလာရ္ထံ ဒူရဒေၑံ ဇဂါမ၊
Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
10 အထ ဖလကာလေ ဖလာနိ ဂြဟီတု ကၖၐီဝလာနာံ သမီပေ ဒါသံ ပြာဟိဏောတ် ကိန္တု ကၖၐီဝလာသ္တံ ပြဟၖတျ ရိက္တဟသ္တံ ဝိသသရ္ဇုး၊
Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
11 တတး သောဓိပတိး ပုနရနျံ ဒါသံ ပြေၐယာမာသ, တေ တမပိ ပြဟၖတျ ကုဝျဝဟၖတျ ရိက္တဟသ္တံ ဝိသသၖဇုး၊
Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
12 တတး သ တၖတီယဝါရမ် အနျံ ပြာဟိဏောတ် တေ တမပိ က္ၐတာင်္ဂံ ကၖတွာ ဗဟိ ရ္နိစိက္ၐိပုး၊
Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
13 တဒါ က္ၐေတြပတိ ရွိစာရယာမာသ, မမေဒါနီံ ကိံ ကရ္တ္တဝျံ? မမ ပြိယေ ပုတြေ ပြဟိတေ တေ တမဝၑျံ ဒၖၐ္ဋွာ သမာဒရိၐျန္တေ၊
“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
14 ကိန္တု ကၖၐီဝလာသ္တံ နိရီက္ၐျ ပရသ္ပရံ ဝိဝိစျ ပြောစုး, အယမုတ္တရာဓိကာရီ အာဂစ္ဆတဲနံ ဟန္မသ္တတောဓိကာရောသ္မာကံ ဘဝိၐျတိ၊
“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
15 တတသ္တေ တံ က္ၐေတြာဒ် ဗဟိ ရ္နိပါတျ ဇဃ္နုသ္တသ္မာတ် သ က္ၐေတြပတိသ္တာန် ပြတိ ကိံ ကရိၐျတိ?
Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
16 သ အာဂတျ တာန် ကၖၐီဝလာန် ဟတွာ ပရေၐာံ ဟသ္တေၐု တတ္က္ၐေတြံ သမရ္ပယိၐျတိ; ဣတိ ကထာံ ၑြုတွာ တေ 'ဝဒန် ဧတာဒၖၑီ ဃဋနာ န ဘဝတု၊
Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
17 ကိန္တု ယီၑုသ္တာနဝလောကျ ဇဂါဒ, တရှိ, သ္ထပတယး ကရိၐျန္တိ ဂြာဝါဏံ ယန္တု တုစ္ဆကံ၊ ပြဓာနပြသ္တရး ကောဏေ သ ဧဝ ဟိ ဘဝိၐျတိ၊ ဧတသျ ၑာသ္တြီယဝစနသျ ကိံ တာတ္ပရျျံ?
Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
18 အပရံ တတ္ပာၐာဏောပရိ ယး ပတိၐျတိ သ ဘံက္ၐျတေ ကိန္တု ယသျောပရိ သ ပါၐာဏး ပတိၐျတိ သ တေန ဓူလိဝစ် စူရ္ဏီဘဝိၐျတိ၊
Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
19 သောသ္မာကံ ဝိရုဒ္ဓံ ဒၖၐ္ဋာန္တမိမံ ကထိတဝါန် ဣတိ ဇ္ဉာတွာ ပြဓာနယာဇကာ အဓျာပကာၑ္စ တဒဲဝ တံ ဓရ္တုံ ဝဝါဉ္ဆုး ကိန္တု လောကေဘျော ဗိဘျုး၊
Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
20 အတဧဝ တံ ပြတိ သတရ္ကား သန္တး ကထံ တဒွါကျဒေါၐံ ဓၖတွာ တံ ဒေၑာဓိပသျ သာဓုဝေၑဓာရိဏၑ္စရာန် တသျ သမီပေ ပြေၐယာမာသုး၊
Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
21 တဒါ တေ တံ ပပြစ္ဆုး, ဟေ ဥပဒေၑက ဘဝါန် ယထာရ္ထံ ကထယန် ဥပဒိၑတိ, ကမပျနပေက္ၐျ သတျတွေနဲၑွရံ မာရ္ဂမုပဒိၑတိ, ဝယမေတဇ္ဇာနီမး၊
Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
22 ကဲသရရာဇာယ ကရောသ္မာဘိ ရ္ဒေယော န ဝါ?
Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
23 သ တေၐာံ ဝဉ္စနံ ဇ္ဉာတွာဝဒတ် ကုတော မာံ ပရီက္ၐဓွေ? မာံ မုဒြာမေကံ ဒရ္ၑယတ၊
Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
24 ဣဟ လိခိတာ မူရ္တိရိယံ နာမ စ ကသျ? တေ'ဝဒန် ကဲသရသျ၊
“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
25 တဒါ သ ဥဝါစ, တရှိ ကဲသရသျ ဒြဝျံ ကဲသရာယ ဒတ္တ; ဤၑွရသျ တု ဒြဝျမီၑွရာယ ဒတ္တ၊
Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
26 တသ္မာလ္လောကာနာံ သာက္ၐာတ် တတ္ကထာယား ကမပိ ဒေါၐံ ဓရ္တုမပြာပျ တေ တသျောတ္တရာဒ် အာၑ္စရျျံ မနျမာနာ မော်နိနသ္တသ္ထုး၊
Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
27 အပရဉ္စ ၑ္မၑာနာဒုတ္ထာနာနင်္ဂီကာရိဏာံ သိဒူကိနာံ ကိယန္တော ဇနာ အာဂတျ တံ ပပြစ္ဆုး,
Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
28 ဟေ ဥပဒေၑက ၑာသ္တြေ မူသာ အသ္မာန် ပြတီတိ လိလေခ ယသျ ဘြာတာ ဘာရျျာယာံ သတျာံ နိးသန္တာနော မြိယတေ သ တဇ္ဇာယာံ ဝိဝဟျ တဒွံၑမ် ဥတ္ပာဒယိၐျတိ၊
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
29 တထာစ ကေစိတ် သပ္တ ဘြာတရ အာသန် တေၐာံ ဇျေၐ္ဌော ဘြာတာ ဝိဝဟျ နိရပတျး ပြာဏာန် ဇဟော်၊
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
30 အထ ဒွိတီယသ္တသျ ဇာယာံ ဝိဝဟျ နိရပတျး သန် မမာရ၊ တၖတီယၑ္စ တာမေဝ ဝျုဝါဟ;
Wachiwiri
31 ဣတ္ထံ သပ္တ ဘြာတရသ္တာမေဝ ဝိဝဟျ နိရပတျား သန္တော မမြုး၊
ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
32 ၑေၐေ သာ သ္တြီ စ မမာရ၊
Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
33 အတဧဝ ၑ္မၑာနာဒုတ္ထာနကာလေ တေၐာံ သပ္တဇနာနာံ ကသျ သာ ဘာရျျာ ဘဝိၐျတိ? ယတး သာ တေၐာံ သပ္တာနာမေဝ ဘာရျျာသီတ်၊
Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
34 တဒါ ယီၑုး ပြတျုဝါစ, ဧတသျ ဇဂတော လောကာ ဝိဝဟန္တိ ဝါဂ္ဒတ္တာၑ္စ ဘဝန္တိ (aiōn g165)
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn g165)
35 ကိန္တု ယေ တဇ္ဇဂတ္ပြာပ္တိယောဂျတွေန ဂဏိတာံ ဘဝိၐျန္တိ ၑ္မၑာနာစ္စောတ္ထာသျန္တိ တေ န ဝိဝဟန္တိ ဝါဂ္ဒတ္တာၑ္စ န ဘဝန္တိ, (aiōn g165)
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn g165)
36 တေ ပုန ရ္န မြိယန္တေ ကိန္တု ၑ္မၑာနာဒုတ္ထာပိတား သန္တ ဤၑွရသျ သန္တာနား သွရ္ဂီယဒူတာနာံ သဒၖၑာၑ္စ ဘဝန္တိ၊
Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
37 အဓိကန္တု မူသား သ္တမ္ဗောပါချာနေ ပရမေၑွရ ဤဗြာဟီမ ဤၑွရ ဣသှာက ဤၑွရော ယာကူဗၑ္စေၑွရ ဣတျုက္တွာ မၖတာနာံ ၑ္မၑာနာဒ် ဥတ္ထာနသျ ပြမာဏံ လိလေခ၊
Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
38 အတဧဝ ယ ဤၑွရး သ မၖတာနာံ ပြဘု ရ္န ကိန္တု ဇီဝတာမေဝ ပြဘုး, တန္နိကဋေ သရွွေ ဇီဝန္တး သန္တိ၊
Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
39 ဣတိ ၑြုတွာ ကိယန္တောဓျာပကာ ဦစုး, ဟေ ဥပဒေၑက ဘဝါန် ဘဒြံ ပြတျုက္တဝါန်၊
Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
40 ဣတး ပရံ တံ ကိမပိ ပြၐ္ဋံ တေၐာံ ပြဂလ္ဘတာ နာဘူတ်၊
Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
41 ပၑ္စာတ် သ တာန် ဥဝါစ, ယး ခြီၐ္ဋး သ ဒါယူဒး သန္တာန ဧတာံ ကထာံ လောကား ကထံ ကထယန္တိ?
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
42 ယတး မမ ပြဘုမိဒံ ဝါကျမဝဒတ် ပရမေၑွရး၊ တဝ ၑတြူနဟံ ယာဝတ် ပါဒပီဌံ ကရောမိ န၊ တာဝတ် ကာလံ မဒီယေ တွံ ဒက္ၐပါရ္ၑွ ဥပါဝိၑ၊
Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
43 ဣတိ ကထာံ ဒါယူဒ် သွယံ ဂီတဂြန္ထေ'ဝဒတ်၊
mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
44 အတဧဝ ယဒိ ဒါယူဒ် တံ ပြဘုံ ဝဒတိ, တရှိ သ ကထံ တသျ သန္တာနော ဘဝတိ?
Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
45 ပၑ္စာဒ် ယီၑုး သရွွဇနာနာံ ကရ္ဏဂေါစရေ ၑိၐျာနုဝါစ,
Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
46 ယေ'ဓျာပကာ ဒီရ္ဃပရိစ္ဆဒံ ပရိဓာယ ဘြမန္တိ, ဟဋ္ဋာပဏယော ရ္နမသ္ကာရေ ဘဇနဂေဟသျ ပြောစ္စာသနေ ဘောဇနဂၖဟသျ ပြဓာနသ္ထာနေ စ ပြီယန္တေ
“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
47 ဝိဓဝါနာံ သရွွသွံ ဂြသိတွာ ဆလေန ဒီရ္ဃကာလံ ပြာရ္ထယန္တေ စ တေၐု သာဝဓာနာ ဘဝတ, တေၐာမုဂြဒဏ္ဍော ဘဝိၐျတိ၊
Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”

< လူကး 20 >