< လူကး 18 >

1 အပရဉ္စ လောကဲရက္လာန္တဲ ရ္နိရန္တရံ ပြာရ္ထယိတဝျမ် ဣတျာၑယေန ယီၑုနာ ဒၖၐ္ဋာန္တ ဧကး ကထိတး၊
Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
2 ကုတြစိန္နဂရေ ကၑ္စိတ် ပြာဍွိဝါက အာသီတ် သ ဤၑွရာန္နာဗိဘေတ် မာနုၐာံၑ္စ နာမနျတ၊
Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
3 အထ တတ္ပုရဝါသိနီ ကာစိဒွိဓဝါ တတ္သမီပမေတျ ဝိဝါဒိနာ သဟ မမ ဝိဝါဒံ ပရိၐ္ကုရွွိတိ နိဝေဒယာမာသ၊
Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
4 တတး သ ပြာဍွိဝါကး ကိယဒ္ဒိနာနိ န တဒင်္ဂီကၖတဝါန် ပၑ္စာစ္စိတ္တေ စိန္တယာမာသ, ယဒျပီၑွရာန္န ဗိဘေမိ မနုၐျာနပိ န မနျေ
“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
5 တထာပျေၐာ ဝိဓဝါ မာံ က္လိၑ္နာတိ တသ္မာဒသျာ ဝိဝါဒံ ပရိၐ္ကရိၐျာမိ နောစေတ် သာ သဒါဂတျ မာံ ဝျဂြံ ကရိၐျတိ၊
koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
6 ပၑ္စာတ် ပြဘုရဝဒဒ် အသာဝနျာယပြာဍွိဝါကော ယဒါဟ တတြ မနော နိဓဓွံ၊
Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
7 ဤၑွရသျ ယေ 'ဘိရုစိတလောကာ ဒိဝါနိၑံ ပြာရ္ထယန္တေ သ ဗဟုဒိနာနိ ဝိလမ္ဗျာပိ တေၐာံ ဝိဝါဒါန် ကိံ န ပရိၐ္ကရိၐျတိ?
Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
8 ယုၐ္မာနဟံ ဝဒါမိ တွရယာ ပရိၐ္ကရိၐျတိ, ကိန္တု ယဒါ မနုၐျပုတြ အာဂမိၐျတိ တဒါ ပၖထိဝျာံ ကိမီဒၖၑံ ဝိၑွာသံ ပြာပ္သျတိ?
Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
9 ယေ သွာန် ဓာရ္မ္မိကာန် ဇ္ဉာတွာ ပရာန် တုစ္ဆီကုရွွန္တိ ဧတာဒၖဂ္ဘျး, ကိယဒ္ဘျ ဣမံ ဒၖၐ္ဋာန္တံ ကထယာမာသ၊
Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
10 ဧကး ဖိရူၑျပရး ကရသဉ္စာယီ ဒွါဝိမော် ပြာရ္ထယိတုံ မန္ဒိရံ ဂတော်၊
“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
11 တတော'သော် ဖိရူၑျေကပါရ္ၑွေ တိၐ္ဌန် ဟေ ဤၑွရ အဟမနျလောကဝတ် လောဌယိတာနျာယီ ပါရဒါရိကၑ္စ န ဘဝါမိ အသျ ကရသဉ္စာယိနသ္တုလျၑ္စ န, တသ္မာတ္တွာံ ဓနျံ ဝဒါမိ၊
Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
12 သပ္တသု ဒိနေၐု ဒိနဒွယမုပဝသာမိ သရွွသမ္ပတ္တေ ရ္ဒၑမာံၑံ ဒဒါမိ စ, ဧတတ္ကထာံ ကထယန် ပြာရ္ထယာမာသ၊
Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
13 ကိန္တု သ ကရသဉ္စာယိ ဒူရေ တိၐ္ဌန် သွရ္ဂံ ဒြၐ္ဋုံ နေစ္ဆန် ဝက္ၐသိ ကရာဃာတံ ကုရွွန် ဟေ ဤၑွရ ပါပိၐ္ဌံ မာံ ဒယသွ, ဣတ္ထံ ပြာရ္ထယာမာသ၊
“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
14 ယုၐ္မာနဟံ ဝဒါမိ, တယောရ္ဒွယော ရ္မဓျေ ကေဝလး ကရသဉ္စာယီ ပုဏျဝတ္တွေန ဂဏိတော နိဇဂၖဟံ ဇဂါမ, ယတော ယး ကၑ္စိတ် သွမုန္နမယတိ သ နာမယိၐျတေ ကိန္တု ယး ကၑ္စိတ် သွံ နမယတိ သ ဥန္နမယိၐျတေ၊
“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
15 အထ ၑိၑူနာံ ဂါတြသ္ပရ္ၑာရ္ထံ လောကာသ္တာန် တသျ သမီပမာနိနျုး ၑိၐျာသ္တဒ် ဒၖၐ္ဋွာနေတၖန် တရ္ဇယာမာသုး,
Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
16 ကိန္တု ယီၑုသ္တာနာဟူယ ဇဂါဒ, မန္နိကဋမ် အာဂန္တုံ ၑိၑူန် အနုဇာနီဓွံ တာံၑ္စ မာ ဝါရယတ; ယတ ဤၑွရရာဇျာဓိကာရိဏ ဧၐာံ သဒၖၑား၊
Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
17 အဟံ ယုၐ္မာန် ယထာရ္ထံ ဝဒါမိ, ယော ဇနး ၑိၑေား သဒၖၑော ဘူတွာ ဤၑွရရာဇျံ န ဂၖဟ္လာတိ သ ကေနာပိ ပြကာရေဏ တတ် ပြဝေၐ္ဋုံ န ၑက္နောတိ၊
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
18 အပရမ် ဧကောဓိပတိသ္တံ ပပြစ္ဆ, ဟေ ပရမဂုရော, အနန္တာယုၐး ပြာပ္တယေ မယာ ကိံ ကရ္တ္တဝျံ? (aiōnios g166)
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
19 ယီၑုရုဝါစ, မာံ ကုတး ပရမံ ဝဒသိ? ဤၑွရံ ဝိနာ ကောပိ ပရမော န ဘဝတိ၊
Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
20 ပရဒါရာန် မာ ဂစ္ဆ, နရံ မာ ဇဟိ, မာ စောရယ, မိထျာသာက္ၐျံ မာ ဒေဟိ, မာတရံ ပိတရဉ္စ သံမနျသွ, ဧတာ ယာ အာဇ္ဉား သန္တိ တာသ္တွံ ဇာနာသိ၊
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
21 တဒါ သ ဥဝါစ, ဗာလျကာလာတ် သရွွာ ဧတာ အာစရာမိ၊
Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
22 ဣတိ ကထာံ ၑြုတွာ ယီၑုသ္တမဝဒတ်, တထာပိ တဝဲကံ ကရ္မ္မ နျူနမာသ္တေ, နိဇံ သရွွသွံ ဝိကြီယ ဒရိဒြေဘျော ဝိတရ, တသ္မာတ် သွရ္ဂေ ဓနံ ပြာပ္သျသိ; တတ အာဂတျ မမာနုဂါမီ ဘဝ၊
Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
23 ကိန္တွေတာံ ကထာံ ၑြုတွာ သောဓိပတိး ၑုၑောစ, ယတသ္တသျ ဗဟုဓနမာသီတ်၊
Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
24 တဒါ ယီၑုသ္တမတိၑောကာနွိတံ ဒၖၐ္ဋွာ ဇဂါဒ, ဓနဝတာမ် ဤၑွရရာဇျပြဝေၑး ကီဒၖဂ် ဒုၐ္ကရး၊
Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
25 ဤၑွရရာဇျေ ဓနိနး ပြဝေၑာတ် သူစေၑ္ဆိဒြေဏ မဟာင်္ဂသျ ဂမနာဂမနေ သုကရေ၊
Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
26 ၑြောတာရး ပပြစ္ဆုသ္တရှိ ကေန ပရိတြာဏံ ပြာပ္သျတေ?
Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 သ ဥက္တဝါန်, ယန် မာနုၐေဏာၑကျံ တဒ် ဤၑွရေဏ ၑကျံ၊
Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
28 တဒါ ပိတရ ဥဝါစ, ပၑျ ဝယံ သရွွသွံ ပရိတျဇျ တဝ ပၑ္စာဒ္ဂါမိနော'ဘဝါမ၊
Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
29 တတး သ ဥဝါစ, ယုၐ္မာနဟံ ယထာရ္ထံ ဝဒါမိ, ဤၑွရရာဇျာရ္ထံ ဂၖဟံ ပိတရော် ဘြာတၖဂဏံ ဇာယာံ သန္တာနာံၑ္စ တျက္တဝါ
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
30 ဣဟ ကာလေ တတော'ဓိကံ ပရကာလေ 'နန္တာယုၑ္စ န ပြာပ္သျတိ လောက ဤဒၖၑး ကောပိ နာသ္တိ၊ (aiōn g165, aiōnios g166)
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
31 အနန္တရံ သ ဒွါဒၑၑိၐျာနာဟူယ ဗဘာၐေ, ပၑျတ ဝယံ ယိရူၑာလမ္နဂရံ ယာမး, တသ္မာတ် မနုၐျပုတြေ ဘဝိၐျဒွါဒိဘိရုက္တံ ယဒသ္တိ တဒနုရူပံ တံ ပြတိ ဃဋိၐျတေ;
Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
32 ဝသ္တုတသ္တု သော'နျဒေၑီယာနာံ ဟသ္တေၐု သမရ္ပယိၐျတေ, တေ တမုပဟသိၐျန္တိ, အနျာယမာစရိၐျန္တိ တဒွပုၐိ နိၐ္ဌီဝံ နိက္ၐေပ္သျန္တိ, ကၑာဘိး ပြဟၖတျ တံ ဟနိၐျန္တိ စ,
Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
33 ကိန္တု တၖတီယဒိနေ သ ၑ္မၑာနာဒ် ဥတ္ထာသျတိ၊
adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
34 ဧတသျား ကထာယာ အဘိပြာယံ ကိဉ္စိဒပိ တေ ဗောဒ္ဓုံ န ၑေကုး တေၐာံ နိကဋေ'သ္ပၐ္ဋတဝါတ် တသျဲတာသာံ ကထာနာမ် အာၑယံ တေ ဇ္ဉာတုံ န ၑေကုၑ္စ၊
Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
35 အထ တသ္မိန် ယိရီဟေား ပုရသျာန္တိကံ ပြာပ္တေ ကၑ္စိဒန္ဓး ပထး ပါရ္ၑွ ဥပဝိၑျ ဘိက္ၐာမ် အကရောတ္
Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
36 သ လောကသမူဟသျ ဂမနၑဗ္ဒံ ၑြုတွာ တတ္ကာရဏံ ပၖၐ္ဋဝါန်၊
anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
37 နာသရတီယယီၑုရျာတီတိ လောကဲရုက္တေ သ ဥစ္စဲရွက္တုမာရေဘေ,
Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
38 ဟေ ဒါယူဒး သန္တာန ယီၑော မာံ ဒယသွ၊
Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
39 တတောဂြဂါမိနသ္တံ မော်နီ တိၐ္ဌေတိ တရ္ဇယာမာသုး ကိန္တု သ ပုနာရုဝန် ဥဝါစ, ဟေ ဒါယူဒး သန္တာန မာံ ဒယသွ၊
Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
40 တဒါ ယီၑုး သ္ထဂိတော ဘူတွာ သွာန္တိကေ တမာနေတုမ် အာဒိဒေၑ၊
Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
41 တတး သ တသျာန္တိကမ် အာဂမတ်, တဒါ သ တံ ပပြစ္ဆ, တွံ ကိမိစ္ဆသိ? တွဒရ္ထမဟံ ကိံ ကရိၐျာမိ? သ ဥက္တဝါန်, ဟေ ပြဘော'ဟံ ဒြၐ္ဋုံ လဘဲ၊
“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
42 တဒါ ယီၑုရုဝါစ, ဒၖၐ္ဋိၑက္တိံ ဂၖဟာဏ တဝ ပြတျယသ္တွာံ သွသ္ထံ ကၖတဝါန်၊
Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
43 တတသ္တတ္က္ၐဏာတ် တသျ စက္ၐုၐီ ပြသန္နေ; တသ္မာတ် သ ဤၑွရံ ဓနျံ ဝဒန် တတ္ပၑ္စာဒ် ယယော်, တဒါလောကျ သရွွေ လောကာ ဤၑွရံ ပြၑံသိတုမ် အာရေဘိရေ၊
Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

< လူကး 18 >