< လူကး 17 >

1 ဣတး ပရံ ယီၑုး ၑိၐျာန် ဥဝါစ, ဝိဃ္နဲရဝၑျမ် အာဂန္တဝျံ ကိန္တု ဝိဃ္နာ ယေန ဃဋိၐျန္တေ တသျ ဒုရ္ဂတိ ရ္ဘဝိၐျတိ၊
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 ဧတေၐာံ က္ၐုဒြပြာဏိနာမ် ဧကသျာပိ ဝိဃ္နဇနနာတ် ကဏ္ဌဗဒ္ဓပေၐဏီကသျ တသျ သာဂရာဂါဓဇလေ မဇ္ဇနံ ဘဒြံ၊
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 ယူယံ သွေၐု သာဝဓာနာသ္တိၐ္ဌတ; တဝ ဘြာတာ ယဒိ တဝ ကိဉ္စိဒ် အပရာဓျတိ တရှိ တံ တရ္ဇယ, တေန ယဒိ မနး ပရိဝရ္တ္တယတိ တရှိ တံ က္ၐမသွ၊
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 ပုနရေကဒိနမဓျေ ယဒိ သ တဝ သပ္တကၖတွော'ပရာဓျတိ ကိန္တု သပ္တကၖတွ အာဂတျ မနး ပရိဝရ္တျ မယာပရာဒ္ဓမ် ဣတိ ဝဒတိ တရှိ တံ က္ၐမသွ၊
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 တဒါ ပြေရိတား ပြဘုမ် အဝဒန် အသ္မာကံ ဝိၑွာသံ ဝရ္ဒ္ဓယ၊
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 ပြဘုရုဝါစ, ယဒိ ယုၐ္မာကံ သရ္ၐပဲကပြမာဏော ဝိၑွာသောသ္တိ တရှိ တွံ သမူလမုတ္ပာဋိတော ဘူတွာ သမုဒြေ ရောပိတော ဘဝ ကထာယာမ် ဧတသျာမ် ဧတဒုဍုမ္ဗရာယ ကထိတာယာံ သ ယုၐ္မာကမာဇ္ဉာဝဟော ဘဝိၐျတိ၊
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 အပရံ သွဒါသေ ဟလံ ဝါဟယိတွာ ဝါ ပၑူန် စာရယိတွာ က္ၐေတြာဒ် အာဂတေ သတိ တံ ဝဒတိ, ဧဟိ ဘောက္တုမုပဝိၑ, ယုၐ္မာကမ် ဧတာဒၖၑး ကောသ္တိ?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 ဝရဉ္စ ပူရွွံ မမ ခါဒျမာသာဒျ ယာဝဒ် ဘုဉ္ဇေ ပိဝါမိ စ တာဝဒ် ဗဒ္ဓကဋိး ပရိစရ ပၑ္စာတ် တွမပိ ဘောက္ၐျသေ ပါသျသိ စ ကထာမီဒၖၑီံ ကိံ န ဝက္ၐျတိ?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 တေန ဒါသေန ပြဘောရာဇ္ဉာနုရူပေ ကရ္မ္မဏိ ကၖတေ ပြဘုး ကိံ တသ္မိန် ဗာဓိတော ဇာတး? နေတ္ထံ ဗုဓျတေ မယာ၊
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 ဣတ္ထံ နိရူပိတေၐု သရွွကရ္မ္မသု ကၖတေၐု သတ္မု ယူယမပီဒံ ဝါကျံ ဝဒထ, ဝယမ် အနုပကာရိဏော ဒါသာ အသ္မာဘိရျဒျတ္ကရ္တ္တဝျံ တန္မာတြမေဝ ကၖတံ၊
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 သ ယိရူၑာလမိ ယာတြာံ ကုရွွန် ၑောမိရောဏ္ဂာလီလ္ပြဒေၑမဓျေန ဂစ္ဆတိ,
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 ဧတရှိ ကုတြစိဒ် ဂြာမေ ပြဝေၑမာတြေ ဒၑကုၐ္ဌိနသ္တံ သာက္ၐာတ် ကၖတွာ
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 ဒူရေ တိၐ္ဌနတ ဥစ္စဲ ရွက္တုမာရေဘိရေ, ဟေ ပြဘော ယီၑော ဒယသွာသ္မာန်၊
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 တတး သ တာန် ဒၖၐ္ဋွာ ဇဂါဒ, ယူယံ ယာဇကာနာံ သမီပေ သွာန် ဒရ္ၑယတ, တတသ္တေ ဂစ္ဆန္တော ရောဂါတ် ပရိၐ္ကၖတား၊
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 တဒါ တေၐာမေကး သွံ သွသ္ထံ ဒၖၐ္ဋွာ ပြောစ္စဲရီၑွရံ ဓနျံ ဝဒန် ဝျာဃုဋျာယာတော ယီၑော ရ္ဂုဏာနနုဝဒန် တစ္စရဏာဓောဘူမော် ပပါတ;
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 သ စာသီတ် ၑောမိရောဏီ၊
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 တဒါ ယီၑုရဝဒတ်, ဒၑဇနား ကိံ န ပရိၐ္ကၖတား? တဟျနျေ နဝဇနား ကုတြ?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 ဤၑွရံ ဓနျံ ဝဒန္တမ် ဧနံ ဝိဒေၑိနံ ဝိနာ ကောပျနျော န ပြာပျတ၊
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 တဒါ သ တမုဝါစ, တွမုတ္ထာယ ယာဟိ ဝိၑွာသသ္တေ တွာံ သွသ္ထံ ကၖတဝါန်၊
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 အထ ကဒေၑွရသျ ရာဇတွံ ဘဝိၐျတီတိ ဖိရူၑိဘိး ပၖၐ္ဋေ သ ပြတျုဝါစ, ဤၑွရသျ ရာဇတွမ် အဲၑွရျျဒရ္ၑနေန န ဘဝိၐျတိ၊
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 အတ ဧတသ္မိန် ပၑျ တသ္မိန် ဝါ ပၑျ, ဣတိ ဝါကျံ လောကာ ဝက္တုံ န ၑက္ၐျန္တိ, ဤၑွရသျ ရာဇတွံ ယုၐ္မာကမ် အန္တရေဝါသ္တေ၊
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 တတး သ ၑိၐျာန် ဇဂါဒ, ယဒါ ယုၐ္မာဘိ ရ္မနုဇသုတသျ ဒိနမေကံ ဒြၐ္ဋုမ် ဝါဉ္ဆိၐျတေ ကိန္တု န ဒရ္ၑိၐျတေ, ဤဒၖက္ကာလ အာယာတိ၊
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 တဒါတြ ပၑျ ဝါ တတြ ပၑျေတိ ဝါကျံ လောကာ ဝက္ၐျန္တိ, ကိန္တု တေၐာံ ပၑ္စာတ် မာ ယာတ, မာနုဂစ္ဆတ စ၊
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 ယတသ္တဍိဒ် ယထာကာၑဲကဒိၑျုဒိယ တဒနျာမပိ ဒိၑံ ဝျာပျ ပြကာၑတေ တဒွတ် နိဇဒိနေ မနုဇသူနုး ပြကာၑိၐျတေ၊
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 ကိန္တု တတ္ပူရွွံ တေနာနေကာနိ ဒုးခါနိ ဘောက္တဝျာနျေတဒွရ္တ္တမာနလောကဲၑ္စ သော'ဝဇ္ဉာတဝျး၊
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 နောဟသျ ဝိဒျမာနကာလေ ယထာဘဝတ် မနုၐျသူနေား ကာလေပိ တထာ ဘဝိၐျတိ၊
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 ယာဝတ္ကာလံ နောဟော မဟာပေါတံ နာရောဟဒ် အာပ္လာဝိဝါရျျေတျ သရွွံ နာနာၑယစ္စ တာဝတ္ကာလံ ယထာ လောကာ အဘုဉ္ဇတာပိဝန် ဝျဝဟန် ဝျဝါဟယံၑ္စ;
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 ဣတ္ထံ လောဋော ဝရ္တ္တမာနကာလေပိ ယထာ လောကာ ဘောဇနပါနကြယဝိကြယရောပဏဂၖဟနိရ္မ္မာဏကရ္မ္မသု ပြာဝရ္တ္တန္တ,
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 ကိန္တု ယဒါ လောဋ် သိဒေါမော နိရ္ဇဂါမ တဒါ နဘသး သဂန္ဓကာဂ္နိဝၖၐ္ဋိ ရ္ဘူတွာ သရွွံ ဝျနာၑယတ္
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 တဒွန် မာနဝပုတြပြကာၑဒိနေပိ ဘဝိၐျတိ၊
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 တဒါ ယဒိ ကၑ္စိဒ် ဂၖဟောပရိ တိၐ္ဌတိ တရှိ သ ဂၖဟမဓျာတ် ကိမပိ ဒြဝျမာနေတုမ် အဝရုဟျ နဲတု; ယၑ္စ က္ၐေတြေ တိၐ္ဌတိ သောပိ ဝျာဃုဋျ နာယာတု၊
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 လောဋး ပတ္နီံ သ္မရတ၊
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 ယး ပြာဏာန် ရက္ၐိတုံ စေၐ္ဋိၐျတေ သ ပြာဏာန် ဟာရယိၐျတိ ယသ္တု ပြာဏာန် ဟာရယိၐျတိ သဧဝ ပြာဏာန် ရက္ၐိၐျတိ၊
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 ယုၐ္မာနဟံ ဝစ္မိ တသျာံ ရာတြော် ၑယျဲကဂတယော ရ္လောကယောရေကော ဓာရိၐျတေ ပရသ္တျက္ၐျတေ၊
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 သ္တြိယော် ယုဂပတ် ပေၐဏီံ ဝျာဝရ္တ္တယိၐျတသ္တယောရေကာ ဓာရိၐျတေ ပရာတျက္ၐျတေ၊
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 ပုရုၐော် က္ၐေတြေ သ္ထာသျတသ္တယောရေကော ဓာရိၐျတေ ပရသ္တျက္ၐျတေ၊
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 တဒါ တေ ပပြစ္ဆုး, ဟေ ပြဘော ကုတြေတ္ထံ ဘဝိၐျတိ? တတး သ ဥဝါစ, ယတြ ၑဝသ္တိၐ္ဌတိ တတြ ဂၖဓြာ မိလန္တိ၊
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< လူကး 17 >