< လူကး 1 >

1 ပြထမတော ယေ သာက္ၐိဏော ဝါကျပြစာရကာၑ္စာသန် တေ'သ္မာကံ မဓျေ ယဒျတ် သပြမာဏံ ဝါကျမရ္ပယန္တိ သ္မ
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 တဒနုသာရတော'နျေပိ ဗဟဝသ္တဒွၖတ္တာန္တံ ရစယိတုံ ပြဝၖတ္တား၊
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 အတဧဝ ဟေ မဟာမဟိမထိယဖိလ် တွံ ယာ ယား ကထာ အၑိက္ၐျထာသ္တာသာံ ဒၖဎပြမာဏာနိ ယထာ ပြာပ္နောၐိ
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 တဒရ္ထံ ပြထမမာရဘျ တာနိ သရွွာဏိ ဇ္ဉာတွာဟမပိ အနုကြမာတ် သရွွဝၖတ္တာန္တာန် တုဘျံ လေခိတုံ မတိမကာရ္ၐမ်၊
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 ယိဟူဒါဒေၑီယဟေရောဒ္နါမကေ ရာဇတွံ ကုရွွတိ အဗီယယာဇကသျ ပရျျာယာဓိကာရီ သိခရိယနာမက ဧကော ယာဇကော ဟာရောဏဝံၑောဒ္ဘဝါ ဣလီၑေဝါချာ
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 တသျ ဇာယာ ဒွါဝိမော် နိရ္ဒောၐော် ပြဘေား သရွွာဇ္ဉာ ဝျဝသ္ထာၑ္စ သံမနျ ဤၑွရဒၖၐ္ဋော် ဓာရ္မ္မိကာဝါသ္တာမ်၊
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 တယေား သန္တာန ဧကောပိ နာသီတ်, ယတ ဣလီၑေဝါ ဗန္ဓျာ တော် ဒွါဝေဝ ဝၖဒ္ဓါဝဘဝတာမ်၊
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 ယဒါ သွပရျျာနုကြမေဏ သိခရိယ ဤၑွာသျ သမက္ၐံ ယာဇကီယံ ကရ္မ္မ ကရောတိ
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 တဒါ ယဇ္ဉသျ ဒိနပရိပါယျာ ပရမေၑွရသျ မန္ဒိရေ ပြဝေၑကာလေ ဓူပဇွာလနံ ကရ္မ္မ တသျ ကရဏီယမာသီတ်၊
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 တဒ္ဓူပဇွာလနကာလေ လောကနိဝဟေ ပြာရ္ထနာံ ကရ္တုံ ဗဟိသ္တိၐ္ဌတိ
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 သတိ သိခရိယော ယသျာံ ဝေဒျာံ ဓူပံ ဇွာလယတိ တဒ္ဒက္ၐိဏပါရ္ၑွေ ပရမေၑွရသျ ဒူတ ဧက ဥပသ္ထိတော ဒရ္ၑနံ ဒဒေါ်၊
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 တံ ဒၖၐ္ဋွာ သိခရိယ ဥဒွိဝိဇေ ၑၑင်္ကေ စ၊
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 တဒါ သ ဒူတသ္တံ ဗဘာၐေ ဟေ သိခရိယ မာ ဘဲသ္တဝ ပြာရ္ထနာ ဂြာဟျာ ဇာတာ တဝ ဘာရျျာ ဣလီၑေဝါ ပုတြံ ပြသောၐျတေ တသျ နာမ ယောဟန် ဣတိ ကရိၐျသိ၊
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 ကိဉ္စ တွံ သာနန္ဒး သဟရ္ၐၑ္စ ဘဝိၐျသိ တသျ ဇန္မနိ ဗဟဝ အာနန္ဒိၐျန္တိ စ၊
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 ယတော ဟေတေား သ ပရမေၑွရသျ ဂေါစရေ မဟာန် ဘဝိၐျတိ တထာ ဒြာက္ၐာရသံ သုရာံ ဝါ ကိမပိ န ပါသျတိ, အပရံ ဇန္မာရဘျ ပဝိတြေဏာတ္မနာ ပရိပူရ္ဏး
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 သန် ဣသြာယေလွံၑီယာန် အနေကာန် ပြဘေား ပရမေၑွရသျ မာရ္ဂမာနေၐျတိ၊
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 သန္တာနာန် ပြတိ ပိတၖဏာံ မနာံသိ ဓရ္မ္မဇ္ဉာနံ ပြတျနာဇ္ဉာဂြာဟိဏၑ္စ ပရာဝရ္တ္တယိတုံ, ပြဘေား ပရမေၑွရသျ သေဝါရ္ထမ် ဧကာံ သဇ္ဇိတဇာတိံ ဝိဓာတုဉ္စ သ ဧလိယရူပါတ္မၑက္တိပြာပ္တသ္တသျာဂြေ ဂမိၐျတိ၊
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 တဒါ သိခရိယော ဒူတမဝါဒီတ် ကထမေတဒ် ဝေတ္သျာမိ? ယတောဟံ ဝၖဒ္ဓေါ မမ ဘာရျျာ စ ဝၖဒ္ဓါ၊
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 တတော ဒူတး ပြတျုဝါစ ပၑျေၑွရသျ သာက္ၐာဒွရ္တ္တီ ဇိဗြာယေလ္နာမာ ဒူတောဟံ တွယာ သဟ ကထာံ ဂဒိတုံ တုဘျမိမာံ ၑုဘဝါရ္တ္တာံ ဒါတုဉ္စ ပြေၐိတး၊
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 ကိန္တု မဒီယံ ဝါကျံ ကာလေ ဖလိၐျတိ တတ် တွယာ န ပြတီတမ် အတး ကာရဏာဒ် ယာဝဒေဝ တာနိ န သေတ္သျန္တိ တာဝတ် တွံ ဝက္တုံမၑက္တော မူကော ဘဝ၊
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 တဒါနီံ ယေ ယေ လောကား သိခရိယမပဲက္ၐန္တ တေ မဓျေမန္ဒိရံ တသျ ဗဟုဝိလမ္ဗာဒ် အာၑ္စရျျံ မေနိရေ၊
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 သ ဗဟိရာဂတော ယဒါ ကိမပိ ဝါကျံ ဝက္တုမၑက္တး သင်္ကေတံ ကၖတွာ နိးၑဗ္ဒသ္တသျော် တဒါ မဓျေမန္ဒိရံ ကသျစိဒ် ဒရ္ၑနံ တေန ပြာပ္တမ် ဣတိ သရွွေ ဗုဗုဓိရေ၊
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 အနန္တရံ တသျ သေဝနပရျျာယေ သမ္ပူရ္ဏေ သတိ သ နိဇဂေဟံ ဇဂါမ၊
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 ကတိပယဒိနေၐု ဂတေၐု တသျ ဘာရျျာ ဣလီၑေဝါ ဂရ္ဗ္ဘဝတီ ဗဘူဝ
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 ပၑ္စာတ် သာ ပဉ္စမာသာန် သံဂေါပျာကထယတ် လောကာနာံ သမက္ၐံ မမာပမာနံ ခဏ္ဍယိတုံ ပရမေၑွရော မယိ ဒၖၐ္ဋိံ ပါတယိတွာ ကရ္မ္မေဒၖၑံ ကၖတဝါန်၊
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 အပရဉ္စ တသျာ ဂရ္ဗ္ဘသျ ၐၐ္ဌေ မာသေ ဇာတေ ဂါလီလ္ပြဒေၑီယနာသရတ္ပုရေ
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 ဒါယူဒေါ ဝံၑီယာယ ယူၐဖ္နာမ္နေ ပုရုၐာယ ယာ မရိယမ္နာမကုမာရီ ဝါဂ္ဒတ္တာသီတ် တသျား သမီပံ ဇိဗြာယေလ် ဒူတ ဤၑွရေဏ ပြဟိတး၊
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 သ ဂတွာ ဇဂါဒ ဟေ ဤၑွရာနုဂၖဟီတကနျေ တဝ ၑုဘံ ဘူယာတ် ပြဘုး ပရမေၑွရသ္တဝ သဟာယောသ္တိ နာရီဏာံ မဓျေ တွမေဝ ဓနျာ၊
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 တဒါနီံ သာ တံ ဒၖၐ္ဋွာ တသျ ဝါကျတ ဥဒွိဇျ ကီဒၖၑံ ဘာၐဏမိဒမ် ဣတိ မနသာ စိန္တယာမာသ၊
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 တတော ဒူတော'ဝဒတ် ဟေ မရိယမ် ဘယံ မာကာရ္ၐီး, တွယိ ပရမေၑွရသျာနုဂြဟောသ္တိ၊
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 ပၑျ တွံ ဂရ္ဗ္ဘံ ဓၖတွာ ပုတြံ ပြသောၐျသေ တသျ နာမ ယီၑုရိတိ ကရိၐျသိ၊
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 သ မဟာန် ဘဝိၐျတိ တထာ သရွွေဘျး ၑြေၐ္ဌသျ ပုတြ ဣတိ ချာသျတိ; အပရံ ပြဘုး ပရမေၑွရသ္တသျ ပိတုရ္ဒာယူဒး သိံဟာသနံ တသ္မဲ ဒါသျတိ;
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 တထာ သ ယာကူဗော ဝံၑောပရိ သရွွဒါ ရာဇတွံ ကရိၐျတိ, တသျ ရာဇတွသျာန္တော န ဘဝိၐျတိ၊ (aiōn g165)
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn g165)
34 တဒါ မရိယမ် တံ ဒူတံ ဗဘာၐေ နာဟံ ပုရုၐသင်္ဂံ ကရောမိ တရှိ ကထမေတတ် သမ္ဘဝိၐျတိ?
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 တတော ဒူတော'ကထယတ် ပဝိတြ အာတ္မာ တွာမာၑြာယိၐျတိ တထာ သရွွၑြေၐ္ဌသျ ၑက္တိသ္တဝေါပရိ ဆာယာံ ကရိၐျတိ တတော ဟေတောသ္တဝ ဂရ္ဗ္ဘာဒ် ယး ပဝိတြဗာလကော ဇနိၐျတေ သ ဤၑွရပုတြ ဣတိ ချာတိံ ပြာပ္သျတိ၊
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 အပရဉ္စ ပၑျ တဝ ဇ္ဉာတိရိလီၑေဝါ ယာံ သရွွေ ဗန္ဓျာမဝဒန် ဣဒါနီံ သာ ဝါရ္ဒ္ဓကျေ သန္တာနမေကံ ဂရ္ဗ္ဘေ'ဓာရယတ် တသျ ၐၐ္ဌမာသောဘူတ်၊
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 ကိမပိ ကရ္မ္မ နာသာဓျမ် ဤၑွရသျ၊
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 တဒါ မရိယမ် ဇဂါဒ, ပၑျ ပြဘေရဟံ ဒါသီ မဟျံ တဝ ဝါကျာနုသာရေဏ သရွွမေတဒ် ဃဋတာမ်; အနနတရံ ဒူတသ္တသျား သမီပါတ် ပြတသ္ထေ၊
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 အထ ကတိပယဒိနာတ် ပရံ မရိယမ် တသ္မာတ် ပရွွတမယပြဒေၑီယယိဟူဒါယာ နဂရမေကံ ၑီဃြံ ဂတွာ
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 သိခရိယယာဇကသျ ဂၖဟံ ပြဝိၑျ တသျ ဇာယာမ် ဣလီၑေဝါံ သမ္ဗောဓျာဝဒတ်၊
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 တတော မရိယမး သမ္ဗောဓနဝါကျေ ဣလီၑေဝါယား ကရ္ဏယေား ပြဝိၐ္ဋမာတြေ သတိ တသျာ ဂရ္ဗ္ဘသ္ထဗာလကော နနရ္တ္တ၊ တတ ဣလီၑေဝါ ပဝိတြေဏာတ္မနာ ပရိပူရ္ဏာ သတီ
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 ပြောစ္စဲရ္ဂဒိတုမာရေဘေ, ယောၐိတာံ မဓျေ တွမေဝ ဓနျာ, တဝ ဂရ္ဗ္ဘသ္ထး ၑိၑုၑ္စ ဓနျး၊
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 တွံ ပြဘောရ္မာတာ, မမ နိဝေၑနေ တွယာ စရဏာဝရ္ပိတော်, မမာဒျ သော်ဘာဂျမေတတ်၊
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 ပၑျ တဝ ဝါကျေ မမ ကရ္ဏယေား ပြဝိၐ္ဋမာတြေ သတိ မမောဒရသ္ထး ၑိၑုရာနန္ဒာန် နနရ္တ္တ၊
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 ယာ သ္တြီ ဝျၑွသီတ် သာ ဓနျာ, ယတော ဟေတောသ္တာံ ပြတိ ပရမေၑွရောက္တံ ဝါကျံ သရွွံ သိဒ္ဓံ ဘဝိၐျတိ၊
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 တဒါနီံ မရိယမ် ဇဂါဒ၊ ဓနျဝါဒံ ပရေၑသျ ကရောတိ မာမကံ မနး၊
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 မမာတ္မာ တာရကေၑေ စ သမုလ္လာသံ ပြဂစ္ဆတိ၊
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 အကရောတ် သ ပြဘု ရ္ဒုၐ္ဋိံ သွဒါသျာ ဒုရ္ဂတိံ ပြတိ၊ ပၑျာဒျာရဘျ မာံ ဓနျာံ ဝက္ၐျန္တိ ပုရုၐား သဒါ၊
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 ယး သရွွၑက္တိမာန် ယသျ နာမာပိ စ ပဝိတြကံ၊ သ ဧဝ သုမဟတ္ကရ္မ္မ ကၖတဝါန် မန္နိမိတ္တကံ၊
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 ယေ ဗိဘျတိ ဇနာသ္တသ္မာတ် တေၐာံ သန္တာနပံက္တိၐု၊ အနုကမ္ပာ တဒီယာ စ သရွွဒဲဝ သုတိၐ္ဌတိ၊
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 သွဗာဟုဗလတသ္တေန ပြာကာၑျတ ပရာကြမး၊ မနးကုမန္တြဏာသာရ္ဒ္ဓံ ဝိကီရျျန္တေ'ဘိမာနိနး၊
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 သိံဟာသနဂတာလ္လောကာန် ဗလိနၑ္စာဝရောဟျ သး၊ ပဒေၐူစ္စေၐု လောကာံသ္တု က္ၐုဒြာန် သံသ္ထာပယတျပိ၊
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 က္ၐုဓိတာန် မာနဝါန် ဒြဝျဲရုတ္တမဲး ပရိတရ္ပျ သး၊ သကလာန် ဓနိနော လောကာန် ဝိသၖဇေဒ် ရိက္တဟသ္တကာန်၊
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 ဣဗြာဟီမိ စ တဒွံၑေ ယာ ဒယာသ္တိ သဒဲဝ တာံ၊ သ္မၖတွာ ပုရာ ပိတၖဏာံ နော ယထာ သာက္ၐာတ် ပြတိၑြုတံ၊ (aiōn g165)
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 ဣသြာယေလ္သေဝကသ္တေန တထောပကြိယတေ သွယံ။
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn g165)
56 အနန္တရံ မရိယမ် ပြာယေဏ မာသတြယမ် ဣလီၑေဝယာ သဟောၐိတွာ ဝျာဃုယျ နိဇနိဝေၑနံ ယယော်၊
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 တဒနန္တရမ် ဣလီၑေဝါယား ပြသဝကာလ ဥပသ္ထိတေ သတိ သာ ပုတြံ ပြာသောၐ္ဋ၊
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 တတး ပရမေၑွရသ္တသျာံ မဟာနုဂြဟံ ကၖတဝါန် ဧတတ် ၑြုတွာ သမီပဝါသိနး ကုဋုမ္ဗာၑ္စာဂတျ တယာ သဟ မုမုဒိရေ၊
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 တထာၐ္ဋမေ ဒိနေ တေ ဗာလကသျ တွစံ ဆေတ္တုမ် ဧတျ တသျ ပိတၖနာမာနုရူပံ တန္နာမ သိခရိယ ဣတိ ကရ္တ္တုမီၐုး၊
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 ကိန္တု တသျ မာတာကထယတ် တန္န, နာမာသျ ယောဟန် ဣတိ ကရ္တ္တဝျမ်၊
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 တဒါ တေ ဝျာဟရန် တဝ ဝံၑမဓျေ နာမေဒၖၑံ ကသျာပိ နာသ္တိ၊
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 တတး ပရံ တသျ ပိတရံ သိခရိယံ ပြတိ သင်္ကေတျ ပပြစ္ဆုး ၑိၑေား ကိံ နာမ ကာရိၐျတေ?
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 တတး သ ဖလကမေကံ ယာစိတွာ လိလေခ တသျ နာမ ယောဟန် ဘဝိၐျတိ၊ တသ္မာတ် သရွွေ အာၑ္စရျျံ မေနိရေ၊
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 တတ္က္ၐဏံ သိခရိယသျ ဇိဟွာဇာဍျေ'ပဂတေ သ မုခံ ဝျာဒါယ သ္ပၐ္ဋဝရ္ဏမုစ္စာရျျ ဤၑွရသျ ဂုဏာနုဝါဒံ စကာရ၊
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 တသ္မာစ္စတုရ္ဒိက္သ္ထား သမီပဝါသိလောကာ ဘီတာ ဧဝမေတား သရွွား ကထာ ယိဟူဒါယား ပရွွတမယပြဒေၑသျ သရွွတြ ပြစာရိတား၊
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 တသ္မာတ် ၑြောတာရော မနးသု သ္ထာပယိတွာ ကထယာမ္ဗဘူဝုး ကီဒၖၑောယံ ဗာလော ဘဝိၐျတိ? အထ ပရမေၑွရသ္တသျ သဟာယောဘူတ်၊
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 တဒါ ယောဟနး ပိတာ သိခရိယး ပဝိတြေဏာတ္မနာ ပရိပူရ္ဏး သန် ဧတာဒၖၑံ ဘဝိၐျဒွါကျံ ကထယာမာသ၊
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 ဣသြာယေလး ပြဘု ရျသ္တု သ ဓနျး ပရမေၑွရး၊ အနုဂၖဟျ နိဇာလ္လောကာန် သ ဧဝ ပရိမောစယေတ်၊
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 ဝိပက္ၐဇနဟသ္တေဘျော ယထာ မောစျာမဟေ ဝယံ၊ ယာဝဇ္ဇီဝဉ္စ ဓရ္မ္မေဏ သာရလျေန စ နိရ္ဘယား၊
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 သေဝါမဟဲ တမေဝဲကမ် ဧတတ္ကာရဏမေဝ စ၊ သွကီယံ သုပဝိတြဉ္စ သံသ္မၖတျ နိယမံ သဒါ၊
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn g165)
71 ကၖပယာ ပုရုၐာန် ပူရွွာန် နိကၐာရ္ထာတ္တု နး ပိတုး၊ ဣဗြာဟီမး သမီပေ ယံ ၑပထံ ကၖတဝါန် ပုရာ၊
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 တမေဝ သဖလံ ကရ္တ္တံ တထာ ၑတြုဂဏသျ စ၊ ၒတီယာကာရိဏၑ္စဲဝ ကရေဘျော ရက္ၐဏာယ နး၊
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 သၖၐ္ဋေး ပြထမတး သွီယဲး ပဝိတြဲ ရ္ဘာဝိဝါဒိဘိး၊ (aiōn g165)
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 ယထောက္တဝါန် တထာ သွသျ ဒါယူဒး သေဝကသျ တု၊
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 ဝံၑေ တြာတာရမေကံ သ သမုတ္ပာဒိတဝါန် သွယမ်၊
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 အတော ဟေ ဗာလက တွန္တု သရွွေဘျး ၑြေၐ္ဌ ဧဝ ယး၊ တသျဲဝ ဘာဝိဝါဒီတိ ပြဝိချာတော ဘဝိၐျသိ၊ အသ္မာကံ စရဏာန် က္ၐေမေ မာရ္ဂေ စာလယိတုံ သဒါ၊ ဧဝံ ဓွာန္တေ'ရ္ထတော မၖတျောၑ္ဆာယာယာံ ယေ တု မာနဝါး၊
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 ဥပဝိၐ္ဋာသ္တု တာနေဝ ပြကာၑယိတုမေဝ ဟိ၊ ကၖတွာ မဟာနုကမ္ပာံ ဟိ ယာမေဝ ပရမေၑွရး၊
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 ဦရ္ဒွွာတ် သူရျျမုဒါယျဲဝါသ္မဘျံ ပြာဒါတ္တု ဒရ္ၑနံ၊ တယာနုကမ္ပယာ သွသျ လောကာနာံ ပါပမောစနေ၊
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 ပရိတြာဏသျ တေဘျော ဟိ ဇ္ဉာနဝိၑြာဏနာယ စ၊ ပြဘော ရ္မာရ္ဂံ ပရိၐ္ကရ္တ္တုံ တသျာဂြာယီ ဘဝိၐျသိ။
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 အထ ဗာလကး ၑရီရေဏ ဗုဒ္ဓျာ စ ဝရ္ဒ္ဓိတုမာရေဘေ; အပရဉ္စ သ ဣသြာယေလော ဝံၑီယလောကာနာံ သမီပေ ယာဝန္န ပြကဋီဘူတသ္တာသ္တာဝတ် ပြာန္တရေ နျဝသတ်၊
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

< လူကး 1 >