< ယောဟနး 2 >

1 အနန္တရံ တြုတီယဒိဝသေ ဂါလီလ် ပြဒေၑိယေ ကာန္နာနာမ္နိ နဂရေ ဝိဝါဟ အာသီတ် တတြ စ ယီၑောရ္မာတာ တိၐ္ဌတ်၊
Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko,
2 တသ္မဲ ဝိဝါဟာယ ယီၑုသ္တသျ ၑိၐျာၑ္စ နိမန္တြိတာ အာသန်၊
ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo.
3 တဒနန္တရံ ဒြာက္ၐာရသသျ နျူနတွာဒ် ယီၑောရ္မာတာ တမဝဒတ် ဧတေၐာံ ဒြာက္ၐာရသော နာသ္တိ၊
Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”
4 တဒါ သ တာမဝေါစတ် ဟေ နာရိ မယာ သဟ တဝ ကိံ ကာရျျံ? မမ သမယ ဣဒါနီံ နောပတိၐ္ဌတိ၊
Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”
5 တတသ္တသျ မာတာ ဒါသာနဝေါစဒ် အယံ ယဒ် ဝဒတိ တဒေဝ ကုရုတ၊
Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”
6 တသ္မိန် သ္ထာနေ ယိဟူဒီယာနာံ ၑုစိတွကရဏဝျဝဟာရာနုသာရေဏာဎကဲကဇလဓရာဏိ ပါၐာဏမယာနိ ၐဍွၖဟတ္ပာတြာဏိအာသန်၊
Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.
7 တဒါ ယီၑုသ္တာန် သရွွကလၑာန် ဇလဲး ပူရယိတုံ တာနာဇ္ဉာပယတ်, တတသ္တေ သရွွာန် ကုမ္ဘာနာကရ္ဏံ ဇလဲး ပရျျပူရယန်၊
Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.
8 အထ တေဘျး ကိဉ္စိဒုတ္တာရျျ ဘောဇျာဓိပါတေးသမီပံ နေတုံ သ တာနာဒိၑတ်, တေ တဒနယန်၊
Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.” Iwo anachita momwemo.
9 အပရဉ္စ တဇ္ဇလံ ကထံ ဒြာက္ၐာရသော'ဘဝတ် တဇ္ဇလဝါဟကာဒါသာ ဇ္ဉာတုံ ၑက္တား ကိန္တု တဒ္ဘေါဇျာဓိပေါ ဇ္ဉာတုံ နာၑက္နောတ် တဒဝလိဟျ ဝရံ သံမ္ဗောဒျာဝဒတ,
Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali
10 လောကား ပြထမံ ဥတ္တမဒြာက္ၐာရသံ ဒဒတိ တၐု ယထေၐ္ဋံ ပိတဝတ္သု တသ္မာ ကိဉ္စိဒနုတ္တမဉ္စ ဒဒတိ ကိန္တု တွမိဒါနီံ ယာဝတ် ဥတ္တမဒြာက္ၐာရသံ သ္ထာပယသိ၊
ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”
11 ဣတ္ထံ ယီၑုရ္ဂာလီလပြဒေၑေ အာၑ္စရျျကာရ္မ္မ ပြာရမ္ဘ နိဇမဟိမာနံ ပြာကာၑယတ် တတး ၑိၐျာသ္တသ္မိန် ဝျၑွသန်၊
Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.
12 တတး ပရမ် သ နိဇမာတြုဘြာတြုသ္ၑိၐျဲး သာရ္ဒ္ဓ္ံ ကဖရ္နာဟူမမ် အာဂမတ် ကိန္တု တတြ ဗဟူဒိနာနိ အာတိၐ္ဌတ်၊
Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.
13 တဒနန္တရံ ယိဟူဒိယာနာံ နိသ္တာရောတ္သဝေ နိကဋမာဂတေ ယီၑု ရျိရူၑာလမ် နဂရမ် အာဂစ္ဆတ်၊
Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu.
14 တတော မန္ဒိရသျ မဓျေ ဂေါမေၐပါရာဝတဝိကြယိဏော ဝါဏိဇက္ၐ္စောပဝိၐ္ဋာန် ဝိလောကျ
Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo.
15 ရဇ္ဇုဘိး ကၑာံ နိရ္မ္မာယ သရွွဂေါမေၐာဒိဘိး သာရ္ဒ္ဓံ တာန် မန္ဒိရာဒ် ဒူရီကၖတဝါန်၊
Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo.
16 ဝဏိဇာံ မုဒြာဒိ ဝိကီရျျ အာသနာနိ နျူဗ္ဇီကၖတျ ပါရာဝတဝိကြယိဘျော'ကထယဒ် အသ္မာတ် သ္ထာနာတ် သရွာဏျေတာနိ နယတ, မမ ပိတုဂၖဟံ ဝါဏိဇျဂၖဟံ မာ ကာရ္ၐ္ဋ၊
Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”
17 တသ္မာတ် တန္မန္ဒိရာရ္ထ ဥဒျောဂေါ ယသ္တု သ ဂြသတီဝ မာမ်၊ ဣမာံ ၑာသ္တြီယလိပိံ ၑိၐျားသမသ္မရန်၊
Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”
18 တတး ပရမ် ယိဟူဒီယလောကာ ယီၐိမဝဒန် တဝမိဒၖၑကရ္မ္မကရဏာတ် ကိံ စိဟ္နမသ္မာန် ဒရ္ၑယသိ?
Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”
19 တတော ယီၑုသ္တာနဝေါစဒ် ယုၐ္မာဘိရေ တသ္မိန် မန္ဒိရေ နာၑိတေ ဒိနတြယမဓျေ'ဟံ တဒ် ဥတ္ထာပယိၐျာမိ၊
Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”
20 တဒါ ယိဟူဒိယာ ဝျာဟာရ္ၐုး, ဧတသျ မန္ဒိရသ နိရ္မ္မာဏေန ၐဋ္စတွာရိံၑဒ် ဝတ္သရာ ဂတား, တွံ ကိံ ဒိနတြယမဓျေ တဒ် ဥတ္ထာပယိၐျသိ?
Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?”
21 ကိန္တု သ နိဇဒေဟရူပမန္ဒိရေ ကထာမိမာံ ကထိတဝါန်၊
Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake.
22 သ ယဒေတာဒၖၑံ ဂဒိတဝါန် တစ္ဆိၐျား ၑ္မၑာနာတ် တဒီယောတ္ထာနေ သတိ သ္မၖတွာ ဓရ္မ္မဂြန္ထေ ယီၑုနောက္တကထာယာံ စ ဝျၑွသိၐုး၊
Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.
23 အနန္တရံ နိသ္တာရောတ္သဝသျ ဘောဇျသမယေ ယိရူၑာလမ် နဂရေ တတ္ကြုတာၑ္စရျျကရ္မ္မာဏိ ဝိလောကျ ဗဟုဘိသ္တသျ နာမနိ ဝိၑွသိတံ၊
Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake.
24 ကိန္တု သ တေၐာံ ကရေၐု သွံ န သမရ္ပယတ်, ယတး သ သရွွာနဝဲတ်၊
Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse.
25 သ မာနဝေၐု ကသျစိတ် ပြမာဏံ နာပေက္ၐတ ယတော မနုဇာနာံ မဓျေ ယဒျဒသ္တိ တတ္တတ် သောဇာနာတ်၊
Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.

< ယောဟနး 2 >