< ယောဟနး 13 >

1 နိသ္တာရောတ္သဝသျ ကိဉ္စိတ္ကာလာတ် ပူရွွံ ပၖထိဝျား ပိတုး သမီပဂမနသျ သမယး သန္နိကရ္ၐောဘူဒ် ဣတိ ဇ္ဉာတွာ ယီၑုရာပြထမာဒ် ယေၐု ဇဂတ္ပြဝါသိၐွာတ္မီယလောကေၐ ပြေမ ကရောတိ သ္မ တေၐု ၑေၐံ ယာဝတ် ပြေမ ကၖတဝါန်၊
Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.
2 ပိတာ တသျ ဟသ္တေ သရွွံ သမရ္ပိတဝါန် သွယမ် ဤၑွရသျ သမီပါဒ် အာဂစ္ဆဒ် ဤၑွရသျ သမီပံ ယာသျတိ စ, သရွွာဏျေတာနိ ဇ္ဉာတွာ ရဇနျာံ ဘောဇနေ သမ္ပူရ္ဏေ သတိ,
Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu.
3 ယဒါ ၑဲတာန် တံ ပရဟသ္တေၐု သမရ္ပယိတုံ ၑိမောနး ပုတြသျ ဤၐ္ကာရိယောတိယသျ ယိဟူဒါ အန္တးကရဏေ ကုပြဝၖတ္တိံ သမာရ္ပယတ်,
Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo;
4 တဒါ ယီၑု ရ္ဘောဇနာသနာဒ် ဥတ္ထာယ ဂါတြဝသ္တြံ မောစယိတွာ ဂါတြမာရ္ဇနဝသ္တြံ ဂၖဟီတွာ တေန သွကဋိမ် အဗဓ္နာတ်,
anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake.
5 ပၑ္စာဒ် ဧကပါတြေ ဇလမ် အဘိၐိစျ ၑိၐျာဏာံ ပါဒါန် ပြက္ၐာလျ တေန ကဋိဗဒ္ဓဂါတြမာရ္ဇနဝါသသာ မာရ္ၐ္ဋုံ ပြာရဘတ၊
Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.
6 တတး ၑိမောန္ပိတရသျ သမီပမာဂတေ သ ဥက္တဝါန် ဟေ ပြဘော ဘဝါန် ကိံ မမ ပါဒေါ် ပြက္ၐာလယိၐျတိ?
Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”
7 ယီၑုရုဒိတဝါန် အဟံ ယတ် ကရောမိ တတ် သမ္ပြတိ န ဇာနာသိ ကိန္တု ပၑ္စာဇ် ဇ္ဉာသျသိ၊
Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”
8 တတး ပိတရး ကထိတဝါန် ဘဝါန် ကဒါပိ မမ ပါဒေါ် န ပြက္ၐာလယိၐျတိ၊ ယီၑုရကထယဒ် ယဒိ တွာံ န ပြက္ၐာလယေ တရှိ မယိ တဝ ကောပျံၑော နာသ္တိ၊ (aiōn g165)
Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.” Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.” (aiōn g165)
9 တဒါ ၑိမောန္ပိတရး ကထိတဝါန် ဟေ ပြဘော တရှိ ကေဝလပါဒေါ် န, မမ ဟသ္တော် ၑိရၑ္စ ပြက္ၐာလယတု၊
Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”
10 တတော ယီၑုရဝဒဒ် ယော ဇနော ဓော်တသ္တသျ သရွွာင်္ဂပရိၐ္ကၖတတွာတ် ပါဒေါ် ဝိနာနျာင်္ဂသျ ပြက္ၐာလနာပေက္ၐာ နာသ္တိ၊ ယူယံ ပရိၐ္ကၖတာ ဣတိ သတျံ ကိန္တု န သရွွေ,
Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.”
11 ယတော ယော ဇနသ္တံ ပရကရေၐု သမရ္ပယိၐျတိ တံ သ ဇ္ဉာတဝါန; အတဧဝ ယူယံ သရွွေ န ပရိၐ္ကၖတာ ဣမာံ ကထာံ ကထိတဝါန်၊
Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.
12 ဣတ္ထံ ယီၑုသ္တေၐာံ ပါဒါန် ပြက္ၐာလျ ဝသ္တြံ ပရိဓာယာသနေ သမုပဝိၑျ ကထိတဝါန် အဟံ ယုၐ္မာန် ပြတိ ကိံ ကရ္မ္မာကာရ္ၐံ ဇာနီထ?
Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu?
13 ယူယံ မာံ ဂုရုံ ပြဘုဉ္စ ဝဒထ တတ် သတျမေဝ ဝဒထ ယတောဟံ သဧဝ ဘဝါမိ၊
Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili.
14 ယဒျဟံ ပြဘု ရ္ဂုရုၑ္စ သန် ယုၐ္မာကံ ပါဒါန် ပြက္ၐာလိတဝါန် တရှိ ယုၐ္မာကမပိ ပရသ္ပရံ ပါဒပြက္ၐာလနမ် ဥစိတမ်၊
Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu.
15 အဟံ ယုၐ္မာန် ပြတိ ယထာ ဝျဝါဟရံ ယုၐ္မာန် တထာ ဝျဝဟရ္တ္တုမ် ဧကံ ပန္ထာနံ ဒရ္ၑိတဝါန်၊
Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira.
16 အဟံ ယုၐ္မာနတိယထာရ္ထံ ဝဒါမိ, ပြဘော ရ္ဒာသော န မဟာန် ပြေရကာစ္စ ပြေရိတော န မဟာန်၊
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma.
17 ဣမာံ ကထာံ ဝိဒိတွာ ယဒိ တဒနုသာရတး ကရ္မ္မာဏိ ကုရုထ တရှိ ယူယံ ဓနျာ ဘဝိၐျထ၊
Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.
18 သရွွေၐု ယုၐ္မာသု ကထာမိမာံ ကထယာမိ ဣတိ န, ယေ မမ မနောနီတာသ္တာနဟံ ဇာနာမိ, ကိန္တု မမ ဘက္ၐျာဏိ ယော ဘုင်္က္တေ မတ္ပြာဏပြာတိကူလျတး၊ ဥတ္ထာပယတိ ပါဒသျ မူလံ သ ဧၐ မာနဝး၊ ယဒေတဒ် ဓရ္မ္မပုသ္တကသျ ဝစနံ တဒနုသာရေဏာဝၑျံ ဃဋိၐျတေ၊
“Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’
19 အဟံ သ ဇန ဣတျတြ ယထာ ယုၐ္မာကံ ဝိၑွာသော ဇာယတေ တဒရ္ထံ ဧတာဒၖၑဃဋနာတ် ပူရွွမ် အဟမိဒါနီံ ယုၐ္မဘျမကထယမ်၊
“Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine.
20 အဟံ ယုၐ္မာနတီဝ ယထာရ္ထံ ဝဒါမိ, မယာ ပြေရိတံ ဇနံ ယော ဂၖဟ္လာတိ သ မာမေဝ ဂၖဟ္လာတိ ယၑ္စ မာံ ဂၖဟ္လာတိ သ မတ္ပြေရကံ ဂၖဟ္လာတိ၊
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”
21 ဧတာံ ကထာံ ကထယိတွာ ယီၑု ရ္ဒုးခီ သန် ပြမာဏံ ဒတ္တွာ ကထိတဝါန် အဟံ ယုၐ္မာနတိယထာရ္ထံ ဝဒါမိ ယုၐ္မာကမ် ဧကော ဇနော မာံ ပရကရေၐု သမရ္ပယိၐျတိ၊
Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”
22 တတး သ ကမုဒ္ဒိၑျ ကထာမေတာံ ကထိတဝါန် ဣတျတြ သန္ဒိဂ္ဓား ၑိၐျား ပရသ္ပရံ မုခမာလောကယိတုံ ပြာရဘန္တ၊
Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani.
23 တသ္မိန် သမယေ ယီၑု ရျသ္မိန် အပြီယတ သ ၑိၐျသ္တသျ ဝက္ၐးသ္ထလမ် အဝါလမ္ဗတ၊
Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake.
24 ၑိမောန္ပိတရသ္တံ သင်္ကေတေနာဝဒတ်, အယံ ကမုဒ္ဒိၑျ ကထာမေတာမ် ကထယတီတိ ပၖစ္ဆ၊
Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”
25 တဒါ သ ယီၑော ရွက္ၐးသ္ထလမ် အဝလမ္ဗျ ပၖၐ္ဌဝါန်, ဟေ ပြဘော သ ဇနး ကး?
Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”
26 တတော ယီၑုး ပြတျဝဒဒ် ဧကခဏ္ဍံ ပူပံ မဇ္ဇယိတွာ ယသ္မဲ ဒါသျာမိ သဧဝ သး; ပၑ္စာတ် ပူပခဏ္ဍမေကံ မဇ္ဇယိတွာ ၑိမောနး ပုတြာယ ဤၐ္ကရိယောတီယာယ ယိဟူဒဲ ဒတ္တဝါန်၊
Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni.
27 တသ္မိန် ဒတ္တေ သတိ ၑဲတာန် တမာၑြယတ်; တဒါ ယီၑုသ္တမ် အဝဒတ် တွံ ယတ် ကရိၐျသိ တတ် က္ၐိပြံ ကုရု၊
Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye. Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.”
28 ကိန္တု သ ယေနာၑယေန တာံ ကထာမကထာယတ် တမ် ဥပဝိၐ္ဋလောကာနာံ ကောပိ နာဗုဓျတ;
Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye.
29 ကိန္တု ယိဟူဒါး သမီပေ မုဒြာသမ္ပုဋကသ္ထိတေး ကေစိဒ် ဣတ္ထမ် အဗုဓျန္တ ပါရွွဏာသာဒနာရ္ထံ ကိမပိ ဒြဝျံ ကြေတုံ ဝါ ဒရိဒြေဘျး ကိဉ္စိဒ် ဝိတရိတုံ ကထိတဝါန်၊
Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka.
30 တဒါ ပူပခဏ္ဍဂြဟဏာတ် ပရံ သ တူရ္ဏံ ဗဟိရဂစ္ဆတ်; ရာတြိၑ္စ သမုပသျိတာ၊
Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.
31 ယိဟူဒေ ဗဟိရ္ဂတေ ယီၑုရကထယဒ် ဣဒါနီံ မာနဝသုတသျ မဟိမာ ပြကာၑတေ တေနေၑွရသျာပိ မဟိမာ ပြကာၑတေ၊
Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso.
32 ယဒိ တေနေၑွရသျ မဟိမာ ပြကာၑတေ တရှီၑွရောပိ သွေန တသျ မဟိမာနံ ပြကာၑယိၐျတိ တူရ္ဏမေဝ ပြကာၑယိၐျတိ၊
Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.
33 ဟေ ဝတ္သာ အဟံ ယုၐ္မာဘိး သာရ္ဒ္ဓံ ကိဉ္စိတ္ကာလမာတြမ် အာသေ, တတး ပရံ မာံ မၖဂယိၐျဓွေ ကိန္တွဟံ ယတ္သ္ထာနံ ယာမိ တတ္သ္ထာနံ ယူယံ ဂန္တုံ န ၑက္ၐျထ, ယာမိမာံ ကထာံ ယိဟူဒီယေဘျး ကထိတဝါန် တထာဓုနာ ယုၐ္မဘျမပိ ကထယာမိ၊
“Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.
34 ယူယံ ပရသ္ပရံ ပြီယဓွမ် အဟံ ယုၐ္မာသု ယထာ ပြီယေ ယူယမပိ ပရသ္ပရမ် တထဲဝ ပြီယဓွံ, ယုၐ္မာန် ဣမာံ နဝီနာမ် အာဇ္ဉာမ် အာဒိၑာမိ၊
“Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake.
35 တေနဲဝ ယဒိ ပရသ္ပရံ ပြီယဓွေ တရှိ လက္ၐဏေနာနေန ယူယံ မမ ၑိၐျာ ဣတိ သရွွေ ဇ္ဉာတုံ ၑက္ၐျန္တိ၊
Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”
36 ၑိမောနပိတရး ပၖၐ္ဌဝါန် ဟေ ပြဘော ဘဝါန် ကုတြ ယာသျတိ? တတော ယီၑုး ပြတျဝဒတ်, အဟံ ယတ္သ္ထာနံ ယာမိ တတ္သ္ထာနံ သာမ္ပြတံ မမ ပၑ္စာဒ် ဂန္တုံ န ၑက္နောၐိ ကိန္တု ပၑ္စာဒ် ဂမိၐျသိ၊
Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”
37 တဒါ ပိတရး ပြတျုဒိတဝါန်, ဟေ ပြဘော သာမ္ပြတံ ကုတော ဟေတောသ္တဝ ပၑ္စာဒ် ဂန္တုံ န ၑက္နောမိ? တွဒရ္ထံ ပြာဏာန် ဒါတုံ ၑက္နောမိ၊
Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”
38 တတော ယီၑုး ပြတျုက္တဝါန် မန္နိမိတ္တံ ကိံ ပြာဏာန် ဒါတုံ ၑက္နောၐိ? တွာမဟံ ယထာရ္ထံ ဝဒါမိ, ကုက္ကုဋရဝဏာတ် ပူရွွံ တွံ တြိ ရ္မာမ် အပဟ္နောၐျသေ၊
Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”

< ယောဟနး 13 >