< ဣဗြိဏး 8 >

1 ကထျမာနာနာံ ဝါကျာနာံ သာရော'ယမ် အသ္မာကမ် ဧတာဒၖၑ ဧကော မဟာယာဇကော'သ္တိ ယး သွရ္ဂေ မဟာမဟိမ္နး သိံဟာသနသျ ဒက္ၐိဏပါရ္ၑွော သမုပဝိၐ္ဋဝါန္
Fundo yayikulu pa zimene tikunenazi ndi iyi: Tili naye ife Mkulu wa ansembe, amene anakhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu Waulemerero kumwamba.
2 ယစ္စ ဒူၐျံ န မနုဇဲး ကိန္တွီၑွရေဏ သ္ထာပိတံ တသျ သတျဒူၐျသျ ပဝိတြဝသ္တူနာဉ္စ သေဝကး သ ဘဝတိ၊
Ndipo akutumikira mʼmalo opatulika, mu Tenti yeniyeni yoyikidwa ndi Ambuye, osati ndi munthu.
3 ယတ ဧကဲကော မဟာယာဇကော နဲဝေဒျာနာံ ဗလီနာဉ္စ ဒါနေ နိယုဇျတေ, အတော ဟေတောရေတသျာပိ ကိဉ္စိဒ် ဥတ္သရ္ဇနီယံ ဝိဒျတ ဣတျာဝၑျကံ၊
Mkulu wa ansembe aliyense amasankhidwa kuti azipereka mphatso ndi nsembe kwa Mulungu, ndipo kunali koyenera kuti wansembe wathunso akhale nʼkanthu kopereka.
4 ကိဉ္စ သ ယဒိ ပၖထိဝျာမ် အသ္ထာသျတ် တရှိ ယာဇကော နာဘဝိၐျတ်, ယတော ယေ ဝျဝသ္ထာနုသာရာတ် နဲဝေဒျာနိ ဒဒတျေတာဒၖၑာ ယာဇကာ ဝိဒျန္တေ၊
Ngati iye akanakhala pa dziko lapansi, sakanakhala wansembe pakuti alipo kale anthu amene amapereka mphatso zolembedwa mʼMalamulo.
5 တေ တု သွရ္ဂီယဝသ္တူနာံ ဒၖၐ္ဋာန္တေန ဆာယယာ စ သေဝါမနုတိၐ္ဌန္တိ ယတော မူသသိ ဒူၐျံ သာဓယိတုမ် ဥဒျတေ သတီၑွရသ္တဒေဝ တမာဒိၐ္ဋဝါန် ဖလတး သ တမုက္တဝါန်, ယထာ, "အဝဓေဟိ ဂိရော် တွာံ ယဒျန္နိဒရ္ၑနံ ဒရ္ၑိတံ တဒွတ် သရွွာဏိ တွယာ ကြိယန္တာံ၊ "
Iwo amatumikira pamalo opatulika amene ndi chithunzi ndi chifanizo cha zimene zili kumwamba. Ichi ndi chifukwa chake Mose anachenjezedwa pamene anali pafupi kumanga Tenti: “Uwonetsetse kuti wapanga zonse monga momwe ndikukuonetsera pa phiri pano.”
6 ကိန္တွိဒါနီမ် အသော် တသ္မာတ် ၑြေၐ္ဌံ သေဝကပဒံ ပြာပ္တဝါန် ယတး သ ၑြေၐ္ဌပြတိဇ္ဉာဘိး သ္ထာပိတသျ ၑြေၐ္ဌနိယမသျ မဓျသ္ထော'ဘဝတ်၊
Koma Yesu analandira utumiki wopambana kuposa wawo monga Iyenso ali Nkhoswe ya pangano lopambana kuposa lakale lija, chifukwa pangano latsopano lakhazikika pa malonjezano opambana kwambiri.
7 သ ပြထမော နိယမော ယဒိ နိရ္ဒ္ဒေါၐော'ဘဝိၐျတ တရှိ ဒွိတီယသျ နိယမသျ ကိမပိ ပြယောဇနံ နာဘဝိၐျတ်၊
Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake.
8 ကိန္တု သ ဒေါၐမာရောပယန် တေဘျး ကထယတိ, ယထာ, "ပရမေၑွရ ဣဒံ ဘာၐတေ ပၑျ ယသ္မိန် သမယေ'ဟမ် ဣသြာယေလဝံၑေန ယိဟူဒါဝံၑေန စ သာရ္ဒ္ဓမ် ဧကံ နဝီနံ နိယမံ သ္ထိရီကရိၐျာမျေတာဒၖၑး သမယ အာယာတိ၊
Koma Mulungu anapeza zolakwika pakati pa anthu ndipo anati, “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
9 ပရမေၑွရော'ပရမပိ ကထယတိ တေၐာံ ပူရွွပုရုၐာဏာံ မိသရဒေၑာဒ် အာနယနာရ္ထံ ယသ္မိန် ဒိနေ'ဟံ တေၐာံ ကရံ ဓၖတွာ တဲး သဟ နိယမံ သ္ထိရီကၖတဝါန် တဒ္ဒိနသျ နိယမာနုသာရေဏ နဟိ ယတသ္တဲ ရ္မမ နိယမေ လင်္ဃိတေ'ဟံ တာန် ပြတိ စိန္တာံ နာကရဝံ၊
Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo, pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto chifukwa iwo sanasunge pangano langa lija ndipo Ine sindinawasamalire, akutero Ambuye.
10 ကိန္တု ပရမေၑွရး ကထယတိ တဒ္ဒိနာတ် ပရမဟံ ဣသြာယေလဝံၑီယဲး သာရ္ဒ္ဓမ် ဣမံ နိယမံ သ္ထိရီကရိၐျာမိ, တေၐာံ စိတ္တေ မမ ဝိဓီန် သ္ထာပယိၐျာမိ တေၐာံ ဟၖတ္ပတြေ စ တာန် လေခိၐျာမိ, အပရမဟံ တေၐာမ် ဤၑွရော ဘဝိၐျာမိ တေ စ မမ လောကာ ဘဝိၐျန္တိ၊
Tsono ili ndi pangano ndidzapangane ndi nyumba ya Israeli: Atapita masiku amenewa, akutero Ambuye, Ine ndidzayika malamulo anga mʼmaganizo mwawo, ndi kulemba mʼmitima mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
11 အပရံ တွံ ပရမေၑွရံ ဇာနီဟီတိဝါကျေန တေၐာမေကဲကော ဇနး သွံ သွံ သမီပဝါသိနံ ဘြာတရဉ္စ ပုန ရ္န ၑိက္ၐယိၐျတိ ယတ အာက္ၐုဒြာတ် မဟာန္တံ ယာဝတ် သရွွေ မာံ ဇ္ဉာသျန္တိ၊
Sipadzafunikanso wina kuti aphunzitse mnzake, kapena munthu kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, udziwe Ambuye chifukwa onse adzandidziwa, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu.
12 ယတော ဟေတောရဟံ တေၐာမ် အဓရ္မ္မာန် က္ၐမိၐျေ တေၐာံ ပါပါနျပရာဓာံၑ္စ ပုနး ကဒါပိ န သ္မရိၐျာမိ၊ "
Pakuti Ine ndidzawakhululukira zoyipa zawo, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
13 အနေန တံ နိယမံ နူတနံ ဂဒိတွာ သ ပြထမံ နိယမံ ပုရာတနီကၖတဝါန်; ယစ္စ ပုရာတနံ ဇီရ္ဏာဉ္စ ဇာတံ တသျ လောပေါ နိကဋော 'ဘဝတ်၊
Ponena kuti, pangano “latsopano” Mulungu wapanga pangano loyamba lija kukhala lotha ntchito, ndipo chilichonse chimene chayamba kutha ntchito ndi kukalamba, chili pafupi kuchokeratu.

< ဣဗြိဏး 8 >