< ဣဗြိဏး 3 >

1 ဟေ သွရ္ဂီယသျာဟွာနသျ သဟဘာဂိနး ပဝိတြဘြာတရး, အသ္မာကံ ဓရ္မ္မပြတိဇ္ဉာယာ ဒူတော'ဂြသရၑ္စ ယော ယီၑုသ္တမ် အာလောစဓွံ၊
Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza.
2 မူသာ ယဒွတ် တသျ သရွွပရိဝါရမဓျေ ဝိၑွာသျ အာသီတ်, တဒွတ် အယမပိ သွနိယောဇကသျ သမီပေ ဝိၑွာသျော ဘဝတိ၊
Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu.
3 ပရိဝါရာစ္စ ယဒွတ် တတ္သ္ထာပယိတုရဓိကံ ဂေါ်ရဝံ ဘဝတိ တဒွတ် မူသသော'ယံ ဗဟုတရဂေါ်ရဝသျ ယောဂျော ဘဝတိ၊
Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo.
4 ဧကဲကသျ နိဝေၑနသျ ပရိဇနာနာံ သ္ထာပယိတာ ကၑ္စိဒ် ဝိဒျတေ ယၑ္စ သရွွသ္ထာပယိတာ သ ဤၑွရ ဧဝ၊
Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu.
5 မူသာၑ္စ ဝက္ၐျမာဏာနာံ သာက္ၐီ ဘၖတျ ဣဝ တသျ သရွွပရိဇနမဓျေ ဝိၑွာသျော'ဘဝတ် ကိန္တု ခြီၐ္ဋသ္တသျ ပရိဇနာနာမဓျက္ၐ ဣဝ၊
Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo.
6 ဝယံ တု ယဒိ ဝိၑွာသသျောတ္သာဟံ ၑ္လာဃနဉ္စ ၑေၐံ ယာဝဒ် ဓာရယာမသ္တရှိ တသျ ပရိဇနာ ဘဝါမး၊
Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.
7 အတော ဟေတေား ပဝိတြေဏာတ္မနာ ယဒွတ် ကထိတံ, တဒွတ်, "အဒျ ယူယံ ကထာံ တသျ ယဒိ သံၑြောတုမိစ္ဆထ၊
Tsono monga Mzimu Woyera akuti, “Lero mukamva mawu ake,
8 တရှိ ပုရာ ပရီက္ၐာယာ ဒိနေ ပြာန္တရမဓျတး၊ မဒါဇ္ဉာနိဂြဟသ္ထာနေ ယုၐ္မာဘိသ္တု ကၖတံ ယထာ၊ တထာ မာ ကုရုတေဒါနီံ ကဌိနာနိ မနာံသိ ဝး၊
musawumitse mitima yanu ngati munachitira pamene munawukira, pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.
9 ယုၐ္မာကံ ပိတရသ္တတြ မတ္ပရီက္ၐာမ် အကုရွွတ၊ ကုရွွဒ္ဘိ ရ္မေ'နုသန္ဓာနံ တဲရဒၖၑျန္တ မတ္ကြိယား၊ စတွာရိံၑတ္သမာ ယာဝတ် ကြုဒ္ဓွာဟန္တု တဒနွယေ၊
Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa, ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.
10 အဝါဒိၐမ် ဣမေ လောကာ ဘြာန္တာန္တးကရဏား သဒါ၊ မာမကီနာနိ ဝရ္တ္မာနိ ပရိဇာနန္တိ နော ဣမေ၊
Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo, ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera, ndipo iwo sadziwa njira zanga.’
11 ဣတိ ဟေတောရဟံ ကောပါတ် ၑပထံ ကၖတဝါန် ဣမံ၊ ပြေဝေက္ၐျတေ ဇနဲရေတဲ ရ္န ဝိၑြာမသ္ထလံ မမ။ "
Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti, ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’”
12 ဟေ ဘြာတရး သာဝဓာနာ ဘဝတ, အမရေၑွရာတ် နိဝရ္တ္တကော ယော'ဝိၑွာသသ္တဒျုက္တံ ဒုၐ္ဋာန္တးကရဏံ ယုၐ္မာကံ ကသျာပိ န ဘဝတု၊
Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo.
13 ကိန္တု ယာဝဒ် အဒျနာမာ သမယော ဝိဒျတေ တာဝဒ် ယုၐ္မန္မဓျေ ကော'ပိ ပါပသျ ဝဉ္စနယာ ယတ် ကဌောရီကၖတော န ဘဝေတ် တဒရ္ထံ ပြတိဒိနံ ပရသ္ပရမ် ဥပဒိၑတ၊
Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo.
14 ယတော ဝယံ ခြီၐ္ဋသျာံၑိနော ဇာတား ကိန္တု ပြထမဝိၑွာသသျ ဒၖဎတွမ် အသ္မာဘိး ၑေၐံ ယာဝဒ် အမောဃံ ဓာရယိတဝျံ၊
Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi.
15 အဒျ ယူယံ ကထာံ တသျ ယဒိ သံၑြောတုမိစ္ဆထ, တရှျာဇ္ဉာလင်္ဃနသ္ထာနေ ယုၐ္မာဘိသ္တု ကၖတံ ယထာ, တထာ မာ ကုရုတေဒါနီံ ကဌိနာနိ မနာံသိ ဝ ဣတိ တေန ယဒုက္တံ,
Monga kunanenedwa kuti, “Lero ngati mumva mawu ake, musawumitse mitima yanu ngati momwe munachitira pamene munawukira.”
16 တဒနုသာရာဒ် ယေ ၑြုတွာ တသျ ကထာံ န ဂၖဟီတဝန္တသ္တေ ကေ? ကိံ မူသသာ မိသရဒေၑာဒ် အာဂတား သရွွေ လောကာ နဟိ?
Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto?
17 ကေဘျော ဝါ သ စတွာရိံၑဒွရ္ၐာဏိ ယာဝဒ် အကြုဓျတ်? ပါပံ ကုရွွတာံ ယေၐာံ ကုဏပါး ပြာန္တရေ 'ပတန် ကိံ တေဘျော နဟိ?
Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja?
18 ပြဝေက္ၐျတေ ဇနဲရေတဲ ရ္န ဝိၑြာမသ္ထလံ မမေတိ ၑပထး ကေၐာံ ဝိရုဒ္ဓံ တေနာကာရိ? ကိမ် အဝိၑွာသိနာံ ဝိရုဒ္ဓံ နဟိ?
Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja.
19 အတသ္တေ တတ် သ္ထာနံ ပြဝေၐ္ဋုမ် အဝိၑွာသာတ် နာၑက္နုဝန် ဣတိ ဝယံ ဝီက္ၐာမဟေ၊
Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

< ဣဗြိဏး 3 >