< ဂါလာတိနး 1 >

1 မနုၐျေဘျော နဟိ မနုၐျဲရပိ နဟိ ကိန္တု ယီၑုခြီၐ္ဋေန မၖတဂဏမဓျာတ် တသျောတ္ထာပယိတြာ ပိတြေၑွရေဏ စ ပြေရိတော ယော'ဟံ ပေါ်လး သော'ဟံ
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 မတ္သဟဝရ္တ္တိနော ဘြာတရၑ္စ ဝယံ ဂါလာတီယဒေၑသ္ထား သမိတီး ပြတိ ပတြံ လိခါမး၊
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 ပိတြေၑွရေဏာသ္မာံက ပြဘုနာ ယီၑုနာ ခြီၐ္ဋေန စ ယုၐ္မဘျမ် အနုဂြဟး ၑာန္တိၑ္စ ဒီယတာံ၊
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 အသ္မာကံ တာတေၑွရေသျေစ္ဆာနုသာရေဏ ဝရ္တ္တမာနာတ် ကုတ္သိတသံသာရာဒ် အသ္မာန် နိသ္တာရယိတုံ ယော (aiōn g165)
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
5 ယီၑုရသ္မာကံ ပါပဟေတောရာတ္မောတ္သရ္ဂံ ကၖတဝါန် သ သရွွဒါ ဓနျော ဘူယာတ်၊ တထာသ္တု၊ (aiōn g165)
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
6 ခြီၐ္ဋသျာနုဂြဟေဏ ယော ယုၐ္မာန် အာဟူတဝါန် တသ္မာန္နိဝၖတျ ယူယမ် အတိတူရ္ဏမ် အနျံ သုသံဝါဒမ် အနွဝရ္တ္တတ တတြာဟံ ဝိသ္မယံ မနျေ၊
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 သော'နျသုသံဝါဒး သုသံဝါဒေါ နဟိ ကိန္တု ကေစိတ် မာနဝါ ယုၐ္မာန် စဉ္စလီကုရွွန္တိ ခြီၐ္ဋီယသုသံဝါဒသျ ဝိပရျျယံ ကရ္တ္တုံ စေၐ္ဋန္တေ စ၊
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 ယုၐ္မာကံ သန္နိဓော် ယး သုသံဝါဒေါ'သ္မာဘိ ရ္ဃောၐိတသ္တသ္မာဒ် အနျး သုသံဝါဒေါ'သ္မာကံ သွရ္ဂီယဒူတာနာံ ဝါ မဓျေ ကေနစိဒ် ယဒိ ဃောၐျတေ တရှိ သ ၑပ္တော ဘဝတု၊
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 ပူရွွံ ယဒွဒ် အကထယာမ, ဣဒါနီမဟံ ပုနသ္တဒွတ် ကထယာမိ ယူယံ ယံ သုသံဝါဒံ ဂၖဟီတဝန္တသ္တသ္မာဒ် အနျော ယေန ကေနစိဒ် ယုၐ္မတ္သန္နိဓော် ဃောၐျတေ သ ၑပ္တော ဘဝတု၊
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 သာမ္ပြတံ ကမဟမ် အနုနယာမိ? ဤၑွရံ ကိံဝါ မာနဝါန်? အဟံ ကိံ မာနုၐေဘျော ရောစိတုံ ယတေ? ယဒျဟမ် ဣဒါနီမပိ မာနုၐေဘျော ရုရုစိၐေယ တရှိ ခြီၐ္ဋသျ ပရိစာရကော န ဘဝါမိ၊
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 ဟေ ဘြာတရး, မယာ ယး သုသံဝါဒေါ ဃောၐိတး သ မာနုၐာန္န လဗ္ဓသ္တဒဟံ ယုၐ္မာန် ဇ္ဉာပယာမိ၊
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 အဟံ ကသ္မာစ္စိတ် မနုၐျာတ် တံ န ဂၖဟီတဝါန် န ဝါ ၑိက္ၐိတဝါန် ကေဝလံ ယီၑေား ခြီၐ္ဋသျ ပြကာၑနာဒေဝ၊
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 ပုရာ ယိဟူဒိမတာစာရီ ယဒါဟမ် အာသံ တဒါ ယာဒၖၑမ် အာစရဏမ် အကရဝမ် ဤၑွရသျ သမိတိံ ပြတျတီဝေါပဒြဝံ ကုရွွန် ယာဒၖက် တာံ ဝျနာၑယံ တဒဝၑျံ ၑြုတံ ယုၐ္မာဘိး၊
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 အပရဉ္စ ပူရွွပုရုၐပရမ္ပရာဂတေၐု ဝါကျေၐွနျာပေက္ၐာတီဝါသက္တး သန် အဟံ ယိဟူဒိဓရ္မ္မတေ မမ သမဝယသ္ကာန် ဗဟူန် သွဇာတီယာန် အတျၑယိ၊
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 ကိဉ္စ ယ ဤၑွရော မာတၖဂရ္ဘသ္ထံ မာံ ပၖထက် ကၖတွာ သွီယာနုဂြဟေဏာဟူတဝါန္
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 သ ယဒါ မယိ သွပုတြံ ပြကာၑိတုံ ဘိန္နဒေၑီယာနာံ သမီပေ ဘယာ တံ ဃောၐယိတုဉ္စာဘျလၐတ် တဒါဟံ ကြဝျၑောဏိတာဘျာံ သဟ န မန္တြယိတွာ
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 ပူရွွနိယုက္တာနာံ ပြေရိတာနာံ သမီပံ ယိရူၑာလမံ န ဂတွာရဝဒေၑံ ဂတဝါန် ပၑ္စာတ် တတ္သ္ထာနာဒ် ဒမ္မေၐကနဂရံ ပရာဝၖတျာဂတဝါန်၊
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 တတး ပရံ ဝရ္ၐတြယေ ဝျတီတေ'ဟံ ပိတရံ သမ္ဘာၐိတုံ ယိရူၑာလမံ ဂတွာ ပဉ္စဒၑဒိနာနိ တေန သာရ္ဒ္ဓမ် အတိၐ္ဌံ၊
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 ကိန္တု တံ ပြဘော ရ္ဘြာတရံ ယာကူဗဉ္စ ဝိနာ ပြေရိတာနာံ နာနျံ ကမပျပၑျံ၊
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 ယာနျေတာနိ ဝါကျာနိ မယာ လိချန္တေ တာနျနၖတာနိ န သန္တိ တဒ် ဤၑွရော ဇာနာတိ၊
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 တတး ပရမ် အဟံ သုရိယာံ ကိလိကိယာဉ္စ ဒေၑော် ဂတဝါန်၊
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 တဒါနီံ ယိဟူဒါဒေၑသ္ထာနာံ ခြီၐ္ဋသျ သမိတီနာံ လောကား သာက္ၐာတ် မမ ပရိစယမပြာပျ ကေဝလံ ဇနၑြုတိမိမာံ လဗ္ဓဝန္တး,
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 ယော ဇနး ပူရွွမ် အသ္မာန် ပြတျုပဒြဝမကရောတ် သ တဒါ ယံ ဓရ္မ္မမနာၑယတ် တမေဝေဒါနီံ ပြစာရယတီတိ၊
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 တသ္မာတ် တေ မာမဓီၑွရံ ဓနျမဝဒန်၊
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.

< ဂါလာတိနး 1 >