< ကလသိနး 1 >

1 ဤၑွရသျေစ္ဆယာ ယီၑုခြီၐ္ဋသျ ပြေရိတး ပေါ်လသ္တီမထိယော ဘြာတာ စ ကလသီနဂရသ္ထာန် ပဝိတြာန် ဝိၑွသ္တာန် ခြီၐ္ဋာၑြိတဘြာတၖန် ပြတိ ပတြံ လိခတး၊
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
2 အသ္မာကံ တာတ ဤၑွရး ပြဘု ရျီၑုခြီၐ္ဋၑ္စ ယုၐ္မာန် ပြတိ ပြသာဒံ ၑာန္တိဉ္စ ကြိယာသ္တာံ၊
Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
3 ခြီၐ္ဋေ ယီၑော် ယုၐ္မာကံ ဝိၑွာသသျ သရွွာန် ပဝိတြလောကာန် ပြတိ ပြေမ္နၑ္စ ဝါရ္တ္တာံ ၑြုတွာ
Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
4 ဝယံ သဒါ ယုၐ္မဒရ္ထံ ပြာရ္ထနာံ ကုရွွန္တး သွရ္ဂေ နိဟိတာယာ ယုၐ္မာကံ ဘာဝိသမ္ပဒး ကာရဏာတ် သွကီယပြဘော ရျီၑုခြီၐ္ဋသျ တာတမ် ဤၑွရံ ဓနျံ ဝဒါမး၊
Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
5 ယူယံ တသျာ ဘာဝိသမ္ပဒေါ ဝါရ္တ္တာံ ယယာ သုသံဝါဒရူပိဏျာ သတျဝါဏျာ ဇ္ဉာပိတား
Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
6 သာ ယဒွတ် ကၖသ္နံ ဇဂဒ် အဘိဂစ္ဆတိ တဒွဒ် ယုၐ္မာန် အပျဘျဂမတ်, ယူယဉ္စ ယဒ် ဒိနမ် အာရဘျေၑွရသျာနုဂြဟသျ ဝါရ္တ္တာံ ၑြုတွာ သတျရူပေဏ ဇ္ဉာတဝန္တသ္တဒါရဘျ ယုၐ္မာကံ မဓျေ'ပိ ဖလတိ ဝရ္ဒ္ဓတေ စ၊
umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
7 အသ္မာကံ ပြိယး သဟဒါသော ယုၐ္မာကံ ကၖတေ စ ခြီၐ္ဋသျ ဝိၑွသ္တပရိစာရကော ယ ဣပဖြာသ္တဒ် ဝါကျံ
Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
8 ယုၐ္မာန် အာဒိၐ္ဋဝါန် သ ဧဝါသ္မာန် အာတ္မနာ ဇနိတံ ယုၐ္မာကံ ပြေမ ဇ္ဉာပိတဝါန်၊
Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
9 ဝယံ ယဒ် ဒိနမ် အာရဘျ တာံ ဝါရ္တ္တာံ ၑြုတဝန္တသ္တဒါရဘျ နိရန္တရံ ယုၐ္မာကံ ကၖတေ ပြာရ္ထနာံ ကုရ္မ္မး ဖလတော ယူယံ ယတ် ပူရ္ဏာဘျာမ် အာတ္မိကဇ္ဉာနဝုဒ္ဓိဘျာမ် ဤၑွရသျာဘိတမံ သမ္ပူရ္ဏရူပေဏာဝဂစ္ဆေတ,
Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
10 ပြဘော ရျောဂျံ သရွွထာ သန္တောၐဇနကဉ္စာစာရံ ကုရျျာတာရ္ထတ ဤၑွရဇ္ဉာနေ ဝရ္ဒ္ဓမာနား သရွွသတ္ကရ္မ္မရူပံ ဖလံ ဖလေတ,
Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
11 ယထာ စေၑွရသျ မဟိမယုက္တယာ ၑက္တျာ သာနန္ဒေန ပူရ္ဏာံ သဟိၐ္ဏုတာံ တိတိက္ၐာဉ္စာစရိတုံ ၑက္ၐျထ တာဒၖၑေန ပူရ္ဏဗလေန ယဒ် ဗလဝန္တော ဘဝေတ,
Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
12 ယၑ္စ ပိတာ တေဇောဝါသိနာံ ပဝိတြလောကာနာမ် အဓိကာရသျာံၑိတွာယာသ္မာန် ယောဂျာန် ကၖတဝါန် တံ ယဒ် ဓနျံ ဝဒေတ ဝရမ် ဧနံ ယာစာမဟေ၊
ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
13 ယတး သော'သ္မာန် တိမိရသျ ကရ္တ္တၖတွာဒ် ဥဒ္ဓၖတျ သွကီယသျ ပြိယပုတြသျ ရာဇျေ သ္ထာပိတဝါန်၊
Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
14 တသ္မာတ် ပုတြာဒ် ဝယံ ပရိတြာဏမ် အရ္ထတး ပါပမောစနံ ပြာပ္တဝန္တး၊
Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
15 သ စာဒၖၑျသျေၑွရသျ ပြတိမူရ္တိး ကၖတ္သ္နာယား သၖၐ္ဋေရာဒိကရ္တ္တာ စ၊
Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
16 ယတး သရွွမေဝ တေန သသၖဇေ သိံဟာသနရာဇတွပရာကြမာဒီနိ သွရ္ဂမရ္တ္တျသ္ထိတာနိ ဒၖၑျာဒၖၑျာနိ ဝသ္တူနိ သရွွာဏိ တေနဲဝ တသ္မဲ စ သသၖဇိရေ၊
Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
17 သ သရွွေၐာမ် အာဒိး သရွွေၐာံ သ္ထိတိကာရကၑ္စ၊
Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
18 သ ဧဝ သမိတိရူပါယာသ္တနော ရ္မူရ္ဒ္ဓါ ကိဉ္စ သရွွဝိၐယေ သ ယဒ် အဂြိယော ဘဝေတ် တဒရ္ထံ သ ဧဝ မၖတာနာံ မဓျာတ် ပြထမတ ဥတ္ထိတော'ဂြၑ္စ၊
Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
19 ယတ ဤၑွရသျ ကၖတ္သ္နံ ပူရ္ဏတွံ တမေဝါဝါသယိတုံ
Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
20 ကြုၑေ ပါတိတေန တသျ ရက္တေန သန္ဓိံ ဝိဓာယ တေနဲဝ သွရ္ဂမရ္တ္တျသ္ထိတာနိ သရွွာဏိ သွေန သဟ သန္ဓာပယိတုဉ္စေၑွရေဏာဘိလေၐေ၊
Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
21 ပူရွွံ ဒူရသ္ထာ ဒုၐ္ကြိယာရတမနသ္ကတွာတ် တသျ ရိပဝၑ္စာသ္တ ယေ ယူယံ တာန် ယုၐ္မာန် အပိ သ ဣဒါနီံ တသျ မာံသလၑရီရေ မရဏေန သွေန သဟ သန္ဓာပိတဝါန်၊
Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
22 ယတး သ သွသမ္မုခေ ပဝိတြာန် နိၐ္ကလင်္ကာန် အနိန္ဒနီယာံၑ္စ ယုၐ္မာန် သ္ထာပယိတုမ် ဣစ္ဆတိ၊
Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
23 ကိန္တွေတဒရ္ထံ ယုၐ္မာဘိ ရ္ဗဒ္ဓမူလဲး သုသ္ထိရဲၑ္စ ဘဝိတဝျမ်, အာကာၑမဏ္ဍလသျာဓးသ္ထိတာနာံ သရွွလောကာနာံ မဓျေ စ ဃုၐျမာဏော ယး သုသံဝါဒေါ ယုၐ္မာဘိရၑြာဝိ တဇ္ဇာတာယာံ ပြတျာၑာယာံ ယုၐ္မာဘိရစလဲ ရ္ဘဝိတဝျံ၊
ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
24 တသျ သုသံဝါဒသျဲကး ပရိစာရကော ယော'ဟံ ပေါ်လး သော'ဟမ် ဣဒါနီမ် အာနန္ဒေန ယုၐ္မဒရ္ထံ ဒုးခါနိ သဟေ ခြီၐ္ဋသျ က္လေၑဘောဂသျ ယောံၑော'ပူရ္ဏသ္တမေဝ တသျ တနေား သမိတေး ကၖတေ သွၑရီရေ ပူရယာမိ စ၊
Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
25 ယတ ဤၑွရသျ မန္တြဏယာ ယုၐ္မဒရ္ထမ် ဤၑွရီယဝါကျသျ ပြစာရသျ ဘာရော မယိ သမပိတသ္တသ္မာဒ် အဟံ တသျား သမိတေး ပရိစာရကော'ဘဝံ၊
Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
26 တတ် နိဂူဎံ ဝါကျံ ပူရွွယုဂေၐု ပူရွွပုရုၐေဘျး ပြစ္ဆန္နမ် အာသီတ် ကိန္တွိဒါနီံ တသျ ပဝိတြလောကာနာံ သန္နိဓော် တေန ပြာကာၑျတ၊ (aiōn g165)
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
27 ယတော ဘိန္နဇာတီယာနာံ မဓျေ တတ် နိဂူဎဝါကျံ ကီဒၖဂ္ဂော်ရဝနိဓိသမ္ဗလိတံ တတ် ပဝိတြလောကာန် ဇ္ဉာပယိတုမ် ဤၑွရော'ဘျလၐတ်၊ ယုၐ္မန္မဓျဝရ္တ္တီ ခြီၐ္ဋ ဧဝ သ နိဓိ ရ္ဂဲရဝါၑာဘူမိၑ္စ၊
Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
28 တသ္မာဒ် ဝယံ တမေဝ ဃောၐယန္တော ယဒ် ဧကဲကံ မာနဝံ သိဒ္ဓီဘူတံ ခြီၐ္ဋေ သ္ထာပယေမ တဒရ္ထမေကဲကံ မာနဝံ ပြဗောဓယာမး ပူရ္ဏဇ္ဉာနေန စဲကဲကံ မာနဝံ ဥပဒိၑာမး၊
Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
29 ဧတဒရ္ထံ တသျ ယာ ၑက္တိး ပြဗလရူပေဏ မမ မဓျေ ပြကာၑတေ တယာဟံ ယတမာနး ၑြာဘျာမိ၊
Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

< ကလသိနး 1 >