< ပြေရိတား 26 >

1 တတ အာဂြိပ္ပး ပေါ်လမ် အဝါဒီတ်, နိဇာံ ကထာံ ကထယိတုံ တုဘျမ် အနုမတိ ရ္ဒီယတေ၊ တသ္မာတ် ပေါ်လး ကရံ ပြသာရျျ သွသ္မိန် ဥတ္တရမ် အဝါဒီတ်၊
Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
2 ဟေ အာဂြိပ္ပရာဇ ယတ္ကာရဏာဒဟံ ယိဟူဒီယဲရပဝါဒိတော 'ဘဝံ တသျ ဝၖတ္တာန္တမ် အဒျ ဘဝတး သာက္ၐာန် နိဝေဒယိတုမနုမတောဟမ် ဣဒံ သွီယံ ပရမံ ဘာဂျံ မနျေ;
“Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
3 ယတော ယိဟူဒီယလောကာနာံ မဓျေ ယာ ယာ ရီတိး သူက္ၐ္မဝိစာရာၑ္စ သန္တိ တေၐု ဘဝါန် ဝိဇ္ဉတမး; အတဧဝ ပြာရ္ထယေ ဓဲရျျမဝလမ္ဗျ မမ နိဝေဒနံ ၑၖဏောတု၊
ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
4 အဟံ ယိရူၑာလမ္နဂရေ သွဒေၑီယလောကာနာံ မဓျေ တိၐ္ဌန် အာ ယော်ဝနကာလာဒ် ယဒြူပမ် အာစရိတဝါန် တဒ် ယိဟူဒီယလောကား သရွွေ ဝိဒန္တိ၊
“Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
5 အသ္မာကံ သရွွေဘျး ၑုဒ္ဓတမံ ယတ် ဖိရူၑီယမတံ တဒဝလမ္ဗီ ဘူတွာဟံ ကာလံ ယာပိတဝါန် ယေ ဇနာ အာ ဗာလျကာလာန် မာံ ဇာနာန္တိ တေ ဧတာဒၖၑံ သာက္ၐျံ ယဒိ ဒဒါတိ တရှိ ဒါတုံ ၑက္နုဝန္တိ၊
Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
6 ကိန္တု ဟေ အာဂြိပ္ပရာဇ ဤၑွရော'သ္မာကံ ပူရွွပုရုၐာဏာံ နိကဋေ ယဒ် အင်္ဂီကၖတဝါန် တသျ ပြတျာၑာဟေတောရဟမ် ဣဒါနီံ ဝိစာရသ္ထာနေ ဒဏ္ဍာယမာနောသ္မိ၊
Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
7 တသျာင်္ဂီကာရသျ ဖလံ ပြာပ္တုမ် အသ္မာကံ ဒွါဒၑဝံၑာ ဒိဝါနိၑံ မဟာယတ္နာဒ် ဤၑွရသေဝနံ ကၖတွာ ယာံ ပြတျာၑာံ ကုရွွန္တိ တသျား ပြတျာၑာယာ ဟေတောရဟံ ယိဟူဒီယဲရပဝါဒိတော'ဘဝမ်၊
Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
8 ဤၑွရော မၖတာန် ဥတ္ထာပယိၐျတီတိ ဝါကျံ ယုၐ္မာကံ နိကဋေ'သမ္ဘဝံ ကုတော ဘဝေတ်?
Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
9 နာသရတီယယီၑော ရ္နာမ္နော ဝိရုဒ္ဓံ နာနာပြကာရပြတိကူလာစရဏမ် ဥစိတမ် ဣတျဟံ မနသိ ယထာရ္ထံ ဝိဇ္ဉာယ
“Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
10 ယိရူၑာလမနဂရေ တဒကရဝံ ဖလတး ပြဓာနယာဇကသျ နိကဋာတ် က္ၐမတာံ ပြာပျ ဗဟူန် ပဝိတြလောကာန် ကာရာယာံ ဗဒ္ဓဝါန် ဝိၑေၐတသ္တေၐာံ ဟနနသမယေ တေၐာံ ဝိရုဒ္ဓါံ နိဇာံ သမ္မတိံ ပြကာၑိတဝါန်၊
Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
11 ဝါရံ ဝါရံ ဘဇနဘဝနေၐု တေဘျော ဒဏ္ဍံ ပြဒတ္တဝါန် ဗလာတ် တံ ဓရ္မ္မံ နိန္ဒယိတဝါံၑ္စ ပုနၑ္စ တာန် ပြတိ မဟာကြောဓာဒ် ဥန္မတ္တး သန် ဝိဒေၑီယနဂရာဏိ ယာဝတ် တာန် တာဍိတဝါန်၊
Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
12 ဣတ္ထံ ပြဓာနယာဇကသျ သမီပါတ် ၑက္တိမ် အာဇ္ဉာပတြဉ္စ လဗ္ဓွာ ဒမ္မေၐက္နဂရံ ဂတဝါန်၊
“Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
13 တဒါဟံ ဟေ ရာဇန် မာရ္ဂမဓျေ မဓျာဟ္နကာလေ မမ မဒီယသင်္ဂိနာံ လောကာနာဉ္စ စတသၖၐု ဒိက္ၐု ဂဂဏာတ် ပြကာၑမာနာံ ဘာသ္ကရတောပိ တေဇသွတီံ ဒီပ္တိံ ဒၖၐ္ဋဝါန်၊
Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
14 တသ္မာဒ် အသ္မာသု သရွွေၐု ဘူမော် ပတိတေၐု သတ္သု ဟေ ၑော်လ ဟဲ ၑော်လ ကုတော မာံ တာဍယသိ? ကဏ္ဋကာနာံ မုခေ ပါဒါဟနနံ တဝ ဒုးသာဓျမ် ဣဗြီယဘာၐယာ ဂဒိတ ဧတာဒၖၑ ဧကး ၑဗ္ဒော မယာ ၑြုတး၊
Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
15 တဒါဟံ ပၖၐ္ဋဝါန် ဟေ ပြဘော ကော ဘဝါန်? တတး သ ကထိတဝါန် ယံ ယီၑုံ တွံ တာဍယသိ သောဟံ,
Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
16 ကိန္တု သမုတ္တိၐ္ဌ တွံ ယဒ် ဒၖၐ္ဋဝါန် ဣတး ပုနဉ္စ ယဒျတ် တွာံ ဒရ္ၑယိၐျာမိ တေၐာံ သရွွေၐာံ ကာရျျာဏာံ တွာံ သာက္ၐိဏံ မမ သေဝကဉ္စ ကရ္တ္တုမ် ဒရ္ၑနမ် အဒါမ်၊
Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
17 ဝိၑေၐတော ယိဟူဒီယလောကေဘျော ဘိန္နဇာတီယေဘျၑ္စ တွာံ မနောနီတံ ကၖတွာ တေၐာံ ယထာ ပါပမောစနံ ဘဝတိ
Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
18 ယထာ တေ မယိ ဝိၑွသျ ပဝိတြီကၖတာနာံ မဓျေ ဘာဂံ ပြာပ္နုဝန္တိ တဒဘိပြာယေဏ တေၐာံ ဇ္ဉာနစက္ၐူံၐိ ပြသန္နာနိ ကရ္တ္တုံ တထာန္ဓကာရာဒ် ဒီပ္တိံ ပြတိ ၑဲတာနာဓိကာရာစ္စ ဤၑွရံ ပြတိ မတီး ပရာဝရ္တ္တယိတုံ တေၐာံ သမီပံ တွာံ ပြေၐျာမိ၊
kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
19 ဟေ အာဂြိပ္ပရာဇ ဧတာဒၖၑံ သွရ္ဂီယပြတျာဒေၑံ အဂြာဟျမ် အကၖတွာဟံ
“Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
20 ပြထမတော ဒမ္မေၐက္နဂရေ တတော ယိရူၑာလမိ သရွွသ္မိန် ယိဟူဒီယဒေၑေ အနျေၐု ဒေၑေၐု စ ယေန လောကာ မတိံ ပရာဝရ္တ္တျ ဤၑွရံ ပြတိ ပရာဝရ္တ္တယန္တေ, မနးပရာဝရ္တ္တနယောဂျာနိ ကရ္မ္မာဏိ စ ကုရွွန္တိ တာဒၖၑမ် ဥပဒေၑံ ပြစာရိတဝါန်၊
Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
21 ဧတတ္ကာရဏာဒ် ယိဟူဒီယာ မဓျေမန္ဒိရံ မာံ ဓၖတွာ ဟန္တုမ် ဥဒျတား၊
Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
22 တထာပိ ခြီၐ္ဋော ဒုးခံ ဘုက္တွာ သရွွေၐာံ ပူရွွံ ၑ္မၑာနာဒ် ဥတ္ထာယ နိဇဒေၑီယာနာံ ဘိန္နဒေၑီယာနာဉ္စ သမီပေ ဒီပ္တိံ ပြကာၑယိၐျတိ
Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
23 ဘဝိၐျဒွါဒိဂဏော မူသာၑ္စ ဘာဝိကာရျျသျ ယဒိဒံ ပြမာဏမ် အဒဒုရေတဒ် ဝိနာနျာံ ကထာံ န ကထယိတွာ ဤၑွရာဒ် အနုဂြဟံ လဗ္ဓွာ မဟတာံ က္ၐုဒြာဏာဉ္စ သရွွေၐာံ သမီပေ ပြမာဏံ ဒတ္တွာဒျ ယာဝတ် တိၐ္ဌာမိ၊
Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
24 တသျမာံ ကထာံ နိၑမျ ဖီၐ္ဋ ဥစ္စဲး သွရေဏ ကထိတဝါန် ဟေ ပေါ်လ တွမ် ဥန္မတ္တောသိ ဗဟုဝိဒျာဘျာသေန တွံ ဟတဇ္ဉာနော ဇာတး၊
Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
25 သ ဥက္တဝါန် ဟေ မဟာမဟိမ ဖီၐ္ဋ နာဟမ် ဥန္မတ္တး ကိန္တု သတျံ ဝိဝေစနီယဉ္စ ဝါကျံ ပြသ္တော်မိ၊
Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
26 ယသျ သာက္ၐာဒ် အက္ၐောဘး သန် ကထာံ ကထယာမိ သ ရာဇာ တဒွၖတ္တာန္တံ ဇာနာတိ တသျ သမီပေ ကိမပိ ဂုပ္တံ နေတိ မယာ နိၑ္စိတံ ဗုဓျတေ ယတသ္တဒ် ဝိဇနေ န ကၖတံ၊
Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
27 ဟေ အာဂြိပ္ပရာဇ ဘဝါန် ကိံ ဘဝိၐျဒွါဒိဂဏောက္တာနိ ဝါကျာနိ ပြတျေတိ? ဘဝါန် ပြတျေတိ တဒဟံ ဇာနာမိ၊
Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
28 တတ အာဂြိပ္ပး ပေါ်လမ် အဘိဟိတဝါန် တွံ ပြဝၖတ္တိံ ဇနယိတွာ ပြာယေဏ မာမပိ ခြီၐ္ဋီယံ ကရောၐိ၊
Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
29 တတး သော'ဝါဒီတ် ဘဝါန် ယေ ယေ လောကာၑ္စ မမ ကထာမ် အဒျ ၑၖဏွန္တိ ပြာယေဏ ဣတိ နဟိ ကိန္တွေတတ် ၑၖင်္ခလဗန္ဓနံ ဝိနာ သရွွထာ တေ သရွွေ မာဒၖၑာ ဘဝန္တွိတီၑွသျ သမီပေ ပြာရ္ထယေ'ဟမ်၊
Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
30 ဧတသျာံ ကထာယာံ ကထိတာယာံ သ ရာဇာ သော'ဓိပတိ ရ္ဗရ္ဏီကီ သဘာသ္ထာ လောကာၑ္စ တသ္မာဒ် ဥတ္ထာယ
Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
31 ဂေါပနေ ပရသ္ပရံ ဝိဝိစျ ကထိတဝန္တ ဧၐ ဇနော ဗန္ဓနာရှံ ပြာဏဟနနာရှံ ဝါ ကိမပိ ကရ္မ္မ နာကရောတ်၊
Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
32 တတ အာဂြိပ္ပး ဖီၐ္ဋမ် အဝဒတ်, ယဒျေၐ မာနုၐး ကဲသရသျ နိကဋေ ဝိစာရိတော ဘဝိတုံ န ပြာရ္ထယိၐျတ် တရှိ မုက္တော ဘဝိတုမ် အၑက္ၐျတ်၊
Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”

< ပြေရိတား 26 >