< ၂ ယောဟနး 1 >

1 ဟေ အဘိရုစိတေ ကုရိယေ, တွာံ တဝ ပုတြာံၑ္စ ပြတိ ပြာစီနော'ဟံ ပတြံ လိခါမိ၊
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
2 သတျမတာဒ် ယုၐ္မာသု မမ ပြေမာသ္တိ ကေဝလံ မမ နဟိ ကိန္တု သတျမတဇ္ဉာနာံ သရွွေၐာမေဝ၊ ယတး သတျမတမ် အသ္မာသု တိၐ္ဌတျနန္တကာလံ ယာဝစ္စာသ္မာသု သ္ထာသျတိ၊ (aiōn g165)
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
3 ပိတုရီၑွရာတ် တတ္ပိတုး ပုတြာတ် ပြဘော ရျီၑုခြီၐ္ဋာစ္စ ပြာပျော 'နုဂြဟး ကၖပါ ၑာန္တိၑ္စ သတျတာပြေမဘျာံ သာရ္ဒ္ဓံ ယုၐ္မာန် အဓိတိၐ္ဌတု၊
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
4 ဝယံ ပိတၖတော ယာမ် အာဇ္ဉာံ ပြာပ္တဝန္တသ္တဒနုသာရေဏ တဝ ကေစိဒ် အာတ္မဇား သတျမတမ် အာစရန္တျေတသျ ပြမာဏံ ပြာပျာဟံ ဘၖၑမ် အာနန္ဒိတဝါန်၊
Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
5 သာမ္ပြတဉ္စ ဟေ ကုရိယေ, နဝီနာံ ကာဉ္စိဒ် အာဇ္ဉာံ န လိခန္နဟမ် အာဒိတော လဗ္ဓာမ် အာဇ္ဉာံ လိခန် တွာမ် ဣဒံ ဝိနယေ ယဒ် အသ္မာဘိး ပရသ္ပရံ ပြေမ ကရ္တ္တဝျံ၊
Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
6 အပရံ ပြေမဲတေန ပြကာၑတေ ယဒ် ဝယံ တသျာဇ္ဉာ အာစရေမ၊ အာဒိတော ယုၐ္မာဘိ ရျာ ၑြုတာ သေယမ် အာဇ္ဉာ သာ စ ယုၐ္မာဘိရာစရိတဝျာ၊
Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
7 ယတော ဗဟဝး ပြဝဉ္စကာ ဇဂတ် ပြဝိၑျ ယီၑုခြီၐ္ဋော နရာဝတာရော ဘူတွာဂတ ဧတတ် နာင်္ဂီကုရွွန္တိ သ ဧဝ ပြဝဉ္စကး ခြီၐ္ဋာရိၑ္စာသ္တိ၊
Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
8 အသ္မာကံ ၑြမော ယတ် ပဏ္ဍၑြမော န ဘဝေတ် ကိန္တု သမ္ပူရ္ဏံ ဝေတနမသ္မာဘိ ရ္လဘျေတ တဒရ္ထံ သွာနဓိ သာဝဓာနာ ဘဝတး၊
Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
9 ယး ကၑ္စိဒ် ဝိပထဂါမီ ဘူတွာ ခြီၐ္ဋသျ ၑိက္ၐာယာံ န တိၐ္ဌတိ သ ဤၑွရံ န ဓာရယတိ ခြီၐ္ဋသျ ၑိဇ္ဉာယာံ ယသ္တိၐ္ဌတိ သ ပိတရံ ပုတြဉ္စ ဓာရယတိ၊
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
10 ယး ကၑ္စိဒ် ယုၐ္မတ္သန္နိဓိမာဂစ္ဆန် ၑိက္ၐာမေနာံ နာနယတိ သ ယုၐ္မာဘိး သွဝေၑ္မနိ န ဂၖဟျတာံ တဝ မင်္ဂလံ ဘူယာဒိတိ ဝါဂပိ တသ္မဲ န ကထျတာံ၊
Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
11 ယတသ္တဝ မင်္ဂလံ ဘူယာဒိတိ ဝါစံ ယး ကၑ္စိတ် တသ္မဲ ကထယတိ သ တသျ ဒုၐ္ကရ္မ္မဏာမ် အံၑီ ဘဝတိ၊
Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
12 ယုၐ္မာန် ပြတိ မယာ ဗဟူနိ လေခိတဝျာနိ ကိန္တု ပတြမသီဘျာံ တတ် ကရ္တ္တုံ နေစ္ဆာမိ, ယတော 'သ္မာကမ် အာနန္ဒော ယထာ သမ္ပူရ္ဏော ဘဝိၐျတိ တထာ ယုၐ္မတ္သမီပမုပသ္ထာယာဟံ သမ္မုခီဘူယ ယုၐ္မာဘိး သမ္ဘာၐိၐျ ဣတိ ပြတျာၑာ မမာသ္တေ၊
Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
13 တဝါဘိရုစိတာယာ ဘဂိနျာ ဗာလကာသ္တွာံ နမသ္ကာရံ ဇ္ဉာပယန္တိ၊ အာမေန်၊
Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

< ၂ ယောဟနး 1 >