< ၁ ပိတရး 3 >

1 ဟေ ယောၐိတး, ယူယမပိ နိဇသွာမိနာံ ဝၑျာ ဘဝတ တထာ သတိ ယဒိ ကေစိဒ် ဝါကျေ ဝိၑွာသိနော န သန္တိ တရှိ
Momwemonso, akazi inu gonjerani amuna anu kuti ngati ena a iwo sakhulupirira Mawu a Mulungu, akopeke ndi makhalidwe a akazi awo ndipo sipadzafunikanso mawu
2 တေ ဝိနာဝါကျံ ယောၐိတာမ် အာစာရေဏာရ္ထတသ္တေၐာံ ပြတျက္ၐေဏ ယုၐ္မာကံ သဘယသတီတွာစာရေဏာကြၐ္ဋုံ ၑက္ၐျန္တေ၊
pamene aona moyo wanu wachiyero ndi moyo woopa Mulungu.
3 အပရံ ကေၑရစနယာ သွရ္ဏာလင်္ကာရဓာရဏောန ပရိစ္ဆဒပရိဓာနေန ဝါ ယုၐ္မာကံ ဝါဟျဘူၐာ န ဘဝတု,
Kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwa maonekedwe akunja, monga kuluka tsitsi ndi kuvala zokometsera zagolide ndi zovala zamberewere.
4 ကိန္တွီၑွရသျ သာက္ၐာဒ် ဗဟုမူလျက္ၐမာၑာန္တိဘာဝါက္ၐယရတ္နေန ယုက္တော ဂုပ္တ အာန္တရိကမာနဝ ဧဝ၊
Mʼmalo mwake kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa munthu wa mʼkatimo, kukongola kosatha kwa mtima ofatsa ndi mzimu wachete, zimene ndi za mtengowapatali pamaso pa Mulungu.
5 ယတး ပူရွွကာလေ ယား ပဝိတြသ္တြိယ ဤၑွရေ ပြတျာၑာမကုရွွန် တာ အပိ တာဒၖၑီမေဝ ဘူၐာံ ဓာရယန္တျော နိဇသွာမိနာံ ဝၑျာ အဘဝန်၊
Pakuti umo ndi mmene akazi oyera mtima akale amene anali ndi chiyembekezo pa Mulungu anadzikongoletsera. Iwo ankagonjera amuna awo,
6 တထဲဝ သာရာ ဣဗြာဟီမော ဝၑျာ သတီ တံ ပတိမာချာတဝတီ ယူယဉ္စ ယဒိ သဒါစာရိဏျော ဘဝထ ဝျာကုလတယာ စ ဘီတာ န ဘဝထ တရှိ တသျား ကနျာ အာဓွေ၊
monga Sara, amene anamvera Abrahamu namutcha iye mbuye wake. Akazi inu ndinu ana ake ngati muchita zoyenera, ndipo musaope choopsa chilichonse.
7 ဟေ ပုရုၐား, ယူယံ ဇ္ဉာနတော ဒုရ္ဗ္ဗလတရဘာဇနဲရိဝ ယောၐိဒ္ဘိး သဟဝါသံ ကုရုတ, ဧကသျ ဇီဝနဝရသျ သဟဘာဂိနီဘျတာဘျး သမာဒရံ ဝိတရတ စ န စေဒ် ယုၐ္မာကံ ပြာရ္ထနာနာံ ဗာဓာ ဇနိၐျတေ၊
Momwemonso amuna inu, khalani mwanzeru ndi akazi anu, ndipo muwachitire ulemu monga anzanu ofowoka ndiponso olandira nanu pamodzi mphatso ya moyo wosatha, kuti pasakhale kanthu kotsekereza mapemphero anu.
8 ဝိၑေၐတော ယူယံ သရွွ ဧကမနသး ပရဒုးခဲ ရ္ဒုးခိတာ ဘြာတၖပြမိဏး ကၖပါဝန္တး ပြီတိဘာဝါၑ္စ ဘဝတ၊
Potsiriza, nonse khalani a mtima umodzi, omverana chisoni. Kondanani monga abale, muchitirane chifundo ndi kudzichepetsa.
9 အနိၐ္ဋသျ ပရိၑောဓေနာနိၐ္ဋံ နိန္ဒာယာ ဝါ ပရိၑောဓေန နိန္ဒာံ န ကုရွွန္တ အာၑိၐံ ဒတ္တ ယတော ယူယမ် အာၑိရဓိကာရိဏော ဘဝိတုမာဟူတာ ဣတိ ဇာနီထ၊
Wina akakuchitirani choyipa musabwezere pochitanso choyipa, kapena kubwezera chipongwe akakuchitirani chipongwe, koma muwadalitse. Munayitanidwa kuti mulandire mdalitso.
10 အပရဉ္စ, ဇီဝနေ ပြီယမာဏော ယး သုဒိနာနိ ဒိဒၖက္ၐတေ၊ ပါပါတ် ဇိဟွာံ မၖၐာဝါကျာတ် သွာဓရော် သ နိဝရ္တ္တယေတ်၊
Pakuti, “Iye amene angakonde moyo ndi kuona masiku abwino, aletse lilime lake kuyankhula zoyipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza.
11 သ တျဇေဒ် ဒုၐ္ဋတာမာရ္ဂံ သတ္ကြိယာဉ္စ သမာစရေတ်၊ မၖဂယာဏၑ္စ ၑာန္တိံ သ နိတျမေဝါနုဓာဝတု၊
Apewe zoyipa, ndipo azichita zabwino. Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuwupeza.
12 လောစနေ ပရမေၑသျောန္မီလိတေ ဓာရ္မ္မိကာန် ပြတိ၊ ပြာရ္ထနာယား ကၖတေ တေၐား တစ္ဆြောတြေ သုဂမေ သဒါ၊ ကြောဓာသျဉ္စ ပရေၑသျ ကဒါစာရိၐု ဝရ္တ္တတေ၊
Pakuti Ambuye amayangʼanira bwino anthu olungama ndipo amatchera khutu ku mapemphero awo. Koma Ambuye sawayangʼana bwino amene amachita zoyipa.”
13 အပရံ ယဒိ ယူယမ် ဥတ္တမသျာနုဂါမိနော ဘဝထ တရှိ ကော ယုၐ္မာန် ဟိံသိၐျတေ?
Ndani angakuchitireni zoyipa ngati muchita changu kuchita zabwino?
14 ယဒိ စ ဓရ္မ္မာရ္ထံ က္လိၑျဓွံ တရှိ ဓနျာ ဘဝိၐျထ၊ တေၐာမ် အာၑင်္ကယာ ယူယံ န ဗိဘီတ န ဝိင်္က္တ ဝါ၊
Koma ngakhale mumve zowawa chifukwa cha chilungamo, ndinu odala. “Musaope anthu, musachite mantha.”
15 မနောဘိး ကိန္တု မနျဓွံ ပဝိတြံ ပြဘုမီၑွရံ၊ အပရဉ္စ ယုၐ္မာကမ် အာန္တရိကပြတျာၑာယာသ္တတ္တွံ ယး ကၑ္စိတ် ပၖစ္ဆတိ တသ္မဲ ၑာန္တိဘီတိဘျာမ် ဥတ္တရံ ဒါတုံ သဒါ သုသဇ္ဇာ ဘဝတ၊
Koma lemekezani Khristu mʼmitima mwanu ngati Ambuye wanu. Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha aliyense amene akufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho.
16 ယေ စ ခြီၐ္ဋဓရ္မ္မေ ယုၐ္မာကံ သဒါစာရံ ဒူၐယန္တိ တေ ဒုၐ္ကရ္မ္မကာရိဏာမိဝ ယုၐ္မာကမ် အပဝါဒေန ယတ် လဇ္ဇိတာ ဘဝေယုသ္တဒရ္ထံ ယုၐ္မာကမ် ဥတ္တမး သံဝေဒေါ ဘဝတု၊
Koma chitani zimenezi mofatsa ndi mwaulemu, mukhale ndi chikumbumtima chosakutsutsani, kuti anthu ena akanena zoyipa za makhalidwe anu abwino mwa Khristu, achite okha manyazi ndi chipongwe chawocho.
17 ဤၑွရသျာဘိမတာဒ် ယဒိ ယုၐ္မာဘိး က္လေၑး သောဎဝျသ္တရှိ သဒါစာရိဘိး က္လေၑသဟနံ ဝရံ န စ ကဒါစာရိဘိး၊
Nʼkwabwino ngati ndi chifuniro cha Mulungu kumva zowawa chifukwa chochita zabwino kusiyana ndi kumva zowawa chifukwa chochita zoyipa.
18 ယသ္မာဒ် ဤၑွရသျ သန္နိဓိမ် အသ္မာန် အာနေတုမ် အဓာရ္မ္မိကာဏာံ ဝိနိမယေန ဓာရ္မ္မိကး ခြီၐ္ဋော 'ပျေကကၖတွး ပါပါနာံ ဒဏ္ဍံ ဘုက္တဝါန်, သ စ ၑရီရသမ္ဗန္ဓေ မာရိတး ကိန္တွာတ္မနး သမ္ဗန္ဓေ ပုန ရ္ဇီဝိတော 'ဘဝတ်၊
Pakuti Khristu anafa chifukwa cha machimo kamodzi kokha kufera onse, wolungama kufera osalungama, kuti akufikitseni kwa Mulungu. Anaphedwa ku thupi koma anapatsidwa moyo mu mzimu.
19 တတ္သမ္ဗန္ဓေ စ သ ယာတြာံ ဝိဓာယ ကာရာဗဒ္ဓါနာမ် အာတ္မနာံ သမီပေ ဝါကျံ ဃောၐိတဝါန်၊
Ndipo ali ngati mzimu chomwecho anapita ndi kukalalikira mizimu imene inali mʼndende,
20 ပုရာ နောဟသျ သမယေ ယာဝတ် ပေါတော နိရမီယတ တာဝဒ် ဤၑွရသျ ဒီရ္ဃသဟိၐ္ဏုတာ ယဒါ ဝျလမ္ဗတ တဒါ တေ'နာဇ္ဉာဂြာဟိဏော'ဘဝန်၊ တေန ပေါတောနာလ္ပေ'ရ္ထာဒ် အၐ္ဋာဝေဝ ပြာဏိနသ္တောယမ် ဥတ္တီရ္ဏား၊
ya anthu amene sanamvere Mulungu atadikira moleza mtima pa nthawi imene Nowa ankapanga chombo. Mʼchombo chija anthu owerengeka okha, asanu ndi atatu, ndiwo anapulumutsidwa ku madzi.
21 တန္နိဒရ္ၑနဉ္စာဝဂါဟနံ (အရ္ထတး ၑာရီရိကမလိနတာယာ ယသ္တျာဂး သ နဟိ ကိန္တွီၑွရာယောတ္တမသံဝေဒသျ ယာ ပြတဇ္ဉာ သဲဝ) ယီၑုခြီၐ္ဋသျ ပုနရုတ္ထာနေနေဒါနီမ် အသ္မာန် ဥတ္တာရယတိ,
Madziwo akufanizira ubatizo umene lero ukukupulumutsaninso, osati chifukwa chochotsa litsiro la mʼthupi koma chifukwa cha chikumbumtima choona pamaso pa Mulungu. Umakupulumutsani chifukwa cha kuuka kwa Yesu Khristu,
22 ယတး သ သွရ္ဂံ ဂတွေၑွရသျ ဒက္ၐိဏေ ဝိဒျတေ သွရ္ဂီယဒူတား ၑာသကာ ဗလာနိ စ တသျ ဝၑီဘူတာ အဘဝန်၊
amene anapita kumwamba ndipo ali kudzanja lamanja la Mulungu komwe angelo ndi maulamuliro ndi amphamvu amamvera Iye.

< ၁ ပိတရး 3 >