< ၁ ယောဟနး 3 >

1 ပၑျတ ဝယမ် ဤၑွရသျ သန္တာနာ ဣတိ နာမ္နာချာမဟေ, ဧတေန ပိတာသ္မဘျံ ကီဒၖက် မဟာပြေမ ပြဒတ္တဝါန်, ကိန္တု သံသာရသ္တံ နာဇာနာတ် တတ္ကာရဏာဒသ္မာန် အပိ န ဇာနာတိ၊
Taonani kukula kwake kwa chikondi chimene Atate anatikonda nacho, kuti titchedwe ana a Mulungu! Ndipo nʼchimene ife tili! Nʼchifukwa chake dziko lapansi silitidziwa chifukwa silinamudziwe Iye.
2 ဟေ ပြိယတမား, ဣဒါနီံ ဝယမ် ဤၑွရသျ သန္တာနာ အာသ္မဟေ ပၑ္စာတ် ကိံ ဘဝိၐျာမသ္တဒ် အဒျာပျပြကာၑိတံ ကိန္တု ပြကာၑံ ဂတေ ဝယံ တသျ သဒၖၑာ ဘဝိၐျာမိ ဣတိ ဇာနီမး, ယတး သ ယာဒၖၑော 'သ္တိ တာဒၖၑော 'သ္မာဘိရ္ဒရ္ၑိၐျတေ၊
Abale okondedwa, tsopano ndife ana a Mulungu, ndipo sichinaoneke chimene tidzakhala. Koma tikudziwa kuti Yesu akadzaonekera, tidzafanana naye, pakuti tidzamuona Iyeyo monga momwe alili.
3 တသ္မိန် ဧၐာ ပြတျာၑာ ယသျ ကသျစိဒ် ဘဝတိ သ သွံ တထာ ပဝိတြံ ကရောတိ ယထာ သ ပဝိတြော 'သ္တိ၊
Aliyense amene ali ndi chiyembekezo ichi mwa Iye adziyeretse yekha, monga Iye ali woyera.
4 ယး ကၑ္စိတ် ပါပမ် အာစရတိ သ ဝျဝသ္ထာလင်္ဃနံ ကရောတိ ယတး ပါပမေဝ ဝျဝသ္ထာလင်္ဃနံ၊
Aliyense amene amachimwa amaphwanya lamulo; pakuti tchimo ndi kuphwanya lamulo.
5 အပရံ သော 'သ္မာကံ ပါပါနျပဟရ္တ္တုံ ပြာကာၑတဲတဒ် ယူယံ ဇာနီထ, ပါပဉ္စ တသ္မိန် န ဝိဒျတေ၊
Koma inu mukudziwa kuti Yesu anabwera kuti adzachotse machimo athu. Ndipo mwa Iye mulibe tchimo.
6 ယး ကၑ္စိတ် တသ္မိန် တိၐ္ဌတိ သ ပါပါစာရံ န ကရောတိ ယး ကၑ္စိတ် ပါပါစာရံ ကရောတိ သ တံ န ဒၖၐ္ဋဝါန် န ဝါဝဂတဝါန်၊
Aliyense wokhala mwa Khristu sachimwa. Aliyense amene amachimwa sanamuone kapena kumudziwa.
7 ဟေ ပြိယဗာလကား, ကၑ္စိဒ် ယုၐ္မာကံ ဘြမံ န ဇနယေတ်, ယး ကၑ္စိဒ် ဓရ္မ္မာစာရံ ကရောတိ သ တာဒၖဂ် ဓာရ္မ္မိကော ဘဝတိ ယာဒၖက် သ ဓာမ္မိကော 'သ္တိ၊
Ana okondedwa, musalole kuti aliyense akusocheretseni. Munthu amene amachita chilungamo ndi wolungama, monga Khristu ali wolungama.
8 ယး ပါပါစာရံ ကရောတိ သ ၑယတာနာတ် ဇာတော ယတး ၑယတာန အာဒိတး ပါပါစာရီ ၑယတာနသျ ကရ္မ္မဏာံ လောပါရ္ထမေဝေၑွရသျ ပုတြး ပြာကာၑတ၊
Iye amene amachimwa ndi wa Satana, chifukwa mdierekezi wakhala akuchimwa kuyambira pa chiyambi. Mwana wa Mulungu anaonekera kuti awononge ntchito za mdierekezi.
9 ယး ကၑ္စိဒ် ဤၑွရာတ် ဇာတး သ ပါပါစာရံ န ကရောတိ ယတသ္တသျ ဝီရျျံ တသ္မိန် တိၐ္ဌတိ ပါပါစာရံ ကရ္တ္တုဉ္စ န ၑက္နောတိ ယတး သ ဤၑွရာတ် ဇာတး၊
Aliyense amene ndi mwana wa Mulungu, sachimwirachimwira, popeza mbewu ya Mulungu ili mwa iye, sangathe kuchimwa, chifukwa ndi mwana wa Mulungu.
10 ဣတျနေနေၑွရသျ သန္တာနား ၑယတာနသျ စ သန္တာနာ ဝျက္တာ ဘဝန္တိ၊ ယး ကၑ္စိဒ် ဓရ္မ္မာစာရံ န ကရောတိ သ ဤၑွရာတ် ဇာတော နဟိ ယၑ္စ သွဘြာတရိ န ပြီယတေ သော 'ပီၑွရာတ် ဇာတော နဟိ၊
Mmenemu ndi mmene timadziwira ana a Mulungu ndi amene ali ana a mdierekezi. Aliyense amene sachita chilungamo si mwana wa Mulungu; ngakhalenso amene sakonda mʼbale wake.
11 ယတသ္တသျ ယ အာဒေၑ အာဒိတော ယုၐ္မာဘိး ၑြုတး သ ဧၐ ဧဝ ယဒ် အသ္မာဘိး ပရသ္ပရံ ပြေမ ကရ္တ္တဝျံ၊
Uthenga umene munawumva kuyambira pachiyambi ndi uwu: Tizikondana wina ndi mnzake.
12 ပါပါတ္မတော ဇာတော ယး ကာဗိလ် သွဘြာတရံ ဟတဝါန် တတ္သဒၖၑဲရသ္မာဘိ ရ္န ဘဝိတဝျံ၊ သ ကသ္မာတ် ကာရဏာတ် တံ ဟတဝါန်? တသျ ကရ္မ္မာဏိ ဒုၐ္ဋာနိ တဒ္ဘြာတုၑ္စ ကရ္မ္မာဏိ ဓရ္မ္မာဏျာသန် ဣတိ ကာရဏာတ်၊
Musakhale ngati Kaini, amene anali wa woyipayo ndipo anapha mʼbale wake. Nanga anamupha chifukwa chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoyipa ndipo zochita za mʼbale wake zinali zolungama.
13 ဟေ မမ ဘြာတရး, သံသာရော ယဒိ ယုၐ္မာန် ဒွေၐ္ဋိ တရှိ တဒ် အာၑ္စရျျံ န မနျဓွံ၊
Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.
14 ဝယံ မၖတျုမ် ဥတ္တီရျျ ဇီဝနံ ပြာပ္တဝန္တသ္တဒ် ဘြာတၖၐု ပြေမကရဏာတ် ဇာနီမး၊ ဘြာတရိ ယော န ပြီယတေ သ မၖတျော် တိၐ္ဌတိ၊
Ife tikudziwa kuti tinatuluka mu imfa ndi kulowa mʼmoyo, chifukwa timakonda abale athu. Aliyense amene sakonda mʼbale wake akanali mu imfa.
15 ယး ကၑ္စိတ် သွဘြာတရံ ဒွေၐ္ဋိ သံ နရဃာတီ ကိဉ္စာနန္တဇီဝနံ နရဃာတိနး ကသျာပျန္တရေ နာဝတိၐ္ဌတေ တဒ် ယူယံ ဇာနီထ၊ (aiōnios g166)
Aliyense amene amadana ndi mʼbale wake ndi wakupha, ndipo inu mukudziwa kuti wopha anthu mwa iye mulibe moyo wosatha. (aiōnios g166)
16 အသ္မာကံ ကၖတေ သ သွပြာဏာံသ္တျက္တဝါန် ဣတျနေန ဝယံ ပြေမ္နသ္တတ္တွမ် အဝဂတား, အပရံ ဘြာတၖဏာံ ကၖတေ 'သ္မာဘိရပိ ပြာဏာသ္တျက္တဝျား၊
Mmene timadziwira chikondi chenicheni ndi umu: Yesu anapereka moyo wake chifukwa cha ife. Ndipo nafenso tiyenera kupereka miyoyo yathu chifukwa cha abale athu.
17 သာံသာရိကဇီဝိကာပြာပ္တော ယော ဇနး သွဘြာတရံ ဒီနံ ဒၖၐ္ဋွာ တသ္မာတ် သွီယဒယာံ ရုဏဒ္ဓိ တသျာန္တရ ဤၑွရသျ ပြေမ ကထံ တိၐ္ဌေတ်?
Ngati wina ali ndi chuma ndipo nʼkuona mʼbale wake akusowa, koma wosamvera chisoni, kodi mwa iyeyo muli chikondi cha Mulungu?
18 ဟေ မမ ပြိယဗာလကား, ဝါကျေန ဇိဟွယာ ဝါသ္မာဘိး ပြေမ န ကရ္တ္တဝျံ ကိန္တု ကာရျျေဏ သတျတယာ စဲဝ၊
Ana okondedwa, chikondi chathu chisakhale cha pakamwa pokha koma cha ntchito zathu ndi mʼchoonadi.
19 ဧတေန ဝယံ ယတ် သတျမတသမ္ဗန္ဓီယာသ္တတ် ဇာနီမသ္တသျ သာက္ၐာတ် သွာန္တးကရဏာနိ သာန္တွယိတုံ ၑက္ၐျာမၑ္စ၊
Pamenepo tidzadziwa kuti tili pa choonadi ndipo tidzakhala okhazikika mtima pamaso pa Mulungu,
20 ယတော 'သ္မဒန္တးကရဏံ ယဒျသ္မာန် ဒူၐယတိ တရှျသ္မဒန္တး ကရဏာဒ် ဤၑွရော မဟာန် သရွွဇ္ဉၑ္စ၊
nthawi zonse pamene mtima wathu utitsutsa. Pakuti Mulungu ndi wamkulu kuposa mitima yathu ndipo Iye amadziwa zonse.
21 ဟေ ပြိယတမား, အသ္မဒန္တးကရဏံ ယဒျသ္မာန် န ဒူၐယတိ တရှိ ဝယမ် ဤၑွရသျ သာက္ၐာတ် ပြတိဘာနွိတာ ဘဝါမး၊
Anzanga okondedwa, ngati mitima yathu sikutitsutsa, tili nako kulimbika mtima pamaso pa Mulungu.
22 ယစ္စ ပြာရ္ထယာမဟေ တတ် တသ္မာတ် ပြာပ္နုမး, ယတော ဝယံ တသျာဇ္ဉား ပါလယာမသ္တသျ သာက္ၐာတ် တုၐ္ဋိဇနကမ် အာစာရံ ကုရ္မ္မၑ္စ၊
Ndipo timalandira chilichonse chimene tichipempha kwa Iye, chifukwa timamvera malamulo ake ndi kuchita zimene zimamukondweretsa.
23 အပရံ တသျေယမာဇ္ဉာ ယဒ် ဝယံ ပုတြသျ ယီၑုခြီၐ္ဋသျ နာမ္နိ ဝိၑွသိမသ္တသျာဇ္ဉာနုသာရေဏ စ ပရသ္ပရံ ပြေမ ကုရ္မ္မး၊
Ndipo lamulo lake ndi ili: kukhulupirira dzina la Mwana wake, Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga Iye anatilamulira.
24 ယၑ္စ တသျာဇ္ဉား ပါလယတိ သ တသ္မိန် တိၐ္ဌတိ တသ္မိန် သော'ပိ တိၐ္ဌတိ; သ စာသ္မာန် ယမ် အာတ္မာနံ ဒတ္တဝါန် တသ္မာတ် သော 'သ္မာသု တိၐ္ဌတီတိ ဇာနီမး၊
Iwo amene amamvera malamulo ake amakhala mwa Iye, ndipo Iye amakhala mwa iwo. Ndipo mmenemu ndi momwe timadziwira kuti Iye akukhala mwa ife. Timadziwa mwa Mzimu Woyera amene anatipatsa.

< ၁ ယောဟနး 3 >