< ၁ ယောဟနး 2 >

1 ဟေ ပြိယဗာလကား, ယုၐ္မာဘိ ရျတ် ပါပံ န ကြိယေတ တဒရ္ထံ ယုၐ္မာန် ပြတျေတာနိ မယာ လိချန္တေ၊ ယဒိ တု ကေနာပိ ပါပံ ကြိယတေ တရှိ ပိတုး သမီပေ 'သ္မာကံ ဧကး သဟာယော 'ရ္ထတော ဓာရ္မ္မိကော ယီၑုး ခြီၐ္ဋော ဝိဒျတေ၊
Inu Ana anga okondedwa, ndikukulemberani zimenezi kuti musachimwe. Koma wina akachimwa, tili nayo Nkhoswe yotinenera kwa Atate, Yesu Khristu, Wolungamayo.
2 သ စာသ္မာကံ ပါပါနာံ ပြာယၑ္စိတ္တံ ကေဝလမသ္မာကံ နဟိ ကိန္တု လိခိလသံသာရသျ ပါပါနာံ ပြာယၑ္စိတ္တံ၊
Iyeyo ndiye nsembe yopepesera machimo athu, ndipo osati athu okha, komanso machimo onse a dziko lapansi.
3 ဝယံ တံ ဇာနီမ ဣတိ တဒီယာဇ္ဉာပါလနေနာဝဂစ္ဆာမး၊
Ife timatsimikiza kuti tikumudziwa ngati tikusunga malamulo ake.
4 အဟံ တံ ဇာနာမီတိ ဝဒိတွာ ယသ္တသျာဇ္ဉာ န ပါလယတိ သော 'နၖတဝါဒီ သတျမတဉ္စ တသျာန္တရေ န ဝိဒျတေ၊
Munthu akamanena kuti, “Ine ndimadziwa Mulungu,” koma samvera malamulo a Mulunguyo, ndi wabodza ameneyo ndipo mwa iye mulibe choonadi.
5 ယး ကၑ္စိတ် တသျ ဝါကျံ ပါလယတိ တသ္မိန် ဤၑွရသျ ပြေမ သတျရူပေဏ သိဓျတိ ဝယံ တသ္မိန် ဝရ္တ္တာမဟေ တဒ် ဧတေနာဝဂစ္ဆာမး၊
Koma munthu aliyense akamvera mawu ake, ndiye kuti chikondi cha Mulungu chafikadi penipeni mwa iyeyo. Pamenepo timatsimikizadi kuti tili mwa Iye.
6 အဟံ တသ္မိန် တိၐ္ဌာမီတိ ယော ဂဒတိ တသျေဒမ် ဥစိတံ ယတ် ခြီၐ္ဋော ယာဒၖဂ် အာစရိတဝါန် သော 'ပိ တာဒၖဂ် အာစရေတ်၊
Aliyense amene amati amakhala mwa Mulungu, ayenera kukhala moyo umene Yesu ankakhala.
7 ဟေ ပြိယတမား, ယုၐ္မာန် ပြတျဟံ နူတနာမာဇ္ဉာံ လိခါမီတိ နဟိ ကိန္တွာဒိတော ယုၐ္မာဘိ ရ္လဗ္ဓာံ ပုရာတနာမာဇ္ဉာံ လိခါမိ၊ အာဒိတော ယုၐ္မာဘိ ရျဒ် ဝါကျံ ၑြုတံ သာ ပုရာတနာဇ္ဉာ၊
Okondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lakale lomwe lija, limene munali nalo kuyambira pachiyambi. Lamulo la kalelo ndi mawu amene munawamva kale.
8 ပုနရပိ ယုၐ္မာန် ပြတိ နူတနာဇ္ဉာ မယာ လိချတ ဧတဒပိ တသ္မိန် ယုၐ္မာသု စ သတျံ, ယတော 'န္ဓကာရော ဝျတျေတိ သတျာ ဇျောတိၑ္စေဒါနီံ ပြကာၑတေ;
Komabe ndi lamulo latsopano limene ndikukulemberani. Choonadi chake chikuoneka mwa Yesu ndiponso mwa inu, chifukwa mdima ukutha ndipo kuwunika kwenikweni kwayamba kale kuwala.
9 အဟံ ဇျောတိၐိ ဝရ္တ္တ ဣတိ ဂဒိတွာ ယး သွဘြာတရံ ဒွေၐ္ဋိ သော 'ဒျာပိ တမိသြေ ဝရ္တ္တတေ၊
Aliyense amene amati ali mʼkuwunika, koma nʼkumadana ndi mʼbale wake ali mu mdima.
10 သွဘြာတရိ ယး ပြီယတေ သ ဧဝ ဇျောတိၐိ ဝရ္တ္တတေ ဝိဃ္နဇနကံ ကိမပိ တသ္မိန် န ဝိဒျတေ၊
Aliyense amene amakonda mʼbale wake amakhalanso mʼkuwunika, ndipo mwa iye mulibe chokhumudwitsa.
11 ကိန္တု သွဘြာတရံ ယော ဒွေၐ္ဋိ သ တိမိရေ ဝရ္တ္တတေ တိမိရေ စရတိ စ တိမိရေဏ စ တသျ နယနေ 'န္ဓီကြိယေတေ တသ္မာတ် က္က ယာမီတိ သ ဇ္ဉာတုံ န ၑက္နောတိ၊
Koma aliyense wodana ndi mʼbale wake ali mu mdima ndipo akuyenda mu mdima. Iyeyo sakudziwa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa mʼmaso mwake.
12 ဟေ ၑိၑဝး, ယူယံ တသျ နာမ္နာ ပါပက္ၐမာံ ပြာပ္တဝန္တသ္တသ္မာဒ် အဟံ ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခါမိ၊
Inu ana okondedwa, ndikukulemberani popeza kuti machimo anu akhululukidwa chifukwa cha dzina la Yesu.
13 ဟေ ပိတရး, ယ အာဒိတော ဝရ္တ္တမာနသ္တံ ယူယံ ဇာနီထ တသ္မာဒ် ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခါမိ၊ ဟေ ယုဝါနး ယူယံ ပါပတ္မာနံ ဇိတဝန္တသ္တသ္မာဒ် ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခါမိ၊ ဟေ ဗာလကား, ယူယံ ပိတရံ ဇာနီထ တသ္မာဒဟံ ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခိတဝါန်၊
Inu abambo, ndikukulemberani popeza kuti munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani popeza kuti munagonjetsa woyipayo.
14 ဟေ ပိတရး, အာဒိတော ယော ဝရ္တ္တမာနသ္တံ ယူယံ ဇာနီထ တသ္မာဒ် ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခိတဝါန်၊ ဟေ ယုဝါနး, ယူယံ ဗလဝန္တ အာဓွေ, ဤၑွရသျ ဝါကျဉ္စ ယုၐ္မဒန္တရေ ဝရ္တတေ ပါပါတ္မာ စ ယုၐ္မာဘိး ပရာဇိဂျေ တသ္မာဒ် ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခိတဝါန်၊
Ana okondedwa, ndikukulemberani chifukwa mumawadziwa Atate. Abambo, ndikukulemberani chifukwa munamudziwa Iye amene analipo kuyambira pachiyambi. Inu anyamata, ndikukulemberani chifukwa ndinu amphamvu. Mawu a Mulungu amakhala mwa inu ndipo mumamugonjetsa woyipayo.
15 ယူယံ သံသာရေ သံသာရသ္ထဝိၐယေၐု စ မာ ပြီယဓွံ ယး သံသာရေ ပြီယတေ တသျာန္တရေ ပိတုး ပြေမ န တိၐ္ဌတိ၊
Musamakonde dziko lapansi kapena chilichonse cha dziko lapansi. Ngati munthu wina aliyense akonda dziko lapansi, mwa iyeyo mulibe chikondi chokonda Atate.
16 ယတး သံသာရေ ယဒျတ် သ္ထိတမ် အရ္ထတး ၑာရီရိကဘာဝသျာဘိလာၐော ဒရ္ၑနေန္ဒြိယသျာဘိလာၐော ဇီဝနသျ ဂရွွၑ္စ သရွွမေတတ် ပိတၖတော န ဇာယတေ ကိန္တု သံသာရဒေဝ၊
Pakuti zonse za mʼdziko lapansi, zilakolako za thupi, zinthu zimene maso amakhumbira ndiponso kuyandikira zinthu za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi.
17 သံသာရသ္တဒီယာဘိလာၐၑ္စ ဝျတျေတိ ကိန္တု ယ ဤၑွရသျေၐ္ဋံ ကရောတိ သော 'နန္တကာလံ ယာဝတ် တိၐ္ဌတိ၊ (aiōn g165)
Dziko lapansi likupita pamodzi ndi zilakolako zake, koma amene amachita chifuniro cha Mulungu amakhalapo mpaka muyaya. (aiōn g165)
18 ဟေ ဗာလကား, ၑေၐကာလော'ယံ, အပရံ ခြီၐ္ဋာရိဏောပသ္ထာဝျမိတိ ယုၐ္မာဘိ ရျထာ ၑြုတံ တထာ ဗဟဝး ခြီၐ္ဋာရယ ဥပသ္ထိတာသ္တသ္မာဒယံ ၑေၐကာလော'သ္တီတိ ဝယံ ဇာနီမး၊
Ana anga, ino ndi nthawi yotsiriza, ndipo monga munamva kale kuti anthu okana Khristu akubwera, ngakhale tsopano okana Khristu ambiri afika kale. Zimenezi zikutisonyeza kuti ino ndi nthawi yotsiriza.
19 တေ 'သ္မန္မဓျာန် နိရ္ဂတဝန္တး ကိန္တွသ္မဒီယာ နာသန် ယဒျသ္မဒီယာ အဘဝိၐျန် တရှျသ္မတ္သင်္ဂေ 'သ္ထာသျန်, ကိန္တု သရွွေ 'သ္မဒီယာ န သန္တျေတသျ ပြကာၑ အာဝၑျက အာသီတ်၊
Anthu amenewa anachoka pakati pathu, komatu sanali a mʼgulu lathu. Pakuti akanakhala a mʼgulu lathu, akanakhalabe nafe, koma kuchoka kwawo kunatisonyeza kuti sanali a mʼgulu lathu.
20 ယး ပဝိတြသ္တသ္မာဒ် ယူယမ် အဘိၐေကံ ပြာပ္တဝန္တသ္တေန သရွွာဏိ ဇာနီထ၊
Koma inu muli ndi kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo nonsenu mukudziwa choonadi.
21 ယူယံ သတျမတံ န ဇာနီထ တတ္ကာရဏာဒ် အဟံ ယုၐ္မာန် ပြတိ လိခိတဝါန် တန္နဟိ ကိန္တု ယူယံ တတ် ဇာနီထ သတျမတာစ္စ ကိမပျနၖတဝါကျံ နောတ္ပဒျတေ တတ္ကာရဏာဒေဝ၊
Sindikukulemberani chifukwa choti simudziwa choonadi ayi, koma chifukwa choti mumadziwa choonadicho, ndipo mukudziwanso kuti bodza silichokera pa choonadi.
22 ယီၑုရဘိၐိက္တသ္တြာတေတိ ယော နာင်္ဂီကရောတိ တံ ဝိနာ ကော 'ပရော 'နၖတဝါဒီ ဘဝေတ်? သ ဧဝ ခြီၐ္ဋာရိ ရျး ပိတရံ ပုတြဉ္စ နာင်္ဂီကရောတိ၊
Wabodzayo ndani? Ndi munthu aliyense amene amanena kuti Yesu si Mpulumutsi. Munthu woteroyo ndi wokana Khristu, ndiponso amakana Atate, ndi Mwana.
23 ယး ကၑ္စိတ် ပုတြံ နာင်္ဂီကရောတိ သ ပိတရမပိ န ဓာရယတိ ယၑ္စ ပုတြမင်္ဂီကရောတိ သ ပိတရမပိ ဓာရယတိ၊
Aliyense wokana Mwana alibenso Atate. Wovomereza Mwana alinso ndi Atate.
24 အာဒိတော ယုၐ္မာဘိ ရျတ် ၑြုတံ တဒ် ယုၐ္မာသု တိၐ္ဌတု, အာဒိတး ၑြုတံ ဝါကျံ ယဒိ ယုၐ္မာသု တိၐ္ဌတိ, တရှိ ယူယမပိ ပုတြေ ပိတရိ စ သ္ထာသျထ၊
Onetsetsani kuti zimene munazimva kuyambira pachiyambi zikhalebe mwa inu. Ngati zikhala mwa inu, inunso mudzakhala mwa Mwana ndiponso mwa Atate.
25 သ စ ပြတိဇ္ဉယာသ္မဘျံ ယတ် ပြတိဇ္ဉာတဝါန် တဒ် အနန္တဇီဝနံ၊ (aiōnios g166)
Ndipo chimene anatilonjeza nʼchimenechi: moyo wosatha. (aiōnios g166)
26 ယေ ဇနာ ယုၐ္မာန် ဘြာမယန္တိ တာနဓျဟမ် ဣဒံ လိခိတဝါန်၊
Ine ndikukulemberani zimenezi kuti ndikuwuzeni za amene akufuna kukusocheretsani.
27 အပရံ ယူယံ တသ္မာဒ် ယမ် အဘိၐေကံ ပြာပ္တဝန္တး သ ယုၐ္မာသု တိၐ္ဌတိ တတး ကော'ပိ ယဒ် ယုၐ္မာန် ၑိက္ၐယေတ် တဒ် အနာဝၑျကံ, သ စာဘိၐေကော ယုၐ္မာန် သရွွာဏိ ၑိက္ၐယတိ သတျၑ္စ ဘဝတိ န စာတထျး, အတး သ ယုၐ္မာန် ယဒွဒ် အၑိက္ၐယတ် တဒွတ် တတြ သ္ထာသျထ၊
Koma za inu, kudzoza kumene munalandira kwa Khristu kuli mwa inu, ndipo sipafunika wina aliyense kuti akuphunzitseni. Koma kudzozako kumakuphunzitsani zinthu zonse, ndipo popeza kudzoza kwakeko nʼkoona osati konama, monga munaphunzira, khalani mwa Iyeyo.
28 အတဧဝ ဟေ ပြိယဗာလကာ ယူယံ တတြ တိၐ္ဌတ, တထာ သတိ သ ယဒါ ပြကာၑိၐျတေ တဒါ ဝယံ ပြတိဘာနွိတာ ဘဝိၐျာမး, တသျာဂမနသမယေ စ တသျ သာက္ၐာန္န တြပိၐျာမဟေ၊
Tsopano ana okondedwa, khalani mwa Yesu, kuti pamene adzaonekera, ife tidzakhale otsimikizika mu mtima ndi wopanda manyazi pamaso pake akamadzabwera.
29 သ ဓာရ္မ္မိကော 'သ္တီတိ ယဒိ ယူယံ ဇာနီထ တရှိ ယး ကၑ္စိဒ် ဓရ္မ္မာစာရံ ကရောတိ သ တသ္မာတ် ဇာတ ဣတျပိ ဇာနီတ၊
Popeza mukudziwa kuti Khristu ndi wolungama, choncho mukudziwanso kuti aliyense amene amachita chilungamo ndi mwana wa Mulungu.

< ၁ ယောဟနး 2 >