< ၁ ကရိန္ထိနး 3 >

1 ဟေ ဘြာတရး, အဟမာတ္မိကဲရိဝ ယုၐ္မာဘိး သမံ သမ္ဘာၐိတုံ နာၑက္နဝံ ကိန္တု ၑာရီရိကာစာရိဘိး ခြီၐ္ဋဓရ္မ္မေ ၑိၑုတုလျဲၑ္စ ဇနဲရိဝ ယုၐ္မာဘိး သဟ သမဘာၐေ၊
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 ယုၐ္မာန် ကဌိနဘက္ၐျံ န ဘောဇယန် ဒုဂ္ဓမ် အပါယယံ ယတော ယူယံ ဘက္ၐျံ ဂြဟီတုံ တဒါ နာၑက္နုတ ဣဒါနီမပိ န ၑက္နုထ, ယတော ဟေတောရဓုနာပိ ၑာရီရိကာစာရိဏ အာဓွေ၊
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 ယုၐ္မန္မဓျေ မာတ္သရျျဝိဝါဒဘေဒါ ဘဝန္တိ တတး ကိံ ၑာရီရိကာစာရိဏော နာဓွေ မာနုၐိကမာရ္ဂေဏ စ န စရထ?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 ပေါ်လသျာဟမိတျာပလ္လောရဟမိတိ ဝါ ယဒွါကျံ ယုၐ္မာကံ ကဲၑ္စိတ် ကဲၑ္စိတ် ကထျတေ တသ္မာဒ် ယူယံ ၑာရီရိကာစာရိဏ န ဘဝထ?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 ပေါ်လး ကး? အာပလ္လော ရွာ ကး? တော် ပရိစာရကမာတြော် တယောရေကဲကသ္မဲ စ ပြဘု ရျာဒၖက် ဖလမဒဒါတ် တဒွတ် တယောရ္ဒွါရာ ယူယံ ဝိၑွာသိနော ဇာတား၊
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 အဟံ ရောပိတဝါန် အာပလ္လောၑ္စ နိၐိက္တဝါန် ဤၑွရၑ္စာဝရ္ဒ္ဓယတ်၊
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 အတော ရောပယိတၖသေက္တာရာဝသာရော် ဝရ္ဒ္ဓယိတေၑွရ ဧဝ သာရး၊
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 ရောပယိတၖသေက္တာရော် စ သမော် တယောရေကဲကၑ္စ သွၑြမယောဂျံ သွဝေတနံ လပ္သျတေ၊
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 အာဝါမီၑွရေဏ သဟ ကရ္မ္မကာရိဏော်, ဤၑွရသျ ယတ် က္ၐေတြမ် ဤၑွရသျ ယာ နိရ္မ္မိတိး သာ ယူယမေဝ၊
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 ဤၑွရသျ ပြသာဒါတ် မယာ ယတ် ပဒံ လဗ္ဓံ တသ္မာတ် ဇ္ဉာနိနာ ဂၖဟကာရိဏေဝ မယာ ဘိတ္တိမူလံ သ္ထာပိတံ တဒုပရိ စာနျေန နိစီယတေ၊ ကိန္တု ယေန ယန္နိစီယတေ တတ် တေန ဝိဝိစျတာံ၊
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 ယတော ယီၑုခြီၐ္ဋရူပံ ယဒ် ဘိတ္တိမူလံ သ္ထာပိတံ တဒနျတ် ကိမပိ ဘိတ္တိမူလံ သ္ထာပယိတုံ ကေနာပိ န ၑကျတေ၊
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 ဧတဒ္ဘိတ္တိမူလသျောပရိ ယဒိ ကေစိတ် သွရ္ဏရူပျမဏိကာၐ္ဌတၖဏနလာန် နိစိနွန္တိ,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 တရှျေကဲကသျ ကရ္မ္မ ပြကာၑိၐျတေ ယတး သ ဒိဝသသ္တတ် ပြကာၑယိၐျတိ၊ ယတော ဟတောသ္တန ဒိဝသေန ဝဟ္နိမယေနောဒေတဝျံ တတ ဧကဲကသျ ကရ္မ္မ ကီဒၖၑမေတသျ ပရီက္ၐာ ဗဟ္နိနာ ဘဝိၐျတိ၊
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 ယသျ နိစယနရူပံ ကရ္မ္မ သ္ထာသ္နု ဘဝိၐျတိ သ ဝေတနံ လပ္သျတေ၊
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 ယသျ စ ကရ္မ္မ ဓက္ၐျတေ တသျ က္ၐတိ ရ္ဘဝိၐျတိ ကိန္တု ဝဟ္နေ ရ္နိရ္ဂတဇန ဣဝ သ သွယံ ပရိတြာဏံ ပြာပ္သျတိ၊
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 ယူယမ် ဤၑွရသျ မန္ဒိရံ ယုၐ္မန္မဓျေ စေၑွရသျာတ္မာ နိဝသတီတိ ကိံ န ဇာနီထ?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 ဤၑွရသျ မန္ဒိရံ ယေန ဝိနာၑျတေ သော'ပီၑွရေဏ ဝိနာၑယိၐျတေ ယတ ဤၑွရသျ မန္ဒိရံ ပဝိတြမေဝ ယူယံ တု တန္မန္ဒိရမ် အာဓွေ၊
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 ကောပိ သွံ န ဝဉ္စယတာံ၊ ယုၐ္မာကံ ကၑ္စန စေဒိဟလောကသျ ဇ္ဉာနေန ဇ္ဉာနဝါနဟမိတိ ဗုဓျတေ တရှိ သ ယတ် ဇ္ဉာနီ ဘဝေတ် တဒရ္ထံ မူဎော ဘဝတု၊ (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 ယသ္မာဒိဟလောကသျ ဇ္ဉာနမ် ဤၑွရသျ သာက္ၐာတ် မူဎတွမေဝ၊ ဧတသ္မိန် လိခိတမပျာသ္တေ, တီက္ၐ္ဏာ ယာ ဇ္ဉာနိနာံ ဗုဒ္ဓိသ္တယာ တာန် ဓရတီၑွရး၊
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 ပုနၑ္စ၊ ဇ္ဉာနိနာံ ကလ္ပနာ ဝေတ္တိ ပရမေၑော နိရရ္ထကား၊
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 အတဧဝ ကော'ပိ မနုဇဲရာတ္မာနံ န ၑ္လာဃတာံ ယတး သရွွာဏိ ယုၐ္မာကမေဝ,
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 ပေါ်လ ဝါ အာပလ္လော ရွာ ကဲဖာ ဝါ ဇဂဒ် ဝါ ဇီဝနံ ဝါ မရဏံ ဝါ ဝရ္တ္တမာနံ ဝါ ဘဝိၐျဒွါ သရွွာဏျေဝ ယုၐ္မာကံ,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 ယူယဉ္စ ခြီၐ္ဋသျ, ခြီၐ္ဋၑ္စေၑွရသျ၊
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< ၁ ကရိန္ထိနး 3 >