< 2 Timothy 1 >

1 Paul, Khrista Jisua taka ringna om inkhâmna thurchi misîrna lama Pathien lungdoa Jisua Khrista tîrton renga han,
Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.
2 Ka nâipasal moroitak, Timothy kôm: Pathien ei Pa le Khrista Jisua ei Pumapa han moroina, inriengmuna le inngêina ngei nang pêk rese.
Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
3 Ki richibulngei renga sielesarietna inthiengtak dôna a sin ko tho pe ngâi Pathien kôm râisânchong ki misîr ngâi. Sûn le jân ku chubaithonangeia zoratin nang riettitin a kôm râisânchong ki misîr ngâi.
Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga.
4 Ni mitrithingei khom ki riettit ngâi, male râisânnân ka sip theina rangin nang mu rang ku nuom sabak ani.
Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe.
5 Taksônna, takintâina no dôn hah ki riettita, ma taksônna hah aphut han ni pi Lois kôm le nu nû Eunice kôm khom aom, nangma no kôm khom aom sa ti ki riet minthâr ani.
Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.
6 Ma sika han nu chunga ku kutngei ki minngam lâia Pathien'n neinunpêk nang a pêk hah minring tit rangin nang ka minrietnôk ani.
Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja.
7 Pathien Ratha mi pêk han ei thâimindôp maka; manêkin, ama Ratha'n sinthotheina, lungkhamna le indîntheinân mi min sip ngâi ani.
Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.
8 Hanchu ei Pumapa rietpuipu nina ha inzakpui nônla; keima Khrista jâra mi intâng khom hih mên zakpui uol no roh. Manêkin, Pathien'n Thurchi Sa sika tuong theina ranak nang a pêk ngâi anghan nu tuong rangtum hah tuong roh.
Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu.
9 Ama han ei sintho ngei sika niloiin, ama neinunkhîn le a moroina sikin mi sanminringa, a mingei ni rangin mi koi ani. Hi moroina hih Khrista Jisua han rammuol insieng mân mi pêk zoia, (aiōnios g166)
Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
10 aniatachu maha mi Sanminringpu Khrista Jisua juongna sikin atûn chu ei kôm minlangin aom zoi ani. Ama han thitheina ranak hah a min monga, male thurchisa renga han thitheiloina ringnun a minlang zoi.
Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe.
11 Thurchi Sa phuong rangin Pathien'n tîrton le minchupu'n ni phun zoi ani,
Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu.
12 male ma sika han kêng hi neinunngei khom hi ku tuong ani. Hannirese atûn tena khom ngamnân ka la sippuia, ka taksônpu hah tumo ani ti ki riet sikin, male ko kôma ni minkol hih ma Nikhuo ha atung mâka a rung thei ti ki riet mindik ani.
Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.
13 Chong dik nang ki minchu ngei hah sûr mindet tit roh, nu jûi ranga minenna ani anghan, Khrista Jisua leh inzoma eita, taksônna le lungkhamna han omtit roh.
Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu.
14 Ei kôma om ngâi, Ratha Inthieng sinthotheinân neinun asa ngei no kôma minkola om hah vong minsa roh.
Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.
15 Asia ramhuola om murdi'n min mâk ti ni rieta, Phygelus le Hermogenes ngei khom an inchel sa.
Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.
16 Pumapa'n Onesiphorus insûngmi ngei inriengmu ngei rese, ama han vêl tamtak mi minhar zoi sikin. Intângna ina ko om khom hi mên zakpui maka,
Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo.
17 aniatachu Rom a hong tung lehan mi roka, ni mu mâka ni rok titir ani.
Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza.
18 Pumapa'n ha Nikhuo han a inriengmuna pêk rese! Male Ephesus taka keima rangin idôrmo sin a tho khom ni riet minthâr sabak ani.
Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

< 2 Timothy 1 >