< Yohana 12 >
1 Isiku ilya sita selisele ePasaka, oYesu abhalile hu Bethania, hwa hali oLazalo, omwene wali avyonshele afume hwa bhafwe.
Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa.
2 Bhalenganyizya eshalye shana ndabhela owho, no Martha abhombelaga owakati owo oLazaro ahali pamo na bhale bhabhakheye pashalye pandwemo no Yesu.
Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho.
3 Pamande oMariamu ahege eratli ye manukato gagalenganyiziwe hu nardo enyinza, gagali ne maana engosi, wapaha oYesu mumagaga, na husyomole hwi sisi lyakwe; enyumba yonti yamemile nunsi gwe manukato.
Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.
4 O Yuda Iskariote, omo we bhanafunzi bhakwe, ambaye wanzahugalushe oYesu, ajile,
Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati,
5 “Yenu amanukato ega segagalu ziwanyaga huu mpeya mia zitatu na bhapele apena?”
“Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi.
6 Wope ayanjile ego, sio aje hubhasajile apena, afuatanaje ali mwibha: omwene ali wa bheshe ehela na ali ahwega zimo zyazibhelwe omwo zya mwene yoyo.
Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.
7 O Yesu ajile, “Leshi abheshe hali naho alengane ni siku lya syelwe hwane.
Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga.
8 Apena mwaibha nabho ensiku zyonti ila ane semwaibha nane ensiku zyontii.”
Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”
9 Owinji ogosi wa Yahudi bhapete amanye aje oYesu ali ohwo bhopebhenza, sio aje yo Yesu tu ila bhalole no Lazaro ola oYesu wavyonsezye afume hwa bhafwe.
Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa.
10 Bhope agosi bhayangene aje wagoje oLazaro;
Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro,
11 alengane no mwale abhinji katika Wayahudi walienda zao bha bhalile ahumweteshela oYesu.
pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.
12 Na isiku ila bhele uwinji gosi wali hushikulukulu bhahonvwezye aje oYesu ahwenza hu Yelusalemu,
Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu.
13 bhahejile amasamba ge mikwige mitende na afume hoze na abhale ahumwejelele na bhakhomile ekelele, “Hosana! Asailwe wahwenza hwitawa lya Gosi, Omwene we Israeli.”
Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti, “Hosana! “Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye! “Yodala Mfumu ya Israeli!”
14 O Yesu ayeje enyana-ye punda ayipandale; nanshi shila shehandihwe,
Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:
15 “Oganje ahwogope, lendu Sayuni; enya, Omwene waho ahwenza, apende enyana-ye punda.”
“Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni; taona mfumu yako ikubwera, itakhala pa mwana wabulu.”
16 Abhanafunzi bhakwe sebhagelee amambo ega epo ahwande; ila oYesu na mwamihwe, nkabhakomboha aje amambo ega gahandihwe na huje abhombile amambo ega hwa mwene.
Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.
17 Lila ikundi lyalya pandwemo no Yesu lula lwa kwizyaga oLazaro afume mwilende, bhahakikisya hwabhanje.
Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni.
18 Yali alengane neshi aje uwinji wa bhantu bhabhalile ahuposhele alenganaje bhahomvwezye aje abhombole embo eyo.
Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi.
19 Amafarisayo bhakwepelana bhene hwa bhene, “Enya, esalezi semuwezizey abhombe lya lyonti; enya, ensi ebhalile hwa mwene.”
Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”
20 Bhamo Ayunani bhali pandwemo na bhala bhabhalile apute hushikulukulu.
Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando.
21 Ebhabhaliye oFilipo, wafumile Betsaida ye Galilaya, bhalabha bhaga, “Gosi, ate tiziliha ahulole oYesu.”
Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.”
22 O Filipo ahabhala abhozya o Andrea; Andrea no Filipo bhabha ahubhozye oYesu.
Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.
23 O Yesu ayanga ahaga, “Esala efishile hwa Mwana wa Adamu amwamihwe.
Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe.
24 Etesheli, etesheli, embabhozya, abhenyu he ngano nkase hagwiye pansi hafwa, hakhala shesho hene; ila nkahafwa, hana pape endondo zinyinji.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’
25 Omwane wasongwa owomi wakwe anzautezye; ila ola wauvitwa owomi wakwe munsi omu anzaugolosye hata womi wewila wila. (aiōnios )
Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. (aiōnios )
26 Omuntu wawonti wanza ambombele ane, andondolelaje; nane pehwendi omuntu wane paibha. Omuntu wawonti wabhombela ane anzanogope.
Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.
27 Esalezi omwoyo gwane guhwalangana: nane enje bhole? 'Odaada, anfyozye esala ene'? Ndio maana enjifishiye esala ene.
“Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi.
28 Odaada, alimwamishe itawa lyaho.” Izu ilinza afume humwanya na huje, “Endimwamisha nantele embali mwamishe nantele.”
Atate, lemekezani dzina lanu!” Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.”
29 Olubhongano lwalwahemeleye peepe nawo bhahonvwa, bhayanga aje huli omungurumo. Bhamo bhajile, “Ohalo ozelu ayanjile nawo.”
Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”
30 O Yesu abhabhoyza naje, “Izu ili selya henzele huline, ila hwalimwe.
Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine.
31 Esalezi oulonje wensi ene ehweli: Esalezi ogosi wensi aitagwa honze.
Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa.
32 Nane nkemwamihwe munsi, embarute bhonti huline.”
Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.”
33 Wayanjile ego abhonesyaga aje enfwa bhole ya mwaifwa.
Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.
34 Olubhongano lwaga, “Ate tonvwezye hundajizyo aje oKillisiti aibha wilawila. Awe oiga bhole, 'Omwana wa Adamu amwamihwe pamwanya'? Ono Omwana wa Muntu wenu?” (aiōn )
Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?” (aiōn )
35 O Yesu abhabhozya, “Olukhozyo luhweli pandwemo namwe omuda ododo. Bhalaji afuatane naje mlinalyo olukhozyo, aje enkisi nkepotwe aitole. Omwene wabhala munkisi samenye hwabhala.
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita.
36 Muli nalwo olukhozyo, lweteshelaji olukhozyo olwo nkamubhe bhana bhelukhozyo.” O Yesu ayanjile ega ahwisogolela ahobha bha salole.
Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.
37 Japo oYesu abhombile eishara nyinji witazi lyabho, ila sebha mwetesheye
Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe.
38 lifishe izu lya kuwaa oIsaya, lyayanjile: “Gosi, wenu waizyeteshela enongwa zyetu? Okhono gwa Gosi gwiguliwe wenu?”
Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti: “Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani, ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”
39 Ndio maana abhene sebhahetesheye, alengane naje oIsaya ayanjile nantele,
Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:
40 “Abhadiye amaso, na agabheshele makhome amoyo gabho, bhageteha engabhaponia.”
“Iye wachititsa khungu maso awo ndi kuwumitsa mitima yawo, kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo, kapena kuzindikira ndi mitima yawo, kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”
41 O Isaya ayanjile enongwa ezi afuatanaje alolile oumwamu wa Yesu na ayanjile enongwa zyakwe.
Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.
42 Ila, hata bhagosi abhinji bhamweteshe oYesu; ila alengane na Mafarisayo, sebhaheteha bhahogope atengwe msibhanza.
Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge;
43 Bhasongwelwe ahwilole hwa bhantu ahwilole ahwilole hwa Ngolobhe.
pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.
44 O Yesu afumizye izu lyakwe naje, “Omwene waneteshela ane, saneteshela nene wene ila nola wantumile ane,
Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine.
45 omwane wambonela ane ahubho ane ahubhonela yayola wantumile.
Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine.
46 Ane nahenzele nanshi olukhozyo munsi aje shila muntu waneteshela aganje akhale munkisi.
Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.
47 Nkashe omuntu wawonti anzahonvwe amazu gane sagakhata, ane sehulonga; afuatanaje sagahenzele ailonje insi ila injifyole insi.
“Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa.
48 Omwene wananza ane nkasage teha amazu gane, ali nawo wahulonga: izu ilyo lyenjenjile lyalyaihulonga isiku lya mwisho.
Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa.
49 Afwanaje ane senayanjile hunafsi yane. Ila yo Daada wantumile, omwene yoyo andajizizye lye mbalombelele na yanje.
Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere.
50 Ane emenye aje endajizyo zyakwe zye womi wewilawila; ila ego gelombelela ane - nanshi Odaada shambozezye, shashesho shelombelela hwa bhene.” (aiōnios )
Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.” (aiōnios )