< Abhagalatia 2 >
1 Afume amaha kuminanne na bhabile habhili muYerusalemu peka nu Barnaba. Pia nahamwejihe u Tito nabhalile pipo Ungulubhi ayimanyisishye huline aje ihwanziwa imbale.
Kenaka, patatha zaka khumi ndi zinayi, ndinapitanso ku Yerusalemu, nthawi iyi ndinapita ndi Barnaba. Ndinatenganso Tito kuti apite nafe.
2 Nahabhishile mwilongolela lyabhoizwi lye mlumbileye hubhantu abhinsi. (Lelo na yinje hwa hwifise yalolosya jobhalongozi kamili). Nabho mbile iishi aje imanye aje sinshimbila pamo senashimbiye lwene.
Ine ndinapita chifukwa Mulungu anachita kundionetsera kuti ndipite ndipo ndinakakumana ndi atsogoleri mu msonkhano mwamseri ndi kuwafotokozera Uthenga Wabwino umene ndimalalikira pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinachita zimenezi kuti ndikhale ndi chitsimikizo kuopa kuti mwina ndinathamanga kapena ndimathamanga liwiro pachabe.
3 Lelo hata yu Tito, ahali peka nani, yahali mu yahali Muyunani, alazimisizwe atahiliwe.
Komatu ngakhale Tito, amene anali nane sanakakamizidwe kuti achite mdulidwe, ngakhale iyeyo anali Mgriki.
4 Ijambo ili lyahafumiye pipo ya holo abhilenga bhebhahinzile hufiso apelelezye uwabhushe wetulinawo mwa Kiristi Yesu. Bhanyonyilwe aje tibhe bhatumwa bhindajizyo.
Nkhani iyi inayambika chifukwa abale ena achinyengo amene analowerera pakati pathu kuti adzaone za ufulu umene tili nawo mwa Khristu Yesu ndikuti atisandutse akapolo.
5 Setwa yifumizye hubhitishe hata hwi saa lyeka, huje izwi ilyilyoli lisyale bila agahuhake humwuyu.
Ife sitinawagonjere ndi pangʼono pomwe, nʼcholinga chakuti choonadi cha Uthenga Wabwino chikhalebe ndi ife.
6 Lelo bhala bhebhayangwilwe aje bhahali bhalongozi sebhasanjiye hohonti huline honti hebhobho mbaga seshali shi maana huline. Ungulubhi sahwitiha uupendeleo wa bhanadamu.
Koma kunena za aja ankaoneka ngati ofunika kwambiri, chimene iwo anali sichisintha kanthu kwa ine; chifukwa Mulungu alibe tsankho, iwowo sanawonjezepo kanthu pa uthenga wanga.
7 Pamandi bhahandola initihwilwe alumbilile izwi hubhala bhesaga bhatahililwe. Ihali ndeshe u Petro alumbilile izwi hwa bhalasaga bhatahililwe.
Makamaka anaona kuti ine ndinapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa anthu a mitundu ina monga momwe Petro anapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa Ayuda.
8 Ungulubhi yayibhombile imbombo muhati uwa Petro hwa tumwa bhebhatahililwe ahabhombile imbombo hati yani na mubhantu abha munsi.
Pakuti Mulungu, amene amagwira ntchito mu utumiki wa Petro monga mtumwi kwa Ayuda, amagwiranso ntchito mu utumiki wanga monga mtumiki kwa anthu a mitundu ina.
9 Lula u Yakobo, nu Yohani, nu Kefa, bhaloleshe aje bhahazenjile ishibhanza, bhahaminye uwene wenapewilwe ani bhatiposhile hushibanza ani nu Barnaba. Bhahabhombilishi aje tibhale hubhantu abha munsi nkebhabhale hubhala bhebhatahiliwilwe.
Yakobo, Petro ndi Yohane, amene ankatengedwa ngati mizati, atazindikira chisomo chimene chinapatsidwa kwa ine, anagwirana chanza ndi ine ndi Barnaba kusonyeza chiyanjano chathu. Iwo anavomereza kuti ife tipite kwa anthu a mitundu ina ndipo iwo apite kwa Ayuda.
10 Tena bhatwanzile ati hubhakumbushe apina nani wayonahasungwizye abhombe imbombo iyo.
Chimene iwo anapempha ndi chakuti ife tipitirize kukumbukira osauka, chinthu chimene ine ndinali okonzeka kuchichita.
11 U Kefa na ahinza huAntiokia, nahankhanile waziwazi pipo ahakosiye.
Petro atafika ku Antiokeya, ine ndinamudzudzula pa gulu chifukwa anapezeka wolakwa.
12 Kabla yi bhantu bhano afume hwa Yakobo na bhantu bhinsi. Lakini abhantu bhala ne bhahinza ahaleshile na sogole afume hwa bhantu abhinsi. Ahogopaga abhantu bhebha hwanza itohala.
Pakuti asanafike anthu otumidwa ndi Yakobo, iye ankadya pamodzi ndi anthu a mitundu ina. Koma atafika, iyeyo anachoka pakati pa anthuwo nakakhala pa yekha chifukwa ankaopa anthu a mʼgulu la mdulidwe.
13 Tena Abhayahudi bhamo bhaha bhwagana nubhunafiki peka nu Kefa. Amatoke gahaliishi hata yu Barnaba ahinjiye mubhunafiki uwo.
Ayuda enanso anamutsata pochita zachinyengozi, kotero kuti ngakhale Barnaba anasocheretsedwa chifukwa cha chinyengo chawocho.
14 Lakini lwenalolaje sebhalifwata ibhangili ilyi lyoli nahamuzizye u Kefa pamaso gabho bhonti amwe nke mwe Bhayahudi, mlinitabia zya bhantu bhi mataifa badala yi tabia zyi shiyahudi?”
Koma nditaona kuti iwo sankachita molingana ndi choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinawuza Petro pamaso pa anthu onse kuti, “Iwe ndiwe Myuda koma ukukhala ngati munthu wa mtundu wina, osati Myuda. Nanga nʼchifukwa chiyani ukukakamiza anthu a mitundu ina kuti akhale ngati Ayuda?
15 Ati twebhayahudi apapwe se bhantu bhi insi abhi mbibhi”
“Ife amene ndife Ayuda mwachibadwa, osati anthu a mitundu ina ochimwa,
16 mmanye aje numo yabhaziwa ilyoli humatendo gisheria. Badala yakwe bhabhaziwa ilyoli muhati mwa Yesu Kilisti, twahonzile nulwitiho muhati mwa Yesu Kristu. Ili huje tibhaziwe ilyoli hulwitiho muhati mwa Yesu na siyo amatendo gi shelia. Humatendo gishelia nagumo umbili gwewayabhaziwa ilyoli.
tikudziwa kuti munthu salungamitsidwa pochita ntchito za lamulo koma ndi chikhulupiriro mwa Yesu Khristu. Chomwecho, ifenso tinakhulupirira Khristu Yesu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro mwa Khristu ndipo osati pochita ntchito za lamulo, chifukwa palibe amene adzalungamitsidwa pochita ntchito za lamulo.
17 Lakini nike tihumwanza Ungulubhi atibhazizye ilyoli, muhati mwa Kilisti tiyilola tiniti aje tilini mbibhi, je uKilisti abhombilwe ntumwa wimbibhi? Seshi nisho!
“Tsono ngati ife, pamene tikufuna kulungamitsidwa mwa Khristu, zikuonekeratu poyera kuti ndifenso ochimwa, kodi zikutanthauza kuti Khristu amalimbikitsa uchimo? Ayi. Nʼkosatheka!
18 Nkenazenga usubhilo gwani adime ishelia isubhuli lyenaluyu injilolesya nini aje imvunza ishelia.
Ngati ine ndimanganso chimene ndinachigumula, ndikuonetsa kuti ndine wophwanya lamulo.
19 Asilile musheha mfwiye mushelia kwahiyo uhwanziwa akhale munyobhe zya Ngulubhi.
“Pakuti pamene ndinayesera kutsatira lamulo, lamulolo linandionetsa kuti ndine wochimwa. Choncho ndinasiya kutsatira lamulo kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu.
20 Injimbihe peka nu Yesu. Senini habhili yikhala ila yu Yesu akhala muhati muline. Amaisha giakala aga mumbili inkhala hulwitiho. Muhati mwa Ngulubhi ya ngiine ani ahayifumya kwajili yaline.
Ndinapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano mʼthupi lino, ndi moyo mwachikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu, amene anandikonda nadzipereka yekha chifukwa cha ine.
21 Tejelezya uweene wa Ngulubhi nkushele ilyoli yaliho ashilile nasi uYesu handi afwiye bure.
Ine sindikukankhira kumbali chisomo cha Mulungu, chifukwa ngati chilungamo chikanapezeka pochita ntchito za lamulo, ndiye kuti Khristu anafa pachabe.”