< Притчи 8 >

1 Не премудрость ли взывает? и не разум ли возвышает голос свой?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Она становится на возвышенных местах, при дороге, на распутиях;
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 она взывает у ворот при входе в город, при входе в двери:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 “К вам, люди, взываю я, и к сынам человеческим голос мой!
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Научитесь, неразумные, благоразумию, и глупые - разуму.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Слушайте, потому что я буду говорить важное, и изречение уст моих - правда;
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 ибо истину произнесет язык мой, и нечестие - мерзость для уст моих;
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 все слова уст моих справедливы; нет в них коварства и лукавства;
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 все они ясны для разумного и справедливы для приобретших знание.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Примите учение мое, а не серебро; лучше знание, нежели отборное золото;
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 потому что мудрость лучше жемчуга, и ничто из желаемого не сравнится с нею.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Я, премудрость, обитаю с разумом и ищу рассудительного знания.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Страх Господень - ненавидеть зло; гордость и высокомерие и злой путь и коварные уста я ненавижу.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 У меня совет и правда; я разум, у меня сила.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Мною цари царствуют и повелители узаконяют правду;
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 мною начальствуют начальники и вельможи и все судьи земли.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Любящих меня я люблю, и ищущие меня найдут меня;
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 богатство и слава у меня, сокровище непогибающее и правда;
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 плоды мои лучше золота, и золота самого чистого, и пользы от меня больше, нежели от отборного серебра.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Я хожу по пути правды, по стезям правосудия,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 чтобы доставить любящим меня существенное благо, и сокровищницы их я наполняю. Когда я возвещу то, что бывает ежедневно, то не забуду исчислить то, что от века.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 Господь имел меня началом пути Своего, прежде созданий Своих, искони;
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 от века я помазана, от начала, прежде бытия земли.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Я родилась, когда еще не существовали бездны, когда еще не было источников, обильных водою.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Я родилась прежде, нежели водружены были горы, прежде холмов,
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 когда еще Он не сотворил ни земли, ни полей, ни начальных пылинок вселенной.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Когда Он уготовлял небеса, я была там. Когда Он проводил круговую черту по лицу бездны,
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 когда утверждал вверху облака, когда укреплял источники бездны,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 когда давал морю устав, чтобы воды не переступали пределов его, когда полагал основания земли:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 тогда я была при Нем художницею, и была радостью всякий день, веселясь пред лицом Его во все время,
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 веселясь на земном кругу Его, и радость моя была с сынами человеческими.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Итак, дети, послушайте меня; и блаженны те, которые хранят пути мои!
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Послушайте наставления и будьте мудры, и не отступайте от него.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Блажен человек, который слушает меня, бодрствуя каждый день у ворот моих и стоя на страже у дверей моих!
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 потому что, кто нашел меня, тот нашел жизнь, и получит благодать от Господа;
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 а согрешающий против меня наносит вред душе своей: все ненавидящие меня любят смерть”.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Притчи 8 >