< Иов 38 >

1 Когда Елиуй перестал говорить, Господь отвечал Иову из бури и сказал:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 кто сей, омрачающий Провидение словами без смысла?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Препояшь ныне чресла твои, как муж: Я буду спрашивать тебя, и ты объясняй Мне:
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 где был ты, когда Я полагал основания земли? Скажи, если знаешь.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Кто положил меру ей, если знаешь? или кто протягивал по ней вервь?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 На чем утверждены основания ее, или кто положил краеугольный камень ее,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 при общем ликовании утренних звезд, когда все сыны Божии восклицали от радости?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Кто затворил море воротами, когда оно исторглось, вышло как бы из чрева,
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 когда Я облака сделал одеждою его и мглу пеленами его,
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 и утвердил ему Мое определение, и поставил запоры и ворота,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 и сказал: доселе дойдешь и не перейдешь, и здесь предел надменным волнам твоим?
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Давал ли ты когда в жизни своей приказания утру и указывал ли заре место ее,
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 чтобы она охватила края земли и стряхнула с нее нечестивых,
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 чтобы земля изменилась, как глина под печатью, и стала, как разноцветная одежда,
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 и чтобы отнялся у нечестивых свет их и дерзкая рука их сокрушилась?
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Нисходил ли ты во глубину моря и входил ли в исследование бездны?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Отворялись ли для тебя врата смерти, и видел ли ты врата тени смертной?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Обозрел ли ты широту земли? Объясни, если знаешь все это.
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Где путь к жилищу света, и где место тьмы?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Ты, конечно, доходил до границ ее и знаешь стези к дому ее.
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Ты знаешь это, потому что ты был уже тогда рожден, и число дней твоих очень велико.
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Входил ли ты в хранилища снега и видел ли сокровищницы града,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 которые берегу Я на время смутное, на день битвы и войны?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 По какому пути разливается свет и разносится восточный ветер по земле?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Кто проводит протоки для излияния воды и путь для громоносной молнии,
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 чтобы шел дождь на землю безлюдную, на пустыню, где нет человека,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 чтобы насыщать пустыню и степь и возбуждать травные зародыши к возрастанию?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Есть ли у дождя отец? или кто рождает капли росы?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Из чьего чрева выходит лед, и иней небесный, - кто рождает его?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Воды, как камень, крепнут, и поверхность бездны замерзает.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Можешь ли ты связать узел Хима и разрешить узы Кесиль?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Можешь ли выводить созвездия в свое время и вести Ас с ее детьми?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Знаешь ли ты уставы неба, можешь ли установить господство его на земле?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Можешь ли возвысить голос твой к облакам, чтобы вода в обилии покрыла тебя?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Можешь ли посылать молнии, и пойдут ли они и скажут ли тебе: вот мы?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Кто вложил мудрость в сердце, или кто дал смысл разуму?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Кто может расчислить облака своею мудростью и удержать сосуды неба,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 когда пыль обращается в грязь и глыбы слипаются?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Ты ли ловишь добычу львице и насыщаешь молодых львов,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 когда они лежат в берлогах или покоятся под тенью в засаде?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Кто приготовляет ворону корм его, когда птенцы его кричат к Богу, бродя без пищи?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Иов 38 >