< Иов 23 >

1 И отвечал Иов и сказал:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 еще и ныне горька речь моя: страдания мои тяжелее стонов моих.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 О, если бы я знал, где найти Его, и мог подойти к престолу Его!
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Я изложил бы пред Ним дело мое и уста мои наполнил бы оправданиями;
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 узнал бы слова, какими Он ответит мне, и понял бы, что Он скажет мне.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Неужели Он в полном могуществе стал бы состязаться со мною? О, нет! Пусть Он только обратил бы внимание на меня.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Тогда праведник мог бы состязаться с Ним, - и я навсегда получил бы свободу от Судии моего.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 Но вот, я иду вперед - и нет Его, назад - и не нахожу Его;
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 делает ли Он что на левой стороне, я не вижу; скрывается ли на правой, не усматриваю.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Но Он знает путь мой; пусть испытает меня, - выйду, как золото.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Нога моя твердо держится стези Его; пути Его я хранил и не уклонялся.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 От заповеди уст Его не отступал; глаголы уст Его хранил больше, нежели мои правила.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Но Он тверд; и кто отклонит Его? Он делает, чего хочет душа Его.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 Так, Он выполнит положенное мне, и подобного этому много у Него.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Поэтому я трепещу пред лицом Его; размышляю - и страшусь Его.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Бог расслабил сердце мое, и Вседержитель устрашил меня.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Зачем я не уничтожен прежде этой тьмы, и Он не сокрыл мрака от лица моего!
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Иов 23 >