< Иов 20 >

1 И отвечал Софар Наамитянин и сказал:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 размышления мои побуждают меня отвечать, и я поспешаю выразить их.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Упрек, позорный для меня, выслушал я, и дух разумения моего ответит за меня.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Разве не знаешь ты, что от века, - с того времени, как поставлен человек на земле, -
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 веселье беззаконных кратковременно, и радость лицемера мгновенна?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Хотя бы возросло до небес величие его, и голова его касалась облаков, -
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 как помет его, на веки пропадает он; видевшие его скажут: где он?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Как сон, улетит, и не найдут его; и, как ночное видение, исчезнет.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Глаз, видевший его, больше не увидит его, и уже не усмотрит его место его.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Сыновья его будут заискивать у нищих, и руки его возвратят похищенное им.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Кости его наполнены грехами юности его, и с ним лягут они в прах.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Если сладко во рту его зло, и он таит его под языком своим,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 бережет и не бросает его, а держит его в устах своих,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 то эта пища его в утробе его превратится в желчь аспидов внутри его.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Имение, которое он глотал, изблюет: Бог исторгнет его из чрева его.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Змеиный яд он сосет; умертвит его язык ехидны.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 Не видать ему ручьев, рек, текущих медом и молоком!
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Нажитое трудом возвратит, не проглотит; по мере имения его будет и расплата его, а он не порадуется.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Ибо он угнетал, отсылал бедных; захватывал дома, которых не строил;
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 не знал сытости во чреве своем и в жадности своей не щадил ничего.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Ничего не спаслось от обжорства его, зато не устоит счастье его.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 В полноте изобилия будет тесно ему; всякая рука обиженного поднимется на него.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Когда будет чем наполнить утробу его, Он пошлет на него ярость гнева Своего и одождит на него болезни в плоти его.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 Убежит ли он от оружия железного, - пронзит его лук медный;
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 станет вынимать стрелу, - и она выйдет из тела, выйдет, сверкая сквозь желчь его; ужасы смерти найдут на него!
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Все мрачное сокрыто внутри его; будет пожирать его огонь, никем не раздуваемый; зло постигнет и оставшееся в шатре его.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Небо откроет беззаконие его, и земля восстанет против него.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Исчезнет стяжание дома его; все расплывется в день гнева Его.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Вот удел человеку беззаконному от Бога и наследие, определенное ему Вседержителем!
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Иов 20 >