< Иов 13 >

1 Вот, все это видело око мое, слышало ухо мое и заметило для себя.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Сколько знаете вы, знаю и я: не ниже я вас.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Но я к Вседержителю хотел бы говорить и желал бы состязаться с Богом.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 А вы сплетчики лжи; все вы бесполезные врачи.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 О, если бы вы только молчали! это было бы вменено вам в мудрость.
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Выслушайте же рассуждения мои и вникните в возражение уст моих.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Надлежало ли вам ради Бога говорить неправду и для Него говорить ложь?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Надлежало ли вам быть лицеприятными к Нему и за Бога так препираться?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Хорошо ли будет, когда Он испытает вас? Обманете ли Его, как обманывают человека?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Строго накажет Он вас, хотя вы и скрытно лицемерите.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Неужели величие Его не устрашает вас, и страх Его не нападает на вас?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Напоминания ваши подобны пеплу; оплоты ваши - оплоты глиняные.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Замолчите предо мною, и я буду говорить, что бы ни постигло меня.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Для чего мне терзать тело мое зубами моими и душу мою полагать в руку мою?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Вот, Он убивает меня, но я буду надеяться; я желал бы только отстоять пути мои пред лицом Его!
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 И это уже в оправдание мне, потому что лицемер не пойдет пред лице Его!
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Выслушайте внимательно слово мое и объяснение мое ушами вашими.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Вот, я завел судебное дело: знаю, что буду прав.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Кто в состоянии оспорить меня? Ибо я скоро умолкну и испущу дух.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Двух только вещей не делай со мною, и тогда я не буду укрываться от лица Твоего:
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 удали от меня руку Твою, и ужас Твой да не потрясает меня.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Тогда зови, и я буду отвечать, или буду говорить я, а Ты отвечай мне.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Сколько у меня пороков и грехов? покажи мне беззаконие мое и грех мой.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Для чего скрываешь лице Твое и считаешь меня врагом Тебе?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Не сорванный ли листок Ты сокрушаешь и не сухую ли соломинку преследуешь?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Ибо Ты пишешь на меня горькое и вменяешь мне грехи юности моей,
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 и ставишь в колоду ноги мои и подстерегаешь все стези мои, - гонишься по следам ног моих.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 А он, как гниль, распадается, как одежда, изъеденная молью.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Иов 13 >