< ЗАХАРИЯ 5 >
1 Ам ридикат дин ноу окий ши м-ам уйтат; ши ятэ кэ ера ун сул де карте каре збура.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 Ел м-а ынтребат: „Че везь?” Еу ам рэспунс: „Вэд ун сул де карте збурынд; аре о лунӂиме де доуэзечь де коць ши о лэциме де зече коць.”
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Ши ел мь-а зис: „Ачеста есте блестемул каре есте песте тоатэ цара, кэч, дупэ кум есте скрис пе ел, орьче хоц ши орьчине журэ стрымб вор фи нимичиць ку десэвыршире де аич.”
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 „Ыл тримит”, зиче Домнул оштирилор, „ка сэ интре ын каса хоцулуй ши а челуй че журэ стрымб ын Нумеле Меу, ка сэ рэмынэ ын каса ачея ши с-о мистуе ымпреунэ ку лемнеле ши петреле ей.”
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 Ынӂерул каре ворбя ку мине а ынаинтат ши мь-а зис: „Ридикэ окий ши привеште че есе де аколо!”
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 Еу ам рэспунс: „Че есте ачаста?” Ши ел а зис: „Иесе ефа.” Ши а адэугат: „Ачаста есте нелеӂюиря лор ын тоатэ цара.”
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 Ши ятэ кэ се ридика ун талант де плумб ши, ын мижлокул ефей, шедя о фемее.
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 Ел а зис: „Ачаста есте нелеӂюиря!” Ши й-а дат брынчь ын ефэ ши а арункат буката де плумб песте гура ефей.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Ам ридикат окий ши м-ам уйтат; ши ятэ кэ с-ау арэтат доуэ фемей. Ын арипиле лор суфла вынтул: еле авяу арипь ка але кокостыркулуй. Ау ридикат ефа ынтре пэмынт ши чер.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Атунчь ам ынтребат пе ынӂерул каре ворбя ку мине: „Унде дук еле ефа?”
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 Ел мь-а рэспунс: „Се дук сэ-й зидяскэ о касэ ын цара Шинеар, ка сэ фие ашезатэ аколо ши сэ рэмынэ пе локул ей.”
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”